< دوم تواریخ 26 >

و تمامی قوم یهودا عزیا را که شانزده ساله بود گرفته، در جای پدرش امصیاپادشاه ساختند. ۱ 1
Kenaka anthu onse a ku Yuda anatenga Uziya amene anali wa zaka 16, namuyika kukhala mfumu mʼmalo mwa Amaziya abambo ake.
و او بعد از آنکه پادشاه باپدرانش خوابیده بود، ایلوت را بنا کرد و آن رابرای یهودا استرداد نمود. ۲ 2
Iye anamanganso mzinda wa Eloti ndi kuwubwezeranso ku Yuda abambo ake atamwalira.
و عزیا شانزده ساله بود که پادشاه شد و پنجاه و دو سال در اورشلیم پادشاهی نمود و اسم مادرش یکلیای اورشلیمی بود. ۳ 3
Uziya anali wa zaka 16 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 70. Dzina la amayi ake linali Yekoliya wa ku Yerusalemu.
و آنچه در نظر خداوند پسند بود، موافق هرچه پدرش امصیا کرده بود، بجا آورد. ۴ 4
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Amaziya abambo ake.
و درروزهای زکریا که در رویاهای خدا بصیر بود، خدا را می‌طلبید و مادامی که خداوند رامی طلبید، خدا او را کامیاب می‌ساخت. ۵ 5
Iye anapembedza Mulungu nthawi ya Zekariya, amene ankamulangiza za kuopa Mulungu amene anamupatsa chipambano.
و او بیرون رفته، با فلسطینیان جنگ کرد وحصار جت و حصار یبنه و حصار اشدود رامنهدم ساخت و شهرها در زمین اشدود وفلسطینیان بنا نمود. ۶ 6
Iyeyo anapita kukachita nkhondo ndi Afilisti ndipo anagwetsa makoma a Gati, Yabine ndi Asidodi. Ndipo kenaka anamanganso mizinda ya pafupi ndi Asidodi ndi malo ena pafupi ndi Afilisti.
و خدا او را بر فلسطینیان وعربانی که در جوربعل ساکن بودند و بر معونیان نصرت داد. ۷ 7
Mulungu anamuthandiza polimbana ndi Afilisti ndi Aarabu amene amakhala ku Guri-Baala ndiponso polimbana ndi Ameuni.
و عمونیان به عزیا هدایا دادند و اسم او تا مدخل مصر شایع گردید، زیرا که بی‌نهایت قوی گشت. ۸ 8
Aamoni ankabweretsa msonkho kwa Uziya ndipo mbiri yake inamveka mpaka ku malire a dziko la Igupto chifukwa anali wamphamvu kwambiri.
و عزیا برجها در اورشلیم نزددروازه زاویه و نزد دروازه وادی و نزد گوشه حصار بنا کرده، آنها را مستحکم گردانید. ۹ 9
Uziya anamanga nsanja ku Yerusalemu ku Chipata Chapangodya, ku Chigwa cha Chipata ndi pokhotera mpanda, ndipo anayikamo chitetezo.
وبرجها در بیابان بنا نمود و چاههای بسیار کند زیراکه مواشی کثیر در همواری و در هامون داشت وفلاحان و باغبانان در کوهستان و در بوستانهاداشت، چونکه فلاحت را دوست می‌داشت. ۱۰ 10
Iye anamanganso nsanja ku chipululu ndi kukumbanso zitsime zambiri chifukwa anali ndi ziweto zambiri mʼmbali mwa phiri ndi ku zigwa. Iye anali ndi anthu amene ankagwira ntchito mʼminda yake ndiponso mʼminda yake ya mphesa mʼphiri ndi malo achonde, pakuti ankakonda nthaka.
وعزیا سپاهیان جنگ آزموده داشت که برای محاربه‌دسته دسته بیرون می‌رفتند، برحسب تعداد ایشان که یعیئیل کاتب و معسیای رئیس زیردست حننیا که یکی از سرداران پادشاه بود، آنها را سان می‌دیدند. ۱۱ 11
Uziya anali ndi gulu lankhondo lophunzitsidwa bwino, lokonzekera kupita ku nkhondo mʼmagulu monga mwa chiwerengero chawo chimene mlembi Yeiyeli ndi Maaseya anasonkhanitsa motsogozedwa ndi Hananiya mmodzi mwa akuluakulu a mfumu.
و عدد تمامی سرداران آبا که شجاعان جنگ آزموده بودند، دو هزار وششصد بود. ۱۲ 12
Chiwerengero chonse cha atsogoleri a mʼmabanja oyangʼanira anthu ochita nkhondo chinali 2,600.
و زیر دست ایشان، سیصد و هفت هزار و پانصد سپاه جنگ آزموده بودند که پادشاه را به ضد دشمنانش مساعدت نموده، با قوت تمام مقاتله می‌کردند. ۱۳ 13
Pansi pa ulamuliro wawo panali asilikali 307,500 ophunzitsidwa nkhondo, gulu lamphamvu lothandiza mfumu kulimbana ndi adani ake.
