< لوقا 3 >

و در سال پانزدهم از سلطنت طیباریوس قیصر، در وقتی که پنطیوس پیلاطس، والی یهودیه بود و هیرودیس، تیترارک جلیل وبرادرش فیلپس تیترارک ایطوریه تراخونیتس ولیسانیوس تیترارک آبلیه ۱ 1
Mʼchaka cha 15 mu ulamuliro wa Tiberiyo Kaisara, Pontiyo Pilato ali bwanamkubwa wa Yudeya, Herode ankalamulira ku Galileya, mʼbale wake Filipo ankalamulira ku Iturea ndi ku dera la Trakoniti, ndipo Lusaniyo ankalamulira ku Abilene.
و حنا و قیافا روسای کهنه بودند، کلام خدا به یحیی ابن زکریا در بیابان نازل شده، ۲ 2
Inalinso nthawi ya mkulu wa ansembe wa Anasi ndi Kayafa, pamene mawu a Mulungu anabwera kwa Yohane mwana wa Zakariya mʼchipululu.
به تمامی حوالی اردن آمده، به تعمیدتوبه بجهت آمرزش گناهان موعظه می‌کرد. ۳ 3
Iye anapita ku dziko lonse lozungulira mtsinje wa Yorodani, nalalikira ubatizo wa kulapa ndi kukhululukidwa kwa machimo.
چنانچه مکتوب است در صحیفه کلمات اشعیای نبی که می‌گوید: «صدای ندا کننده‌ای دربیابان که راه خداوند را مهیا سازید و طرق او راراست نمایید. ۴ 4
Monga analembera mʼbuku la Yesaya mneneri kuti: “Mawu a wofuwula mʼchipululu, konzani njira ya Ambuye, wongolani njira zake.
هر وادی انباشته و هر کوه و تلی پست و هر کجی راست و هر راه ناهموار صاف خواهد شد ۵ 5
Chigwa chilichonse chidzadzazidwa ndipo phiri lililonse ndi mtunda uliwonse zidzasalazidwa, misewu yokhotakhota idzawongoledwa, ndi njira zosasalala zidzasalazidwa.
و تمامی بشر نجات خدا را خواهنددید.» ۶ 6
Ndipo anthu onse adzaona chipulumutso cha Mulungu.”
آنگاه به آن جماعتی که برای تعمید وی بیرون می‌آمدند، گفت: «ای افعی‌زادگان، که شمارا نشان داد که از غضب آینده بگریزید؟ ۷ 7
Yohane anati kwa magulu a anthu amene amabwera kudzabatizidwa ndi iye, “Ana anjoka inu! Anakuchenjezani ndani kuti muthawe mkwiyo umene ukubwera?
پس ثمرات مناسب توبه بیاورید و در خاطر خود این سخن را راه مدهید که ابراهیم پدر ماست، زیرا به شما می‌گویم خدا قادر است که از این سنگها، فرزندان برای ابراهیم برانگیزاند. ۸ 8
Onetsani zipatso zakutembenuka mtima, ndipo musamanene mwa inu nokha kuti, ‘Tili nalo kholo lathu Abrahamu,’ pakuti ndikuwuzani kuti kuchokera ku miyala iyi, Mulungu akhoza kumuwutsira Abrahamuyo ana.
و الان نیز تیشه بر ریشه درختان نهاده شده است، پس هر درختی که میوه نیکو نیاورد، بریده و در آتش افکنده می‌شود.» ۹ 9
Nkhwangwa ili kale pa muzu wamitengo, ndipo mtengo uliwonse umene subala chipatso chabwino udzadulidwa ndi kuponyedwa pa moto.”
پس مردم از وی سوال نموده گفتند: «چه کنیم؟» ۱۰ 10
Gulu la anthuwo linafunsa kuti, “Nanga tsono tichite chiyani?”
او در جواب ایشان گفت: «هر‌که دوجامه دارد، به آنکه ندارد بدهد. و هرکه خوراک دارد نیز چنین کند.» ۱۱ 11
Yohane anayankha kuti, “Munthu amene ali ndi malaya awiri apatseko amene alibe, ndi amene ali ndi chakudya achitenso chimodzimodzi.”
