< حزقیال 20 >

و در روز دهم ماه پنجم از سال هفتم بعضی از مشایخ اسرائیل به جهت طلبیدن خداوند آمدند و پیش من نشستند. ۱ 1
Tsiku lakhumi la mwezi wachisanu, chaka chachisanu ndi chiwiri, ena mwa akuluakulu a Israeli anabwera kudzapempha nzeru kwa Yehova, ndipo anakhala pansi pamaso panga.
آنگاه کلام خداوند بر من نازل شده، گفت: ۲ 2
Tsono Yehova anandiyankhula nati:
«ای پسر انسان مشایخ اسرائیل را خطاب کرده، به ایشان بگو: خداوند یهوه چنین می‌فرماید: آیاشما برای طلبیدن من آمدید؟ خداوند یهوه می‌گوید: به حیات خودم قسم که از شما طلبیده نخواهم شد. ۳ 3
“Iwe mwana wa munthu, ayankhule akuluakulu a Israeli ndi kuwawuza kuti, ‘Ambuye Yehova akuti: Kodi mwabwera kudzapempha nzeru kwa Ine? Ndithu pali Ine wamoyo, Ine sindidzakulolani kupempha nzeru kwa Ine, akutero Ambuye Yehova.’
‌ای پسر انسان آیا بر ایشان حکم خواهی کرد؟ آیا بر ایشان حکم خواهی کرد؟ پس رجاسات پدران ایشان را بدیشان بفهمان. ۴ 4
“Kodi uwaweruza? Iwe mwana wa munthu, kodi ugamula mlandu wawo? Uwadziwitse tsono zonyansa zimene anachita makolo awo, uwawuze kuti,
وبه ایشان بگو: خداوند یهوه چنین می‌فرماید درروزی که اسرائیل را برگزیدم و دست خود رابرای ذریت خاندان یعقوب برافراشتم و خود را به ایشان در زمین مصر معروف ساختم و دست خودرا برای ایشان برافراشته، گفتم: من یهوه خدای شما هستم، ۵ 5
‘Ambuye Yehova akuti: Pa tsiku limene ndinasankha Israeli, ndinalumbira kwa zidzukulu za nyumba ya Yakobo ndipo ndinadziwulula kwa iwo ku Igupto. Ndinalumbira ndi kuwawuza kuti: Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
در همان روز دست خود را برای ایشان برافراشتم که ایشان را از زمین مصر به زمینی که برای ایشان بازدید کرده بودم بیرون آورم. زمینی که به شیر و شهد جاری است و فخرهمه زمینها می‌باشد. ۶ 6
Pa tsiku limenelo ndinalumbira kwa iwo kuti ndidzawatulutsa mʼdziko la Igupto ndi kupita nawo ku dziko limene ndinawapezera, dziko la mwana alirenji, dziko lokongola kwambiri kupambana mayiko ena.
و به ایشان گفتم: هر کس ازشما رجاسات چشمان خود را دور کند وخویشتن را به بتهای مصر نجس نسازد، زیرا که من یهوه خدای شما هستم. ۷ 7
Ndipo ndinawawuza kuti, ‘Aliyense ataye zinthu zonse zonyansa zimene ankasangalala nazo, ndipo musadziyipitse ndi mafano a Igupto, Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’
اما ایشان از من عاصی شده، نخواستند که به من گوش گیرند. وهر کس از ایشان رجاسات چشمان خود را دورنکرد و بتهای مصر را ترک ننمود. آنگاه گفتم که خشم خود را بر ایشان خواهم ریخت و غضب خویش را در میان زمین مصر بر ایشان به اتمام خواهم رسانید. ۸ 8
“‘Koma iwo anandiwukira ndipo sanafune kundimvera. Palibe amene anataya zonyansa zonse zimene ankasangalala nazo. Panalibenso amene anasiya mafano a ku Igupto. Tsono ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwaonetsa mkwiyo wanga mʼdziko la Igupto momwemo.
لیکن محض خاطر اسم خودعمل نمودم تا آن در نظر امت هایی که ایشان درمیان آنها بودند و در نظر آنها خود را به بیرون آوردن ایشان از زمین مصر، به ایشان شناسانیدم، بی‌حرمت نشود. ۹ 9
Koma sindinachite zimenezi chifukwa cha dzina langa, kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene ankakhala pakati pawo. Paja ndinali nditaonetsa mphamvu zanga pamaso pa mitunduyo potulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto.
