< I Samuela 2 >

1 Tedy się modliła Anna, i rzekła: Rozweseliło się serce moje w Panu, wywyższon jest róg mój w Panu, rozszerzyły się usta moje przeciw nieprzyjaciołom moim; albowiemem się rozradowała w zbawieniu twojem.
Ndipo Hana anapemphera nati, “Moyo wanga ukukondwera mwa Yehova; Ndiyenda mwa tukumutukumu chifukwa cha Yehova. Pakamwa panga pakula ndi kuseka adani anga mowanyogodola. Ndikukondwa chifukwa mwandipulumutsa.
2 Niemaszci świętego jako Pan; bo niemasz innego oprócz ciebie, i niemasz tak mocnego, jak Bóg nasz.
“Palibe wina woyera ngati Yehova, palibe wina koma inu nokha, palibe thanthwe lofanana ndi Mulungu wathu.
3 Niemówcież napotem słów pysznych, a niech nie wychodzą słowa harde z ust waszych; albowiem Bóg jest umiejętności Panem, a nadawają się sprawy jego.
“Musandiyankhulenso modzitama, pakamwa panu pasatuluke zonyada, pakuti Yehova ndi Mulungu wanzeru, ndipo ndiye amene amayesa ntchito za anthu onse.
4 Łuk i mocarze pokruszeni są, a mdli przepasani są mocą.
“Mauta a anthu ankhondo athyoka koma anthu ofowoka avala dzilimbe.
5 Którzy byli nasyceni, najmują się za chleb, a głodni przestali łaknąć; tak iż niepłodna siedmioro porodziła, a która rodziła wiele dziatek, zemdlała.
Amene kale anali okhuta tsopano akukagula chakudya, koma iwo amene anali ndi njala sakumvanso njala. Amene anali wosabereka, wabereka ana aamuna asanu ndi awiri, koma iye wobereka ana ambiri watsala yekha.
6 Pan zabija i ożywia, wwodzi do grobu i wywodzi. (Sheol h7585)
“Yehova amabweretsa imfa ndipo amaperekanso moyo, amatsitsira ku manda ndipo amawatulutsakonso. (Sheol h7585)
7 Pan ubogiego czyni i zbogaca, uniża i wywyższa.
Yehova amasaukitsa ndipo amalemeretsa, amatsitsa ndipo amakweza.
8 Wzbudza z prochu ubogiego, a z gnoju podnosi żebraka, aby je posadził z książęty, a dał im stolicę chwalebną osiadać; albowiem Pańskie są grunty ziemi, a na nich założył świat.
Iye amakweza osauka kuwachotsa pa fumbi, ndipo amachotsa anthu osowa pa dzala. Iye amawakhazika pamodzi ndi ana a mafumu, amawapatsa mpando waulemu. “Pakuti nsanamira za dziko lapansi ndi za Yehova, anakhazika dziko lapansi pa nsanamirazo.
9 Nóg świętych swoich ochrania, a niepobożni w ciemnościach zamilkną; bo nie w sile swojej będzie się mąż zmacniał.
Iye adzateteza moyo wa anthu okhulupirika koma anthu oyipa adzawonongedwa mu mdima. “Pakuti munthu sapambana ndi mphamvu zake.
10 Pan pokruszy przeciwniki swoje, a zagrzmi na nie z nieba; Pan będzie sądził granice ziemi, a da moc królowi swemu, i wywyższy róg pomazańca swego.
Yehova adzaphwanya omutsutsa. Adzawaopsa ndi bingu kuchokera kumwamba; Yehova adzaweruza mathero a dziko lapansi. “Koma adzapereka mphamvu kwa mfumu yake, adzakuza mphamvu za odzozedwa wake.”
11 A tak odszedł Elkana do Ramaty do domu swego, a dziecię służyło Panu przed Heli kapłanem.
Tsono Elikana anapita ku mudzi kwawo ku Rama, koma mnyamatayo amatumikira Yehova pansi pa ulamuliro wa wansembe Eli.
12 Ale synowie Heli byli synowie bezbożni, a nie znali Pana.
Ana a Eli anali ana achabechabe pakuti samasamala za Yehova.
13 Albowiem obyczaj kapłanów ten był około ludu: ktokolwiek sprawował ofiary, przychodził sługa kapłański, gdy warzono mięso, mając widełki o trzech zębach w ręce swojej.
Ndipo chizolowezi cha ansembe pakati pa anthu chinali motere kuti pamene munthu aliyense ankapereka nsembe ndipo nyama ija ikuwira pa moto, mtumiki wa wansembe ankabwera ndi chifoloko cha mano atatu mʼdzanja lake.
14 I wrażał je w statek, albo w kocieł, albo w panew, albo w garniec, a coklowiek wyjął widełkami, to sobie brał kapłan. Tak czynili wszystkim Izraelczykom, którzy tam do Sylo przychodzili.
