< 4 Mosebok 28 >

1 Og Herren talte til Moses og sa:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Byd Israels barn og si til dem: Mitt offer, min mat, mine ildoffer, som er til velbehagelig duft for mig, skal I akte på å bære frem for mig til fastsatt tid.
“Lamula Aisraeli kuti, ‘Onetsetsani kuti mukupereka kwa Ine pa nthawi yoyikika, chopereka cha chakudya chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Ine.’
3 Og du skal si til dem: Dette er det ildoffer som I skal bære frem for Herren: hver dag to årsgamle lam uten lyte til et stadig brennoffer.
Awuze kuti, ‘Nsembe ya chakudya imene muzipereka pa moto kwa Yehova tsiku ndi tsiku ndi iyi: Ana ankhosa a chaka chimodzi awiri, wopanda chilema.
4 Det ene lam skal du ofre om morgenen, og det andre skal du ofre mellem de to aftenstunder,
Mmawa muzipereka mwana wankhosa mmodzi ndipo winayo madzulo.
5 og som matoffer tiendedelen av en efa fint mel blandet med fjerdedelen av en hin olje av støtte oliven.
Muziperekanso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi lita imodzi ya mafuta a olivi.
6 Dette er det stadige brennoffer, det samme som blev ofret ved Sinai berg til en velbehagelig duft, et ildoffer for Herren.
Iyi ndi nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku imene analamula pa phiri la Sinai kuti ikhale fungo lokoma, nsembe yopsereza pa moto yopereka kwa Yehova.
7 Og drikkofferet som hører til det første lam, skal være fjerdedelen av en hin; i helligdommen skal du ofre drikkoffer av sterk drikk til Herren.
Chopereka chachakumwa chikhale lita imodzi yachakumwa chaukali pa nkhosa iliyonse. Muzithira pamalo opatulika, kupereka kwa Yehova.
8 Det andre lam skal du ofre mellem de to aftenstunder; med det samme matoffer som om morgenen og med det samme drikkoffer skal du ofre det; det er et ildoffer til en velbehagelig duft for Herren.
Muzipereka mwana wankhosa winayo madzulo, pamodzi ndi chopereka chachakudya monga poyamba paja ndi chopereka chachakumwa monga mmawa. Ichi ndi chopereka chachakudya, fungo lokoma kwa Yehova.’”
9 På sabbatsdagen skal du ofre to årsgamle lam uten lyte og som matoffer to tiendedeler av en efa fint mel blandet med olje, og drikkofferet som hører til.
“‘Pa tsiku la Sabata, muzipereka nsembe ana ankhosa awiri a chaka chimodzi wopanda chilema, pamodzi ndi chopereka chachakumwa ndi chopereka chachakudya chokwana makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta.
10 Dette er sabbats-brennofferet, som skal bæres frem hver sabbat, foruten det stadige brennoffer med tilhørende drikkoffer.
Iyi ndi nsembe yopsereza ya pa Sabata iliyonse, kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake chachakumwa.’”
11 Den første dag i hver måned skal I ofre Herren et brennoffer: to unge okser og en vær og syv årsgamle lam uten lyte,
“Pa tsiku loyamba la mwezi uliwonse muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, onse wopanda chilema.
12 og til matoffer tre tiendedeler av en efa fint mel blandet med olje for hver okse, og til væren to tiendedeler fint mel blandet med olje
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; ndi nkhosa yayimuna, chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta;
13 og en tiendedel fint mel blandet med olje for hvert lam; da er det et brennoffer til en velbehagelig duft, et ildoffer for Herren;
ndipo pa mwana wankhosa aliyense, chopereka cha ufa wa kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, izi ndi za nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yotentha pa moto ya kwa Yehova.
14 og drikkofferne som hører til, skal være en halv hin vin for hver okse og tredjedelen av en hin til væren og fjerdedelen av en hin for hvert lam. Dette er måneds-brennofferet, som skal bæres frem hver nymånedag i året.