پس ایشان را از زمین مصربیرون آورده، به بیابان رسانیدم. ۱۰ 10
Choncho ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto ndi kubwera nawo mʼchipululu.
و فرایض خویش را به ایشان دادم و احکام خود را که هر‌که به آنها عمل نماید به آنها زنده خواهد ماند، به ایشان تعلیم دادم. ۱۱ 11
Ndinawapatsa malangizo anga ndi kuwadziwitsa malamulo anga amene munthu aliyense akawamvera adzakhala ndi moyo.
و نیز سبت های خود را به ایشان عطا فرمودم تا علامتی در میان من و ایشان بشود و بدانند که من یهوه هستم که ایشان راتقدیس می‌نمایم. ۱۲ 12
Ndinawapatsanso Masabata ngati chizindikiro pakati pathu, kuti adziwe kuti Ine Yehova ndinawapatula.
«لیکن خاندان اسرائیل در بیابان از من عاصی شده، در فرایض من سلوک ننمودند. واحکام مرا که هر‌که به آنها عمل نماید از آنها زنده ماند، خوار شمردند و سبت هایم را بسیاربی حرمت نمودند. آنگاه گفتم که خشم خود را بر ایشان ریخته، ایشان را در بیابان هلاک خواهم ساخت. ۱۳ 13
“‘Komabe anthu a Israeli anandiwukira mʼchipululu. Iwo sanatsatire malangizo anga koma anakana malamulo anga amene munthu aliyense akawamvera adzakhala ndi moyo. Ndipo anayipitsa kotheratu Masabata anga. Choncho, ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwawononga mʼchipululu.
لیکن محض خاطر اسم خود عمل نمودم تا آن به نظر امت هایی که ایشان را به حضور آنها بیرون آوردم بی‌حرمت نشود. ۱۴ 14
Koma sindinachite zimenezi chifukwa cha dzina langa, kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene anandiona ndikutulutsa Aisraeliwo mu Igupto.
ومن نیز دست خود را برای ایشان در بیابان برافراشتم که ایشان را به زمینی که به ایشان داده بودم، داخل نسازم. زمینی که به شیر و شهدجاری است و فخر تمامی زمینها می‌باشد. ۱۵ 15
Ndinalumbiranso kwa iwo mʼchipululu muja, nditakweza dzanja, kuti sindidzawalowetsanso mʼdziko limene ndinawapatsa, dziko la mwana alirenji, lokoma kwambiri kuposa mayiko ena onse.
زیرا که احکام مرا خوار شمردند وبه فرایضم سلوک ننمودند و سبت های مرا بی‌حرمت ساختند، چونکه دل ایشان به بتهای خود مایل می‌بود. ۱۶ 16
Paja anakana malamulo anga, sanatsatire malangizo anga ndipo anayipitsa masabata anga. Mitima yawo inakonda mafano.
لیکن خشم من بر ایشان رقت نموده، ایشان را هلاک نساختم و ایشان را در بیابان، نابودننمودم. ۱۷ 17
Komabe ndinawamvera chisoni ndipo sindinawawononge kapena kuwatheratu mʼchipululu.
و به پسران ایشان در بیابان گفتم: به فرایض پدران خود سلوک منمایید و احکام ایشان را نگاه مدارید و خویشتن را به بتهای ایشان نجس مسازید. ۱۸ 18
Tsono kwa ana awo mʼchipululu ndinati, ‘Musatsatire malangizo a makolo anu kapena kusunga malamulo awo kapena kudziyipitsa ndi mafano awo.
من یهوه خدای شما هستم. پس به فرایض من سلوک نمایید و احکام مرا نگاه داشته، آنها را بجا آورید. ۱۹ 19
Ine ndine Yehova Mulungu wanu; tsatirani malangizo anga ndipo sungani malamulo anga.
و سبت های مراتقدیس نمایید تا در میان من و شما علامتی باشدو بدانید که من یهوه خدای شما هستم. ۲۰ 20
Masabata anga muziwasunga ngati opatulika kuti akhale chizindikiro pakati pa Ine ndi inu. Mukatero mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’
«لیکن پسران از من عاصی شده، به فرایض من سلوک ننمودند و احکام مرا که هر‌که آنها رابجا آورد از آنها زنده خواهد ماند، نگاه نداشتند وبه آنها عمل ننمودند و سبت های مرا بی‌حرمت ساختند. آنگاه گفتم که خشم خود را بر ایشان ریخته، غضب خویش را بر ایشان در بیابان به اتمام خواهم رسانید. ۲۱ 21
“‘Koma ana awo anandiwukira. Iwo sanatsatire malangizo anga, sanamvere malamulo anga, ngakhale kuti amapereka moyo kwa munthu amene amawamvera. Ndiponso anayipitsa Masabata anga. Choncho ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwawonongeratu mʼchipululu momwemo.
