< Nehemias 3 >

1 Ypperstepresten Eljasib og hans brødre og prestene gjorde sig rede og bygget Fåreporten; de helliget den og satte inn dørene; så bygget de videre til Mea-tårnet, som de helliget, og videre frem til Hananel-tårnet.
Pambuyo pake Eliyasibu mkulu wa ansembe ndi ansembe anzake anayamba kugwira ntchito ndipo anamanganso Chipata cha Nkhosa. Iwo anachipatulira Mulungu ndipo anayika zitseko zake. Khoma limene analipatula linafika mpaka pa Nsanja ya Zana ndi Nsanja ya Hananeli.
2 Ved siden av dem bygget mennene fra Jeriko og ved siden av dem Sakkur, Imris sønn.
Anthu a ku Yeriko anamanga chigawo china pambali pake ndipo Zakuri mwana wa Imuri anamanga chigawo chinanso choyandikana nawo.
3 Fiskeporten blev bygget av Sena'as barn; de tømret den op og satte inn dører, låser og slåer.
Chipata cha Nsomba chinamangidwanso ndi ana a fuko la Hasena. Iwo anayika mitanda yake ndi zitseko, zotsekera zake, ndi mipiringidzo yake.
4 Ved siden av dem arbeidet Meremot, sønn av Uria, Hakkos' sønn, ved siden av ham Mesullam, sønn av Berekja, Mesesabels sønn, og ved siden av ham Sadok, Ba'anas sønn.
Meremoti mwana wa Uriya, mwana wa Hakozi, anakonza chigawo choyandikana nacho. Motsatana naye, Mesulamu mwana wa Berekiya, mwana wa Mesezabeli anakonza chigawo china. Pambali pake, Zadoki mwana wa Baana anakonzanso chigawo china.
5 Ved siden av ham arbeidet folkene fra Tekoa; men de fornemme blandt dem bøide ikke sin nakke under arbeidet for sin Herre.
Pambali pa iwowa anthu a ku Tekowa anakonza chigawo china. Koma wolemekezeka awo anakana kugwira ntchito imene akuluakulu awo anawapatsa.
6 Den gamle port blev satt i stand av Jojada, Paseahs sønn, og Mesullam, Besodjas sønn; de tømret den op og satte inn dører og låser og slåer.
Chipata cha Yesana chinakonzedwa ndi Yoyada mwana wa Paseya ndi Mesulamu mwana wa Besodeya. Iwo anayika mitanda yake ndi kuyika zitseko, zotsekera zake ndi mipiringidzo yake.
7 Ved siden av dem arbeidet gibeonitten Melatja og meronotitten Jadon med mennene fra Gibeon og Mispa, som hørte under stattholderens domstol hinsides elven.
Pambali pawo Melatiya Mgibeyoni ndi Yadoni Mmerenoti ndiponso anthu a ku Gibiyoni ndi a ku Mizipa anakonza chigawo chawo mpaka ku nyumba ya bwanamkubwa wa chigawo cha Patsidya pa Yufurate.
8 Ved siden av dem arbeidet Ussiel, Harhajas sønn, en gullsmed, og ved siden av ham Hananja, en av salvelagerne. Det næste stykke av Jerusalems mur lot de være like til den brede mur.
Pambali pawo Uzieli mwana wa Harihaya wa mʼgulu amisiri osula golide anakonzanso chigawo china. Pambali pake Hananiya mmodzi mwa anthu oyenga mafuta onunkhira, anakonzanso chigawo china. Iwo anakonzanso Yerusalemu mpaka ku Khoma Lotambasuka.
9 Ved siden av dem arbeidet Refaja, Hurs sønn, høvdingen over den ene halvdel av Jerusalems distrikt.
Refaya mwana wa Huri wolamulira theka la chigawo cha Yerusalemu anakonza chigawo china motsatana nawo.
10 Ved siden av ham arbeidet Jedaja, Harumafs sønn, midt imot sitt eget hus, og ved siden av ham Hattus, Hasabnejas sønn.
Kulumikiza ichi, Yedaya mwana wa Harumafi anakonza chigawo choyangʼanana ndi nyumba yake, ndipo Hatusi mwana wa Hasabaneya anakonzanso motsatana naye.
11 Et annet stykke blev satt i stand av Malkia, Harims sønn, og Hassub, Pahat-Moabs sønn, og dessuten Ovnstårnet.
Malikiya mwana wa Harimu ndi Hasubu mwana wa Pahati-Mowabu anakonzanso chigawo china ndiponso Nsanja ya Ngʼanjo.
12 Ved siden av ham arbeidet Sallum, sønn av Hallohes, høvdingen over den andre halvdel av Jerusalems distrikt, og sammen med ham hans døtre.
Salumu mwana wa Halohesi wolamulira theka la chigawo cha Yerusalemu, anakonzanso chigawo chotsatana nawo mothandizidwa ndi ana ake akazi.
13 Dalporten blev satt i stand av Hanun og innbyggerne i Sanoah; de bygget den og satte inn dører, låser og slåer; de bygget også tusen alen av muren, til Møkkporten.
Chipata cha ku chigwa chinakonzedwa ndi Hanuni ndi anthu okhala ku Zanowa. Iwo anachimanganso ndi kuyika zitseko zake ndi zotsekera ndi mipiringidzo yake. Iwo anakonzanso khoma lotalika mamita 450 mpaka ku Chipata cha Zinyalala.
14 Og Møkkporten blev satt i stand av Malkia, Rekabs sønn, høvdingen over Bet-Hakkerems distrikt; han bygget den op og satte inn dører og låser og slåer.
