< مزامیر 6 >

برای سالار مغنیان برذوات اوتار برثمانی. مزمور داود ای خداوند، مرا در غضب خود توبیخ منما. و مرا در خشم خویش تادیب مکن! ۱ 1
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Molingana ndi seminiti. Salimo la Davide. Inu Yehova, musandidzudzule mu mkwiyo wanu, kapena kundilanga mu ukali wanu.
‌ای خداوند، بر من کرم فرما زیرا که پژمرده‌ام! ای خداوند، مرا شفا ده زیرا که استخوانهایم مضطرب است، ۲ 2
Ndichitireni chifundo Inu Yehova, pakuti ndalefuka; Inu Yehova chiritseni, pakuti mafupa anga ali pa ululu waukulu.
و جان من بشدت پریشان است. پس تو‌ای خداوند، تا به کی؟ ۳ 3
Moyo wanga uli pa mazunzo aakulu. Mpaka liti, Inu Yehova, mpaka liti?
‌ای خداوند، رجوع کن و جانم را خلاصی ده! به رحمت خویش مرا نجات‌بخش! ۴ 4
Tembenukani Inu Yehova, ndipo mundilanditse; pulumutseni chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika.
زیرا که در موت ذکرتو نمی باشد! در هاویه کیست که تو را حمدگوید؟ (Sheol h7585) ۵ 5
Palibe amene amakukumbukirani pamene wamwalira; Amakutamandani ndani ali ku manda? (Sheol h7585)
از ناله خود وامانده‌ام! تمامی شب تخت خواب خود را غرق می‌کنم، و بسترخویش را به اشکها تر می‌سازم! ۶ 6
Ine ndatopa ndi kubuwula; usiku wonse pa bedi panga pamadzaza ndi misozi yanga; ndimanyowetsa pogona panga ndi misozi.
چشم من ازغصه کاهیده شد و بسبب همه دشمنانم تارگردید. ۷ 7
Maso anga atupa chifukwa cha chisoni; akulephera kuona chifukwa cha adani anga.
‌ای همه بدکاران از من دور شوید، زیراخداوند آواز گریه مرا شنیده است! ۸ 8
Chokani kwa ine inu nonse amene mumachita zoyipa, pakuti Yehova wamva kulira kwanga.
خداونداستغاثه مرا شنیده است. خداوند دعای مرااجابت خواهد نمود. ۹ 9
Yehova wamva kupempha kwanga kofuna chifundo; Yehova walandira pemphero langa.
همه دشمنانم به شدت خجل و پریشان خواهند شد. روبرگردانیده، ناگهان خجل خواهند گردید. ۱۰ 10
Adani anga onse adzachita manyazi ndipo adzakhala ndi mantha; adzabwerera msangamsanga mwa manyazi.

< مزامیر 6 >