< اول پادشاهان 21 >

و بعد از این امور، واقع شد که نابوت یزرعیلی، تاکستانی در یزرعیل به پهلوی قصر اخاب، پادشاه سامره، داشت. ۱ 1
Zitatha izi, panachitika nkhani yokhudza Naboti wa ku Yezireeli amene anali ndi munda wamphesa ku Yezireeli, pafupi ndi nyumba ya mfumu Ahabu, mfumu ya ku Samariya.
واخاب، نابوت را خطاب کرده، گفت: «تاکستان خود را به من بده تا باغ سبزی کاری، برای من بشود زیرا نزدیک خانه من است، و به عوض آن تاکستانی نیکوتر از آن به تو خواهم داد، یا اگر درنظرت پسند آید قیمتش را نقره خواهم داد.» ۲ 2
Ahabu anawuza Naboti kuti, “Patse munda wako wa mpesa kuti ukhale munda wanga wa ndiwo zamasamba, popeza uli pafupi ndi nyumba yanga yaufumu. Mosinthana ndi mundawu ndidzakupatsa wina wabwino, kapena ngati ungafune, ndidzakupatsa ndalama pa mtengo wake wa mundawu.”
نابوت به اخاب گفت: «حاشا بر من از خداوندکه ارث اجداد خود را به تو بدهم.» ۳ 3
Koma Naboti anayankha Ahabu kuti, “Pali Yehova, sindingakupatseni cholowa cha makolo anga.”
پس اخاب به‌سبب سخنی که نابوت یزرعیلی به او گفته بود، پریشان حال و مغموم شده، به خانه خود رفت زیرا گفته بود ارث اجداد خود را به تو نخواهم داد. و بر بستر خود دراز شده، رویش را برگردانیدو طعام نخورد. ۴ 4
Pamenepo Ahabu anapita ku nyumba yake, wachisoni ndi wokwiya chifukwa Naboti wa ku Yezireeli anamuwuza kuti, “Sindidzakupatsani cholowa cha makolo anga.” Ahabu anakagona pa bedi lake atayangʼana kumbali ndipo anakana chakudya.
و زنش، ایزابل نزد وی آمده، وی را گفت: «روح تو چرا پریشان است که طعام نمی خوری؟» ۵ 5
Yezebeli mkazi wake analowa ndipo anamufunsa kuti, “Chifukwa chiyani mukuoneka achisoni? Chifukwa chiyani simukufuna chakudya?”
او وی را گفت: «از این جهت که نابوت یزرعیلی را خطاب کرده، گفتم: تاکستان خود را به نقره به من بده یا اگر بخواهی به عوض آن، تاکستان دیگری به تو خواهم داد، و او جواب داد که تاکستان خود را به تو نمی دهم.» ۶ 6
Ahabu anayankha mkazi wake kuti, “Chifukwa chake nʼchakuti ine ndinamuwuza Naboti wa ku Yezireeli kuti, ‘Gulitse munda wako wa mpesa kapena ngati ungakonde ine ndidzakupatsa munda wina wabwino mʼmalo mwake.’ Koma iye anandiyankha kuti, ‘Sindidzakupatsani munda wanga wa mpesa.’”
زنش ایزابل به او گفت: «آیا تو الان بر اسرائیل سلطنت می‌کنی؟ برخیز و غذا بخور و دلت خوش باشد. من تاکستان نابوت یزرعیلی را به تو خواهم داد.» ۷ 7
Ndipo Yezebeli mkazi wake anati, “Kodi umu ndi mmene mumachitira ngati mfumu ya Israeli? Dzukani, idyani! Sangalalani. Ine ndidzakutengerani munda wamphesa wa Naboti wa ku Yezireeli.”
آنگاه مکتوبی به اسم اخاب نوشته، آن را به مهر او مختوم ساخت و مکتوب را نزد مشایخ ونجبایی که با نابوت در شهرش ساکن بودند، فرستاد. ۸ 8
Choncho Yezebeli analemba makalata mʼdzina la Ahabu, nawadinda chidindo cha mfumu, nawatumiza makalatawo kwa akuluakulu ndi kwa anthu olemekezeka amene ankakhala ndi Naboti mu mzinda mwake.
و در مکتوب بدین مضمون نوشت: «به روزه اعلان کنید و نابوت را به صدر قوم بنشانید. ۹ 9
Mʼmakalatamo Yezebeli analemba kuti: “Lengezani kuti anthu asale chakudya ndipo muyike Naboti pa malo aulemu pakati pa anthu.
