< حزقیال 32 >

و در روز اول ماه دوازدهم از سال دوازدهم واقع شد که کلام خداوند برمن نازل شده، گفت: ۱ 1
Pa tsiku loyamba la mwezi wa khumi ndi chiwiri, chaka chakhumi ndi chiwiri, Yehova anandiyankhula kuti:
«ای پسر انسان برای فرعون پادشاه مصر مرثیه بخوان و او را بگو تو به شیرژیان امت‌ها مشابه می‌بودی، اما مانند اژدها دردریا هستی و آب را از بینی خود می‌جهانی و آبهارا به پایهای خود حرکت داده، نهرهای آنها راگل آلود می‌سازی.» ۲ 2
“Iwe mwana wa munthu imba nyimbo ya maliro a Farao mfumu ya Igupto ndipo uyiwuze kuti, “Iwe umadziyesa ngati mkango pakati pa mitundu ya anthu. Koma iwe uli ngati ngʼona mʼnyanja. Umakhuvula mʼmitsinje yako, kuvundula madzi ndi mapazi ako ndi kudetsa madzi mʼmitsinje.
خداوند یهوه چنین می‌گوید: «دام خود را به واسطه گروهی از قوم های عظیم بر تو خواهم گسترانید و ایشان تورا در دام من بر خواهند کشید. ۳ 3
“Tsono Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Pogwiritsa ntchito gulu la anthu a mitundu yambiri, ndidzakuponyera khoka langa ndi kukugwira mu ukonde wanga.
و تو را بر زمین ترک نموده، بر روی صحرا خواهم‌انداخت وهمه مرغان هوا را بر تو فرود آورده، جمیع حیوانات زمین را از تو سیر خواهم ساخت. ۴ 4
Ndidzakuponya ku mtunda ndi kukutayira pansi. Ndidzabweretsa mbalame zamumlengalenga kuti zidzatere pa iwe, ndipo zirombo zonse za dziko lapansi zidzakudya.
وگوشت تو را بر کوهها نهاده، دره‌ها را از لاش تو پرخواهم کرد. ۵ 5
Ndidzayanika mnofu wako pa mapiri ndipo zigwa zidzadzaza ndi zotsalira zako.
و زمینی را که در آن شنا می‌کنی ازخون تو تا به کوهها سیراب می‌کنم که وادیها از توپر خواهد شد. ۶ 6
Ndidzanyowetsa dziko ndi magazi ako, mpaka kumapiri komwe, ndipo mitsinje idzadzaza ndi mnofu wako.
و هنگامی که تو را منطفی گردانم، آسمان را خواهم پوشانید و ستارگانش راتاریک کرده، آفتاب را به ابرها مستور خواهم ساخت و ماه روشنایی خود را نخواهد داد. ۷ 7
Ndikadzakuwononga, ndidzaphimba miyamba ndikudetsa nyenyezi zake. Ndidzaphimba dzuwa ndi mtambo, ndipo mwezi sudzawala.
وخداوند یهوه می‌فرماید، که تمامی نیرهای درخشنده آسمان را برای تو سیاه کرده، تاریکی بر زمینت خواهم آورد. ۸ 8
Zowala zonse zamumlengalenga ndidzazizimitsa; ndidzachititsa mdima pa dziko lako, akutero Ambuye Yehova.
و چون هلاکت تو را درمیان امت‌ها بر زمینهایی که ندانسته‌ای آورده باشم، آنگاه دلهای قوم های عظیم را محزون خواهم ساخت. ۹ 9
Ndidzasautsa mitima ya anthu a mitundu yambiri pamene ndidzakupititsa ku ukapolo pakati pa mitundu ya anthu, ku mayiko amene iwe sunawadziwe.
و قوم های عظیم را بر تومتحیر خواهم ساخت. و چون شمشیر خود راپیش روی ایشان جلوه دهم، پادشاهان ایشان به شدت دهشتناک خواهند شد. و در روز انهدام توهر یک از ایشان برای جان خود هر لحظه‌ای خواهند لرزید.» ۱۰ 10
Ine ndidzachititsa kuti anthu a mitundu yambiri adabwe nawe, ndipo mafumu awo adzanjenjemera ndi mantha aakulu chifukwa cha iwe pamene ndidzaonetsa lupanga langa pamaso pawo. Pa nthawi ya kugwa kwako, aliyense wa iwo adzanjenjemera moyo wake wonse.
زیرا خداوند یهوه چنین می‌گوید: «شمشیرپادشاه بابل بر تو خواهد آمد. ۱۱ 11
“‘Pakuti ndikunena Ine Ambuye Yehova kuti, “‘Lupanga la mfumu ya ku Babuloni lidzabwera kudzalimbana nawe.
