< کولسیان 4 >

ای آقایان، با غلامان خود عدل و انصاف رابه‌جا آرید، چونکه می‌دانید شما را نیزآقایی هست در آسمان. ۱ 1
Mabwana, antchito anu muzikhala nawo mwachilungamo ndi moyenera, podziwa kuti nanunso muli nawo Ambuye anu mmwamba.
در دعا مواظب باشید و در آن با شکرگزاری بیدار باشید. ۲ 2
Pempherani modzipereka, mukhale atcheru ndiponso oyamika.
و درباره ما نیز دعا کنید که خدا در کلام را به روی ما بگشاید تا سر مسیح را که بجهت آن در قید هم افتاده‌ام بگویم، ۳ 3
Ndipo muzitipemphereranso ife kuti Mulungu atitsekulire khomo la uthenga wathu, kuti tilalikire chinsinsi cha Khristu, chimene ndine womangidwa nacho mʼndende.
و آن رابطوری که می‌باید تکلم کنم و مبین سازم. ۴ 4
Pempherani kuti ndilalikire momveka bwino, monga ndikuyenera.
زمان را دریافته، پیش اهل خارج به حکمت رفتار کنید. ۵ 5
Mayendedwe anu pakati pa akunja, akhale anzeru ndipo mugwiritse ntchito mpata uliwonse umene muli nawo.
گفتگوی شما همیشه با فیض باشد و اصلاح شده به نمک، تا بدانید هرکس را چگونه جواب باید داد. ۶ 6
Mayankhulidwe anu nthawi zonse akhale odzaza ndi chisomo ndi okoma, kuti mudziwe kuyankha aliyense.
تیخیکس، برادر عزیز و خادم امین وهمخدمت من در خداوند، از همه احوال من شمارا خواهد آگاهانید، ۷ 7
Tukiko adzakuwuzani zonse za ine. Iye ndi mʼbale wokondedwa, mtumiki wokhulupirika ndiponso wantchito mnzanga mwa Ambuye.
که او را به همین جهت نزدشما فرستادم تا از حالات شما آگاه شود و دلهای شما را تسلی دهد، ۸ 8
Ine ndikumutumiza kwa inu ndi cholinga choti mudziwe zimene tikukumana nazo ndiponso kuti alimbikitse mitima yanu.
با انیسیمس، برادر امین وحبیب که از خود شماست، شما را از همه گزارش اینجا آگاه خواهند ساخت. ۹ 9
Iye akubwera ndi Onesimo, mʼbale wathu wokhulupirika ndi wokondedwa, amene ndi mmodzi mwa inu. Iwo adzakuwuzani zonse zimene zikuchitika kuno.
ارسترخس همزندان من شما را سلام می‌رساند، و مرقس عموزاده برنابا که درباره او حکم یافته‌اید، هرگاه نزد شما آید او را بپذیرید، ۱۰ 10
Aristariko, wamʼndende mnzanga akupereka moni, Marko akuperekanso moni, msuweni wa Barnaba. (Inu munawuzidwa kale za Iye. Iye akabwera kwanuko, mulandireni).
و یسوع، ملقب به یسطس که ایشان تنها از اهل ختنه برای ملکوت خدا همخدمت شده، باعث تسلی من گردیدند. ۱۱ 11
Yesu wotchedwa Yusto, akuperekanso moni. Amenewa ndi Ayuda okhawo pakati pa atumiki anzanga mu ufumu wa Mulungu, ndipo aonetsa kuti ndi chitonthozo kwa ine.
اپفراس به شما سلام می‌رساند که یکی از شماو غلام مسیح است و پیوسته برای شما دردعاهای خود جد و جهد می‌کند تا در تمامی اراده خدا کامل و متیقن شوید. ۱۲ 12
Epafra ndi mmodzi mwa inu ndiponso mtumiki wa Khristu Yesu, akupereka moni. Iyeyu nthawi zonse amakupemphererani mwamphamvu, kuti mukhazikike pa chifuniro chonse cha Mulungu, mukhale okhwima ndi otsimikiza kwathunthu.
و برای اوگواهی می‌دهم که درباره شما و اهل لاودکیه واهل هیراپولس بسیار محنت می‌کشد. ۱۳ 13
Ine ndikumuchitira umboni kuti amagwira ntchito mwamphamvu chifukwa cha inu ndiponso kwa amene ali ku Laodikaya ndi Herapoli.
و لوقای طبیب حبیب و دیماس به شما سلام می‌رسانند. ۱۴ 14
Luka, dotolo wathu wokondedwa ndi Dema, akupereka moni.
برادران در لاودکیه و نیمفاس و کلیسایی را که در خانه ایشان است سلام رسانید. ۱۵ 15
Perekani moni kwa abale a ku Laodikaya, ndiponso kwa Numfa ndi mpingo wa mʼnyumba mwake.
و چون این رساله برای شما خوانده شد، مقرر دارید که در کلیسای لاودکیان نیز خوانده شود و رساله از لاودکیه را هم شما بخوانید. ۱۶ 16
Kalata iyi ikawerengedwa pakati panu, muonetsetse kuti ikawerengedwenso ku mpingo wa ku Laodikaya ndipo inunso muwerenge kalata yochokera ku Laodikaya.
و به ارخپس گویید: «باخبر باش تا آن خدمتی را که در خداوند یافته‌ای به‌کمال رسانی.» ۱۷ 17
Uzani Arkipo kuti, “Wonetsetsa kuti wamaliza ntchito imene unayilandira mwa Ambuye.”
تحیت من، پولس، به‌دست خودم. زنجیرهای مرا بخاطر دارید. فیض با شما باد. آمین. ۱۸ 18
Ine Paulo, ndikulemba ndi dzanja langa moni uwu. Kumbukirani kuti ndili mu unyolo. Chisomo chikhale ndi inu.

< کولسیان 4 >