< مزامیر 98 >

مزمور برای خداوند سرود تازه بسرایید زیراکارهای عجیب کرده است. دست راست و بازوی قدوس او، او را مظفر ساخته است. ۱ 1
Salimo. Imbirani Yehova nyimbo yatsopano, pakuti Iyeyo wachita zinthu zodabwitsa; dzanja lake lamanja ndi mkono wake woyera zamuchitira chipulumutso.
خداوند نجات خود را اعلام نموده، وعدالتش را به نظر امت‌ها مکشوف کرده است. ۲ 2
Yehova waonetsa chipulumutso chake ndipo waulula chilungamo chake kwa anthu a mitundu ina.
رحمت و امانت خود را با خاندان اسرائیل به یادآورد. همه اقصای زمین نجات خدای ما رادیده‌اند. ۳ 3
Iye wakumbukira chikondi chake ndi kukhulupirika kwake pa Aisraeli; malekezero onse a dziko lapansi aona chipulumutso cha Mulungu wathu.
‌ای تمامی زمین، خداوند را آواز شادمانی دهید. بانگ زنید و ترنم نمایید و بسرایید. ۴ 4
Fuwulani mwachimwemwe kwa Yehova, dziko lonse lapansi, muyimbireni nyimbo mofuwula ndi mokondwera.
خداوند را با بربط بسرایید! با بربط و با آوازنغمات! ۵ 5
Imbirani Yehova nyimbo ndi zeze, ndi zeze ndi mawu a kuyimba,
با کرناها و آواز سرنا! به حضور یهوه پادشاه آواز شادمانی دهید! ۶ 6
ndi malipenga ndi kuliza kwa nyanga ya nkhosa yayimuna fuwulani mwachimwemwe pamaso pa Yehova Mfumu.
دریا و پری آن بخروشد! ربع مسکون و ساکنان آن! ۷ 7
Nyanja ikokome pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo, dziko lonse ndi onse amene amakhala mʼmenemo.
نهرهادستک بزنند! و کوهها با هم ترنم نمایند. ۸ 8
Mitsinje iwombe mʼmanja mwawo, mapiri ayimbe pamodzi mwachimwemwe;
به حضور خداوند زیرا به داوری جهان می‌آید. ربع مسکون را به انصاف داوری خواهد کرد و قومهارا به راستی. ۹ 9
izo ziyimbe pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi. Adzaweruza dziko lonse mwachilungamo, ndi mitundu ya anthu mosakondera.

< مزامیر 98 >