< عاموس 8 >

خداوند یهوه به من چنین نمودار ساخت واینک سبدی پر از میوه‌ها. ۱ 1
Zimene Ambuye Yehova anandionetsa ndi izi: dengu la zipatso zakupsa.
و گفت: «ای عاموس چه می‌بینی؟» من جواب دادم که «سبدی از میوه.» و خداوند به من گفت: «انتها بر قوم من اسرائیل رسیده است و از ایشان دیگر درنخواهم گذشت.» ۲ 2
Iye anandifunsa kuti, “Amosi nʼchiyani ukuona?” Ine ndinayankha kuti, “Dengu la zipatso zakupsa.” Ndipo Yehova anati kwa ine, “Nthawi yachimaliziro yawakwanira anthu anga Aisraeli; sindidzawakhululukiranso.
خداوند یهوه می‌گوید که در آن روزسرودهای هیکل به ولوله مبدل خواهد شد ولاشهای بسیار خواهد بود و آنها را در هر جا به خاموشی بیرون خواهند انداخت. ۳ 3
“Tsiku limenelo,” Ambuye Yehova akulengeza kuti, “Nyimbo za mʼNyumba ya Mulungu zidzasanduka kulira kofuwula. Mitembo ya anthu idzachuluka, ndipo adzayiponya ponseponse! Kudzangoti zii!”
‌ای شما که می‌خواهید فقیران را ببلعید ومسکینان زمین را هلاک کنید این را بشنوید. ۴ 4
Imvani izi, inu amene mumapondereza anthu osowa ndipo simulabadira anthu osauka a mʼdzikomu.
ومی گویید که غره ماه کی خواهد گذشت تا غله رابفروشیم و روز سبت تا انبارهای گندم را بگشاییم و ایفا را کوچک و مثقال را بزرگ ساخته، میزانهارا قلب و معوج نماییم. ۵ 5
Mumanena kuti, “Kodi chikondwerero cha mwezi watsopano chidzatha liti kuti tigulitse zinthu? Ndipo tsiku la Sabata litha liti kuti tigulitse tirigu, kuti tichepetse miyeso, kukweza mitengo kuti tibere anthu ndi miyeso ya chinyengo,
و مسکینان را به نقره و فقیران را به نعلین بخریم و پس مانده گندم رابفروشیم. ۶ 6
tigule osauka ndi ndalama zasiliva ndi osowa powapatsa nsapato, tigulitse ngakhale mungu wa tirigu?”
خداوند به جلال یعقوب قسم خورده است که هیچکدام از اعمال ایشان را هرگزفراموش نخواهم کرد. ۷ 7
Yehova amene Yakobo amamunyadira, walumbira kuti: Ine sindidzayiwala chilichonse chimene anachita.
آیا به این سبب زمین متزلزل نخواهد شد و همه ساکنانش ماتم نخواهند گرفت و تمامش مثل نهر برنخواهد آمدو مثل نیل مصر سیلان نخواهد کرد و فرو نخواهدنشست. ۸ 8
“Kodi dziko silidzagwedezeka chifukwa cha zimenezi, ndi onse okhala mʼmenemo kulira mwachisoni? Dziko lonse lidzavunduka ngati mtsinje wa Nailo; lidzagwedezeka kenaka nʼkukhala bata ngati mtsinje wa ku Igupto.
و خداوند یهوه می‌گوید: «که در آن روزآفتاب را در وقت ظهر فرو خواهم برد و زمین رادر روز روشن تاریک خواهم نمود. ۹ 9
“Tsiku limenelo,” Ambuye Yehova akunena kuti, “Ndidzadetsa dzuwa masana ndi kugwetsa mdima pa dziko lapansi dzuwa likuswa mtengo.
و عیدهای شما را به ماتم و همه سرودهای شما را به مرثیه هامبدل خواهم ساخت. و بر هر کمر پلاس و بر هرسر گری برخواهم آورد و آن را مثل ماتم پسریگانه و آخرش را مانند روز تلخی خواهم گردانید.» ۱۰ 10
Maphwando anu achipembedzo ndidzawasandutsa kulira kwa chisoni ndipo kuyimba kwanu konse ndidzakusandutsa maliro. Ndidzakuvekani chiguduli nonsenu ndi kumeta mipala mitu yanu. Nthawi imeneyo idzakhala ngati yolira mwana wamwamuna mmodzi yekhayo, ndipo tsikulo lidzakhala lowawa mpaka kutha kwake.
اینک خداوند یهوه می‌گوید: «ایامی می‌آید که گرسنگی بر زمین خواهم فرستاد نه گرسنگی از نان و نه تشنگی از آب بلکه از شنیدن کلام خداوند. ۱۱ 11
“Nthawi ikubwera,” Ambuye Yehova akunena kuti, “Ndidzagwetsa njala mʼdziko lonse; osati njala ya chakudya kapena ludzu la madzi, koma njala yofuna kumva mawu a Yehova.
و ایشان از دریا تا دریا و ازشمال تا مشرق پراکنده خواهند شد و گردش خواهند کرد تا کلام خداوند را بطلبند اما آن رانخواهند یافت. ۱۲ 12
Anthu azidzangoyendayenda kuchoka ku nyanja ina kupita ku nyanja ina. Azidzangoyendayenda kuchoka kumpoto kupita kummawa, kufunafuna mawu a Yehova, koma sadzawapeza.
در آن روز دوشیزگان جمیل وجوانان از تشنگی ضعف خواهند کرد. ۱۳ 13
“Tsiku limenelo “anamwali okongola ndi anyamata amphamvu adzakomoka ndi ludzu.
آنانی که به گناه سامره قسم خورده، می‌گویند که «ای دان به حیات خدای تو و به طریقت بئرشبع قسم می‌خوریم»، خواهند افتاد و بار دیگر نخواهندبرخاست. ۱۴ 14
Onse amene amalumbira pa tchimo la Samariya, kapena kumanena kuti, ‘Iwe Dani, pali mulungu wako wamoyo,’ kapena, ‘Pali mulungu wamoyo wa ku Beeriseba.’ Iwowo adzagwa ndipo sadzadzukanso.”

< عاموس 8 >