< Jobs 39 >

1 Steingeiti, veit du når ho kidar? Vaktar du riderne åt hindi?
“Kodi iwe umadziwa nthawi imene mbalale yayikazi imaswera? Kodi umaonerera pamene nswala ikubala?
2 Tel måna’rne dei gjeng med unge, og kjenner du deira fødetid?
Kodi umawerenga miyezi imene zimakhala ndi bere? Kodi nthawi imene zimaswana iwe umayidziwa?
3 Dei bøygjer seg, fø’r sine ungar, so er det slutt med deira rider.
Zimakhala tsonga ndi kuswa ana awo; pamenepo ululu wobereka nʼkutha.
4 På marki kidi veks seg store, spring burt og kjem’kje att til deim.
Ana a nyamazi amakhala ndi mphamvu ndipo amakulira mʼthengo; kenaka amachoka ndipo sabwereranso.
5 Kven let villasnet renna fritt, tok bandet av det skjerre dyr,
“Kodi bulu wakuthengo amamupatsa ndani ufulu wongodziyendera? Ndani amamasula zingwe zake?
6 som eg gav øydemark til heim, den salte steppa til ein bustad?
Ine ndinamupatsa chipululu kuti chikhale mudzi wake, nthaka ya mchere kuti ikhale malo ake okhalamo
7 Det lær åt byen med sitt ståk, slepp høyra skjenn frå drivaren.
Iye amakhala kutali ndi phokoso la mu mzinda; ndipo samva kufuwula kwa oyendetsa nyama zakatundu.
8 Det finn seg beite millom fjell, og leitar upp kvart grøne strå.
Amayendayenda mʼmapiri kudya msipu ndipo amafunafuna msipu uliwonse wobiriwira.
9 Skal tru villuksen vil deg tena, og natta yver ved di krubba?
“Kodi njati ingavomere kukutumikira? Kodi ingagone mu gome lako usiku?
10 Kann du til fori honom tøyma, horvar han dalar etter deg?
Kodi ungathe kuyimanga ndi zingwe kuti izilima? Kodi ingasalaze nthumbira mʼmunda mwako?
11 Lit du på honom for hans styrke? Og yverlet du han ditt arbeid?
Kodi ungadalire njatiyo chifukwa champhamvu zake? Kodi ungayilekere kuti igwire ntchito zako zolemetsa?
12 Trur du han til å føra grøda heim og draga henne inn i løda?
Kodi ungadalire kuti idzakubweretsera tirigu wako ndi kumuyika ku malo opunthira?
13 Struss-hoa flaksar kåt med vengen, men viser fjør og veng morskjærleik?
“Nthiwatiwa imakupiza mapiko ake monyadira, koma mapikowo sangafanane ndi mapiko ndi nthenga za kakowa.
14 Nei, ho legg sine egg på jordi, og let so sanden verma deim;
Nthiwatiwa imakwirira mazira ake pansi ndipo amafundidwa ndi nthaka,
15 ho gløymer at ein fot kann treda og villdyr trakka deim i kras.
nthiwatiwayo sidera nkhawa kuti mazira ake angathe kuswanyidwa, ndi kuti nyama zakuthengo zitha kuwaponda.
16 Hardt fer ho åt med sine ungar, som var dei ikkje hennar eigne; for fåfengt stræv ho ikkje ræddast.
Nthiwatiwa imachitira nkhanza ana ake ngati anawo si ake; Imayiwala zoti inavutika powabala.
17 For Gud let henne gløyma visdom, han ei tiletla henne vit.
Chifukwa Mulungu anayimana nzeru, simvetsa kanthu kalikonse.
18 Men når ho baskar seg i veg, ho lær åt både hest og mann.
Komatu nthiwatiwa ikadzambatuka ndi kuyamba kuthamanga, imamusiya kutali kavalo ndi wokwerapo wake.
19 Skal tru um du gjev hesten kraft og klæder halsen hans med mån?
“Kodi ndiwe amene umamupatsa mphamvu kavalo kapena kumuveka chenjerere mʼkhosi mwake?
20 Let du han som grashoppen springa alt med han frøser skræmeleg.
Kodi ndiwe amene umalipatsa dzombe ulemerero wolumphira, ukali wake nʼkumachititsa mantha?
21 Glad i si kraft han marki skrapar og fer so fram mot væpna flokk.
Iye amalumphalumpha moopseza, kukondwerera mphamvu zake, ndipo amapita ku nkhondo ndi mphamvu zake zonse.
22 Han urædd er og lær åt rædsla, for sverdet ei han vender um,
Iye sachita mantha, saopa chilichonse; sabwerera mʼmbuyo akaona lupanga.
23 det skranglar pilhus yver honom, det blenkjer spjot til styng og skot.
Zida zankhondo zimachita kwichikwichi mʼchimake pambali pake pamodzi ndi mkondo wonyezimira ndi nthungo.
24 Med ståk og bråk han slukar jordi, ustyrleg når stridsluren gjeng.
Kavaloyo amanjenjemera ndi ukali ndi kulumphalumpha; satha kungoyima pamene wamva kulira kwa lipenga.
25 Han kneggjar: «Hui!» når luren læt, han verar striden langan leid, med skrik frå hovdingar og herrop!
Lipenga likalira amati, ‘Twee!’ Amamva fungo la nkhondo ali patali, kufuwula kwa anthu olamulira nkhondo ndi mfuwu wankhondo.
26 Flyg hauken upp ved ditt forstand og spilar vengjerne mot sud?
“Kodi kabawi amawuluka ndi nzeru zako, ndi kutambasula mapiko ake kupita kummwera?
27 Stig ørnen høgt av di du byd, og byggjer reiret sitt i høgdi?
Kodi umalamulira chiwombankhanga ndiwe kuti chiziwuluka ndi kumanga chisa chake pamwamba penipeni?
28 Han bur på berg og held seg der, på kvasse tind og høge nut.
Chimakhala pa phiri ndipo chimakhala pamenepo usiku; chimakhala pa msonga penipeni pa mwala.
29 Derfrå han spæjar etter mat, hans augo yver viddi skodar.
Chili pamenepo chimayangʼanayangʼana choti chigwire kuti chidye; maso ake amachionera patali chinthucho.
30 Hans ungar gløypar i seg blod; der det finst lik, der er han og.»
Ana ake amayamwa magazi, ndipo kumene kuli mitembo ndiko chimapezeka.”

< Jobs 39 >