< Salmenes 113 >

1 Halleluja! Lov, I Herrens tjenere, lov Herrens navn!
Tamandani Yehova. Mutamandeni, inu atumiki a Yehova, tamandani dzina la Yehova.
2 Herrens navn være lovet fra nu av og inntil evig tid!
Yehova atamandidwe, kuyambira tsopano mpaka muyaya.
3 Fra solens opgang til dens nedgang er Herrens navn høilovet.
Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake, dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.
4 Herren er ophøiet over alle hedninger, hans ære er over himmelen.
Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse, ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.
5 Hvem er som Herren vår Gud, han som troner så høit,
Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu, Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?
6 som ser så dypt ned, i himmelen og på jorden,
amene amawerama pansi kuyangʼana miyamba ndi dziko lapansi?
7 som reiser den ringe av støvet, ophøier den fattige av skarnet
Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;
8 for å sette ham hos fyrster, hos sitt folks fyrster,
amawakhazika pamodzi ndi mafumu, pamodzi ndi mafumu a anthu ake.
9 han som lar den ufruktbare hustru bo som glad barnemor! Halleluja!
Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake monga mayi wa ana wosangalala. Tamandani Yehova.

< Salmenes 113 >