< مزامیر 8 >

برای سالار مغنیان برجتیت. مزمور داود ای یهوه خداوند ما، چه مجید است نام تودر تمامی زمین، که جلال خود را فوق آسمانها گذارده‌ای! ۱ 1
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa gititi. Salimo la Davide. Inu Yehova Ambuye athu, dzina lanu ndi la lamphamvudi pa dziko lonse lapansi! Inu mwakhazikitsa ulemerero wanu mʼmayiko onse akumwamba.
از زبان کودکان وشیرخوارگان به‌سبب خصمانت قوت را بنا نهادی تا دشمن و انتقام گیرنده را ساکت گردانی. ۲ 2
Kuchokera mʼkamwa mwa ana ndi makanda, Inu mwakhazikitsa mphamvu chifukwa cha adani anu, kukhazikitsa bata adani ndi anthu obwezera zoyipa.
چون به آسمان تو نگاه کنم که صنعت انگشتهای توست، و به ماه و ستارگانی که تو آفریده‌ای، ۳ 3
Pamene ndilingalira za mayiko anu akumwamba, ntchito ya zala zanu, mwezi ndi nyenyezi, zimene mwaziyika pa malo ake,
پس انسان چیست که او را به یادآوری، وبنی آدم که از او تفقد نمایی؟ ۴ 4
munthu ndani kuti Inu mumamukumbukira, ndi mwana wa munthu kuti inu mumacheza naye?
او را از فرشتگان اندکی کمتر ساختی و تاج جلال و اکرام را بر سراو گذاردی. ۵ 5
Inu munamupanga kukhala wocheperapo kusiyana ndi zolengedwa zakumwamba ndipo mwamuveka ulemerero ndi ulemu.
او را بر کارهای دست خودت مسلط نمودی، و همه‌چیز را زیر پای وی نهادی، ۶ 6
Inu munamuyika wolamulira ntchito ya manja anu; munayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake;
گوسفندان و گاوان جمیع، و بهایم صحرا را نیز؛ ۷ 7
nkhosa, mbuzi ndi ngʼombe pamodzi ndi nyama zakuthengo,
مرغان هوا و ماهیان دریا را، و هر‌چه بر راههای آبها سیر می‌کند. ۸ 8
mbalame zamlengalenga ndi nsomba zamʼnyanja zonse zimene zimayenda pansi pa nyanja.
‌ای یهوه خداوند ما، چه مجیداست نام تو در تمامی زمین! ۹ 9
Inu Yehova, Ambuye athu, dzina lanu ndi lamphamvudi pa dziko lonse lapansi!

< مزامیر 8 >