< Lukaj 3 >

1 PAR eijoklimau murin nanmarki Tiperiuj a japwiledu ni muein Pontiuj Pilatuj kopina en Iudaa, o Erodej nanmarki en Kalilaa, o ri a ol Pilipuj nanmarki en Ituraa o Trakonitij, o Lijaniaj nanmarki en Apilene,
Mʼchaka cha 15 mu ulamuliro wa Tiberiyo Kaisara, Pontiyo Pilato ali bwanamkubwa wa Yudeya, Herode ankalamulira ku Galileya, mʼbale wake Filipo ankalamulira ku Iturea ndi ku dera la Trakoniti, ndipo Lusaniyo ankalamulira ku Abilene.
2 Ni muein Anaj o Kaipaj jamero lapalap, majan en Kot ap pwara don Ioanej nain Jakariaj nan jap tan.
Inalinso nthawi ya mkulu wa ansembe wa Anasi ndi Kayafa, pamene mawu a Mulungu anabwera kwa Yohane mwana wa Zakariya mʼchipululu.
3 I ari kotikot jili nan jap karoj ni kail en Iordan, padapadak duen paptaij en kalula on lapwada dip akan,
Iye anapita ku dziko lonse lozungulira mtsinje wa Yorodani, nalalikira ubatizo wa kulapa ndi kukhululukidwa kwa machimo.
4 Duen a intinidier nan puk en majan akan en jaukop Iejaia, me majani: Nil eu likelikwir jili nan jap tan: Komail kaonopada al en Kaun o, kaineneda al a!
Monga analembera mʼbuku la Yesaya mneneri kuti: “Mawu a wofuwula mʼchipululu, konzani njira ya Ambuye, wongolani njira zake.
5 Wau karoj pan audaud o nana o dol karoj pan patapatedi, o me pirok, pan inenla, o mo ululen, pan patapatela.
Chigwa chilichonse chidzadzazidwa ndipo phiri lililonse ndi mtunda uliwonse zidzasalazidwa, misewu yokhotakhota idzawongoledwa, ndi njira zosasalala zidzasalazidwa.
6 Uduk karoj pan udial kamaur on Kot.
Ndipo anthu onse adzaona chipulumutso cha Mulungu.”
7 A ap majani on aramaj akan, me koieila, pwen paptaijla re a: Dakot, wan oter komail; ij me padaki on komail, eh piti jan ni kamakam, me kokodo?
Yohane anati kwa magulu a anthu amene amabwera kudzabatizidwa ndi iye, “Ana anjoka inu! Anakuchenjezani ndani kuti muthawe mkwiyo umene ukubwera?
8 Ari komail kapareda wan kalula mau. A komail depa lamelame, me komail pan indan pein komail: Nan Apraam jam atail. Pwe i indai on komail, me Kot kotin kak on wiaki on Apraam na jeri kai takai pukat.
Onetsani zipatso zakutembenuka mtima, ndipo musamanene mwa inu nokha kuti, ‘Tili nalo kholo lathu Abrahamu,’ pakuti ndikuwuzani kuti kuchokera ku miyala iyi, Mulungu akhoza kumuwutsira Abrahamuyo ana.
9 Jile o mier ni tapin tuka kan. Ari, tuka karoj, me jo wa mau, pan palepaledi o lokidokila nan iai.
Nkhwangwa ili kale pa muzu wamitengo, ndipo mtengo uliwonse umene subala chipatso chabwino udzadulidwa ndi kuponyedwa pa moto.”
10 Pokon o ap idok re a indada: A da me kit en wia?
Gulu la anthuwo linafunsa kuti, “Nanga tsono tichite chiyani?”
11 A kotin japen majani on irail: Meamen, me a jakit riau, I en ki on, me jota a. O me kan a kijin mana mia, i en wia dueta.
Yohane anayankha kuti, “Munthu amene ali ndi malaya awiri apatseko amene alibe, ndi amene ali ndi chakudya achitenso chimodzimodzi.”
12 A jaunopwei kan pil pwara don i pwen paptaij, irail potoan on i: Jaunpadak, a da me kit en wia?
Amisonkho nawonso anabwera kudzabatizidwa. Iwo anafunsa kuti, “Aphunzitsi, ife tichite chiyani?”
13 A majani on irail: Komail der ale laude jan me kileledier.
Iye anawawuza kuti, “Musalandire moposa zimene muyenera.”
14 Jaunpei kan ap pil kalelapok re a indada: A da me kit en wia? A majani on irail: Komail der kaloke mal meamen, o der wia japun on meamen, a komail ale pwain omail o injenemau kila.
Kenaka asilikali ena anamufunsa kuti, “Nanga ife tichite chiyani?” Iye anayankha kuti, “Musamalande ndalama moopseza ndipo musamanamizire anthu, khutitsidwani ndi malipiro anu.”
15 Aramaj akan lao kiki on o monemoneloleki, me Ioanej me Krijtllj,
Anthu ankadikira ndi chiyembekezo ndipo ankasinkhasinkha mʼmitima mwawo kuti mwina Yohane nʼkukhala Khristu.
16 Ioanej ap japen majani on irail karoj: I paptaij kin komail pil, a me laude jan ia kotido muri, me i jowar on, en lapwada jal en japwilim a jut, i me pan paptaij kin komail Nen jaraui o kijiniai.
Yohane anayankha onse kuti, “Ine ndikubatizani ndi madzi. Koma wina wondiposa ine mphamvu adzabwera amene sindili woyenera kumasula lamba wa nsapato zake. Iyeyu adzakubatizani inu ndi Mzimu Woyera ndi moto.
