< لاویان 5 >

بشنود، و او شاهد باشد خواه دیده و خواه دانسته، اگر اطلاع ندهد گناه او را متحمل خواهدبود. ۱ 1
“‘Ngati munthu anayitanidwa ku bwalo kuti akachitire umboni pa zimene anaziona kapena kuzimva koma iye nʼkukana kuchitira umboni, munthu ameneyo wachimwa ndipo ayenera kulangidwa.
یا کسی‌که هر چیز نجس را لمس کند، خواه لاش وحش نجس، خواه لاش بهیمه نجس، خواه لاش حشرات نجس، و از او مخفی باشد، پس نجس و مجرم می‌باشد. ۲ 2
“‘Munthu akakhudza chinthu chilichonse chodetsedwa, monga nyama yakufa ya mʼthengo, kapena chiweto chakufa kapenanso chokwawa chakufa, ngakhale iyeyo wachikhudza mosadziwa, wasanduka wodetsedwa ndipo wachimwa.
یا اگر نجاست آدمی را لمس کند، از هر نجاست او که به آن نجس می‌شود، و از وی مخفی باشد، چون معلوم شد آنگاه مجرم خواهد بود. ۳ 3
“‘Munthu akakhudza choyipitsa munthu cha mtundu uliwonse, ndipo pochikhudzapo ndi kuyipitsidwa nacho mosadziwa, munthuyo adzakhala wopalamula akangodziwa chimene wachitacho.
و اگر کسی غفلت به لبهای خود قسم خورد برای کردن کار بد یا کارنیک، یعنی در هر چیزی که آدمی غفلت قسم خورد، و از او مخفی باشد، چون بر او معلوم شودآنگاه در هر کدام که باشد مجرم خواهد بود. ۴ 4
“‘Munthu akalumbira mofulumira kapena mosasamala kuti adzachita chinthu, choyipa kapena chabwino, ngakhale kuti wachita izi mosadziwa kuti nʼkulakwa, pamene wazindira kulakwa kwake, iye adzakhalabe wopalamula akangodziwa chimene wachitacho.
وچون در هر کدام از اینها مجرم شد، آنگاه به آن چیزی که در آن گناه کرده است اعتراف بنماید. ۵ 5
“‘Pamene munthu wazindikira kuti wachimwa motere, awulule tchimo limene wachitalo.
و قربانی جرم خود را برای گناهی که کرده است نزد خداوند بیاورد، یعنی ماده‌ای از گله بره‌ای یابزی بجهت قربانی گناه، و کاهن برای وی گناهش را کفاره خواهد کرد. ۶ 6
Pambuyo pake, munthuyo abwere kwa Yehova ndi mwana wankhosa wamkazi kapena mbuzi kuti ikhale chopereka chopepesera tchimo ndipo wansembe achite mwambo wopepesera tchimo lomwe wachitalo. Tsono wansembe achite mwambo wopepesera tchimo la munthuyo.
و اگر دست او به قیمت بره نرسد، پس قربانی جرم خود را برای گناهی که کرده است دو فاخته یا دو جوجه کبوتر نزدخداوند بیاورد، یکی برای قربانی گناه و دیگری برای قربانی سوختنی. ۷ 7
“‘Ngati munthuyo alibe mwana wankhosa, abweretse njiwa ziwiri kapena nkhunda ziwiri kwa Yehova ngati chopereka chopepesera tchimo lake. Imodzi ikhale nsembe yopepesera tchimo, ndipo inayo ikhale nsembe yopsereza.
و آنها را نزد کاهن بیاورد، و او آن را که برای قربانی گناه است اول بگذراند وسرش را از گردنش بکند و آن را دو پاره نکند، ۸ 8
Tsono abwere nazo kwa wansembe, ndipo wansembeyo ayambe wapereka mbalame imodzi ngati yopepesera tchimo. Apotole khosi koma osayidula mutu,
وقدری از خون قربانی گناه را بر پهلوی مذبح بپاشد، و باقی خون بر بنیان مذبح افشرده شود. این قربانی گناه است. ۹ 9
kenaka awaze magazi a chopereka chopepesera tchimocho mʼmbali mwa guwa. Magazi ena onse awathire pa tsinde la guwa. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo.
و دیگری را برای قربانی سوختنی موافق قانون بگذراند، و کاهن برای وی گناهش را که کرده است کفاره خواهد کرد وآمرزیده خواهدشد. ۱۰ 10
Pambuyo pake wansembe apereke mbalame inayo kuti ikhale chopereka chopsereza potsata mwambo wake. Wansembe atatha kupereka nsembe yopepesera tchimo limene munthu uja wachita, wochimwayo adzakhululukidwa.