و دو نفر از بنی بلیعال را پیش او وا دارید که براو شهادت داده، بگویند که تو خدا و پادشاه را کفرگفته‌ای. پس او را بیرون کشیده، سنگسار کنید تابمیرد.» ۱۰ 10
Koma muyike anthu awiri oyipa mtima moyangʼanana naye ndipo iwo achitire umboni kuti watemberera Mulungu ndiponso mfumu. Ndipo mumutulutse ndi kumuponya miyala ndi kumupha.”
پس اهل شهرش، یعنی مشایخ ونجبایی که در شهر ساکن بودند، موافق پیغامی که ایزابل نزد ایشان فرستاده، و بر‌حسب مضمون مکتوبی که نزد ایشان ارسال کرده بود، به عمل آوردند. ۱۱ 11
Choncho akuluakulu ndi anthu olemekezeka amene ankakhala ndi Naboti mu mzinda mwake anachita monga analamulira Yezebeli mʼmakalata amene anawalembera.
و به روزه اعلان کرده، نابوت را درصدر قوم نشانیدند. ۱۲ 12
Iwo analengeza kuti anthu asale chakudya ndipo anayika Naboti pa malo aulemu pakati pa anthu.
و دو نفر از بنی بلیعال درآمده، پیش وی نشستند و آن مردان بلیعال به حضور قوم بر نابوت شهادت داده، گفتند که نابوت بر خدا و پادشاه کفر گفته است، و او را ازشهر بیرون کشیده، وی را سنگسار کردند تا بمرد. ۱۳ 13
Ndipo anthu awiri oyipa anabwera nakhala moyangʼanana naye ndipo anamunenera zoyipa Naboti pamaso pa anthu, ponena kuti, “Naboti watemberera Mulungu ndiponso mfumu.” Choncho anamutulutsira kunja kwa mzinda ndi kumuponya miyala ndi kumupha.
و نزد ایزابل فرستاده، گفتند که نابوت سنگسارشده و مرده است. ۱۴ 14
Atatero anatumiza mawu kwa Yezebeli akuti, “Naboti amuponya miyala ndipo wafa.”
و چون ایزابل شنید که نابوت سنگسارشده، و مرده است، ایزابل به اخاب گفت: «برخیزو تاکستان نابوت یزرعیل را که او نخواست آن رابه تو به نقره بدهد، متصرف شو، زیرا که نابوت زنده نیست بلکه مرده است.» ۱۵ 15
Yezebeli atangomva kuti Naboti amuponya miyala ndipo wafa, iye anakamuwuza Ahabu kuti, “Dzukani, katengeni munda wamphesa wa Naboti wa ku Yezireeli umene anawukaniza kukugulitsani. Naboti sali moyonso, koma wafa.”
و چون اخاب شنید که نابوت مرده است اخاب برخاسته، به جهت تصرف تاکستان نابوت یزرعیلی فرود آمد. ۱۶ 16
Ahabu atamva kuti Naboti wafa, ananyamuka kukatenga munda wamphesa wa Naboti.
و کلام خداوند نزد ایلیای تشبی نازل شده، گفت: ۱۷ 17
Ndipo Yehova anayankhula ndi Eliya wa ku Tisibe kuti,
«برخیز و برای ملاقات اخاب، پادشاه اسرائیل که در سامره است فرود شو اینک او در تاکستان نابوت است که به آنجا فرود شد تا آن رامتصرف شود. ۱۸ 18
“Nyamuka, pita ukakumane ndi Ahabu, mfumu ya Israeli amene amalamulira ku Samariya. Pano ali ku munda wamphesa wa Naboti kumene wapita kuti akatenge mundawo kuti ukhale wake.
و او را خطاب کرده، بگوخداوند چنین می‌گوید: آیا هم قتل نمودی و هم متصرف شدی؟ و باز او را خطاب کرده، بگوخداوند چنین می‌گوید: در جایی که سگان خون نابوت را لیسیدند سگان خون تو را نیز خواهندلیسید.» ۱۹ 19
Ukamuwuze kuti: ‘Yehova akuti, Kodi siwapha munthu ndi kumulandanso munda wake?’ Ndipo ukamuwuzenso kuti, ‘Yehova akuti, Pamalo pamene agalu ananyambita magazi a Naboti, pamalo pomwepo agalu adzanyambita magazi ako, inde, akonso!’”
