< مزامیر 106 >

هللویاه! خداوند را حمد بگوییدزیرا که او نیکو است و رحمت او تاابدالاباد! ۱ 1
Tamandani Yehova. Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.
کیست که اعمال عظیم خداوند رابگوید و همه تسبیحات او را بشنواند؟ ۲ 2
Ndani angathe kufotokoza za ntchito zamphamvu za Yehova kapena kumutamanda mokwanira?
خوشابحال آنانی که انصاف را نگاه دارند و آن که عدالت را در همه وقت به عمل آورد. ۳ 3
Odala ndi amene amasunga chilungamo, amene amachita zolungama nthawi zonse.
‌ای خداوند مرا یاد کن به رضامندیی که با قوم خودمی داری و به نجات خود از من تفقد نما. ۴ 4
Mundikumbukire Yehova, pamene mukuonetsa kukoma mtima kwanu kwa anthu anu, bwerani mudzandithandize pamene mukuwapulumutsa iwo,
تاسعادت برگزیدگان تو را ببینم و به شادمانی قوم تو مسرور شوم و با میراث تو فخر نمایم. ۵ 5
kuti ndidzasangalale ndi chuma cha anthu anu osankhika, kuti ndidzakhale nacho chimwemwe cha anthu anu ndi kukhala pamodzi ndi cholowa chanu pa kukutamandani.
با پدران خود گناه نموده‌ایم و عصیان ورزیده، شرارت کرده‌ایم. ۶ 6
Ife tachimwa monga momwe anachitira makolo athu; tachita zolakwa ndipo tachita moyipa.
پدران ما کارهای عجیب تو را در مصر نفهمیدند و کثرت رحمت تو را به یاد نیاوردند بلکه نزد دریا یعنی بحر قلزم فتنه انگیختند. ۷ 7
Pamene makolo athu anali mu Igupto, sanalingalire za zozizwitsa zanu; iwo sanakumbukire kukoma mtima kwanu kochuluka, ndipo anawukira Inu pa Nyanja Yofiira.
لیکن به‌خاطر اسم خود ایشان رانجات داد تا توانایی خود را اعلان نماید. ۸ 8
Komabe Iye anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake, kuti aonetse mphamvu zake zazikulu.
و بحرقلزم را عتاب کرد که خشک گردید. پس ایشان رادر لجه‌ها مثل بیابان رهبری فرمود. ۹ 9
Anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo inawuma; anawatsogolera mʼnyanja yakuya ngati akuyenda mʼchipululu.
و ایشان رااز دست دشمن نجات داد و از دست خصم رهایی بخشید. ۱۰ 10
Anawapulumutsa mʼdzanja la amaliwongo; anawawombola mʼdzanja la mdani.
و آب، دشمنان ایشان را پوشانید که یکی از ایشان باقی نماند. ۱۱ 11
Madzi anamiza adani awo, palibe mmodzi wa iwo anapulumuka.
آنگاه به کلام اوایمان آوردند و حمد او را سراییدند. ۱۲ 12
Kenaka iwo anakhulupirira malonjezo ake ndi kuyimba nyimbo zamatamando.
لیکن اعمال او را به زودی فراموش کردند و مشورت اورا انتظار نکشیدند. ۱۳ 13
Koma posachedwa anayiwala zimene Iye anachita, ndipo sanayembekezere uphungu wake.
بلکه شهوت‌پرستی نمودنددر بادیه؛ و خدا را امتحان کردند در هامون. ۱۴ 14
Mʼchipululu, anadzipereka ku zilakolako zawo; mʼdziko lopanda kanthu anayesa Mulungu.
ومسالت ایشان را بدیشان داد. لیکن لاغری درجانهای ایشان فرستاد. ۱۵ 15
Choncho Iye anawapatsa chimene anapempha, koma anatumiza nthenda yowondetsa.
پس به موسی در اردو حسد بردند و به هارون، مقدس یهوه. ۱۶ 16
Mʼmisasa, anachitira nsanje Mose ndi Aaroni, amene Yehova anadzipatulira.
و زمین شکافته شده، داتان را فرو برد و جماعت ابیرام را پوشانید. ۱۷ 17
Nthaka inatsekuka ndipo inameza Datani; inakwirira gulu la Abiramu.
وآتش، در جماعت ایشان افروخته شده، شعله آتش شریران را سوزانید. ۱۸ 18
Moto unayaka pakati pa otsatira awo; lawi lamoto linapsereza anthu oyipa.
گوساله‌ای درحوریب ساختند و بتی ریخته شده را پرستش نمودند. ۱۹ 19
Iwo anapanga mwana wangʼombe pa Horebu ndi kulambira fano loyengedwa kuchokera ku chitsulo.
و جلال خود را تبدیل نمودند به مثال گاوی که علف می‌خورد. ۲۰ 20
Anasinthanitsa ulemerero wawo ndi fano la ngʼombe yayimuna imene imadya udzu.
و خدای نجات‌دهنده خود را فراموش کردند که کارهای عظیم در مصر کرده بود. ۲۱ 21
Anayiwala Mulungu amene anawapulumutsa, amene anachita zinthu zazikulu mu Igupto,
و اعمال عجیبه را در زمین حام و کارهای ترسناک را در بحر قلزم. ۲۲ 22
zozizwitsa mʼdziko la Hamu ndi machitidwe ake woopsa pa Nyanja Yofiira.
آنگاه گفت که ایشان را هلاک بکند. اگر برگزیده اوموسی در شکاف به حضور وی نمی ایستاد، تاغضب او را از هلاکت ایشان برگرداند. ۲۳ 23
Choncho Iye anawawuza kuti adzawawononga, pakanapanda Mose, mtumiki wake wosankhidwa, kuyima pamaso pake, ndi kuletsa mkwiyo wake kuti usawawononge.