لیکن دست خود رابرگردانیده، محض خاطر اسم خود عمل نمودم تا آن به نظر امت هایی که ایشان را به حضور آنها بیرون آوردم بی‌حرمت نشود. ۲۲ 22
Koma sindinatero chifukwa cha dzina langa kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene anandiona ndikutulutsa Aisraeliwo mu Iguptomo.
و من نیز دست خود را برای ایشان در بیابان برافراشتم که ایشان را در میان امت‌ها پراکنده نمایم و ایشان را درکشورها متفرق سازم. ۲۳ 23
Choncho ndinalumbira mʼchipululu, nditakweza dzanja langa, kuti ndidzawabalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwamwazira ku mayiko akutali,
زیرا که احکام مرا بجانیاوردند و فرایض مرا خوار شمردند و سبت های مرا بی‌حرمت ساختند و چشمان ایشان بسوی بتهای پدران ایشان نگران می‌بود. ۲۴ 24
chifukwa sanamvere malamulo anga, anakana malangizo anga, nayipitsa masabata anga, ndi kupembedza mafano a makolo awo.
بنابراین من نیز فرایضی را که نیکو نبود و احکامی را که از آنهازنده نمانند به ایشان دادم. ۲۵ 25
Ine ndinawapatsanso malangizo amene sanali abwino ndi malamulo amene sakanatha kupeza nawo moyo.
و ایشان را به هدایای ایشان که هر کس را که رحم را می‌گشوداز آتش می‌گذرانیدند، نجس ساختم تا ایشان راتباه سازم و بدانند که من یهوه هستم. ۲۶ 26
Ndinawalekerera kuti adziyipitse ndi mphatso zawo zomwe, makamaka popereka ana awo oyamba kubadwa ngati nsembe zopsereza. Ndinatero kuti ndiwadetse nkhawa ndi kuti adziwe kuti Ine ndine Yehova.’
«بنابراین‌ای پسر انسان خاندان اسرائیل راخطاب کرده، به ایشان بگو: خداوند یهوه چنین می‌فرماید: در این دفعه نیز پدران شما خیانت کرده، به من کفر ورزیدند. ۲۷ 27
“Tsono iwe mwana wa munthu, yankhula nawo Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ambuye Yehova akuti makolo anu anandinyozanso posaonetsa moyo wokhulupirika.
زیرا که چون ایشان را به زمینی که دست خود را برافراشته بودم که آن را به ایشان بدهم در‌آوردم، آنگاه به هر تل بلند وهر درخت کشن نظر انداختند و ذبایح خود را درآنجا ذبح نمودند و قربانی های غضب انگیزخویش را گذرانیدند. و در آنجا هدایای خوشبوی خود را آوردند و در آنجا هدایای ریختنی خود را ریختند. ۲۸ 28
Nditawalowetsa mʼdziko limene ndinachita kulumbirira kuti ndidzawapatsa, iwo tsono ankapita kulikonse kumene anaona chitunda chachitali ndi mtengo wa masamba ambiri kukapereka kumeneko nsembe ndi zopereka zawo zimene zinkandikwiyitsa. Kumeneko ankapereka nsembe za fungo lokoma ndiponso nsembe za zakumwa.
و به ایشان گفتم: این مکان بلند که شما به آن می‌روید چیست؟ پس اسم آن تا امروز بامه خوانده می‌شود. ۲۹ 29
Tsono ndinawafunsa kuti: Kodi chitunda chimene mukupitako nʼchotani? Chitundachi chakhala chikutchedwa mpaka lero kuti ‘Chitunda cha Chipembedzo.’
«بنابراین به خاندان اسرائیل بگو: خداوندیهوه چنین می‌فرماید: آیا شما به رفتار پدران خود خویشتن را نجس می‌سازید و رجاسات ایشان را پیروی نموده، زنا می‌کنید؟ ۳۰ 30
“Tsono uwawuze Aisraeli kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Kodi mudzadziyipitsa nokha monga anachitira makolo anu ndi kuchita chigololo ndi milungu yawo yonyansa?
