< اشعیا 52 >

بیدار شو‌ای صهیون! بیدار شو و قوت خود را بپوش‌ای شهر مقدس اورشلیم! لباس زیبایی خویش را در بر کن زیرا که نامختون و ناپاک بار دیگر داخل تو نخواهد شد. ۱ 1
Dzambatuka, dzambatuka iwe Ziyoni, vala zilimbe. Vala zovala zako zokongola, iwe Yerusalemu, mzinda wopatulika. Pakuti kuyambira tsopano anthu osachita mdulidwe ndi odetsedwa sadzalowanso pa zipata zako.
‌ای اورشلیم خود را از گرد بیفشان و برخاسته، بنشین! و‌ای دختر صهیون که اسیر شده‌ای بندهای گردن خود را بگشا! ۲ 2
Sasa fumbi lako; imirira nukhale pa mpando waufumu, iwe Yerusalemu. Inu omangidwa a ku Ziyoni, masulani maunyolo amene ali mʼkhosi mwanumo.
زیرا خداوند چنین می‌گوید: مفت فروخته کشتید و بی‌نقره فدیه داده خواهیدشد. ۳ 3
Pakuti Yehova akuti, “Sindinalandirepo kanthu pamene ndinakugulitsani, choncho mudzawomboledwa wopanda ndalama.”
چونکه خداوند یهوه چنین می‌گوید: که درایام سابق قوم من به مصر فرود شدند تا در آنجاساکن شوند و بعد از آن آشور بر ایشان بی‌سبب ظلم نمودند. ۴ 4
Pakuti Ambuye Yehova akuti, “Poyamba paja anthu anga anapita kukakhala ku Igupto; nawonso Asiriya awapondereza popanda chifukwa.”
اما الان خداوند می‌گوید: در اینجامرا چه‌کار است که قوم من مجان گرفتار شده‌اند. و خداوند می‌گوید: آنانی که بر ایشان تسلط دارندصیحه می‌زنند و نام من دائم هر روز اهانت می‌شود. ۵ 5
Tsopano Ine Yehova ndikuti, “Kodi nditani pakuti anthu anga atengedwa ukapolo osaperekapo kanthu, amene amawalamulira amawanyoza,” akutero Yehova. “Ndipo tsiku lonse, akungokhalira kuchita chipongwe dzina langa.
بنابراین قوم من اسم مرا خواهندشناخت. و در آن روز خواهند فهمید که تکلم کننده من هستم، هان من هستم. ۶ 6
Tsono tsiku limenelo anthu anga adzadziwa dzina langa; kotero adzadziwa kuti ndi Ine amene ndikuyankhula, Indedi, ndine.”
چه زیبا است بر کوهها پایهای مبشر که سلامتی را ندا می‌کند و به خیرات بشارت می‌دهدو نجات را ندا می‌کند و به صهیون می‌گوید که خدای تو سلطنت می‌نماید. ۷ 7
Ngokongoladi mapazi a amithenga obweretsa nkhani yabwino amene akuyenda pa mapiri. Iwo akukubweretserani nkhani zabwino za mtendere, chisangalalo ndi chipulumutso. Iwo akubwera kudzawuza anthu a ku Ziyoni kuti, “Mulungu wako ndi mfumu!”
آواز دیده بانان تواست که آواز خود را بلند کرده، با هم ترنم می‌نمایند زیرا وقتی که خداوند به صهیون رجعت می‌کند ایشان معاینه خواهند دید. ۸ 8
Mverani! Alonda anu akukweza mawu awo; akuyimba pamodzi mwachimwemwe. Popeza akuona chamaso kubwera kwa Yehova ku Yerusalemu.
‌ای خرابه های اورشلیم به آواز بلند با هم ترنم نمایید، زیرا خداوند قوم خود را تسلی داده، و اورشلیم را فدیه نموده است. ۹ 9
Imbani pamodzi mofuwula nyimbo zachimwemwe, inu mabwinja a Yerusalemu, pakuti Yehova watonthoza mtima anthu ake, wapulumutsa Yerusalemu.
خداوند ساعد قدوس خود را در نظر تمامی امت‌ها بالا زده است وجمیع کرانه های زمین نجات خدای ما را دیده‌اند. ۱۰ 10
Yehova wagwiritsa ntchito mphamvu zake zopatulika pamaso pa anthu a mitundu yonse, ndipo anthu onse a dziko lapansi adzaona chipulumutso cha Mulungu wathu.
‌ای شما که ظروف خداوند را برمی داریدبیکسو شوید بیکسو شوید و از اینجا بیرون رویدو چیز ناپاک را لمس منمایید و از میان آن بیرون رفته، خویشتن را طاهر سازید. ۱۱ 11
Nyamukani, nyamukani, chokaniko ku Babuloniko! Musakhudze kanthu kodetsedwa! Inu amene mumanyamula ziwiya za Yehova tulukanimo ndipo mudziyeretse.
زیرا که به تعجیل بیرون نخواهید رفت و گریزان روانه نخواهید شد، چونکه یهوه پیش روی شماخواهد خرامید و خدای اسرائیل ساقه شماخواهد بود. ۱۲ 12
Koma simudzachoka mofulumira kapena kuchita chothawa; pakuti Yehova adzayenda patsogolo panu, Mulungu wa Israeli adzakutetezani kumbuyo kwanu.
اینک بنده من با عقل رفتار خواهد کرد وعالی و رفیع و بسیار بلند خواهد شد. ۱۳ 13
Taonani, mtumiki wanga adzapambana pa ntchito yake adzakwezedwa ndi kulemekezedwa ndipo adzalandira ulemu waukulu kwambiri.
چنانکه بسیاری از تو در عجب بودند (از آن جهت که منظر او از مردمان و صورت او از بنی آدم بیشترتباه گردیده بود). ۱۴ 14
Anthu ambiri atamuona anadzidzimuka, chifukwa nkhope yake inali itasakazika; sinalinso ngati ya munthu. Ndipo thupi lake linasakazika; silinalinso ngati la munthu.
همچنان بر امت های بسیارخواهد پاشید و به‌سبب او پادشاهان دهان خود را خواهند بست زیرا چیزهایی را که برای ایشان بیان نشده بود خواهند دید و آنچه را که نشنیده بودند خواهند فهمید. ۱۵ 15
Momwemonso anthu a mitundu yonse adzadodoma naye, ndipo mafumu adzatseka pakamwa pawo kusowa chonena chifukwa cha iye. Pakuti zinthu zimene iwo sanawuzidwepo, adzaziona, ndipo zimene sanazimvepo, adzazimvetsa.

< اشعیا 52 >