< تثنیه 32 >

و زمین سخنان دهانم را بشنود. ۱ 1
Mverani, inu mayiko a mmwamba ndipo ine ndidzayankhula; imva, iwe dziko lapansi, mawu a pakamwa panga.
تعلیم من مثل باران خواهد بارید. و کلام من مثل شبنم خواهد ریخت. مثل قطره های باران بر سبزه تازه، و مثل بارشها بر نباتات. ۲ 2
Chiphunzitso changa chigwe ngati mvula ndipo mawu anga atsike ngati mame, ngati mvumbi pa udzu watsopano, ngati mvula yochuluka pa zomera zanthete.
زیرا که نام یهوه را ندا خواهم کرد. خدای ما رابه عظمت وصف نمایید. ۳ 3
Ndidzalalikira dzina la Yehova. Aa, tamandani ukulu wa Mulungu wathu!
او صخره است و اعمال او کامل. زیرا همه طریقهای او انصاف است. خدای امین و از ظلم مبرا. عادل و راست است او. ۴ 4
Iye ndi Thanthwe, ntchito zake ndi zangwiro, njira zake zonse ndi zolungama. Mulungu wokhulupirika amene salakwitsa, Iye ndiye wolungama ndi wosalakwa.
ایشان خود را فاسد نموده، فرزندان او نیستندبلکه عیب ایشانند. طبقه کج و متمردند. ۵ 5
Koma iwo achita mosakhulupirika pamaso pake, iwo si ana akenso, koma iwo ndi mʼbado wachinyengo ndi wokhotakhota.
آیا خداوند را چنین مکافات می‌دهید، ای قوم احمق و غیر حکیم. آیا او پدر و مالک تو نیست. او تو را آفرید و استوار نمود. ۶ 6
Kodi mukumubwezera Yehova chotere, inu anthu opusa ndi opanda nzeru? Kodi Iye si Atate anu, Mlengi wanu, amene anakupangani ndi kukuwumbani?
ایام قدیم را بیاد آور. در سالهای دهر به دهرتامل نما. از پدر خود بپرس تا تو را آگاه سازد. واز مشایخ خویش تا تو را اطلاع دهند. ۷ 7
Kumbukirani masiku amakedzana; ganizirani za mibado yakalekale. Funsa abambo ako ndipo adzakuwuza, akuluakulu ako, ndipo adzakufotokozera.
چون حضرت اعلی به امتها نصیب ایشان را دادو بنی آدم را منتشر ساخت، آنگاه حدود امتها راقرار داد، برحسب شماره بنی‌اسرائیل. ۸ 8
Pamene Wammwambamwamba anapereka mayiko kwa anthu a mitundu ina kukhala cholowa chawo, pamene analekanitsa anthu onse, anayikira malire anthu onse molingana ndi chiwerengero cha ana a Israeli.
زیرا که نصیب یهوه قوم وی است. و یعقوب قرعه میراث اوست. ۹ 9
Pakuti gawo la Yehova ndi anthu ake, Yakobo ndiye cholowa chake.
او را در زمین ویران یافت. و در بیابان خراب وهولناک. او را احاطه کرده، منظور داشت. و او را مثل مردمک چشم خود محافظت نمود. ۱۰ 10
Anamupeza mʼchipululu, ku malo owuma ndi kopanda kanthu. Anamuteteza ndi kumusamalira; anamutchinjiriza ngati mwanadiso wake,
مثل عقابی که آشیانه خود را حرکت دهد. وبچه های خود را فرو‌گیرد. و بالهای خود را پهن کرده، آنها را بردارد. و آنها را بر پرهای خود ببرد. ۱۱ 11
ngati chiwombankhanga chimene chimasasula chisa chake nʼkumazungulira pamwamba pa ana ake, chimene chimatambalalitsa mapiko ake kuti chigwire anawo ndi kuwanyamula pa mapiko ake otambalalawo.
