< مزامیر 66 >
برای سالار مغنیان. سرود و مزمور ای تمامی زمین، برای خدا بانگ شادمانی بزنید! | ۱ 1 |
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo. Fuwulani kwa Mulungu ndi chimwemwe, dziko lonse lapansi!
جلال نام او رابسرایید! و در تسبیح او جلال او را توصیف نمایید! | ۲ 2 |
Imbani ulemerero wa dzina lake; kumutamanda kwake kukhale kwaulemerero.
خدا را گویید: «چه مهیب است کارهای تو! از شدت قوت تو دشمنانت نزد تو تذلل خواهند کرد! | ۳ 3 |
Nenani kwa Mulungu, “Ntchito zanu ndi zoopsa ndithu! Mphamvu yanu ndi yayikulu kwambiri kotero kuti adani anu amawerama pamaso panu.
تمامی زمین تو را پرستش خواهند کرد و تو را خواهند سرایید و به نام توترنم خواهند نمود.» سلاه. | ۴ 4 |
Dziko lonse lapansi limaweramira inu; limayimba matamando kwa Inu; limayimba matamando pa dzina lanu.” (Sela)
بیایید کارهای خدا را مشاهده کنید. او درکارهای خود به بنی آدم مهیب است. | ۵ 5 |
Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita, ntchito zanu ndi zoopsa ndithu pakati pa anthu.
دریا را به خشکی مبدل ساخت و مردم از نهر با پا عبورکردند. در آنجا بدو شادی نمودیم. | ۶ 6 |
Iye anasandutsa nyanja kukhala malo owuma, iwo anawoloka pa madzi ndi mapazi. Bwerani, tiyeni tikondwere mwa Iye.
در توانایی خود تا به ابد سلطنت میکند و چشمانش مراقب امتها است. فتنه انگیزان خویشتن را برنیفرازند، سلاه. | ۷ 7 |
Iye amalamulira ndi mphamvu zake mpaka muyaya, maso ake amayangʼanira anthu a mitundu ina. Anthu owukira asadzitukumule.
ای قومها، خدای ما را متبارک خوانید وآواز تسبیح او را بشنوانید. | ۸ 8 |
Tamandani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthu, mulole kuti mawu a matamando ake amveke;
که جانهای ما را درحیات قرار میدهد و نمی گذارد که پایهای مالغزش خورد. | ۹ 9 |
Iye watchinjiriza miyoyo yathu ndi kusunga mapazi athu kuti angaterereke.
زیراای خدا تو ما را امتحان کردهای و ما را غال گذاشتهای چنانکه نقره راغال میگذارند. | ۱۰ 10 |
Pakuti Inu Mulungu munatiyesa; munatiyenga ngati siliva.
ما را به دام درآوردی و باری گران بر پشتهای ما نهادی. | ۱۱ 11 |
Inu mwatilowetsa mʼndende ndi kutisenzetsa zolemera pa misana yathu.
مردمان را بر سرما سوار گردانیدی و به آتش و آب درآمدیم. پس ما را بهجای خرم بیرون آوردی. | ۱۲ 12 |
Inu munalola kuti anthu akwere pa mitu yathu; ife tinadutsa mʼmoto ndi mʼmadzi, koma Inu munatibweretsa ku malo a zinthu zochuluka.
قربانی های سوختنی به خانه تو خواهم آورد. نذرهای خود را به تو وفا خواهم نمود، | ۱۳ 13 |
Ine ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza ndi kukwaniritsa malumbiro anga.
که لبهای خود را بر آنها گشودم و در زمان تنگی خودآنها را به زبان خود آوردم. | ۱۴ 14 |
Malumbiro amene milomo yanga inalonjeza ndi pakamwa panga panayankhula pamene ndinali pa mavuto.
قربانی های سوختنی پرواری را نزد تو خواهم گذرانید. گوسالهها و بزها را با بخور قوچها ذبح خواهم کرد، سلاه. | ۱۵ 15 |
Ndidzapereka nsembe nyama zonenepa kwa Inu ndi chopereka cha nkhosa zazimuna; ndidzapereka ngʼombe zamphongo ndi mbuzi. (Sela)
ای همه خداترسان بیایید و بشنوید تا ازآنچه او برای جان من کرده است خبر دهم. | ۱۶ 16 |
Bwerani ndipo mudzamve inu nonse amene mumaopa Mulungu. Ndidzakuwuzani zimene Iyeyo wandichitira.
به دهانم نزد او آواز خود را بلند کردم و تسبیح بلند بر زبان من بود. | ۱۷ 17 |
Ndinafuwula kwa Iye ndi pakamwa panga, matamando ake anali pa lilime panga.
اگر بدی را در دل خودمنظور میداشتم، خداوند مرا نمی شنید. | ۱۸ 18 |
Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga Ambuye sakanamvera;
لیکن خدا مرا شنیده است و به آواز دعای من توجه فرموده. | ۱۹ 19 |
koma ndithu Mulungu wamvetsera ndipo watchera khutu ku mawu a kupempha kwanga.
متبارک باد خدا که دعای مرا ازخود، و رحمت خویش را از من برنگردانیده است. | ۲۰ 20 |
Matamando akhale kwa Mulungu amene sanakane pemphero langa kapena kuletsa chikondi chake pa ine!