< اول سموئیل 7 >

خداوند را آوردند، و آن را به خانه ابیناداب در جبعه داخل کرده، پسرش العازار راتقدیس نمودند تا تابوت خداوند را نگاهبانی کند. ۱ 1
Choncho anthu a ku Kiriati-Yearimu anabwera ndi kudzatenga Bokosi la Yehova. Iwo anapita nalo ku nyumba ya Abinadabu ya ku phiri ndipo anapatula Eliezara mwana wake kuti aziyangʼanira Bokosi la Yehovalo.
و از روزی که تابوت در قریه یعاریم ساکن شد، وقت طول کشید تا بیست سال گذشت، و بعداز آن خاندان اسرائیل برای پیروی خداوند جمع شدند. ۲ 2
Zaka makumi awiri zinapita kuyambira pamene Bokosi la Yehova linakhala ku Kiriati-Yearimu, ndipo anthu a Israeli onse analira kupempha Yehova kuti awathandize.
و سموئیل تمامی خاندان اسرائیل را خطاب کرده، گفت: «اگر به تمامی دل به سوی خداوندبازگشت نمایید، و خدایان غیر و عشتاروت را ازمیان خود دور کنید، و دلهای خود را برای خداوند حاضر ساخته، او را تنها عبادت نمایید، پس او، شما را از دست فلسطینیان خواهدرهانید.» ۳ 3
Ndipo Samueli anati kwa nyumba yonse ya Israeli, “Ngati mukubwerera kwa Yehova ndi mtima wanu wonse, muchotse milungu yachilendo ndi Asiteroti pakati panu ndipo mitima yanu ikhazikike pa Yehova ndi kutumikira Iye yekha. Mukatero Iye adzakupulumutsani mʼmanja mwa Afilisti.”
آنگاه بنی‌اسرائیل بعلیم و عشتاروت رادور کرده، خداوند را تنها عبادت نمودند. ۴ 4
Choncho Aisraeli anachotsa milungu yawo ya Baala ndi Asitoreti ndi kutumikira Yehova yekha.
و سموئیل گفت: «تمامی اسرائیل را درمصفه جمع کنید تا درباره شما نزد خداوند دعانمایم.» ۵ 5
Kenaka Samueli anati, “Sonkhanitsani Aisraeli onse ku Mizipa ndipo ine ndidzakupemphererani kwa Yehova.”
و در مصفه جمع شدند و آب کشیده، آن را به حضور خداوند ریختند، و آن روز راروزه داشته، در آنجا گفتند که بر خداوند گناه کرده‌ایم، و سموئیل بنی‌اسرائیل را در مصفه داوری نمود. ۶ 6
Choncho anasonkhana ku Mizipa, ndipo anatunga madzi ndi kuwathira pansi pamaso pa Yehova. Pa tsiku limenelo anasala kudya namanena kuti, “Ife tachimwira Yehova.” Ndipo Samueli anali mtsogoleri wa Israeli ku Mizipa.
و چون فلسطینیان شنیدند که بنی‌اسرائیل درمصفه جمع شده‌اند، سروران فلسطینیان براسرائیل برآمدند، و بنی‌اسرائیل چون این راشنیدند، از فلسطینیان ترسیدند. ۷ 7
Afilisti anamva kuti Aisraeli asonkhana ku Mizipa, choncho akalonga awo anabwera kudzawathira nkhondo. Ndipo Aisraeli atamva anachita mantha chifukwa cha Afilisti.
و بنی‌اسرائیل به سموئیل گفتند: «از تضرع نمودن برای ما نزدیهوه خدای ما ساکت مباش تا ما را از دست فلسطینیان برهاند.» ۸ 8
Choncho anati kwa Samueli, “Musasiye kutipempherera kwa Yehova Mulungu wathu, kuti atipulumutse mʼdzanja la Afilistiwa.”
