< Lukas 8 >

1 KADEKADEO murin mepukat a kotin kakan sili nan kanim laud o me tikitik kan, padapadak o kaloki rongamau en wein Kot, o ekriamen iang i.
Zitatha izi, Yesu anayendayenda kuchoka mzinda wina kupita wina ndiponso mudzi wina kupita wina, akulalikira Uthenga Wabwino wa ufumu wa Mulungu. Ophunzira ake khumi ndi awiri aja anali naye,
2 O pil li akai, me a kotin kakelailada sang ngen sued o somau kan, iet akan: Maria, me pil adaneki men Makdala, me tewil isimen koiei sang.
komanso akazi ena amene anachiritsidwa ku mizimu yoyipa ndi matenda: Mariya, wotchedwa Magadalena, amene mwa iye munatuluka ziwanda zisanu ndi ziwiri;
3 O Ioana iei likond en Kusas en Erodes a saunkoa men, o Susana, o me toto, me papaki i ar kapwa kan.
Yohana mkazi wa Kuza, woyangʼanira mʼnyumba ya Herode; Suzana; ndi ena ambiri analinso. Akazi awa ankawathandiza ndi chuma chawo.
4 A aramas totoia lao pokon dong i sang nan kanim akan, karos, ap kotin karaseras masani:
Anthu ambiri ankasonkhana, ndipo pamene anthu ankabwera kwa Yesu kuchokera ku midzi, Iye anawawuza fanizo ili,
5 Saunkamor kolan kamor a war akan. Ni a kamokamorok akai ap moredi ong pon kailan al ap tiatidi o manpir en pan lang nam ir ala.
“Mlimi anapita kukafesa mbewu zake. Akufesa mbewuzo, zina zinagwa mʼmbali mwa njira; zinapondedwa, ndipo mbalame zamlengalenga zinadya.
6 A akai moredi ong pon paip. A lao wosada, a mongedi, pweki a sota lamelamur.
Zina zinagwa pa thanthwe, ndipo pamene zinamera, zinafota chifukwa panalibe chinyezi.
7 Akai moredi nan tuka teketek, a tuka teketek wosada, kasokä ir ala.
Mbewu zina zinagwera pakati pa minga, zinakulira pamodzi ndi mingazo ndipo zinalepheretsa mmerawo kukula.
8 A akai moredi nan pwel mau, ap wosada o wada pan me epuki. Ni a kotin masanier mepukat, ap masan laudeda: Me salong a mia, men rong, i en rong!
Mbewu zina zinagwera pa nthaka yabwino. Zinamera ndipo zinabala mowirikiza 100 kuposa zimene zinafesedwa zija.” Atanena izi, anafuwula kuti, “Amene ali ndi makutu, amve.”
9 A sapwilim a tounpadak kan ap kalelapok re a: Ia wewe en karaseras wet?
Ophunzira ake anamufunsa tanthauzo lake la fanizolo.
10 I ari kotin masani: A muei ong komail er, en asa me rir en wein Kot, a met akan en asa ni karaseras akan pwe ren kilang, ap sota kilang, o rong, ap sota weweki.
Iye anati, “Kudziwa zinsinsi za ufumu wa Mulungu kwapatsidwa kwa inu, koma kwa ena ndimawayankhula mʼmafanizo kuti, “ngakhale akuona, asapenye; ngakhale akumva, asazindikire.”
11 A iet wewe en karaseras o: Masan en Kot iei war akan.
“Tanthauzo la fanizoli ndi ili: Mbewu ndi mawu a Mulungu.
12 A me mi pon kailan al o, iei ir, me rongadar, a muri tewil pwarada katia sang masan en Kot nan mongiong arail, pwe ren der poson, rap maurela.
Mbewu za mʼmbali mwa njira ndi anthu amene amamva mawu, ndipo kenaka mdierekezi amabwera ndi kuchotsa mawuwo mʼmitima mwawo kuti asakhulupirire ndi kupulumutsidwa.
13 A me mi pon paip, iei ir, me kin rong masan o ap pereperen ale, a sota kalau re’rail. Ansau kis re kin poson, a ni ansaun songesong, irail kin pupe sang.
Mbewu za pa thanthwe ndi anthu amene amalandira mawu mwachimwemwe pamene akumva, koma mawuwo sazika mizu. Iwo amakhulupirira kwa kanthawi, koma pa nthawi ya mayesero, amagwa.
14 A me moredi nan tuka teketek, iei irail me kin rong, ap koieila tiropeki anan o pai, o inong sued en maur et, rap sokekila, ap sota wa.
Mbewu zimene zinagwa pakati pa minga zikuyimira anthu amene amamva mawu, koma akamayenda mʼnjira zawo amatsamwitsidwa ndi zodandaulitsa za moyo uno, chuma ndi zosangalatsa, ndipo iwo samakhwima.