Iye ankachipisa mu mʼphikamo, ndipo wansembeyo amatenga chilichonse chimene folokoyo yabaya. Umu ndi mmene ansembewo amachitira ndi Aisraeli onse amene amabwera ku Silo.
15 Także pierwej niż zapalono tłustość, tedy przychodził sługa kapłański, a mówił do człowieka ofiarującego: Oddaj mięso, abym je upiekł kapłanowi; albowiem nie weźmie od ciebie mięsa warzonego, jedno surowe.
Ndipo ngakhale mafuta asanatenthedwe, mtumiki wansembe amabwera ndi kunena kwa munthu amene akupereka nsembeyo kuti, “Ndipatse nyama kuti ndiwotche, pakuti Yehova salandira nyama yophika koma yayiwisi.”
16 A jeźliż mu odpowiedział on człowiek: Niech się pierwej spali tłustość, potem sobie weźmiesz, czego będzie żądała dusza twoje, tedy on mówił: Nic z tego; teraz daj! a nie daszli, wezmę gwałtem.
Ngati munthuyo anena kuti, “Apseretu mafuta poyamba, ndipo kenaka mutenge mmene mufunira,” mtumikiyo amayankha kuti, “Ayi ndipatse tsopano lino. Ngati sutero, ine nditenga molanda.”
17 I był to grzech onych sług bardzo wielki przed Panem; bo się odtrącali ludzie od ofiar Pańskich.
Tchimo la ana a Eli linali lalikulu kwambiri pamaso pa Yehova pakuti iwo amanyoza nsembe za Yehova.
18 Ale Samuel służył przed Panem, ubrane chłopiątko w efod lniany.
Koma Samueli amatumikira pamaso pa Yehova atavala efodi ya nsalu yofewa yosalala.
19 A matka jego uczyniwszy mu sukienkę małą, przynaszała mu co rok, gdy chadzała z mężem swym sprawować ofiarę uroczystą.
Chaka chilichonse amayi ake ankamusokera kamkanjo ndi kukamupatsa akamapita ndi mwamuna wake kukapereka nsembe za pa chaka.
20 I błogosławił Heli Elkanie, i żonie jego, mówiąc: Niech ci da Pan potomstwo z tej niewiasty za oddanego, którego wyprosiła u Pana. I poszli na miejsca swoje.
Tsono Eli amadalitsa Elikana ndi mkazi wake ndi mawu akuti “Yehova akupatseni ana mwa mkazi uyu kulowa mʼmalo mwa amene anapempha ndi kumupereka kwa Yehova.”
21 Tedy nawiedził Pan Annę, która poczęła i porodziła trzech synów, i dwie córek; a pacholę Samuel urósł przed Panem.
Ndipo Yehova anamukomera mtima Hana. Anakhala ndi pathupi ndi kubereka ana aamuna atatu ndi ana aakazi awiri. Ndipo Samueli ankakula pamaso pa Yehova.
22 Ale Heli zstarzał się był bardzo, i słyszał wszystko, co czynili synowie jego całemu Izraelowi, i jako sypiali z niewiastami, które się schadzały przede drzwi namiotu zgromadzenia.
Tsono Eli anakalamba kwambiri. Iye ankamva zonse zimene ana ake aamuna ankachitira Aisraeli onse, ndiponso kuti ankagona ndi akazi pa chipata cha tenti ya msonkhano.
23 I rzekł do nich: Przeczże takie rzeczy czynicie? Cóż ja słyszę o waszych złych sprawach od wszystkiego ludu?
Choncho anawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mukuchita zinthu zotere? Ine ndikumva kuchokera kwa anthu onse za zoyipa zanuzo.
24 Nie tak synowie moi; bo nie dobra sława, którą ja słyszę, że przywodzicie ku przestępstwu lud Pański.
Ayi, ana anga si mbiri yabwino imene ndikumva anthu a Mulungu akufalitsa.
25 Gdy kto zgrzeszy przeciw człowiekowi, sądzić go będzie sędzia, ale jeźli przeciw Panu kto zgrzeszy, któż się za nim ujmie? Lecz nie usłuchali głosu ojca swego; bo je chciał Pan pobić.
Ngati munthu alakwira munthu mnzake, mwina Mulungu adzamupepesera, koma ngati munthu achimwira Yehova adzamupepesera ndani?” Koma ana ake sanamvere kudzudzula kwa abambo awo, pakuti chinali cholinga cha Yehova kuti awaphe.
26 Ale pacholę Samuel postępował a rósł, i podobał się tak Panu jako i ludziom.
Ndipo mnyamata Samueli anapitirira kukula mu msinkhu, ndipo ankapeza kuyanja pamaso pa Yehova ndi anthu.
27 Potem przyszedł mąż Boży do Heli, i rzekł mu: Tak mówi Pan: Azalim się nie jawnie objawił domowi ojca twego, gdy byli w Egipcie w domu Faraonowym?