و زمین مرغوب را خوار شمردند و به کلام وی ایمان نیاوردند. ۲۴ 24
Motero iwo ananyoza dziko lokoma; sanakhulupirire malonjezo ake.
و در خیمه های خود همهمه کردندو قول خداوند را استماع ننمودند. ۲۵ 25
Anangʼungʼudza mʼmatenti mwawo ndipo sanamvere Yehova.
لهذا دست خود را برایشان برافراشت، که ایشان را در صحرااز پا درآورد. ۲۶ 26
Kotero Iye analumbira atakweza dzanja lake, kuti adzachititsa kuti iwowo afere mʼchipululu,
و ذریت ایشان را در میان امتهابیندازد و ایشان را در زمینها پراکنده کند. ۲۷ 27
kuchititsa kuti zidzukulu zawo zifere pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsa mʼdziko lonse.
پس به بعل فغور پیوستند و قربانی های مردگان راخوردند. ۲۸ 28
Iwo anayamba kupembedza Baala-Peori ndi kudya nsembe zoperekedwa kwa milungu yopanda moyo;
و به‌کارهای خود خشم او را به هیجان آوردند و وبا بر ایشان سخت آمد. ۲۹ 29
anaputa mkwiyo wa Yehova pa machitidwe awo oyipa, ndipo mliri unabuka pakati pawo.
آنگاه فینحاس بر پا ایستاده، داوری نمود ووبا برداشته شد. ۳۰ 30
Koma Finehasi anayimirira ndi kulowererapo, ndipo mliri unaleka.
و این برای او به عدالت محسوب گردید، نسلا بعد نسل تا ابدالاباد. ۳۱ 31
Chimenechi ndicho chinayesedwa chilungamo chake, kwa mibado yosatha imene ikubwera.
واو را نزد آب مریبه غضبناک نمودند. حتی موسی را به‌خاطر ایشان آزاری عارض گردید. ۳۲ 32
Pa madzi a ku Meriba iwo anakwiyitsa Yehova ndipo mavuto anabwera kwa Mose chifukwa cha anthuwo,
زیراکه روح او را تلخ ساختند، تا از لبهای خود ناسزاگفت. ۳۳ 33
pakuti iwowo anawukira mzimu wa Mulungu, ndipo pa milomo ya Mose panatuluka mawu osayenera.
و آن قوم‌ها را هلاک نکردند، که درباره ایشان خداوند امر فرموده بود. ۳۴ 34
Aisraeliwo sanawononge mitundu ya anthu monga momwe Yehova anawalamulira.
بلکه خویشتن را با امتها آمیختند و کارهای ایشان را آموختند. ۳۵ 35
Koma anasakanizana ndi anthu a mitundu inayo ndi kuphunzira miyambo yawo.
و بتهای ایشان را پرستش نمودند تا آنکه برای ایشان دام گردید. ۳۶ 36
Ndipo anapembedza mafano awo, amene anakhala msampha kwa iwowo.
و پسران و دختران خویش رابرای دیوها قربانی گذرانیدند. ۳۷ 37
Anapereka nsembe ana awo aamuna ndi ana awo aakazi kwa ziwanda.
و خون بی‌گناه راریختند یعنی خون پسران و دختران خود را که آن را برای بتهای کنعان ذبح کردند و زمین از خون ملوث گردید. ۳۸ 38
Anakhetsa magazi a anthu osalakwa, magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi, amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanaani, ndipo dziko linayipitsidwa ndi magazi awo.
و از کارهای خود نجس شدند ودر افعال خویش زناکار گردیدند. ۳۹ 39
Iwo anadzidetsa okha ndi zimene anachita; ndi machitidwe awo amakhala ngati munthu wachigololo.
لهذا خشم خداوند بر قوم خود افروخته شد و میراث خویش را مکروه داشت. ۴۰ 40
Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake.
و ایشان را به‌دست امتها تسلیم نمود تا آنانی که از ایشان نفرت داشتند، بر ایشان حکمرانی کردند. ۴۱ 41
Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina, ndipo adani awo anawalamulira.
و دشمنان ایشان بر ایشان ظلم نمودند و زیر دست ایشان ذلیل گردیدند. ۴۲ 42
Adani awo anawazunza ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo.
بارهای بسیار ایشان راخلاصی داد. لیکن به مشورتهای خویش براو فتنه کردند و به‌سبب گناه خویش خوار گردیدند. ۴۳ 43
Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri, koma iwo ankatsimikiza za kuwukira ndipo anawonongeka mʼmachimo awo.
با وجود این، بر تنگی ایشان نظر کرد، وقتی که فریاد ایشان را شنید. ۴۴ 44
Koma Iye anaona kuzunzika kwawo pamene anamva kulira kwawo;
و به‌خاطر ایشان، عهدخود را به یاد آورد و در کثرت رحمت خویش بازگشت نمود. ۴۵ 45
Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake.
و ایشان را حرمت داد، در نظرجمیع اسیرکنندگان ایشان. ۴۶ 46
Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo awamvere chisoni.
‌ای یهوه خدای ما، ما را نجات ده! و ما را از میان امتها جمع کن! تا نام قدوس تو را حمد گوییم و در تسبیح تو فخرنماییم. ۴۷ 47
Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu, ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera ndi kunyadira mʼmatamando anu.
یهوه خدای اسرائیل متبارک باد از ازل تا ابدالاباد. و تمامی قوم بگویند آمین. هللویاه! ۴۸ 48
Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, Kuyambira muyaya mpaka muyaya. Anthu onse anene kuti, “Ameni!” Tamandani Yehova.

< مزامیر 106 >