< هوشع 7 >
چون اسرائیل را شفا میدادم، آنگاه گناه افرایم و شرارت سامره منکشف گردید، زیرا که مرتکب فریب شدهاند. دزدان داخل میشوند و رهزنان در بیرون تاراج مینمایند. | ۱ 1 |
Pamene ndichiritsa Israeli, machimo a Efereimu amaonekera poyera ndiponso milandu ya Samariya sibisika. Iwo amachita zachinyengo, mbala zimathyola nyumba, achifwamba amalanda anthu katundu mʼmisewu.
ودر دل خود تفکر نمی کنند که من تمامی شرارت ایشان را به یاد آوردهام. الان اعمالشان ایشان رااحاطه مینماید و آنها در نظر من واقع شده است. | ۲ 2 |
Koma sazindikira kuti Ine ndimakumbukira zoyipa zawo zonse. Azunguliridwa ndi zolakwa zawo; ndipo sizichoka mʼmaso mwanga.
پادشاه را بشرارت خویش و سروران را به دروغهای خود شادمان میسازند. | ۳ 3 |
“Anthuwa amasangalatsa mfumu ndi zoyipa zawozo, akalonga amasekerera mabodza awo.
جمیع ایشان زناکارند مثل تنوری که خباز آن را مشتعل سازدکه بعد از سرشتن خمیر تا مخمر شدنش ازبرانگیختن آتش باز میایستد. | ۴ 4 |
Onsewa ndi anthu azigololo, otentha ngati moto wa mu uvuni, umene wophika buledi sasonkhezera kuyambira pamene akukanda buledi mpaka atafufuma.
در یوم پادشاه ما، سروران از گرمی شراب، خود را بیمار ساختند واو دست خود را به استهزاکنندگان دراز کرد. | ۵ 5 |
Pa tsiku la chikondwerero cha mfumu yathu akalonga amaledzera ndi vinyo, ndipo amalowa mʼgulu la anthu achipongwe.
زیرا که دل خود را به مکاید خویش مثل تنورنزدیک آوردند؛ و تمامی شب خباز ایشان میخوابد و صبحگاهان آن مثل آتش ملتهب مشتعل میشود. | ۶ 6 |
Mitima yawo ili ngati uvuni; amayandikira Mulungu mwachiwembu. Ukali wawo umanyeka usiku wonse, mmawa umayaka ngati malawi a moto.
جمیع ایشان مثل تنور گرم شده، داوران خویش را میبلعند و همه پادشاهان ایشان میافتند و در میان ایشان کسی نیست که مرابخواند. | ۷ 7 |
Onsewa ndi otentha ngati uvuni, amapha olamulira awo. Mafumu awo onse amagwa, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amandiyitana Ine.
افرایم با قومها مخلوط شده است. افرایم قرص نانی است که برگردانیده نشده است. | ۸ 8 |
“Efereimu wasakanikirana ndi mitundu ya anthu ena; Efereimu ndi buledi amene wapsa mbali imodzi.
غریبان قوتش را خوردهاند و او نمی داند. سفیدی بر مویهای او پاشیده شده است و اونمی داند. | ۹ 9 |
Alendo atha mphamvu zake, koma iye sakuzindikira. Tsitsi lake layamba imvi koma iye sakudziwa.
فخر اسرائیل پیش رویش شهادت میدهد اما ایشان به یهوه خدای خود بازگشت نمی نمایند و با وجود این همه او را نمی طلبند. | ۱۰ 10 |
Kunyada kwake Israeli kukumutsutsa, koma pa zonsezi iye sakubwerera kwa Yehova Mulungu wake kapena kumufunafuna.
افرایم مانند کبوتر ساده دل، بیفهم است. مصر را میخوانند و بسوی آشور میروند. | ۱۱ 11 |
“Efereimu ali ngati nkhunda yopusa yopanda nzeru. Amayitana Igupto namapita ku Asiriya.
وچون میروند من دام خود را بر ایشان میگسترانم و ایشان را مثل مرغان هوا به زیر میاندازم وایشان را بر وفق اخباری که به جماعت ایشان رسیده است، تادیب مینمایم. | ۱۲ 12 |
Akamadzapita, ndidzawakola ndi ukonde wanga; ndidzawagwetsa pansi ngati mbalame zamumlengalenga. Ndikadzamva kuti asonkhana pamodzi ndidzawakola.
وای بر ایشان زیرا که از من فرار کردند. هلاکت بر ایشان باد زیراکه به من عصیان ورزیدند. اگرچه من ایشان رافدیه دادم، لکن به ضد من دروغ گفتند. | ۱۳ 13 |
Tsoka kwa iwo, chifukwa andisiya Ine! Chiwonongeko kwa iwo, chifukwa andiwukira! Ndimafunitsitsa kuwapulumutsa koma amayankhula za Ine monama.
و از دل خود نزد من استغاثه نمی نمایند بلکه بر بسترهای خود ولوله میکنند. برای روغن و شراب جمع شده، بر من فتنه میانگیزند. | ۱۴ 14 |
Iwo salirira kwa Ine kuchokera pansi pa mtima, koma amalira mofuwula ali pa bedi pawo. Amadzichekacheka chifukwa chofuna tirigu ndi vinyo watsopano, koma amandifulatira.
و اگرچه من بازوهای ایشان را تعلیم دادم و تقویت نمودم لیکن با من بداندیشی نمودند. | ۱۵ 15 |
Ine ndinawaphunzitsa ndikuwalimbitsa, koma amandikonzera chiwembu.
ایشان رجوع میکنند اما نه به حضرت اعلی. مثل کمان خطاکننده شدهاند. سروران ایشان بهسبب غیظزبان خویش به شمشیر میافتند و بهسبب همین در زمین مصر ایشان را استهزا خواهند نمود. | ۱۶ 16 |
Iwo satembenukira kwa Wammwambamwamba; ali ngati uta woonongeka. Atsogoleri awo adzaphedwa ndi lupanga chifukwa cha mawu awo achipongwe. Motero iwo adzasekedwa mʼdziko la Igupto.