< زکریا 1 >

در ماه هشتم از سال دوم داریوش، کلام خداوند بر زکریا ابن برکیا ابن عدوی نبی نازل شده، گفت: ۱ 1
Mwezi wachisanu ndi chitatu, mʼchaka chachiwiri cha ulamuliro wa Dariyo, Yehova anayankhula ndi mneneri Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido, kuti:
«خداوند بر پدران شما بسیارغضبناک بود. ۲ 2
“Yehova anakwiya kwambiri ndi makolo anu.
پس به ایشان بگو: یهوه صبایوت چنین می‌گوید بسوی من بازگشت کنید. قول یهوه صبایوت این است. و یهوه صبایوت می‌گوید: من به سوی شما رجوع خواهم نمود. ۳ 3
Choncho awuze anthuwa kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Bwererani kwa Ine,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. ‘Ndipo Ine ndidzabwerera kwa inu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
شما مثل پدران خود مباشید که انبیا سلف ایشان را نداکرده، گفتند یهوه صبایوت چنین می‌گوید ازراههای زشت خود و از اعمال بد خویش بازگشت نمایید، اما خداوند می‌گوید که ایشان نشنیدند و به من گوش ندادند. ۴ 4
Musakhale ngati makolo anu, amene aneneri akale anawalalikira kuti: Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Tsopano lekani njira zanu zoyipa ndi machitidwe anu oyipawo.’ Koma iwo sanamvere kapena kulabadira za Ine, akutero Yehova.
پدران شما کجاهستند و آیا انبیا همیشه زنده می‌مانند؟ ۵ 5
Kodi makolo anuwo ali kuti tsopano? Nanga aneneri, kodi amakhalapo mpaka muyaya?
لیکن کلام و فرایض من که به بندگان خود انبیاامرفرموده بودم، آیا پدران شما را در نگرفت؟ وچون ایشان بازگشت نمودند، گفتند چنانکه یهوه صبایوت قصد نمود که موافق راهها و اعمال ما به ما عمل نماید همچنان به ما عمل نموده است.» ۶ 6
Kodi mawu anga ndi malangizo anga, amene ndinawawuza atumiki anga aneneri, suja anawachitira makolo anu? “Tsono iwo analapa ndi kunena kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse watichitira zomwe zikuyenera njira zathu ndi machitidwe athu, monga anatsimikiza kuti adzachita.’”
در روز بیست و چهارم ماه یازدهم که ماه شباط باشد، از سال دوم داریوش، کلام خداوندبر زکریا ابن برکیا ابن عدوی نبی نازل شده، گفت: ۷ 7
Tsiku la 24 la mwezi wa 11, mwezi wa Sebati, chaka chachiwiri cha ulamuliro wa Dariyo, Yehova anayankhula ndi Zekariya mwana wa Berekiya, mwana wa Ido.
در وقت شب دیدم که اینک مردی بر اسب سرخ سوار بود و در میان درختان آس که در وادی بود ایستاده و در عقب او اسبان سرخ و زرد و سفیدبود. ۸ 8
Nthawi ya usiku ndinaona masomphenya. Ndinaona munthu atakwera pa kavalo wofiira. Iye anayima pakati pa mitengo ya mchisu mʼchigwa. Kumbuyo kwake kunali akavalo ofiira, akhofi ndi oyera.
و گفتم: «ای آقایم اینها چیستند؟» وفرشته‌ای که با من تکلم می‌نمود، مرا گفت: «من تورا نشان می‌دهم که اینها چیستند.» ۹ 9
Ine ndinafunsa kuti, “Mbuye wanga, kodi zimenezi ndi chiyani?” Mngelo amene amayankhula nane anayankha kuti, “Ndidzakuonetsa kuti zimenezi ndi chiyani.”
پس آن مرد که در میان درختان آس ایستاده بود، جواب داد و گفت: «اینها کسانی می‌باشند که خداوند ایشان را برای تردد نمودن در جهان فرستاده است.» ۱۰ 10
Pamenepo munthu amene anayima pakati pa mitengo ya mchisu anafotokoza kuti, “Amenewa ndiwo amene Yehova wawatuma kuti ayendere dziko lonse lapansi.”
و ایشان به فرشته خداوند که در میان درختان آس ایستاده بودجواب داده، گفتند: «ما در جهان تردد نموده‌ایم واینک تمامی جهان مستریح و آرام است.» ۱۱ 11
Ndipo okwera pa akavalo enawo anafotokoza kwa mngelo wa Yehova, amene anayima pakati pa mitengo ya mchisu kuti, “Ife tayendera dziko lonse lapansi ndipo tapeza kuti dziko lonselo lili pa bata ndi mtendere.”
