< Salmenes 17 >

1 En bønn av David. Hør, Herre, på rettferdighet, merk på mitt klagerop, vend øret til min bønn fra leber uten svik!
Pemphero la Davide. Imvani Inu Yehova pempho langa lachilungamo; mverani kulira kwanga. Tcherani khutu kuti mumve pemphero langa popeza silikuchokera pakamwa pachinyengo.
2 La min rett gå ut fra ditt åsyn, dine øine skue hvad rett er!
Kusalakwa kwanga kuchokera kwa inu; maso anu aone chimene ndi cholungama.
3 Du har prøvd mitt hjerte, gjestet det om natten, du har ransaket mig, du fant intet; min munn viker ikke av fra mine tanker.
Ngakhale Inu mutafufuza mtima wanga ndi kundisanthula usiku, ngakhale mutandiyesa, simudzapeza kanthu; Ine ndatsimikiza kuti pakamwa panga sipadzachimwa.
4 Mot menneskenes gjerninger har jeg efter dine lebers ord tatt mig i vare for voldsmannens stier.
Kunena za ntchito za anthu, monga mwa mawu a pakamwa panu, Ine ndadzisunga ndekha posatsata njira zachiwawa.
5 Mine skritt holdt fast ved dine fotspor, mine trin vaklet ikke.
Mayendedwe anga akhazikika pa njira zanu; mapazi anga sanaterereke.
6 Jeg roper til dig, for du svarer mig, Gud! Bøi ditt øre til mig, hør mitt ord!
Ine ndikuyitana Inu, Mulungu wanga, pakuti mudzandiyankha; tcherani khutu lanu kwa ine ndipo mumve pemphero langa.
7 Vis din miskunnhet i underfulle gjerninger, du som med din høire hånd frelser dem som flyr til dig, fra deres motstandere!
Onetsani kudabwitsa kwa chikondi chanu chachikulu, Inu amene mumapulumutsa ndi dzanja lanu lamanja iwo amene amathawira kwa inu kuchoka kwa adani awo.
8 Vokt mig som din øiesten, skjul under dine vingers skygge
Mundisunge ine ngati mwanadiso; mundibise mu mthunzi wa mapiko anu,
9 for de ugudelige, som ødelegger mig, mine dødsfiender, som omringer mig!
kuchoka kwa oyipa amene amandizinga ine, kuchoka kwa anthu amene ndi adani anga, amene andizungulira ine.
10 Sitt fete hjerte lukker de til, med sin munn taler de overmodig.
Iwo amatseka mitima yawo yopanda chifundo, ndi pakamwa pawo amayankhula modzitamandira.
11 Hvor vi går, kringsetter de mig nu; sine øine retter de på å felle mig til jorden.
Andisaka, tsopano andizungulira ndi maso awo atcheru, kuti andigwetse pansi.
12 Han er lik en løve som stunder efter å sønderrive, og en ung løve som ligger på lønnlige steder.
Iwo ali ngati mkango wofuna nyama; ngati mkango waukulu wokhala mobisala.
13 Reis dig, Herre, tred ham i møte, slå ham ned, frels min sjel fra den ugudelige med ditt sverd,
Dzukani Yehova, mulimbane nawo ndipo muwagwetse pansi; landitseni kuchoka kwa oyipa ndi lupanga lanu.
14 fra menneskene med din hånd, Herre, fra denne verdens mennesker, som har sin del i livet, og hvis buk du fyller med dine skatter, som er rike på sønner og efterlater sin overflod til sine barn.
Inu Yehova, pulumutseni ndi dzanja lanu kwa anthu otere, kwa anthu a dziko lino amene mphotho yawo ili mʼmoyo uno. Inu mumaletsa njala kwa amene asangalatsidwa nanu; ana awo aamuna ali ndi zinthu zambiri, ndipo iwo amasunga chuma cha ana awo.
15 Jeg skal i rettferdighet skue ditt åsyn, jeg skal, når jeg våkner, mettes ved din skikkelse.
Ndipo ine mʼchilungamo ndidzaona nkhope yanu; pamene ndidzadzuka, ndidzakondwera kwambiri poonana nanu.

< Salmenes 17 >