و هدایای خود را آورده، پسران خویش را از آتش می‌گذرانید و خویشتن را از تمامی بتهای خود تاامروز نجس می‌سازید؟ پس‌ای خاندان اسرائیل آیا من از شما طلبیده بشوم؟ خداوند یهوه می‌فرماید به حیات خودم قسم که از شما طلبیده نخواهم شد. ۳۱ 31
Pamene mubwera kudzapereka mphatso zanu ndi kudzapereka ana kuti akhale ngati nsembe zopsereza mumadziyipitsa ndi mafano anu mpaka lero. Kodi Aisraeli, ndingathe kukulolani bwanji kuti mulandire malangizo kwa Ine? Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, sindidzalola kuti mupemphe nzeru kwa Ine.
و آنچه به‌خاطر شما خطورمی کند هرگز واقع نخواهد شد که خیال می‌کنید. مثل امت‌ها و مانند قبایل کشورها گردیده، (بتهای ) چوب و سنگ را عبادت خواهید نمود. ۳۲ 32
“‘Inu munanena kuti, ‘Tikufuna tikhale ngati anthu a mitundu ina, ngati anthu adziko lapansi, amene amapembedza mtengo ndi mwala.’ Koma zimene mukuganizazo sizidzachitika.
زیرا خداوند یهوه می‌فرماید: به حیات خودم قسم که هرآینه با دست قوی و بازوی برافراشته وخشم ریخته شده بر شما سلطنت خواهم نمود. ۳۳ 33
Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, ndi dzanja langa lamphamvu, nditasamula mkono wanga mokwiya kwambiri, Ine ndidzakhala wokulamulani.
و شما را از میان امت‌ها بیرون آورده، به‌دست قوی و بازوی برافراشته و خشم ریخته شده اززمینهایی که در آنها پراکنده شده‌اید جمع خواهم نمود. ۳۴ 34
Ndidzakuchotsani pakati pa anthu a mitundu ina ndikukusonkhanitsani kuchokera ku mayiko kumene munamwazikirako, ndi dzanja langa lamphamvu ndi lotambasuka ndili wokwiya kwambiri.
و شما را به بیابان امت‌ها در‌آورده، درآنجا بر شما روبرو داوری خواهم نمود. ۳۵ 35
Ndidzakulowetsani mʼchipululu cha anthu a mitundu ina ndipo kumeneko, moonana maso ndi maso, ndidzakuzengani mlandu.
وخداوند یهوه می‌گوید: چنانکه بر پدران شما دربیابان زمین مصر داوری نمودم، همچنین بر شماداوری خواهم نمود. ۳۶ 36
Monga ndinawalangira makolo anu mʼchipululu cha dziko la Igupto, motero ndidzakulangani, akutero Ambuye Yehova.
و شما را زیر عصاگذرانیده، به بند عهد درخواهم آورد. ۳۷ 37
Ndidzakuwerengani ndi ndodo ya mʼbusa, kukulowetsani mʼchimango cha pangano langa.
و آنانی را که متمرد شده و از من عاصی گردیده‌اند، ازمیان شما جدا خواهم نمود و ایشان را از زمین غربت ایشان بیرون خواهم آورد. لیکن به زمین اسرائیل داخل نخواهند شد و خواهید دانست که من یهوه هستم.» ۳۸ 38
Ndidzakuchotserani anthu amene anandigalukira ndi kundiwukira. Ngakhale ndidzawatulutsa mʼdziko limene akukhalamo, koma sadzalowamo mʼdziko la Israeli. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
اما به شما‌ای خاندان اسرائیل خداوند یهوه چنین می‌گوید: «همه شما نزدبتهای خود رفته، آنها را عبادت کنید. لیکن بعد ازاین البته مرا گوش خواهید داد. و اسم قدوس مرا دیگر با هدایا و بتهای خود بی‌عصمت نخواهیدساخت. ۳۹ 39
“‘Koma inu Aisraeli, zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi: Pitani katumikireni mafano anu onse, aliyense wa inu! Koma mʼtsogolo mwake mudzandimvera ndithu ndipo simudzayipitsa dzina langa lopatulika popereka mphatso zanu kwa mafano.