و عزیا برای ایشان یعنی برای تمامی لشکر سپرها و نیزه‌ها و خودها وزره‌ها و کمانها و فلاخنها مهیا ساخت. ۱۴ 14
Uziya anawapangira asilikaliwo zishango, mikondo, zipewa zankhondo, malaya ankhondo achitsulo, mauta ndi miyala yogendera.
ومنجنیقهایی را که مخترع صنعتگران ماهر بود دراورشلیم ساخت تا آنها را بر برجها و گوشه های حصار برای انداختن تیرها و سنگهای بزرگ بگذارند. پس آوازه او تا جایهای دور شایع شدزیرا که نصرت عظیمی یافته، بسیار قوی گردید. ۱۵ 15
Mu Yerusalemu anapanga makina okonzedwa ndi anthu aluso amene amagwiritsidwa ntchito pa malo otetezera a pa nsanja ndi pa ngodya kuponyera mivi ndi kugubuduzira miyala. Mbiri yake inamveka kutali ndi ponseponse pakuti anathandizidwa kwambiri mpaka anakhala wamphamvu kwambiri.
لیکن چون زورآور شد، دل او برای هلاکتش متکبر گردید و به یهوه خدای خودخیانت ورزیده، به هیکل خداوند درآمد تا بخوربر مذبح بخور بسوزاند. ۱۶ 16
Koma pamene Uziya anakhala wamphamvu kwambiri, kunyada kwake kunamuwononga. Iye sanakhulupirike kwa Yehova Mulungu wake, ndipo analowa mʼNyumba ya Yehova kukafukiza lubani pa guwa lofukizira.
و عزریای کاهن ازعقب او داخل شد و همراه او هشتاد مرد رشید ازکاهنان خداوند درآمدند. ۱۷ 17
Wansembe Azariya pamodzi ndi ansembe a Yehova ena 80 olimba mtima anamutsatira.
و ایشان با عزیاپادشاه مقاومت نموده، او را گفتند: «ای عزیاسوزانیدن بخور برای خداوند کار تو نیست بلکه کار کاهنان پسران هارون است که برای سوزانیدن بخور تقدیس شده‌اند. پس از مقدس بیرون شوزیرا خطا کردی و این کار از جانب یهوه خداموجب عزت تو نخواهد بود.» ۱۸ 18
Iwo anatsutsana naye ndipo anati, “Sibwino kuti inu mfumu muzifukiza lubani koma zidzukulu za Aaroni, zimene zinapatulidwa kuti zizifukiza lubani. Chokani pa malo opatulika ano, pakuti inu mwakhala osakhulupirika, ndipo simudzalemekezedwa ndi Yehova Mulungu.”
آنگاه عزیا که مجمری برای سوزانیدن بخور در دست خود داشت، غضبناک شد و چون خشمش بر کاهنان افروخته گردید، برص به حضور کاهنان در خانه خداوند به پهلوی مذبح بخور بر پیشانی‌اش پدید آمد. ۱۹ 19
Uziya, amene anali ndi chofukizira mʼmanja mwake wokonzeka kuti afukize lubani, anapsa mtima. Iye anakwiyira ansembewo. Ndipo ansembe aja akuona patsogolo pa guwa lofukizira lubani mʼNyumba ya Mulungu, khate linayamba pamphumi pake.
و عزریای رئیس کهنه و سایر کاهنان بر او نگریستند و اینک برص بر پیشانی‌اش ظاهر شده بود. پس او را ازآنجا به شتاب بیرون کردند و خودش نیز به تعجیل بیرون رفت، چونکه خداوند او را مبتلاساخته بود. ۲۰ 20
Azariya, mkulu wa ansembe pamodzi ndi ansembe ena onse atamuyangʼana anaona kuti anali ndi khate pamphumi pake, ndipo anamutulutsa mofulumira. Ndipo iye mwini anafulumira kutuluka, chifukwa Yehova anamulanga.
و عزیا پادشاه تا روز وفاتش ابرص بود و در مریضخانه مبروص ماند، زیرا از خانه خداوند ممنوع بود و پسرش یوتام، ناظر خانه پادشاه و حاکم قوم زمین می‌بود. ۲۱ 21
Mfumu Uziya anali ndi khate mpaka tsiku limene anamwalira. Iye amakhala mʼnyumba ya yekha ngati wakhate, ndipo samalowa mʼNyumba ya Yehova. Yotamu mwana wake ndiye amayangʼanira nyumba yaufumu ndipo ankalamulira anthu a mʼdzikomo.
و اشعیا ابن آموص نبی بقیه وقایع اول وآخر عزیا را نوشت. ۲۲ 22
Ntchito zina za mfumu Uziya, kuyambira pachiyambi mpaka pa mapeto, zinalembedwa ndi mneneri Yesaya mwana wa Amozi.
پس عزیا با پدران خودخوابید و او را با پدرانش در زمین مقبره پادشاهان دفن کردند، زیرا گفتند که ابرص است و پسرش یوتام در جایش پادشاه شد. ۲۳ 23
Uziya analondola makolo ake, ndipo anamuyika pamodzi ndi makolo ake ku malo a manda a mafumu, koma osati mʼmanda mwawomo poti anthu anati, “Iyeyu anali ndi khate.” Ndipo Yotamu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< دوم تواریخ 26 >