و اگر دستش به دو فاخته یا دو جوجه کبوتر نرسد، آنگاه قربانی خود رابرای گناهی که کرده است ده‌یک ایفه آرد نرم بجهت قربانی گناه بیاورد، و روغن برآن ننهد وکندر برآن نگذارد زیرا قربانی گناه است. ۱۱ 11
“‘Koma ngati munthuyo alibe njiwa ziwiri kapena nkhunda ziwiri, abweretse ufa wosalala wokwanira kilogalamu imodzi kuti ukhale chopereka chopepesera tchimo limene wachita. Asathiremo mafuta kapena lubani chifukwa ndi chopereka chopepesera tchimo.
و آن را نزد کاهن بیاورد و کاهن یک مشت از آن را برای یادگاری گرفته، بر هدایای آتشین خداوند برمذبح بسوزاند. این قربانی گناه است. ۱۲ 12
Abweretse ufawo kwa wansembe ndipo wansembeyo atapeko dzanja limodzi kuti ukhale ufa wachikumbutso ndi kuwutentha pa guwa pamodzi ndi chopereka chopsereza kwa Yehova. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo.
و کاهن برای وی گناهش را که در هرکدام از اینها کرده است کفاره خواهد کرد، و آمرزیده خواهد شد، ومثل هدیه آردی از آن کاهن خواهد بود.» ۱۳ 13
Umu ndi mmene wansembe adzachitire mwambo wopepesera machimo ena aliwonse amene munthu wachita, ndipo munthuyo adzakhululukidwa. Zopereka zonse zotsala zidzakhala za wansembeyo monga momwe amachitira ndi chopereka chachakudya.’”
و خداوند موسی را خطاب کرده، گفت: ۱۴ 14
Yehova anawuza Mose kuti,
«اگر کسی خیانت ورزد، و درباره چیزهای مقدس خداوند سهو گناه کند، آنگاه قربانی جرم خود را قوچی بی‌عیب از گله نزد خداوند موافق برآورد، وبه مثقالهای نقره مطابق مثقال قدس بیاورد، واین قربانی جرم است. ۱۵ 15
“Munthu akachita zinthu mosakhulupirika, nachimwa mosadziwa posapereka zinthu zopatulika zofunika kwa Yehova, munthuyo apereke kwa Yehova nsembe yopepesera machimo ake. Nsembeyo ikhale nkhosa yayimuna yopanda chilema ndipo mtengo wake ukhale wokwana masekeli oyenera a siliva pakawerengedwe ka ku Nyumba ya Mulungu. Imeneyi ndi nsembe yopepesera kupalamula.
وبه عوض نقصانی که در چیز مقدس رسانیده است عوض بدهد، و پنج یک بر آن اضافه کرده، و آن را به کاهن بدهد و کاهن برای وی به قوچ قربانی جرم کفاره خواهد کرد، و آمرزیده خواهد شد. ۱۶ 16
Munthuyo ayenera kubweza zinthu zopatulika zimene sanaperekezo. Awonjezepo chimodzi mwa zigawo zisanu zilizonse ndi kuzipereka zonsezo kwa wansembe amene adzachita mwambo wopepesera machimo a munthuyo, popereka nkhosa yayimuna ija ngati nsembe yopepesera ndipo wochimwayo adzakhululukidwa.
واگر کسی گناه کند و کاری از جمیع نواهی خداوند که نباید کرد بکند، و آن را نداند، پس مجرم است و متحمل گناه خود خواهد بود. ۱۷ 17
“Ngati munthu wachimwa mosadziwa pochita chilichonse chimene Yehova salola, munthuyo ndi wopalamula ndithu, ndipo ayenera kulangidwa.
وقوچی بی‌عیب از گله موافق برآورد و نزد کاهن بیاورد، و کاهن برای وی غفلت او را که کرده است کفاره خواهد کرد، و آمرزیده خواهد شد. ۱۸ 18
Abwere kwa wansembe ndi chopereka chopepesera kupalamula kwake. Chopereka chikhale nkhosa yayimuna yopanda chilema ndipo mtengo wake ukhale woyenera nsembe yopepesera kupalamula kumene anachimwa mosadziwako, ndipo munthuyo adzakhululukidwa.
این قربانی جرم است البته نزد خداوند مجرم می‌باشد.» ۱۹ 19
Imeneyi ndi nsembe yopepesera kupalamula popeza munthuyo wapezeka wolakwa pamaso pa Yehova.”

< لاویان 5 >