همچنین خداوند تنها او را رهبری نمود. وهیچ خدای بیگانه با وی نبود. ۱۲ 12
Yehova yekha ndiye anamutsogolera; popanda thandizo la mulungu wachilendo.
او را بر بلندیهای زمین سوار کرد تا ازمحصولات زمین بخورد. و شهد را از صخره به اوداد تا مکید. و روغن را از سنگ خارا. ۱۳ 13
Anamuyendetsa pamwamba pa mapiri a mʼdziko ndi kumudyetsa zipatso za mʼminda. Anamudyetsa uchi wofula pa thanthwe, ndiponso mafuta ochokera mʼnthaka ya miyala,
کره گاوان و شیر گوسفندان را با پیه بره‌ها وقوچها را از جنس باشان و بزها. و پیه گرده های گندم را. و شراب از عصیر انگور نوشیدی. ۱۴ 14
pamodzi ndi chambiko ndi mkaka wochokera ku ngʼombe ndi nkhosa, ndiponso ana ankhosa onenepa ndi mbuzi, pamodzinso ndi nkhosa zazimuna zabwino za ku Basani ndiponso tirigu wabwino kwambiri. Munamwa vinyo wa thovu lofiira.
لیکن یشورون فربه شده، لگد زد. تو فربه وتنومند و چاق شده‌ای. پس خدایی را که او راآفریده بود، ترک کرد. و صخره نجات خود راحقیر شمرد. ۱۵ 15
Yesuruni ananenepa ndi kuyamba kuwukira; atakhuta, ananenepa ndi kukula thupi. Anasiya Mulungu amene anamulenga ndipo anakana Thanthwe ndi Mpulumutsi wake.
او را به خدایان غریب به غیرت آوردند. وخشم او را به رجاسات جنبش دادند. ۱۶ 16
Anamuchititsa nsanje ndi milungu yawo yachilendo ndiponso anamukwiyitsa ndi mafano awo onyansa.
برای دیوهایی که خدایان نبودند، قربانی گذرانیدند، برای خدایانی که نشناخته بودند، برای خدایان جدید که تازه به وجود آمده، وپدران ایشان از آنها نترسیده بودند. ۱۷ 17
Anapereka nsembe kwa ziwanda zimene si Mulungu, milungu imene sankayidziwa nʼkale lomwe, milungu yongobwera kumene, milungu imene makolo anu sankayiopa.
و به صخره‌ای که تو را تولید نمود، اعتناننمودی. و خدای آفریننده خود را فراموش کردی. ۱۸ 18
Inu munasiya Thanthwe limene linakulerani; munayiwala Mulungu amene anakubalani.
چون یهوه این را دید ایشان را مکروه داشت. چونکه پسران و دخترانش خشم او را به هیجان آوردند. ۱۹ 19
Yehova anaona zimenezi ndipo anawakana chifukwa ana ake aamuna ndi aakazi anamukwiyitsa.
پس گفت روی خود را از ایشان خواهم پوشید. تا ببینم که عاقبت ایشان چه خواهد بود. زیرا طبقه بسیار گردن کشند. و فرزندانی که امانتی در ایشان نیست. ۲۰ 20
Iye anati, “Ndidzawabisira nkhope yanga, ndi kuona kuti mathero awo adzakhala otani; pakuti ndi mʼbado wopotoka, ana amene ndi osakhulupirika.
ایشان مرا به آنچه خدا نیست به غیرت آوردند. و به اباطیل خود مرا خشمناک گردانیدند. و من ایشان را به آنچه قوم نیست به غیرت خواهم آورد. و به امت باطل، ایشان را خشمناک خواهم ساخت. ۲۱ 21
Anandichititsa kukhala wansanje pamene ankapembedza chimene si mulungu ndi kundikwiyitsa chifukwa cha mafano awo achabechabe. Ine ndidzawachititsa kuti achite nsanje ndi mtundu wina wopandapake; ndidzawakwiyitsa ndi mtundu wina wachabechabe.