15 A nan sap mau, iei irail, me kin rong masan o, ap nekinek nan mongiong ar inen o mau, o wada nin tiak en kanongama.
Koma mbewu za pa nthaka yabwino zikuyimira anthu amene ali ndi mtima woona ndi wabwino, amene amamva mawu nawasunga, ndipo amalimbikira mpaka amabala zipatso.
16 Sota me kin isikeda lamp, ap pwainekidi kopa eu, de ki ong pan men wendi a pon deu a, pwe me pan pedelong ong en kilang marain o.
“Palibe amayatsa nyale ndi kuyibisa mu mtsuko kapena kuyika pansi pa bedi. Koma mʼmalo mwake, amayika pa choyikapo chake, kuti anthu olowamo aone kuwala.
17 Pwe sota me rir kot, me so pan sansaleta, pil sota me okiok kot, me so pan kalok sili.
Pakuti palibe kanthu kobisika kamene sikadzawululika, ndipo palibe kanthu kophimbika kamene sikadzadziwika kapena kuonetsedwa poyera.
18 Komail ari kalaka duen omail kin rongerong, pwe me a mia, ekis pan ko ong; a me sota a mia, i, me a kiki ong, me a, pan katia sang.
Choncho ganizirani mozama. Iye amene ali nazo adzapatsidwa zambiri, iye amene alibe, ngakhale chimene akuganiza kuti ali nacho adzalandidwa.”
19 In a o ri a kan ap ko dong i, a re sota kak kaiong impa pweki pokon o.
Tsopano amayi ndi abale a Yesu anabwera kudzamuona Iye, koma analephera kuti afike pafupi ndi Iye chifukwa cha gulu la anthu.
20 A ap loki ong i: In ar o ri ar akan poto liki, re men udial ir.
Wina anamuwuza Iye kuti, “Amayi ndi abale anu ayima kunja, akufuna kukuonani.”
21 A kotin sapeng masani ong irail: In ai o ri ai mepukat, me kin rongerong masan en Kot o apapwali.
Yesu anayankha kuti, “Amayi ndi abale anga ndi amene amamva mawu a Mulungu ndi kumachita zimene mawuwo akunena.”
22 Kadekadeo ni eu ran a kotilang pon apot sop, a sapwilim a tounpadak kan iang i. A kotin masani ong irail: Kitail en kotela le en: Irail ari tangetang koieila.
Tsiku lina Yesu anati kwa ophunzira ake, “Tiyeni tiwolokere tsidya lina la nyanja.” Ndipo analowa mʼbwato nanyamuka.
23 O ni ar tangetang kokowei, a kotin saimokela; melimel ap koda nan sed. A sop o pwilipwil, a pan mauidi.
Akuwoloka, Iye anagona tulo. Namondwe wamkulu anayamba pa nyanja, ndipo bwatolo linayamba kudzaza ndi madzi ndipo anali pa chiopsezo chachikulu.
24 Irail ap kai dong i, kaopada i, potoan ong: Maing, Maing, kit pan mela! I ari kipada masani ong ang o iluk en sed akan, rap tikitikala o molelar.
Ophunzira anapita ndi kukamudzutsa Iye, nati, “Ambuye, Ambuye, ife tikumira!” Anadzuka ndipo anadzudzula mphepo ndi madzi owindukawo. Namondwe anasiya, ndipo panali bata.
25 I ap kotin masani ong irail: Ia omail poson? A irail masakada inda nan pung ar: Daduen, is men et, pwe a kin masani ong ang o sed, ir ari duki ong.
Iye anafunsa ophunzira ake kuti, “Chikhulupiriro chanu chili kuti?” Koma pogwidwa ndi mantha ndi kudabwa anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Uyu ndi ndani? Iye alamulira ngakhale mphepo ndi madzi, ndipo zimumvera Iye.”
26 Irail ap lele dong sap en Kadara, me sal ong Kaliläa.
Iwo anawolokera ku chigawo cha Gerasa chimene chili tsidya lina la nyanja kuchokera ku Galileya.
27 I lao kotidi sang, ol amen tu ong i, me kodo sang kanim o, me tanwar en tewil sang mas kokodo, o me kiliso, o a sota kin kauson nan im, pwe a kin mimi nan sousou kan.
Yesu ataponda pa mtunda, anakumana ndi munthu wogwidwa ndi ziwanda wochokera mu mzindawo. Kwa nthawi yayitali munthuyu sanavale zovala kapena kukhala mʼnyumba, koma amakhala ku manda.
28 I lao kilang Iesus, ap werida, poridi sang mo a indaki ngil laud: Menda re omui ngai, Iesus Sapwilim en Kot lapalap? I men poeki re omui, kom der kalok ia la!