Tsiku lina munthu wa Mulungu anabwera kwa Eli ndipo anamuwuza kuti, “Yehova akuti, ‘Kodi Ine sindinadziwulule ndekha kwa banja la kholo lako pamene iwo anali akapolo a Farao ku Igupto?
28 I obrałem go sobie ze wszystkich pokoleń Izraelskich za kapłana, aby ofiarował na ołtarzu moim, a kadził rzeczami wonnemi, i nosił efod przedemną, i dałem domowi ojca twego wszystkie ofiary palone od synów Izraelskich.
Ndipo ndinamusankha pakati pa mafuko a Israeli kuti akhale wansembe wanga ndi kuti azipita pa guwa langa la nsembe, kufukiza Lubani ndi kuvala efodi pamaso panga. Ndinapatsa banja la abambo ako gawo la nsembe zonse zopsereza zimene Aisraeli amapereka.
29 Przeczżeście podeptali ofiarę moję, i śniedną ofiarę moję, którąm rozkazał sprawować w przybytku? i więcejś uczcił syny swoje nad mię, abyście się utuczyli z pierwocin wszystkich ofiar śniednych Izraela, ludu mego?
Nʼchifukwa chiyani ukunyoza nsembe ndi zopereka zanga zimene ndinalamula? Nʼchifukwa chiyani ukupereka ulemu kwa ana ako kuposa Ine podzinenepetsa nokha ndi zopereka zabwino kwambiri za nsembe zimene Aisraeli amapereka?’”
30 Prztoż mówi Pan, Bóg Izraelski: Rzekłem wprawdzie: Dom twój i dom ojca twego będzie służył przedemną aż na wieki; ale teraz mówi Pan: Nie będzieć to, gdyż ja te, którzy nie czczą, czcić będę, a którzy mną gardzą, będą wzgardzeni.
“Paja Ine Yehova Mulungu wa Israeli ‘Ndinalonjeza kuti anthu a pa banja lako ndi a pa banja la abambo ako azidzanditumikira nthawi zonse.’ Koma tsopano ndikuti, ‘Zonsezi zithe!’ Tsopano anthu amene amandilemekeza Inenso ndidzawalemekeza koma iwo amene amandinyoza Ine ndidzawanyoza.
31 Oto, dni przychodzą, a odetnę ramię twe, i ramię domu ojca twego, aby nie było starca w domu twoim;
Nthawi ikubwera imene ndidzachotsa anyamata ako ndi anyamata a pa banja la abambo ako, kotero kuti sipadzakhala munthu wokalamba pa banja lako.
32 I oglądasz wielki ucisk przybytku Pańskiego, miasto szczęścia, które Pan dawał Izraelowi, i nie będzie starca w domu twoim po wszystkie dni.
Pa mavuto ako udzayangʼana ndi maso ansanje zabwino zimene ndidzachitira Aisraeli ena. Mʼbanja lako simudzapezeka munthu wokalamba.
33 Wszakże męża nie wytracę z ciebie do końca od ołtarza mego, abym utrapił oczy twe, a boleścią ścisnął duszę twoję; a wszystko mnóstwo domu twego pomrze, dorosłszy lat męskich.
Komabe pa banja lako mmodzi yekha ndidzamuleka wosamuchotsa kuti azidzanditumikira. Iyeyu azidzakuliritsa ndi kukumvetsa chisoni. Koma ena onse pa banja lako adzafa akanali aangʼono.”
34 A toć będzie na znak, co przyjdzie na dwóch synów twoich, Ofni i Fineesa; dnia jednego pomrą ci oba.
“‘Ndipo chimene chidzachitike kwa ana ako awiriwa, Hofini ndi Finehasi, chidzakhala chizindikiro kwa iwe. Onse awiri adzafa pa tsiku limodzi.
35 I wzbudzę sobie kapłana wiernego, który według serca mego, i według myśli mojej czynić będzie, i zbuduję mu dom trwały, a będzie służył przed pomazańcem moim po wszystkie dni.
Pambuyo pake ndidzasankha wansembe wokhulupirika, amene adzachita zimene zili mu mtima ndi mʼmaganizo mwanga. Ndidzakhazikitsa banja lako kolimba ndipo adzatumikira pamaso pa wodzozedwa wanga nthawi zonse.
36 I stanie się, ktokolwiek pozostanie z domu twego, przyjdzie, aby mu się ukłonił za pieniądz srebrny i za sztukę chleba, mówiąc: Przypuść mię proszę do jednej cząstki kapłańskiej, aby jadł sztuczkę chleba.
Ndipo aliyense wotsala wa banja lako adzabwera ndi kugwada pamaso pake kupempha ndalama kapena chakudya.’ Adzati, ‘Chonde ndiloleni kuti ndizithandizako pa ntchito iliyonse ya unsembe kuti ndipeze chakudya.’”

< I Samuela 2 >