زیرا آتشی در غضب من افروخته شده. و تاهاویه پایین‌ترین شعله‌ور شده است. و زمین را باحاصلش می‌سوزاند. و اساس کوهها را آتش خواهد زد. (Sheol h7585) ۲۲ 22
Pakuti mkwiyo wanga wayaka ngati moto, umene umayaka mpaka ku dziko la anthu akufa. Motowo udzanyeketsa dziko lapansi ndi zokolola zake ndipo udzapsereza maziko a mapiri. (Sheol h7585)
بر ایشان بلایا را جمع خواهم کرد. و تیرهای خود را تمام بر ایشان صرف خواهم نمود. ۲۳ 23
“Ndidzawawunjikira masautso ndipo mivi yanga yonse idzathera pa iwo.
از گرسنگی کاهیده، و از آتش تب، و از وبای تلخ تلف می‌شوند. و دندانهای وحوش را به ایشان خواهم فرستاد، با زهر خزندگان زمین. ۲۴ 24
Ndidzawatumizira njala yoopsa, malungo woopsa ndi nthenda zofa nazo; ndidzawatumizira zirombo zakuthengo zowavuta, ululu wa njoka ya mʼphiri imene imakwawa pa fumbi.
شمشیر از بیرون و دهشت از اندرون. ایشان رابی اولاد خواهد ساخت. هم جوان و هم دوشیزه را. شیرخواره را با ریش سفید هلاک خواهد کرد. ۲۵ 25
Mʼmisewu lupanga lidzawasandutsa kukhala wopanda ana; mantha adzalamulira nyumba zawo. Anyamata ndi atsikana adzafa, ngakhalenso makanda ndi okalamba.
می‌گفتم ایشان را پراکنده کنم و ذکر ایشان را ازمیان مردم، باطل سازم. ۲۶ 26
Ine ndinanena kuti ndidzawamwaza ndi kuwafafaniza kuti anthu asawakumbukirenso,
اگر از کینه دشمن نمی ترسیدم که مبادامخالفان ایشان برعکس آن فکر کنند، و بگوینددست ما بلند شده، و یهوه همه این را نکرده است. ۲۷ 27
koma sindinafune kuti adani anga adzandinyoze, mwina adani anga sadzandimvetsetsa ndipo adzanena kuti, ‘Tagonjetsa anthuwa ndife; Yehova sanachite zonsezi.’”
زیرا که ایشان قوم گم کرده تدبیر هستند. و درایشان بصیرتی نیست. ۲۸ 28
Iwo ndi mtundu wopanda maganizo, iwo alibe nzeru nʼpangʼono pomwe.
کاش که حکیم بوده، این را می‌فهمیدید. و درعاقبت خود تامل می‌نمودند. ۲۹ 29
Ngati iwo akanakhala anzeru akanamvetsetsa izi ndi kuzindikira kuti mathero awo adzakhala otani!
چگونه یک نفر هزار را تعاقب می‌کرد. و دو نفرده هزار را منهزم می‌ساختند. اگر صخره ایشان، ایشان را نفروخته. و خداوند، ایشان را تسلیم ننموده بود. ۳۰ 30
Kodi munthu mmodzi akanathamangitsa bwanji anthu 1,000 kapena anthu awiri kuthamangitsa anthu 10,000, kuti awagonjetse, Thanthwe lawo likanapanda kuwagulitsa, Yehova akanapanda kuwataya?
زیرا که صخره ایشان مثل صخره ما نیست. اگرچه هم دشمنان ما خود، حکم باشند. ۳۱ 31
Pakuti thanthwe lawo silofanana ndi Thanthwe lathu, ngakhale adani athu amavomereza zimenezi.
