< مزامیر 66 >

برای سالار مغنیان. سرود و مزمور ای تمامی زمین، برای خدا بانگ شادمانی بزنید! ۱ 1
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo. Fuwulani kwa Mulungu ndi chimwemwe, dziko lonse lapansi!
جلال نام او رابسرایید! و در تسبیح او جلال او را توصیف نمایید! ۲ 2
Imbani ulemerero wa dzina lake; kumutamanda kwake kukhale kwaulemerero.
خدا را گویید: «چه مهیب است کارهای تو! از شدت قوت تو دشمنانت نزد تو تذلل خواهند کرد! ۳ 3
Nenani kwa Mulungu, “Ntchito zanu ndi zoopsa ndithu! Mphamvu yanu ndi yayikulu kwambiri kotero kuti adani anu amawerama pamaso panu.
تمامی زمین تو را پرستش خواهند کرد و تو را خواهند سرایید و به نام توترنم خواهند نمود.» سلاه. ۴ 4
Dziko lonse lapansi limaweramira inu; limayimba matamando kwa Inu; limayimba matamando pa dzina lanu.” (Sela)
بیایید کارهای خدا را مشاهده کنید. او درکارهای خود به بنی آدم مهیب است. ۵ 5
Bwerani mudzaone zimene Mulungu wachita, ntchito zanu ndi zoopsa ndithu pakati pa anthu.
دریا را به خشکی مبدل ساخت و مردم از نهر با پا عبورکردند. در آنجا بدو شادی نمودیم. ۶ 6
Iye anasandutsa nyanja kukhala malo owuma, iwo anawoloka pa madzi ndi mapazi. Bwerani, tiyeni tikondwere mwa Iye.
در توانایی خود تا به ابد سلطنت می‌کند و چشمانش مراقب امت‌ها است. فتنه انگیزان خویشتن را برنیفرازند، سلاه. ۷ 7
Iye amalamulira ndi mphamvu zake mpaka muyaya, maso ake amayangʼanira anthu a mitundu ina. Anthu owukira asadzitukumule.
‌ای قوم‌ها، خدای ما را متبارک خوانید وآواز تسبیح او را بشنوانید. ۸ 8
Tamandani Mulungu wathu, inu mitundu ya anthu, mulole kuti mawu a matamando ake amveke;
که جانهای ما را درحیات قرار می‌دهد و نمی گذارد که پایهای مالغزش خورد. ۹ 9
Iye watchinjiriza miyoyo yathu ndi kusunga mapazi athu kuti angaterereke.
زیرا‌ای خدا تو ما را امتحان کرده‌ای و ما را غال گذاشته‌ای چنانکه نقره راغال می‌گذارند. ۱۰ 10
Pakuti Inu Mulungu munatiyesa; munatiyenga ngati siliva.
ما را به دام درآوردی و باری گران بر پشتهای ما نهادی. ۱۱ 11
Inu mwatilowetsa mʼndende ndi kutisenzetsa zolemera pa misana yathu.
مردمان را بر سرما سوار گردانیدی و به آتش و آب در‌آمدیم. پس ما را به‌جای خرم بیرون آوردی. ۱۲ 12
Inu munalola kuti anthu akwere pa mitu yathu; ife tinadutsa mʼmoto ndi mʼmadzi, koma Inu munatibweretsa ku malo a zinthu zochuluka.
قربانی های سوختنی به خانه تو خواهم آورد. نذرهای خود را به تو وفا خواهم نمود، ۱۳ 13
Ine ndidzabwera ku Nyumba yanu ndi nsembe zopsereza ndi kukwaniritsa malumbiro anga.
که لبهای خود را بر آنها گشودم و در زمان تنگی خودآنها را به زبان خود آوردم. ۱۴ 14
Malumbiro amene milomo yanga inalonjeza ndi pakamwa panga panayankhula pamene ndinali pa mavuto.
قربانی های سوختنی پرواری را نزد تو خواهم گذرانید. گوساله‌ها و بزها را با بخور قوچها ذبح خواهم کرد، سلاه. ۱۵ 15
Ndidzapereka nsembe nyama zonenepa kwa Inu ndi chopereka cha nkhosa zazimuna; ndidzapereka ngʼombe zamphongo ndi mbuzi. (Sela)
‌ای همه خداترسان بیایید و بشنوید تا ازآنچه او برای جان من کرده است خبر دهم. ۱۶ 16
Bwerani ndipo mudzamve inu nonse amene mumaopa Mulungu. Ndidzakuwuzani zimene Iyeyo wandichitira.
به دهانم نزد او آواز خود را بلند کردم و تسبیح بلند بر زبان من بود. ۱۷ 17
Ndinafuwula kwa Iye ndi pakamwa panga, matamando ake anali pa lilime panga.
اگر بدی را در دل خودمنظور می‌داشتم، خداوند مرا نمی شنید. ۱۸ 18
Ndikanasekerera tchimo mu mtima mwanga Ambuye sakanamvera;
لیکن خدا مرا شنیده است و به آواز دعای من توجه فرموده. ۱۹ 19
koma ndithu Mulungu wamvetsera ndipo watchera khutu ku mawu a kupempha kwanga.
متبارک باد خدا که دعای مرا ازخود، و رحمت خویش را از من برنگردانیده است. ۲۰ 20
Matamando akhale kwa Mulungu amene sanakane pemphero langa kapena kuletsa chikondi chake pa ine!

< مزامیر 66 >