< مزامیر 56 >

برای سالار مغنیان بر فاخته ساکت در بلاد بعیده. مکتوم داود وقتی که فلسطینیان او را در جت گرفتند ای خدا بر من رحم فرما، زیرا که انسان مرا به شدت تعاقب می‌کند. تمامی روزجنگ کرده، مرا اذیت می‌نماید. ۱ 1
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Njiwa pa Mtengo wa Thundu wa Kutali.” Mikitamu ya Davide, pamene Afilisti anamugwira ku Gati. Mundichitire chifundo Inu Mulungu, pakuti anthu akundithamangitsa kwambiri; tsiku lonse akundithira nkhondo.
خصمانم تمامی روز مرا به شدت تعاقب می‌کنند. زیرا که بسیاری با تکبر با من می‌جنگند. ۲ 2
Ondinyoza akundithamangitsa tsiku lonse, ambiri akumenyana nane monyada.
هنگامی که ترسان شوم، من بر تو توکل خواهم داشت. ۳ 3
Ndikachita mantha ndimadalira Inu.
در خدا کلام او را خواهم ستود. بر خداتوکل کرده، نخواهم ترسید. انسان به من چه می‌تواند کرد؟ ۴ 4
Mwa Mulungu, amene mawu ake ine ndimatamanda, mwa Mulungu ine ndimadaliramo; sindidzachita mantha. Kodi munthu amene amafa angandichite chiyani?
هر روزه سخنان مرا منحرف می‌سازند. همه فکرهای ایشان درباره من برشرارت است. ۵ 5
Tsiku lonse amatembenuza mawu anga; nthawi zonse amakonza zondivulaza.
ایشان جمع شده، کمین می‌سازند. بر قدمهای من چشم دارند زیرا قصدجان من دارند. ۶ 6
Iwo amakambirana, amandibisalira, amayangʼanitsitsa mayendedwe anga ndipo amakhala ndi chidwi chofuna kuchotsa moyo wanga.
آیا ایشان به‌سبب شرارت خودنجات خواهند یافت؟ ای خدا امت‌ها را درغضب خویش بینداز. ۷ 7
Musalole konse kuti athawe; mu mkwiyo wanu Mulungu mugwetse mitundu ya anthu.
تو آوارگیهای مرا تقریر کرده‌ای. اشکهایم را در مشک خود بگذار. آیا این در دفتر تو نیست؟ ۸ 8
Mulembe za kulira kwanga, mulembe chiwerengero cha misozi yanga mʼbuku lanu. Kodi zimenezi sizinalembedwe mʼbuku lanulo?
آنگاه در روزی که تو رابخوانم دشمنانم روخواهند گردانید. این رامی دانم زیرا خدا با من است. ۹ 9
Adani anga adzabwerera mʼmbuyo pamene ndidzalirira kwa Inu. Pamenepo ndidzadziwa kuti Mulungu ali ku mbali yanga.
در خدا کلام او را خواهم ستود. درخداوند کلام او را خواهم ستود. ۱۰ 10
Mwa Mulungu amene mawu ake ndimawatamanda, mwa Yehova amene mawu ake ndimawatamanda,
بر خدا توکل دارم پس نخواهم ترسید. آدمیان به من چه می‌توانند کرد؟ ۱۱ 11
mwa Mulungu ine ndimadalira ndipo sindidzachita mantha. Kodi munthu angandichite chiyani?
‌ای خدا نذرهای تو بر من است. قربانی های حمد را نزد تو خواهم گذرانید. ۱۲ 12
Ndiyenera kuchita zomwe ndinalumbira kwa Mulungu; ndidzapereka nsembe zanga zachiyamiko kwa inu.
زیرا که جانم را از موت رهانیده‌ای. آیا پایهایم را نیز از لغزیدن نگاه نخواهی داشت تا در نورزندگان به حضور خدا سالک باشم؟ ۱۳ 13
Pakuti mwawombola moyo wanga ku imfa ndi mapazi anga kuti ndingagwe, kuti ndiyende pamaso pa Mulungu mʼkuwala kwa moyo.

< مزامیر 56 >