17 Tanir mi nan lim a, a pan kotin koko melel japwilim a pera, ap nekid pena wan korn nan japwilim a im en nak, a dip a pan kotin karon kila kijiniai jokun.
Mʼdzanja lake muli chopetera kuti ayeretse powomberapo tirigu ndi kusonkhanitsa tirigu ndipo adzatentha zotsalira zonse ndi moto wosazimitsika.”
18 O jon toto, me a kotin panaui aramaj akan o padaki on pokon o ronamau.
Ndipo ndi mawu ena ambiri, Yohane anawachenjeza anthu ndi kuwalalikira Uthenga Wabwino.
19 A nanmarki Erodej, me Ioanej kapun pweki Erodiaj en ri a ol a paud, o pweki jued karoj, me Erodej wiadar,
Koma pamene Yohane anadzudzula Herode wolamulirayo chifukwa chokwatira Herodia, mkazi wa mʼbale wake, ndi zoyipa zina zonse anazichita,
20 Kalaudela dip a ni a jaliedi Ioanej nan imaten.
Herode anawonjezanso choyipa ichi pa zonsezo: Anatsekera Yohane mʼndende.
21 A kadekadeo aramaj karoj lao paptaij elar, o Iejuj pil paptaijelar o kotin laolaoki, nanlan ap ritida,
Pamene anthu onse ankabatizidwa, Yesu anabatizidwanso. Ndipo akupemphera, kumwamba kunatsekuka.
22 O Nen jaraui kotidi don i ni mom en muroi men, o nil eu jan nanlan majani: Koe nai ol kompok, me I kin peren kida.
Mzimu Woyera anatsika pa Iye mumaonekedwe a nkhunda ndipo mawu anamveka kuchokera kumwamba: “Iwe ndiwe Mwana wanga wokondedwa; ndimakondwera nawe.”
23 Iejuj impan jaunpar jileijok ni a kotin tapiada jaunpadak, o re kikion me i nain Iojep, me nain Eli,
Ndipo Yesu anali ndi zaka makumi atatu pamene anayamba ntchito yake. Monga mmene anthu ankaganizira, Iyeyo anali mwana wa Yosefe, mwana wa Heli,
24 Me nain Matat, me nain Lewi, me nain Melki, me nain Ianej, me nain Iojep,
mwana wa Matate, mwana wa Levi, mwana wa Meliki, mwana wa Yaneyi, mwana wa Yosefe
25 Me nain Matatia, me nain Amoj, me nain Naum, me nain Ejli, me nain Nakai,
mwana wa Matati, mwana wa Amosi, mwana wa Naomi, mwana wa Esli, mwana wa Nagai,
26 Me nain Maat, me nain Matatia, me nain Jimei, me nain Iojep, me nain Iuda,
mwana wa Maati, mwana wa Matatiyo, mwana wa Simeoni, mwana wa Yosefe, mwana wa Yoda
27 Me nain Ioanan, me nain Reja, me nain Jerupapel, me nain Jalatiel, me nain Neri,
mwana wa Yohanani, mwana wa Resa, mwana wa Zerubabeli, mwana wa Salatieli, mwana wa Neri,
28 Me nain Melki, me nain Adi, me nain Kojam, me nain Elmodam, me nain Er,
mwana wa Meliki, mwana wa Adi, mwana wa Kosamu, mwana wa Elmadama, mwana wa Ere,
29 Me nain Iojej, me nain Eliejer, me nain lorim, me nain Matat, me nain Lewi,
mwana wa Jose, mwana wa Eliezara, mwana wa Yorimu, mwana wa Matati, mwana wa Levi,
30 Me nain Jimeon, me nain Iuda, me nain Jojep, me nain Ionam, me nain Eliakim,
mwana wa Simeoni, mwana wa Yuda, mwana wa Yosefe, mwana wa Yonamu, mwana wa Eliakimu,
31 Me nain Melia, me nain Mena, me nain Matatan, me nain Natan, Me nain Dawid,
mwana wa Meleya, mwana wa Mena, mwana wa Matata, mwana wa Natani, mwana wa Davide,
32 Me nain Ieje, me nain Oped, me nain Poaj, me nain Jala, me nain Naajan,
mwana wa Yese, mwana wa Obedi, mwana wa Bowazi, mwana wa Salimoni, mwana wa Naasoni,
33 Me nain Aminadap, me nain Aram, me nain Ejron, me nain Perej, me nain Iuda,
mwana wa Aminadabu, mwana wa Arni, mwana wa Hezronu, mwana wa Perezi, mwana wa Yuda,
34 Me nain Iakop, me nain Ijaak, me nain Apraam, me nain Tara, me nain Naor,
mwana wa Yakobo, mwana wa Isake, mwana wa Abrahamu, mwana wa Tera, mwana wa Nakoro,
35 Me nain Jeruk, me nain Reku, me nain Palek, me nain Eper, me nain Jala,
mwana wa Serugi, mwana wa Reu, mwana wa Pelegi, mwana wa Eberi, mwana wa Sela,
36 Me nain Kainan, me nain Arpakjad, me nain Jem, me nain Noa, me nain Lamek,
mwana wa Kainane, mwana wa Arfaksadi, mwana wa Semu, mwana wa Nowa, mwana wa Lameki,
37 Me nain Metujala, me nain Enok, me nain Iared, me nain Maalaleel, me nain Kainan,
mwana wa Metusela, mwana wa Enoki, mwana wa Yaredi mwana wa Malaleeli, mwana wa Kainane,
38 Me nain Enos, me nain Jet, me nain Adam, me japwilim en Kot.
mwana wa Enosi, mwana wa Seti, mwana wa Adamu, mwana wa Mulungu.

< Lukaj 3 >