وفرشته خداوند جواب داده، گفت: «ای یهوه صبایوت تا به کی بر اورشلیم و شهرهای یهودا که در این هفتاد سال غضبناک می‌بودی رحمت نخواهی نمود؟» ۱۲ 12
Tsono mngelo wa Yehova anati, “Yehova Wamphamvuzonse, kodi mpaka liti mudzakhala osaonetsa chifundo chanu kwa Yerusalemu ndi mizinda ya Yuda, amene mwawakwiyira kwa zaka izi 70?”
و خداوند با سخنان نیکو وکلام تسلی آمیز آن فرشته‌ای را که با من تکلم می‌نمود جواب داد. ۱۳ 13
Choncho Yehova anayankhula mawu abwino ndi achitonthozo kwa mngelo amene ankayankhula nane.
پس فرشته‌ای که با من تکلم می‌نمود مراگفت: «ندا کرده بگو یهوه صبایوت چنین می‌گوید: در باره اورشلیم و صهیون غیرت عظیمی داشتم. ۱۴ 14
Pamenepo mngelo amene ankayankhula nane anati, “Lengeza mawu awa: Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndikuchitira nsanje Yerusalemu ndi Ziyoni,
و برامت های مطمئن سخت غضبناک شدم زیرا که اندک غضبناک می‌بودم لیکن ایشان بلا را زیاده کردند. ۱۵ 15
koma ndakwiya kwambiri ndi anthu a mitundu ina amene akuganiza kuti ali pa mtendere. Ndinakwiyira anthu anga pangʼono pokha, koma iwo anawonjeza kuzunza anthu angawo.’
بنابراین خداوندچنین می‌گوید: به اورشلیم با رحمت‌ها رجوع خواهم نمود و خانه من در آن بنا خواهد شد. قول یهوه صبایوت این است و ریسمانکاری بر اورشلیم کشیده خواهد شد. ۱۶ 16
“Choncho, Yehova akuti, ‘Ndidzabwerera ku Yerusalemu ndi mtima wachifundo, nyumba yanga adzayimanganso kumeneko. Ndipo adzatenganso chingwe choyezera kuti amange Yerusalemu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
بار دیگر نداکرده، بگو که یهوه صبایوت چنین می‌گوید: شهرهای من بار دیگر به سعادتمندی لبریزخواهد شد و خداوند صهیون را باز تسلی خواهد داد و اورشلیم را بار دیگر خواهدبرگزید.» ۱۷ 17
“Lengezanso kuti, Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Mizinda yanga idzakhalanso ndi zokoma zosefukira ndipo Yehova adzatonthoza Ziyoni ndi kusankhanso Yerusalemu.’”
پس چشمان خود را برافراشته، نگریستم واینک چهار شاخ بود. ۱۸ 18
Kenaka ndinayangʼananso, ndipo patsogolo panga panali nyanga zinayi.
و به فرشته‌ای که با من تکلم می‌نمود گفتم: «اینها چیستند؟» او مرا گفت: «اینها شاخها می‌باشند که یهودا و اسرائیل واورشلیم را پراکنده ساخته‌اند.» ۱۹ 19
Ndinamufunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Kodi zimenezi ndi chiyani?” Iye anandiyankha kuti, “Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda, Israeli ndi Yerusalemu.”
و خداوندچهار آهنگر به من نشان داد. ۲۰ 20
Kenaka Yehova anandionetsa amisiri azitsulo anayi.
و گفتم: «اینان برای چه‌کار می‌آیند؟» او در جواب گفت: «آنهاشاخها می‌باشند که یهودا را چنان پراکنده نموده‌اند که احدی سر خود را بلند نمی تواند کردو اینها می‌آیند تا آنها را بترسانند و شاخهای امت هایی را که شاخ خود را بر زمین یهودابرافراشته، آن را پراکنده ساخته‌اند بیرون افکنند.» ۲۱ 21
Ndinafunsa kuti, “Amisiri a zitsulowa akudzachita chiyani?” Iye anayankha kuti, “Izi ndi nyanga zimene zinabalalitsa Yuda kotero kuti panalibe wina amene akanalimbana nazo, koma amisiri a zitsulowa abwera kudzaziopseza ndi kugwetsa nyanga zimenezi za mitundu ya anthu amene analimbana ndi dziko la Yuda ndi kubalalitsa anthu ake.”

< زکریا 1 >