< Salmenes 35 >

1 Av David. Trett, Herre, med dem som tretter med mig! Strid mot dem som strider mot mig!
Salimo la Davide. Inu Yehova, mulimbane nawo amene akulimbana nane; mumenyane nawo amene akumenyana nane.
2 Grip skjold og verge og reis dig til hjelp for mig!
Tengani chishango ndi lihawo; dzukani ndipo bwerani mundithandize.
3 Dra spydet frem og steng veien for mine forfølgere! Si til min sjel: Jeg er din frelse!
Tengani mkondo ndi nthungo, kulimbana ndi iwo amene akundithamangitsa. Uzani moyo wanga kuti, “Ine ndine chipulumutso chako.”
4 La dem blues og bli til skamme som står mig efter livet! La dem vike tilbake med skam som tenker ondt imot mig!
Iwo amene akufunafuna moyo wanga anyozedwe ndi kuchita manyazi; iwo amene akukonza kuti moyo wanga uwonongeke abwerere mʼmbuyo mochititsa mantha.
5 La dem bli som agner for vinden, og Herrens engel støte dem bort!
Akhale ngati mankhusu owuluka ndi mphepo pamene mngelo wa Yehova akuwapirikitsa.
6 La deres vei bli mørk og glatt, og Herrens engel forfølge dem!
Njira yawo ikhale ya mdima ndi yoterera pamene mngelo wa Yehova akuwathamangitsa.
7 For uten årsak har de lønnlig gjort i stand sin garngrav for mig, uten årsak har de gravd en grav for mitt liv.
Popeza ananditchera ukonde popanda chifukwa ndipo popanda chifukwa andikumbira dzenje,
8 La ødeleggelse komme over ham, uten at han merker det, og la hans garn som han lønnlig har utlagt, fange ham, la ham falle i det til sin ødeleggelse!
chiwonongeko chiwapeza modzidzimutsa ukonde umene iwo abisa uwakole, agwere mʼdzenje kuti awonongedwe.
9 Da skal min sjel glede sig i Herren, fryde sig i hans frelse;
Pamenepo moyo wanga udzakondwera mwa Yehova ndi kusangalala ndi chipulumutso chake.
10 alle mine ben skal si: Herre, hvem er som du, du som frir den elendige fra den som er ham for sterk, og den elendige og fattige fra den som plyndrer ham?
Thupi langa lidzafuwula mokondwera, “Ndani angafanane nanu Yehova? Mumalanditsa osauka kwa amene ali ndi mphamvu zambiri, osauka ndi osowa kwa iwo amene amawalanda.”
11 Der opstår urettferdige vidner, de spør mig om det jeg ikke vet.
Mboni zopanda chisoni zinayimirira, zinandifunsa zinthu zimene sindikuzidziwa.
12 De gjengjelder mig godt med ondt; min sjel er forlatt.
Iwo anandibwezera zoyipa pa zabwino ndipo anasiya moyo wanga pa chisoni.
13 Og jeg, jeg klædde mig i sørgeklær, da de var syke; jeg plaget min sjel med faste, og min bønn vendte tilbake til min barm.
Koma pamene iwo ankadwala, ine ndinavala chiguduli ndi kudzichepetsa ndekha posala zakudya. Pamene mapemphero anga anabwerera kwa ine osayankhidwa,
14 Jeg gikk omkring, som om det var min venn, min bror; jeg gikk nedbøiet i sørgeklær som en som sørger over sin mor.
ndinayendayenda ndi kulira maliro, kumulira ngati bwenzi langa kapena mʼbale wanga. Ndinaweramitsa mutu wanga mosweka mtima kukhala ngati ndikulira amayi anga.
15 Men nu da jeg vakler, gleder de sig og flokker sig sammen; skarns-folk flokker sig om mig uten at jeg visste det; de sønderriver og hviler ikke.
Koma pamene ndinaphunthwa, iwo anasonkhana mosangalala; ondithira nkhondo anasonkhana kutsutsana nane, ineyo osadziwa. Iwo sanasiye kundiyankhulira mawu onyoza.
16 Som skamløse som spotter for et stykke brød, skjærer de tenner imot mig.
Monga anthu osapembedza, iwo anandinyoza mwachipongwe; anandikukutira mano awo.
17 Herre, hvor lenge vil du se til? Fri min sjel ut fra deres ødeleggelser, mitt eneste fra de unge løver.
Ambuye, mpaka liti mudzakhala mukungoyangʼana? Landitsani moyo wanga ku chiwonongeko chawo, moyo wanga wopambana ku mikango.
18 Jeg vil prise dig i en stor forsamling, love dig blandt meget folk.
Ndidzakuyamikani mu msonkhano waukulu; pakati pa gulu lalikulu la anthu ndidzakutamandani.
19 La ikke dem glede sig over mig, som uten grunn er mine fiender! La ikke dem som hater mig uten årsak, blinke med øiet!
Musalole adani anga onyenga akondwere chifukwa cha masautso anga; musalole kuti amene amadana nane popanda chifukwa andiyangʼane chamʼmbali mondinyoza.
20 For de taler ikke fred, men optenker svik mot de stille i landet.
Iwowo sayankhula mwamtendere, koma amaganizira zonamizira iwo amene amakhala mwabata mʼdziko.
21 Og de lukker sin munn vidt op imot mig, de sier: Ha, ha! Der ser vårt øie!
Iwo amandiseka mofuwula ndipo amati, “Haa! Haa! Ndipo ndi maso athuwa ife taziona.”
22 Du ser det, Herre, ti ikke! Herre, vær ikke langt borte fra mig!
Yehova mwaona zimenezi; musakhale chete. Ambuye musakhale kutali ndi ine.
23 Våkn op og bli våken for å gi mig rett, min Gud og Herre, for å føre min sak!
Dzukani, ndipo nyamukani kunditeteza! Mulimbane nawo chifukwa cha ine, Mulungu wanga ndi Ambuye anga.
24 Døm mig efter din rettferdighet, Herre min Gud, og la dem ikke glede sig over mig!
Onetsani kusalakwa kwanga mwa chilungamo chanu, Inu Yehova Mulungu wanga. Musalole kuti akondwere chifukwa cha mavuto anga.
25 La dem ikke si i sitt hjerte: Ha! Efter ønske! La dem ikke si: Vi har opslukt ham!
Musalole kuti aganize kuti, “Amati atani, zachitika monga momwe timafunira!” Kapena kunena kuti, “Tamutha ameneyu basi.”
26 La alle dem få skam og bli til skamme som gleder sig ved min ulykke! La dem som ophøier sig over mig, klæs i skam og skjensel!
Onse amene amakondwera ndi masautso anga achite manyazi ndi kusokonezeka. Onse amene amadzikweza kufuna kundipambana, avekedwe manyazi ndi mnyozo ngati zovala.
27 La dem juble og glede sig som unner mig min rett, og la dem alltid si: Høilovet være Herren, som unner sin tjener at det går ham vel!
Koma amene amakondwera chifukwa chakuti ndine wosalakwa, afuwule mwachimwemwe ndi chisangalalo. Nthawi zonse azinena kuti, “Yehova akwezeke, Iye amene amakondwera ndi kupeza bwino kwa mtumiki wake.”
28 Da skal min tunge synge om din rettferdighet, hele dagen om din pris.
Pakamwa panga padzayankhula za chilungamo chanu ndi za matamando anu tsiku lonse.

< Salmenes 35 >