زیرا که مو ایشان از موهای سدوم است، و ازتاکستانهای عموره. انگورهای ایشان انگورهای حنظل است، و خوشه های ایشان تلخ است. ۳۲ 32
Mpesa wawo umachokera ku mpesa wa ku Sodomu ndiponso ku minda ya ku Gomora. Mphesa zawo zili ndi ululu wakupha ndipo maphava ake ndi owawa.
شراب ایشان زهر اژدرهاست. و سم قاتل افعی. ۳۳ 33
Vinyo wawo ndi wa ululu wa njoka, ululu woopsa wa mphiri.
آیا این نزد من مکنون نیست. و درخزانه های من مختوم نی. ۳۴ 34
“Kodi zimenezi sindinazisunge ndi kuzitsekera mʼkatikati mwa chuma changa?
انتقام و جزا از آن من است، هنگامی که پایهای ایشان بلغزد، زیرا که روز هلاکت ایشان نزدیک است و قضای ایشان می‌شتابد. ۳۵ 35
Kubwezera chilango nʼkwanga; ndidzawalanga ndine. Pa nthawi yake phazi lawo lidzaterera; tsiku lawo la masautso layandikira ndipo chiwonongeko chawo chikubwera pa iwo mofulumira.”
زیرا خداوند، قوم خود را داوری خواهدنمود. و بر بندگان خویش شفقت خواهد کرد. چون می‌بیند که قوت ایشان نابود شده، وهیچکس چه غلام و چه آزاد باقی نیست. ۳۶ 36
Yehova adzaweruza anthu ake ndipo adzachitira atumiki ake chifundo pamene adzaona kuti mphamvu zawo zatha ndipo kuti palibe amene watsala, kapolo kapena mfulu.
و خواهد گفت: خدایان ایشان کجایند، وصخره‌ای که بر آن اعتماد می‌داشتند. ۳۷ 37
Iye adzanena kuti, “Nanga ili kuti milungu yawo, thanthwe limene ankabisalamo,
که پیه قربانی های ایشان را می‌خوردند. و شراب هدایای ریختنی‌ایشان را می‌نوشیدند. آنهابرخاسته، شما را امداد کنند. و برای شما ملجاباشند. ۳۸ 38
milungu imene inkadya mafuta a nsembe zawo ndi kumwa vinyo wa chopereka chawo cha chakumwa?” Iwuzeni ibwere kuti idzakuthandizeni! Ibwere kuti idzakutetezenitu!
الان ببینید که من خود، او هستم. و با من خدای دیگری نیست. من می‌میرانم و زنده می‌کنم. مجروح می‌کنم و شفا می‌دهم. و از دست من رهاننده‌ای نیست. ۳۹ 39
“Onani tsopano kuti Ine ndine Iyeyo! Palibe mulungu wina koma Ine ndekha. Ine ndimapha ndiponso kupereka moyo, ndavulaza ndipo ndidzachiritsa, ndipo palibe angathe kupulumutsa munthu mʼmanja mwanga.
زیرا که دست خود را به آسمان برمی افرازم، ومی گویم که من تا ابدالاباد زنده هستم. ۴۰ 40
Ndikweza dzanja langa kumwamba ndi kulumbira kuti, ‘Pali Ine wamoyo wamuyaya,
اگر شمشیر براق خود را تیز کنم. و قصاص رابه‌دست خود گیرم. آنگاه از دشمنان خود انتقام خواهم کشید. و به خصمان خود مکافات خواهم رسانید. ۴۱ 41
pamene ndidzanola lupanga langa lonyezimira ndipo dzanja liligwira pakubweretsa chiweruzo, ndidzabwezera chilango adani anga ndi kulanga onse odana nane.
تیرهای خود را از خون مست خواهم ساخت. و شمشیر من گوشت را خواهد خورد. از خون کشتگان و اسیران، با روسای سروران دشمن. ۴۲ 42
Mivi yanga idzakhuta magazi awo pamene lupanga langa lidzawononga mnofu: magazi a anthu ophedwa ndi ogwidwa ukapolo, mitu ya atsogoleri a adani.’”