و به شمشیرهای جباران که جمیع ایشان از ستمکیشان امت هامی باشند، جمعیت تو را به زیر خواهم‌انداخت. وایشان غرور مصر را نابود ساخته، تمامی جمعیتش هلاک خواهند شد. ۱۲ 12
Ndidzachititsa gulu lako lankhondo kuti ligwe ndi lupanga la anthu amphamvu, anthu ankhanza kwambiri pakati pa mitundu yonse ya anthu. Adzathetsa kunyada kwa Igupto, ndipo gulu lake lonse la nkhondo lidzagonjetsedwa.
و تمامی بهایم او را از کنارهای آبهای عظیم هلاک خواهم ساخت. و پای انسان دیگر آنها را گل آلودنخواهد ساخت. و سم بهایم آنها را گل آلودنخواهد ساخت. ۱۳ 13
Ndidzawononga ziweto zake zonse zokhala mʼmbali mwa madzi ambiri. Ku madziko sikudzaonekanso phazi la munthu kapena kudetsedwa ndi phazi la ziweto.
آنگاه خداوند یهوه می‌گوید: آبهای آنها را ساکت گردانیده، نهرهای آنها رامانند روغن جاری خواهم ساخت. ۱۴ 14
Pambuyo pake ndidzayeretsa madzi ake ndipo mitsinje yake idzayenda mokometsera ngati mafuta, akutero Ambuye Yehova.
و چون زمین مصر را ویران کنم و آن زمین از هرچه در آن باشد خالی شود و چون جمیع ساکنانش را هلاک کنم، آنگاه خواهند دانست که من یهوه هستم.» ۱۵ 15
Ndikadzasandutsa dziko la Igupto kukhala bwinja; ndikadzawononga dziko lonse ndi kukantha onse okhala kumeneko, adzadziwa kuti ndine Yehova.’
و خداوند یهوه می‌گوید: «مرثیه‌ای که ایشان خواهند خواند همین است. دختران امت‌ها این مرثیه را خواهند خواند. برای مصر و تمامی جمعیتش این مرثیه را خواهند خواند.» ۱۶ 16
“Mawu angawa adzakhala nyimbo ya maliro. Ana a akazi amitundu ya anthu adzayimba, kuyimbira Igupto ndi gulu lake lonse la nkhondo, akutero Ambuye Yehova.”
و در روز پانزدهم ماه از سال دوازدهم واقع شد که کلام خداوند بر من نازل شده، گفت: ۱۷ 17
Pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, chaka cha khumi ndi chiwiri, Yehova anayankhula kuti:
«ای پسر انسان برای جمعیت مصر ولوله نما و هم اورا و هم دختران امت های عظیم را با آنانی که به هاویه فرود می‌روند، به اسفلهای زمین فرود آور. ۱۸ 18
“Iwe mwana wa munthu, lirira gulu lankhondo la Igupto ndipo uwalowetse pamodzi ndi anthu ena amphamvu a mayiko ena ku dziko la anthu akufa.
از چه کس زیباتر هستی؟ فرود بیا و بانامختونان بخواب. ۱۹ 19
Ufunse kuti, ‘Ndani amene akukuposa kukongola? Tsikirani ku manda ndi kukhala pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe.’
ایشان در میان مقتولان شمشیر خواهند افتاد. (مصر) به شمشیر تسلیم شده است. پس او را و تمامی جمعیتش رابکشید. ۲۰ 20
Aigupto adzagwa pakati pa amene akuphedwa ndi lupanga. Lupanga ndi losololedwa kale. Iye adzaphedwa pamodzi ndi gulu lake lankhondo.
اقویای جباران از میان عالم اموات اورا و انصار او را خطاب خواهند کرد. ایشان نامختون به شمشیر کشته شده، فرود آمده، خواهند خوابید. (Sheol h7585) ۲۱ 21
Mʼkati mwa manda atsogoleri amphamvu pamodzi ndi ogwirizana nawo azidzakambirana za Igupto nʼkumati, ‘Afika kuno anthu osachita mdulidwe aja! Ndi awa agona apawa, ophedwa pa nkhondo.’ (Sheol h7585)
«در آنجا آشور و تمامی جمعیت اوهستند. قبرهای ایشان گرداگرد ایشان است وجمیع ایشان کشته شده از شمشیر افتاده‌اند. ۲۲ 22
“Asiriya ali komweko ndipo ankhondo ake onse ali mʼmanda omuzungulira. Onsewo anaphedwa pa nkhondo.
که قبرهای ایشان به اسفلهای هاویه قرار داده شد وجمعیت ایشان به اطراف قبرهای ایشان‌اند. ۲۳ 23
Manda awo ali kumalo ozama a dzenje, ndipo ankhondo ake azungulira manda ake. Onse amene anaopseza dziko la anthu amoyo aphedwa, agwa ndi lupanga.
در آنجاعیلام و تمامی جمعیتش هستند. قبرهای ایشان گرداگرد ایشان است و جمیع ایشان مقتول و ازشمشیر افتاده‌اند و به اسفلهای زمین نامختون فرود رفته‌اند، زیرا که در زمین زندگان باعث هیبت بوده‌اند. پس با آنانی که به هاویه فرود می‌روند، متحمل خجالت خویش خواهند بود. ۲۴ 24
“Elamu ali komweko ndipo ankhondo ake ali mʼmanda omuzungulira. Onsewa anaphedwa pa nkhondo, natsikira ku manda ali osachita mdulidwe. Iwowa kale ankaopseza anthu pa dziko lapansi. Tsopano akuchita manyazi pamodzi ndi amene ali mʼmanda.