و باجگیران نیز برای تعمید آمده، بدو گفتند: «ای استاد چه کنیم؟» ۱۲ 12
Amisonkho nawonso anabwera kudzabatizidwa. Iwo anafunsa kuti, “Aphunzitsi, ife tichite chiyani?”
بدیشان گفت: «زیادتر از آنچه مقرر است، مگیرید.» ۱۳ 13
Iye anawawuza kuti, “Musalandire moposa zimene muyenera.”
سپاهیان نیز از او پرسیده، گفتند: «ماچه کنیم؟» به ایشان گفت: «بر کسی ظلم مکنید وبر هیچ‌کس افترا مزنید و به مواجب خود اکتفاکنید.» ۱۴ 14
Kenaka asilikali ena anamufunsa kuti, “Nanga ife tichite chiyani?” Iye anayankha kuti, “Musamalande ndalama moopseza ndipo musamanamizire anthu, khutitsidwani ndi malipiro anu.”
و هنگامی که قوم مترصد می‌بودند و همه در خاطر خود درباره یحیی تفکر می‌نمودندکه این مسیح است یا نه، ۱۵ 15
Anthu ankadikira ndi chiyembekezo ndipo ankasinkhasinkha mʼmitima mwawo kuti mwina Yohane nʼkukhala Khristu.
یحیی به همه متوجه شده گفت: «من شما را به آب تعمیدمی دهم، لیکن شخصی تواناتر از من می‌آید که لیاقت آن ندارم که بند نعلین او را باز کنم. اوشما را به روح‌القدس و آتش تعمید خواهد داد. ۱۶ 16
Yohane anayankha onse kuti, “Ine ndikubatizani ndi madzi. Koma wina wondiposa ine mphamvu adzabwera amene sindili woyenera kumasula lamba wa nsapato zake. Iyeyu adzakubatizani inu ndi Mzimu Woyera ndi moto.
او غربال خود را به‌دست خود دارد وخرمن خویش را پاک کرده، گندم را در انبارخود ذخیره خواهد نمود و کاه را در آتشی که خاموشی نمی پذیرد خواهد سوزانید.» ۱۷ 17
Mʼdzanja lake muli chopetera kuti ayeretse powomberapo tirigu ndi kusonkhanitsa tirigu ndipo adzatentha zotsalira zonse ndi moto wosazimitsika.”
وبه نصایح بسیار دیگر، قوم را بشارت می‌داد. ۱۸ 18
Ndipo ndi mawu ena ambiri, Yohane anawachenjeza anthu ndi kuwalalikira Uthenga Wabwino.
اما هیرودیس تیترارک چون به‌سبب هیرودیا، زن برادر او فیلپس و سایر بدیهایی که هیرودیس کرده بود از وی توبیخ یافت، ۱۹ 19
Koma pamene Yohane anadzudzula Herode wolamulirayo chifukwa chokwatira Herodia, mkazi wa mʼbale wake, ndi zoyipa zina zonse anazichita,
این رانیز بر همه افزود که یحیی را در زندان حبس نمود. ۲۰ 20
Herode anawonjezanso choyipa ichi pa zonsezo: Anatsekera Yohane mʼndende.
اما چون تمامی قوم تعمید یافته بودند وعیسی هم تعمید گرفته دعا می‌کرد، آسمان شکافته شد ۲۱ 21
Pamene anthu onse ankabatizidwa, Yesu anabatizidwanso. Ndipo akupemphera, kumwamba kunatsekuka.
و روح‌القدس به هیات جسمانی، مانند کبوتری بر او نازل شد. و آوازی از آسمان در‌رسید که تو پسر حبیب من هستی که به توخشنودم. ۲۲ 22
Mzimu Woyera anatsika pa Iye mumaonekedwe a nkhunda ndipo mawu anamveka kuchokera kumwamba: “Iwe ndiwe Mwana wanga wokondedwa; ndimakondwera nawe.”