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakumwa cha malita awiri a vinyo; ndipo pa nkhosa yayimuna, lita limodzi ndi theka, ndipo pa mwana wankhosa, lita limodzi. Iyi ndi nsembe yopsereza ya mwezi ndi mwezi yoperekedwa pa mwezi watsopano mʼkati mwa chaka.
15 Der skal også ofres en gjetebukk som syndoffer til Herren, foruten det stadige brennoffer med tilhørende drikkoffer.
Powonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake cha chakumwa, mbuzi yayimuna imodzi iperekedwe kwa Yehova ngati nsembe yopepesera machimo.
16 I den første måned, på den fjortende dag i måneden, er det påske for Herren.
“‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita Paska wa Yehova.
17 Og på den femtende dag i samme måned er det høitid; i syv dager skal der etes usyret brød.
Pa tsiku la 15 la mwezi womwewo pazikhala chikondwerero. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.
18 På den første dag skal det være en hellig sammenkomst; I skal ikke gjøre nogen arbeidsgjerning.
Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
19 Og I skal ofre et ildoffer, et brennoffer for Herren: to unge okser og en vær og syv årsgamle lam - uten lyte skal de være -
Koma muzipereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri aamuna a chaka chimodzi, onsewo wopanda chilema.
20 og som tilhørende matoffer fint mel blandet med olje; tre tiendedeler av en efa skal I ofre for hver okse og til væren to tiendedeler,
Pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; makilogalamu awiri pa nkhosa yayimuna iliyonse.
21 og en tiendedel for hvert av de syv lam,
Kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa asanu ndi awiri aja.
22 og en gjetebukk som syndoffer, til å gjøre soning for eder.
Muziphatikizapo mbuzi yayimuna monga nsembe yopepesera machimo anu.
23 Dette skal I ofre foruten morgen-brennofferet, som hører til det stadige brennoffer.
Muzikonza zimenezi nthawi zonse, powonjezera pa nsembe yopsereza ya mmawa.
24 Sådanne offer skal I ofre hver dag i syv dager; det er ildoffermat til en velbehagelig duft for Herren; foruten det stadige brennoffer med tilhørende drikkoffer skal det ofres.
Motere muzikonza chakudya cha nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pa masiku asanu ndi awiri ngati fungo lokomera Yehova. Zimenezi ziziperekedwa kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse pamodzi ndi nsembe yachakumwa.
25 Og på den syvende dag skal I holde en hellig sammenkomst; I skal ikke gjøre nogen arbeidsgjerning.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
26 På førstegrødens dag, når I bærer frem for Herren et offer av den nye grøde, på ukenes høitid, skal I holde en hellig sammenkomst; I skal ikke gjøre nogen arbeidsgjerning.
“‘Pa tsiku la zipatso zoyambirira kucha, pamene mukupereka chopereka cha chakudya chatsopano kwa Yehova, pa nthawi ya chikondwerero cha Masabata, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa.
27 Og I skal ofre et brennoffer til en velbehagelig duft for Herren: to unge okser og en vær og syv årsgamle lam,
Muzipereka nsembe zopsereza za ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa imodzi yayimuna ndi ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi monga fungo lokomera Yehova.
28 og som tilhørende matoffer fint mel blandet med olje, tre tiendedeler av en efa for hver okse og til væren to tiendedeler,
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pazikhala chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri.
29 og en tiendedel for hvert av de syv lam,
Ndipo pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja, kilogalamu imodzi.
30 og en gjetebukk til å gjøre soning for eder.
Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
31 Foruten det stadige brennoffer med tilhørende matoffer skal I ofre disse offer - uten lyte skal de være - med tilhørende drikkoffer.
Muzipereka zimenezi pamodzi ndi zopereka za zakumwa ndi nsembe yake ya chakudya. Onetsetsani kuti nyamazo zilibe chilema.

< 4 Mosebok 28 >