بستری برای او و تمامی جمعیتش در میان مقتولان قرارداده‌اند. قبرهای ایشان گرداگرد ایشان است وجمیع ایشان نامختون و مقتول شمشیرند. زیرا که در زمین زندگان باعث هیبت بودند. پس با آنانی که به هاویه فرود می‌روند، متحمل خجالت خویش خواهند بود. در میان کشتگان قرار داده شد. ۲۵ 25
Amukonzera pogona pakati pa anthu ophedwa, pamodzi ndi gulu lake lonse la nkhondo litazungulira manda ake. Onsewo ndi anthu osachita mdulidwe ophedwa ndi lupanga. Paja anthuwa ankaopsa mʼdziko la anthu a moyo. Koma tsopano akuchita manyazi pamodzi ndi amene ali mʼmanda. Iwo ayikidwa pakati pa anthu ophedwa.
درآنجا ماشک و توبال و تمامی جمعیت آنهاهستند. قبرهای ایشان گرداگرد ایشان است وجمیع ایشان نامختون و مقتول شمشیرند. زیرا که در زمین زندگان باعث هیبت بودند. ۲۶ 26
“Mesaki ndi Tubala ali komweko, pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo litazungulira manda awo. Onsewo ndi anthu osachita mdulidwe, ophedwa ndi lupanga. Paja ankaopsa mʼdziko la anthu amoyo.
پس ایشان با جباران و نامختونانی که افتاده‌اند که با اسلحه جنگ خویش به هاویه فرود رفته‌اند، نخواهندخوابید. و ایشان شمشیرهای خود را زیر سرهای خود نهادند. و گناه ایشان بر استخوانهای ایشان خواهد بود. زیرا که در زمین زندگان باعث هیبت جباران بودند. (Sheol h7585) ۲۷ 27
Iwo sanayikidwe mwaulemu ngati ankhondo amphamvu amakedzana, amene anatsikira ku dziko la anthu akufa ndi zida zawo zomwe za nkhondo. Malupanga awo anawayika ku mitu yawo, ndipo zishango zawo anaphimba mafupa awo. Kale anthu amphamvu amenewa ankaopsa dziko la anthu amoyo. (Sheol h7585)
و اما تو در میان نامختونان شکسته شده، با مقتولان شمشیر خواهی خوابید. ۲۸ 28
“Iwenso Farao, udzaphwanyidwa ndi kuyikidwa pakati pa anthu osachita mdulidwe, amene anaphedwa ndi lupanga.
در آنجا ادوم و پادشاهانش و جمیع سرورانش هستند که در جبروت خود با مقتولان شمشیرقرار داده شدند. و ایشان با نامختونان و آنانی که به هاویه فرود می‌روند خواهند خوابید. ۲۹ 29
“Edomu ali kumeneko pamodzi ndi mafumu ake ndi akalonga ake onse. Ngakhale anali amphamvu, koma anayikidwa. Ayikidwa pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje.
در آنجاجمیع روسای شمال و همه صیدونیان هستند که با مقتولان فرود رفتند. از هیبتی که به جبروت خویش باعث آن بودند، خجل خواهند شد. پس با مقتولان شمشیر نامختون خواهند خوابید و باآنانی که به هاویه فرود می‌روند، متحمل خجالت خود خواهند شد. ۳۰ 30
“Akalonga onse akumpoto pamodzi ndi anthu onse a ku Sidoni ali kumeneko. Anatsikira ku dziko la anthu akufa mwamanyazi ngakhale anali owopsa ndi mphamvu zawo. Iwo akugona osachita mdulidwe pamodzi ndi amene anaphedwa ndi lupanga ndipo akuchita manyazi pamodzi ndi iwo amene anatsikira kale ku manda.
و خداوند یهوه می‌گوید که فرعون چون این را بیند درباره تمامی جمعیت خود خویشتن را تسلی خواهد داد و فرعون وتمامی لشکر او به شمشیر کشته خواهند شد. ۳۱ 31
“Farao ndi gulu lake lankhondo akadzawaona iwowa adzathunza mtima pokumbukira kuchuluka kwa gulu lake lankhondo limene linaphedwa pa nkhondo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
زیرا خداوند یهوه می‌گوید: من او را در زمین زندگان باعث هیبت گردانیدم. پس فرعون وتمامی جمعیت او را با مقتولان شمشیر در میان نامختونان خواهند خوابانید.» ۳۲ 32
Paja ankaopsa mʼdziko la anthu amoyo. Koma Faraoyo pamodzi ndi ankhondo ake onse adzayikidwa pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, pamodzi ndi amene anaphedwa pa nkhondo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”

< حزقیال 32 >