و خود عیسی وقتی که شروع کرد، قریب به سی ساله بود. و حسب گمان خلق، پسر یوسف ابن هالی ۲۳ 23
Ndipo Yesu anali ndi zaka makumi atatu pamene anayamba ntchito yake. Monga mmene anthu ankaganizira, Iyeyo anali mwana wa Yosefe, mwana wa Heli,
ابن متات، بن لاوی، بن ملکی، بن ینا، بن یوسف، ۲۴ 24
mwana wa Matate, mwana wa Levi, mwana wa Meliki, mwana wa Yaneyi, mwana wa Yosefe
ابن متاتیا، بن آموس، بن ناحوم، بن حسلی، بن نجی، ۲۵ 25
mwana wa Matati, mwana wa Amosi, mwana wa Naomi, mwana wa Esli, mwana wa Nagai,
ابن مات، بن متاتیا، بن شمعی، بن یوسف، بن یهودا، ۲۶ 26
mwana wa Maati, mwana wa Matatiyo, mwana wa Simeoni, mwana wa Yosefe, mwana wa Yoda
ابن یوحنا، بن ریسا، بن زروبابل، بن سالتیئیل، بن نیری، ۲۷ 27
mwana wa Yohanani, mwana wa Resa, mwana wa Zerubabeli, mwana wa Salatieli, mwana wa Neri,
ابن ملکی، بن ادی، بن قوسام، بن ایلمودام، بن عیر، ۲۸ 28
mwana wa Meliki, mwana wa Adi, mwana wa Kosamu, mwana wa Elmadama, mwana wa Ere,
ابن یوسی، بن ایلعاذر، بن یوریم، بن متات، بن لاوی، ۲۹ 29
mwana wa Jose, mwana wa Eliezara, mwana wa Yorimu, mwana wa Matati, mwana wa Levi,
ابن شمعون، بن یهودا، بن یوسف، بن یونان، بن ایلیاقیم، ۳۰ 30
mwana wa Simeoni, mwana wa Yuda, mwana wa Yosefe, mwana wa Yonamu, mwana wa Eliakimu,
ابن ملیا، بن مینان، بن متاتا بن ناتان، بن داود، ۳۱ 31
mwana wa Meleya, mwana wa Mena, mwana wa Matata, mwana wa Natani, mwana wa Davide,
ابن یسی، بن عوبید، بن بوعز، بن شلمون، بن نحشون، ۳۲ 32
mwana wa Yese, mwana wa Obedi, mwana wa Bowazi, mwana wa Salimoni, mwana wa Naasoni,
ابن عمیناداب، بن ارام، بن حصرون، بن فارص، بن یهودا، ۳۳ 33
mwana wa Aminadabu, mwana wa Arni, mwana wa Hezronu, mwana wa Perezi, mwana wa Yuda,
ابن یعقوب، بن اسحق، بن ابراهیم، بن تارح، بن ناحور، ۳۴ 34
mwana wa Yakobo, mwana wa Isake, mwana wa Abrahamu, mwana wa Tera, mwana wa Nakoro,
ابن سروج، بن رعور، بن فالج، بن عابر، بن صالح، ۳۵ 35
mwana wa Serugi, mwana wa Reu, mwana wa Pelegi, mwana wa Eberi, mwana wa Sela,
ابن قینان، بن ارفکشاد، بن سام، بن نوح، بن لامک، ۳۶ 36
mwana wa Kainane, mwana wa Arfaksadi, mwana wa Semu, mwana wa Nowa, mwana wa Lameki,
ابن متوشالح، بن خنوخ، بن یارد، بن مهللئیل، بن قینان، ۳۷ 37
mwana wa Metusela, mwana wa Enoki, mwana wa Yaredi mwana wa Malaleeli, mwana wa Kainane,
ابن انوش، بن شیث، بن آدم، بن الله. ۳۸ 38
mwana wa Enosi, mwana wa Seti, mwana wa Adamu, mwana wa Mulungu.

< لوقا 3 >