اخاب به ایلیا گفت: «ای دشمن من، آیا مرایافتی؟» او جواب داد: «بلی تو را یافتم زیرا توخود را فروخته‌ای تا آنچه در نظر خداوند بداست، بجا آوری. ۲۰ 20
Ahabu anati kwa Eliya, “Tsono wandipeza, iwe mdani wanga!” Eliya anayankha kuti, “Inde ndakupezani chifukwa mwadzigulitsa kuti muchite zoyipa pamaso pa Yehova.
اینک من بر تو بلا آورده، تورا بالکل هلاک خواهم ساخت، و از اخاب هرمرد را خواه محبوس و خواه آزاد در اسرائیل منقطع خواهم ساخت. ۲۱ 21
Iye akuti ‘Taonani, ine ndidzabweretsa mavuto pa iwe. Ndidzawononga kotheratu zidzukulu zako ndi kuchotsa mu Israeli munthu aliyense wamwamuna wa banja la Ahabu, kapolo kapena mfulu.
و خاندان تو را مثل خاندان یربعام بن نباط و مانند خاندان بعشا ابن اخیا خواهم ساخت به‌سبب اینکه خشم مرا به هیجان آورده، و اسرائیل را مرتکب گناه ساخته‌ای.» ۲۲ 22
Ndidzawononga nyumba yako monga momwe ndinawonongera nyumba ya Yeroboamu mwana wa Nebati ndiponso ngati nyumba ya Baasa mwana wa Ahiya, chifukwa wandikwiyitsa Ine ndi kuchimwitsa Israeli.’
و درباره ایزابل نیز خداوند تکلم نموده، گفت: «سگان ایزابل را نزد حصار یزرعیل خواهند خورد. ۲۳ 23
“Ndipo kunena za Yezebeli, Yehova akuti, ‘Agalu adzadya Yezebeli mʼmbali mwa khoma la Yezireeli.’
هر‌که را از کسان اخاب درشهر بمیرد، سگان بخورند و هر‌که را در صحرابمیرد مرغان هوا بخورند.» ۲۴ 24
“Agalu adzadya munthu aliyense wa nyumba ya Ahabu amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame za mu mlengalenga zidzadya aliyense wofera ku thengo.”
و کسی نبود مثل اخاب که خویشتن رابرای بجا آوردن آنچه در نظر خداوند بد است فروخت، و زنش ایزابل او را اغوا نمود. ۲۵ 25
(Kunalibe munthu ngati Ahabu, amene anadzigulitsa kuchita zoyipa pamaso pa Yehova, amene anakopedwa ndi mkazi wake Yezebeli.
و درپیروی بتها رجاسات بسیار می‌نمود، برحسب آنچه اموریانی که خداوند ایشان را از حضوربنی‌اسرائیل اخراج نموده بود، می‌کردند. ۲۶ 26
Iye anachita zonyansa kwambiri popembedza mafano, monga mmene ankachitira Aamori amene Yehova anawachotsa pamene Aisraeli ankafika).
و چون اخاب این سخنان را شنید، جامه خود را چاک زده، پلاس در بر کرد و روزه گرفته، بر پلاس خوابید و به سکوت راه می‌رفت. ۲۷ 27
Ahabu atamva mawu amenewa, anangʼamba zovala zake, navala ziguduli ndi kusala chakudya. Anagona pa ziguduli, nayenda pangʼonopangʼono.
آنگاه کلام خداوند بر ایلیای تشبی نازل شده، گفت: ۲۸ 28
Pamenepo Yehova anayankhula ndi Eliya wa ku Tisibe kuti,
«آیا اخاب را دیدی چگونه به حضورمن متواضع شده است؟ پس از این جهت که درحضور من تواضع می‌نماید، این بلا را در ایام وی نمی آوردم، لیکن در ایام پسرش، این بلا را برخاندانش عارض خواهم گردانید.» ۲۹ 29
“Kodi waona mmene Ahabu wadzichepetsera pamaso panga? Chifukwa wadzichepetsa, sindidzabweretsa mavuto amenewa pa nthawi ya moyo wake, koma ndidzawabweretsa pa nyumba yake pa nthawi ya mwana wake.”

< اول پادشاهان 21 >