‌ای امتها با قوم او آواز شادمانی دهید. زیراانتقام خون بندگان خود را گرفته است. و ازدشمنان خود انتقام کشیده و برای زمین خود وقوم خویش کفاره نموده است. ۴۳ 43
Kondwerani, inu mitundu yonse ya anthu pamodzi ndi anthu ake, pakuti Iye adzabwezera chilango anthu amene anapha atumiki ake; adzabwezera chilango adani ake ndipo adzakhululukira dziko lake ndi la anthu ake.
و موسی آمده، تمامی سخنان این سرود رابه سمع قوم رسانید، او و یوشع بن نون. ۴۴ 44
Mose anabwera ndi Yoswa mwana wa Nuni ndipo anayankhula mawu onsewa mʼnyimbo anthu akumva.
و چون موسی از گفتن همه این سخنان به تمامی اسرائیل فارغ شد، ۴۵ 45
Mose atatsiriza kunena mawu onsewa pamtima kwa Aisraeli,
به ایشان گفت: «دل خود را به همه سخنانی که من امروز به شما شهادت می‌دهم، مشغول سازید، تا فرزندان خود را حکم دهید که متوجه شده، تمامی کلمات این تورات را به عمل آورند. ۴۶ 46
iye anawawuza kuti, “Muwasunge bwino mu mtima mwanu, mawu onse amene lero lino ndikukuwuzani kuti mudzawuze ana anu, kuti adzamvere mosamalitsa mawu onse a malamulo amenewa.
زیرا که این برای شما امر باطل نیست، بلکه حیات شماست، و به واسطه این امر، عمرخود را در زمینی که شما برای تصرفش از اردن به آنجا عبور می‌کنید، طویل خواهید ساخت.» ۴۷ 47
Mawuwa sikuti ndi mawu achabe kwa inu. Mawuwa ndi moyo wanu. Mukawamvera mudzakhala ndi moyo wautali mʼdziko limene mukukalitenga kukhala lanu mukawoloka Yorodani.”
و خداوند در همان روز موسی را خطاب کرده، گفت: ۴۸ 48
Tsiku lomwelo Yehova anawuza Mose kuti,
«به این کوه عباریم یعنی جبل نبوکه در زمین موآب در مقابل اریحاست برآی، وزمین کنعان را که من آن را به بنی‌اسرائیل به ملکیت می‌دهم ملاحظه کن. ۴۹ 49
“Pita ku mapiri a ku Abarimu ukakwere pa Phiri la Nebo ku Mowabu, moyangʼanana ndi Yeriko, ndipo ukaone dziko la Kanaani, dziko limene ndikulipereka kwa Aisraeli kukhala lawo.
و تو در کوهی که به آن برمی آیی وفات کرده، به قوم خود ملحق شو، چنانکه برادرت هارون در کوه هور مرد و به قوم خود ملحق شد. ۵۰ 50
Iwe udzafera pa phiri limenelo ndipo udzapita kumene makolo ako anapita, monga mʼbale wako Aaroni anafera pa phiri la Hori ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.
زیرا که شما در میان بنی‌اسرائیل نزد آب مریبا قادش در بیابان سین به من تقصیر نمودید، چون که مرا در میان بنی‌اسرائیل تقدیس نکردید. ۵۱ 51
Chifukwa chake nʼchakuti inu nonse awiri simunakhulupirike kwa Ine pamaso pa Aisraeli pa madzi a Meriba ku Kadesi mʼchipululu cha Zini chifukwa simunandilemekeze kokwanira pakati pa Aisraeli.
پس زمین را پیش روی خود خواهی دید، لیکن به آنجا به زمینی که به بنی‌اسرائیل می‌دهم، داخل نخواهی شد.» ۵۲ 52
Choncho udzalionera kutali dziko limene ndikupereka kwa Aisraeli. Sudzalowa mʼdziko limene ndi kulipereka kwa Aisraeli.”

< تثنیه 32 >