زیرا خداوند یهوه می‌فرماید: در کوه مقدس من بر کوه بلند اسرائیل تمام خاندان اسرائیل جمیع در آنجا مرا عبادت خواهند کردو در آنجا از ایشان راضی شده، ذبایح جنبانیدنی شما و نوبرهای هدایای شما را با تمامی موقوفات شما خواهم طلبید. ۴۰ 40
Pakuti pa phiri langa lopatulika, phiri lalitali la ku Israeli, akutero Ambuye Yehova, Aisraeli onse adzanditumikira, ndipo kumeneko Ine ndidzawalandira. Kumeneko ndidzayembekeza zopereka zanu ndi mphatso zanu zopambana, pamodzi ndi nsembe zanu zonse zopatulika.
و چون شما را ازامت‌ها بیرون آورم و شما را از زمینهایی که درآنها پراکنده شده‌اید جمع نمایم، آنگاه هدایای خوشبوی شما را از شما قبول خواهم کرد و به نظر امت‌ها در میان شما تقدیس کرده خواهم شد. ۴۱ 41
Ndidzakulandirani ngati nsembe ya fungo lokoma ndikadzakutulutsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukusokhanitsani kuchokera ku mayiko kumene munabalalitsidwirako. Motero ndidzadzionetsa pakati panu kuti ndine woyera ndipo mitundu ya anthu idzaona.
و چون شما را به زمین اسرائیل یعنی به زمینی که درباره‌اش دست خود را برافراشتم که آن را به پدران شما بدهم بیاورم، آنگاه خواهید دانست که من یهوه هستم. ۴۲ 42
Tsono mudzadziwa kuti ndine Yehova ndikadzabwera nanu ku dziko la Israeli, dziko limene ndinalumbira kuti ndidzapereka kwa makolo anu.
و در آنجا طریق های خود وتمامی اعمال خویش را که خویشتن را به آنهانجس ساخته‌اید، به یاد خواهید آورد. و از همه اعمال قبیح که کرده‌اید، خویشتن را به نظر خودمکروه خواهید داشت. ۴۳ 43
Kumeneko mudzakumbukira makhalidwe anu ndi machitidwe anu onse amene munadziyipitsa nawo, ndipo mudzanyansidwa nokha chifukwa cha zoyipa zimene munachita.
و‌ای خاندان اسرائیل خداوند یهوه می‌فرماید: هنگامی که با شمامحض خاطر اسم خود و نه به سزای رفتار قبیح شما و نه موافق اعمال فاسد شما عمل نموده باشم، آنگاه خواهید دانست که من یهوه هستم.» ۴۴ 44
Inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzakuchitirani zabwino chifukwa cha dzina langa koma osati molingana ndi njira zanu zoyipa ndi machitidwe anu okhota, inu Aisraeli, akutero Ambuye Yehova.’”
و کلام خداوند بر من نازل شده، گفت: ۴۵ 45
Yehova anandiyankhula nati:
«ای پسر انسان روی خود را بسوی جنوب متوجه ساز و به سمت جنوب تکلم نما و برجنگل صحرای جنوب نبوت کن. ۴۶ 46
“Iwe mwana wa munthu, tembenuka uyangʼane kummwera; ndipo lalika mawu odzudzula anthu akummwera ndipo unenere zodzudzula dziko la nkhalango ya kummwera.
و به آن جنگل جنوب بگو: کلام خداوند را بشنو. خداوند یهوه چنین می‌فرماید: اینک من آتشی درتو می‌افروزم که هر درخت سبز و هر درخت خشک را در تو خواهد سوزانید. و لهیب ملتهب آن خاموش نخواهد شد و همه رویها از جنوب تا شمال از آن سوخته خواهد شد. ۴۷ 47
Iwuze nkhalango yakummwera kuti, ‘Imvani mawu a Yehova! Ambuye Yehova akuti: Ndikuyatsa moto ndipo motowo udzapsereza mitengo yako yonse yayiwisi ndi yowuma yomwe. Malawi ake sadzazimitsika ndipo aliyense kuchokera kummwera mpaka kumpoto adzapsa nawo.
و تمامی بشرخواهند فهمید که من یهوه آن را افروخته‌ام تاخاموشی نپذیرد.» ۴۸ 48
Aliyense adzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndayatsa motowo, ndipo sudzazimitsidwa.’”
و من گفتم: «آه‌ای خداوند یهوه ایشان درباره من می‌گویند آیا او مثلها نمی آورد؟» ۴۹ 49
Ndipo ine ndinati, “Aa, Ambuye Yehova! Anthu akungondinena kuti, ‘Kodi suja amangonena nthano chabe ameneyu!’”

< حزقیال 20 >