Iye ataona Yesu, anakuwa nagwa pa mapazi ake akufuwula kwambiri kuti, “Mukufuna chiyani ndi ine, Yesu Mwana wa Mulungu Wammwambamwamba? Ndikupemphani Inu, musandizunze ine!”
29 Pwe a kotin masani ong ngen saut o, en koiei sang ren aramas o, pwe pan pak toto a saikidi i; i ari kin sali kidi sal mata o sal en nä kai. A i kamueit ir pasang, o tewil paki i lang sap tan.
Pakuti Yesu analamula mzimu woyipawo kuti utuluke mwa munthuyo. Kawirikawiri umamugwira iye, ndipo ngakhale anali womangidwa ndi unyolo dzanja ndi mwendo ndi kuti ankamuyangʼanira, koma amadula maunyolo akewo ndipo ziwanda zimamutengera kumalo a yekha.
30 Iesus kotin kainoma re a masani: Ia ad om? A potoan ong: Lekion; pwe tewil toto mi re a.
Yesu anamufunsa kuti, “Dzina lako ndani?” Iye anayankha kuti, “Legiyo,” chifukwa ziwanda zambiri zinalowa mwa iye.
31 Ir ari poeki re a, ender masani ong irail, me ren kodilang pweleko. (Abyssos g12)
Ndipo ziwandazo zimamupempha mobwerezabwereza kuti asazitumize ku dzenje la mdima. (Abyssos g12)
32 Ari, pwin pwik kalaimun mi wasa o mangamanga sili nin nana o. Irail ari poeki i, en kotin mueid ong irail re en til ong irail. I ari kotin mueid ong irail.
Gulu lalikulu la nkhumba limadya pamenepo mʼmbali mwa phiri. Ziwandazo zinamupempha Yesu kuti azilole kuti zikalowe mu nkhumbazo ndipo Iye anazilola.
33 Tewil oko ap kodi sang ren aramas o, ap tilong nan pwin pwik o. Pwin pwik o ap tangedi wei ni aul ong nan sed ap mopila.
Ziwanda zija zitatuluka mwa munthuyo, zinakalowa mwa nkhumbazo, ndipo gulu lonselo linathamangira ku mtsetse ndi kukalowa mʼnyanja ndi kumira.
34 Silepa ko lao kilanger me wiauier, rap tangdaui, kolang kanim laud o tikitik kan, kaireki sili.
Oweta nkhumbazo ataona zimene zinachitikazo, anathamanga ndi kukanena izi mu mzinda ndi ku madera a ku midzi.
35 Irail ap koieila, kilang me wiauier, re ap kola ren Iesus, diarada aramas o, me tewil oko keredi sang lole, momod ni aluwilu en Iesus, likauda o lolekonglar; irail karos masakadar.
Ndipo anthu anapita kukaona zimene zinachitika. Atafika kwa Yesu, anapeza munthu amene anatulutsidwa ziwanda uja atakhala pa mapazi a Yesu, atavala ndipo ali ndi nzeru zake; ndipo iwo anachita mantha.
36 Me iang udialer, ap kaire kin irail duen tanwar en tewil a kakeladar.
Amene anaona izi anawuza anthu mmene munthu wogwidwa ndi ziwandayo anachiritsidwira.
37 Men Kadara karos ap poekipoeki i, en koti wei sang re’rail, pwe re masakadar kaualap. I ari kotida pon sop o, ap kotin purelar.
Kenaka anthu onse a ku chigawo cha Gerasa anamupempha Yesu kuti achoke kwa iwo, chifukwa anadzazidwa ndi mantha. Choncho Iye analowa mʼbwato nachoka.
38 A ol o, me tewil oko kodi sanger, poeki re a, en iang i; a Iesus sota kotin mueid ong i masani:
Munthu amene anatulutsidwa ziwanda uja, anapempha Yesu kuti apite nawo, koma Yesu anamubweza nati,
39 Purelang deu om, kalok sili duen manaman lapalap, me Kot wiai ong uk er! I ari kola, kalok sili nan kanim o duen manaman lapalap, me Iesus kotin wiai ong i.
“Bwerera kwanu kafotokoze zimene Mulungu wakuchitira.” Ndipo munthuyo anachoka ndi kukanena ku mzinda wonsewo zimene Yesu anamuchitira iye.
40 Kadekadeo Iesus lao kotin puredo, aramas akan ap kasamo i, pwe irail karos auiaui i.
Yesu atabwerera, gulu lalikulu la anthu linamulandira, chifukwa onse ankamuyembekezera.
41 A kilang, ol amen, ad a Iairus, saumas en sinakoke, kotido poridi ni aluwilu en Iesus o poeki i, en kotilong ong nan im a.