و سموئیل بره شیرخواره گرفته، آن را به جهت قربانی سوختنی تمام برای خداوند گذرانید، و سموئیل درباره اسرائیل نزدخداوند تضرع نموده، خداوند او را اجابت نمود. ۹ 9
Ndipo Samueli anatenga mwana wankhosa wamkazi woyamwa ndi kumupereka monga nsembe yopsereza kwa Yehova. Iye anapemphera kwa Yehova mʼmalo mwa Aisraeli, ndipo Yehova anamuyankha.
و چون سموئیل قربانی سوختنی رامی گذرانید، فلسطینیان برای مقاتله اسرائیل نزدیک آمدند، و در آن روز خداوند به صدای عظیم بر فلسطینیان رعد کرده، ایشان را منهزم ساخت، و از حضور اسرائیل شکست یافتند. ۱۰ 10
Samueli akupereka nsembe yopsereza, Afilisti anayandikira kuti ayambe kuwathira nkhondo Aisraeli. Koma tsiku limenelo Yehova anawaopseza Afilisti aja ndi mawu aakulu ngati bingu. Choncho anasokonezeka motero kuti Aisraeli anawagonjetsa.
ومردان اسرائیل از مصفه بیرون آمدند و فلسطینیان را تعاقب نموده، ایشان را تا زیر بیت کار شکست دادند. ۱۱ 11
Aisraeli anatuluka ku Mizipa kuthamangitsa Afilisti aja nʼkumawapha mʼnjira yonse mpaka kumunsi kwa Beti-Kari.
و سموئیل سنگی گرفته، آن را میان مصفه وسن برپا داشت و آن را ابن عزر نامیده، گفت: «تابحال خداوند ما را اعانت نموده است.» ۱۲ 12
Kenaka Samueli anatenga mwala nawuyika pakati pa Mizipa ndi Seni. Iye anawutcha Ebenezeri, popeza anati, “Yehova watithandiza mpaka pano.”
پس فلسطینیان مغلوب شدند، و دیگر به حدوداسرائیل داخل نشدند، و دست خداوند در تمامی روزهای سموئیل بر فلسطینیان سخت بود. ۱۳ 13
Kotero Afilisti anagonjetsedwa ndipo sanadzalowenso mʼdziko la Israeli. Yehova analimbana ndi Afilisti masiku onse a Samueli.
وشهرهایی که فلسطینیان از اسرائیل گرفته بودند، از عقرون تا جت، به اسرائیل پس دادند، و اسرائیل حدود آنها را از دست فلسطینیان رهانیدند، و در میان اسرائیل و اموریان صلح شد. ۱۴ 14
Mizinda yonse imene Afilisti analanda kuchokera ku Ekroni mpaka ku Gati inabwezedwa kwa Aisraeli. Choncho Aisraeli anapulumutsa dziko lawo. Ndipo panalinso mtendere pakati pa Aisraeli ndi Aamori.
و سموئیل در تمام روزهای عمر خود براسرائیل داوری می‌نمود. ۱۵ 15
Samueli anatsogolera Aisraeli moyo wake wonse.
و هر سال رفته، به بیت ئیل و جلجال و مصفه گردش می‌کردند، و درتمامی این‌جاها بر اسرائیل داوری می‌نمود. ۱۶ 16
Chaka ndi chaka Samueli ankakonza ulendo wozungulira kuchokera ku Beteli mpaka ku Giligala ndi Mizipa, kuweruza milandu ya Aisraeli mʼmadera onsewa.
وبه رامه بر می‌گشت زیرا خانه‌اش در آنجا بود و درآنجا بر اسرائیل داوری می‌نمود، و مذبحی درآنجا برای خداوند بنا کرد. ۱۷ 17
Koma pambuyo pake ankabwerera ku Rama, kumene kunali nyumba yake. Ankaweruza Aisraeli kumeneko. Ndipo iye anamanga guwa lansembe la Yehova kumeneko.

< اول سموئیل 7 >