< Salmenes 25 >

1 Av David. Til dig, Herre, løfter jeg min sjel.
Salimo la Davide. Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
2 Min Gud, til dig har jeg satt min lit; la mig ikke bli til skamme, la ikke mine fiender fryde sig over mig!
Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
3 Ja, ingen av dem som bier på dig, skal bli til skamme; de skal bli til skamme som er troløse uten årsak.
Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
4 Herre, la mig kjenne dine veier, lær mig dine stier!
Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
5 Led mig frem i din trofasthet og lær mig! for du er min frelses Gud, på dig bier jeg hele dagen.
tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
6 Herre, kom din barmhjertighet i hu og din miskunnhets gjerninger! for de er fra evighet.
Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
7 Kom ikke min ungdoms synder og mine misgjerninger i hu! Kom mig i hu efter din miskunnhet for din godhets skyld, Herre!
Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
8 Herren er god og rettvis; derfor lærer han syndere veien.
Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
9 Han leder de saktmodige i det som rett er, og lærer de saktmodige sin vei.
Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
10 Alle Herrens stier er miskunnhet og trofasthet imot dem som holder hans pakt og hans vidnesbyrd.
Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
11 For ditt navns skyld, Herre, forlat mig min misgjerning! for den er stor.
Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
12 Hvem er den mann som frykter Herren? Ham lærer han den vei han skal velge.
Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
13 Hans sjel skal stadig ha det godt, og hans avkom skal arve landet.
Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
14 Herren har fortrolig samfund med dem som frykter ham, og hans pakt skal bli dem kunngjort.
Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
15 Mine øine er alltid vendt til Herren, for han drar mine føtter ut av garnet.
Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
16 Vend dig til mig og vær mig nådig! for jeg er enslig og elendig.
Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
17 Mitt hjertes angst har de gjort stor; før mig ut av mine trengsler!
Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
18 Se min elendighet og min nød, og forlat mig alle mine synder!
Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
19 Se mine fiender, de er mange, og de hater mig med urettferdig hat.
Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
20 Bevar min sjel og redd mig, la mig ikke bli til skamme! for jeg tar min tilflukt til dig.
Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
21 La uskyld og opriktighet verge mig! for jeg bier på dig.
Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
22 Forløs, Gud, Israel av alle dets trengsler!
Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!

< Salmenes 25 >