Nthawi yomweyo munthu wotchedwa Yairo, woweruza wa mu sunagoge, anabwera ndi kugwa pa mapazi a Yesu, namupempha Iye kuti apite ku nyumba kwake,
42 Pwe na ieros seripein amen, me a par ngaulriau, me koren iong mela. A ni a kotikot kokodo, pokon o koi dong i.
chifukwa mwana wake yekhayo wamkazi, kamtsikana ka zaka khumi ndi ziwiri, kanali pafupi kufa. Pamene Yesu ankapita gulu la anthu linkamupanikiza.
43 A li amen, me nta pwilipwil par ngaulriau, me pwaineki ong saunwini kan a dipisou karos. A sota me kak kakelailada i.
Ndipo pomwepo panali mayi wina amene ankataya magazi kwa zaka khumi ndi ziwiri, koma panalibe wina akanamuchiritsa.
44 I me apedo mur i, doke ni kailan sapwilim a likau. A pwilipwil en nta madang madada.
Iye anafika kumbuyo kwake ndi kukhudza mothera mwa chovala chake, ndipo nthawi yomweyo magazi ake analeka kutuluka.
45 Iesus ap kotin masani: Is i me sair ia? A karos lao inda me sota, Petrus o me iang i ap potoan ong: Maing, pokon o kin kapil pena o koi dong ir, a iaduen, re kotin masani: Is i me sair ia?
Yesu anafunsa kuti, “Wandikhudza ndani?” Onse atakana, Petro anati, “Anthu akukupanikizani ndi kukukankhani.”
46 A Iesus kotin masani: Nan meamen sair ia, pwe I pam, me kel eu ko sang ia er.
Koma Yesu anati, “Wina wandikhudza; ndikudziwa chifukwa mphamvu yachoka mwa Ine.”
47 A li o lao asaer, me a so kak rirala, ap masapwekada, apedi poridi sang mo a, ap katitiki mon aramas karos, karepan a sair i, o duen a kelailada madang.
Ndipo mayiyo podziwa kuti sanathe kuchoka wosadziwika, anabwera akunjenjemera ndipo anagwa pa mapazi a Yesu. Pamaso pa anthu onse, anafotokoza chifukwa chimene anamukhudzira Iye ndi mmene iye anachiritsidwira nthawi yomweyo.
48 A ap kotin masani ong i: Seripein popoleta, om poson me kakel uk ada, kowei popol.
Kenaka anati kwa iye, “Mwana wamkazi, chikhulupiriro chako chakuchiritsa. Pita mu mtendere.”
49 A ni a kotin masaniata, amen potodo sang ren saumas en sinakoke o katitiki ong i: Sapwilim omui seripein melar. Menda kom kangirieki saunpadak o.
Pamene Yesu ankayankhulabe, munthu wina anabwera kuchokera ku nyumba ya Yairo, woweruza wa ku sunagoge uja. Iye anati, “Mwana wanu wa mkazi wamwalira, musawavutitsenso Aphunzitsiwa.”
50 A Iesus lao mangi mepukat, ap kotin sapeng i masani: Koe der masak, koe poson ta, a ap pan maureda.
Atamva zimenezi, Yesu anati kwa Yairo, “Usachite mantha, ingokhulupirira basi ndipo adzachiritsidwa.”
51 A lao kotilong ong nan im o, a sota kotin mueid ong amen en iang pedelong ong nan pera, Petrus, o Ioanes, o Iakupus eta, o sam en seripein o in a.
Iye atafika ku nyumba ya Yairo, sanalole wina aliyense kulowa kupatula Petro, Yohane, ndi Yakobo ndi abambo ndi amayi a mwanayo.
52 A irail karos sangesang o mamaukeki i. A i kotin masani: Komail der sangesang! Pwe a sota melar, a mamair eta.
Pa nthawiyi nʼkuti anthu onse akubuma ndi kumulirira iye. Yesu anati, “Lekani kulira, sanafe koma wagona tulo.”
53 Rap kaururki, pwe re asa, me a melar.
Iwo anamuseka podziwa kuti anali atamwalira.
54 I ari kotikiiei sang ir nan pera o, a ap kotin ale pa a warong ong i masani: Seripein, paurida!
Koma Iye anamugwira dzanja lake ndipo anati, “Mwana wanga, dzuka!”
55 Ngen en seripein ap pure dong i, i ari madang uda. I ap kotin masani, kisin manga en ko ong.
Mzimu wake unabwerera, ndipo nthawi yomweyo anayimirira. Kenaka Yesu anawawuza kuti amupatse chakudya.
56 A sam a in a puriamui kila. I ari kotin inapwiedi irail ren der indang meamen me wiauier.
Makolo ake anadabwa, koma Iye anawalamulira kuti asawuze wina aliyense zimene zinachitikazo.

< Lukas 8 >