Chipata cha Zinyalala chinakonzedwa ndi Malikiya mwana wa Rekabu, wolamulira chigawo cha Beti-Hakeremu. Iye anachimanganso ndi kuyika zitseko zake, zotsekera zake ndi mipiringidzo.
15 Kildeporten blev satt i stand av Sallun, Kol-Hoses sønn, høvdingen over Mispas distrikt; han bygget den, la tak på den og satte inn dører, låser og slåer; likeledes bygget han muren ved Selah-dammen ved kongens have helt frem til de trapper som går ned fra Davids stad.
Chipata cha Kasupe chinakonzedwa ndi Saluni mwana wa Koli-Hoze, wolamulira chigawo cha Mizipa. Iye anachimanganso ndi kuyikanso denga ndiponso zitseko, zotsekera ndi mipiringidzo yake. Iye anakonzanso khoma la Dziwe la Siloamu limene lili pafupi ndi munda wa mfumu mpaka ku makwerero otsikira potuluka mzinda wa Davide.
16 Efter ham arbeidet Nehemias, Asbuks sønn, høvdingen over den ene halvdel av Betsurs distrikt, til midt imot Davids graver og til den gravde dam og til heltenes hus.
Pambali pa iyeyo, Nehemiya mwana wa Azibuki, wolamulira theka la chigawo cha Beti Zuri anakonza chigawo china mpaka kumalo oyangʼanana ndi manda a Davide, mpaka ku dziwe lokumba ndi ku nyumba ya anthu ankhondo.
17 Efter ham arbeidet levittene under Rehum, Banis sønn; ved siden av ham arbeidet Hasabja, høvdingen over den ene halvdel av Ke'ilas distrikt, for sitt distrikt.
Pambali pake Alevi anakonza chigawo china, ndipo mtsogoleri wawo anali Rehumi mwana wa Bani. Pambali pa iye Hasabiya wolamulira theka la chigawo cha Keyila anagwira ntchito ku chigawo chake.
18 Efter ham arbeidet deres brødre under Bavvai, Henadads sønn, høvdingen over den andre halvdel av Ke'ilas distrikt.
Pambuyo pa iyeyu abale awo anapitiriza kukonza, ndipo mtsogoleri wawo anali Bawai mwana wa Henadadi, wolamulira theka lina la chigawo cha Keyila.
19 Ved siden av ham arbeidet Eser, Josvas sønn, høvdingen over Mispa, på et annet stykke, fra plassen midt imot opgangen til våbenhuset i Vinkelen.
Motsatana naye Ezeri mwana wa Yesuwa, wolamulira Mizipa anakonza chigawo chinanso choyangʼanana ndi chikweza chofikira ku nyumba yosungira zida za nkhondo pa ngodya.
20 Efter ham arbeidet Baruk, Sabbais sønn, med stor iver på et annet stykke, fra Vinkelen og til døren på ypperstepresten Eljasibs hus.
Motsatana naye, Baruki mwana wa Zakai anakonzanso chigawo china kuchokera pa ngodya mpaka pa chitseko cha nyumba ya Eliyasibu mkulu wa ansembe.
21 Efter ham arbeidet Meremot, sønn av Uria, Hakkos' sønn, på et annet stykke, fra døren på Eljasibs hus og til enden av hans hus.
Motsatana naye, Meremoti mwana wa Uriya, mwana wa Hakozi anakonzanso chigawo china kuchokera ku chitseko cha nyumba ya Eliyasibu mpaka kumapeto kwake.
22 Efter ham arbeidet prestene, mennene fra Jordan-sletten.
Pambuyo pake ansembe okhala ku chidikha anakonzanso chigawo china.
23 Efter dem arbeidet Benjamin og Hasub midt imot sitt eget hus; efter dem arbeidet Asarja, sønn av Ma'aseja, Ananjas sønn, ved siden av sitt hus.
Pambuyo pawo, Benjamini ndi Hasubu anakonza kutsogolo kwa nyumba zawo. Ndipo motsatana nawo, Azariya mwana wa Maaseya mwana wa Ananiya, anakonza chigawo choyangʼanana ndi nyumba zawo.
24 Efter ham arbeidet Binnui, Henadads sønn, på et annet stykke, fra Asarjas hus til Vinkelen og til det sted hvor muren bøier av.
Motsatana naye, Binuyi mwana wa Henadadi anakonzanso chigawo china, kuchokera pa nyumba ya Azariya kukafika potsirizira pa ngodya.
25 Palal, Usais sønn, arbeidet fra stedet midt imot Vinkelen og det tårn som springer frem fra kongens øvre hus ved fengselsgården; efter ham arbeidet Pedaja, Paros' sønn.
Palali mwana Uzai anakonza chigawo china choyangʼanana ndi ngodya ndi nsanja yotuluka pa nyumba yapamwamba ya mfumu ku bwalo la alonda. Motsatana naye, Pedaya mwana wa Parosi,
26 - Tempeltjenerne bodde på Ofel, til plassen midt imot Vannporten mot øst og det fremspringende tårn -.
ndi otumikira mʼNyumba ya Mulungu amene amakhala pa khoma la Ofeli anakonza chigawo china mpaka pa malo oyangʼanana ndi Chipata cha Madzi kuloza kummawa ndiponso nsanja yayitali ija.
27 Efter ham arbeidet folkene fra Tekoa på et annet stykke, fra plassen midt imot det store fremspringende tårn og til Ofel-muren.
Motsatana nawo, anthu a ku Tekowa anakonzanso chigawo china choyangʼanana ndi nsanja ija yayikulu ndi yayitali mpaka ku khoma la Ofeli.
28 Ovenfor Hesteporten arbeidet prestene, hver av dem midt imot sitt eget hus.
Kuyambira ku Chipata cha Akavalo anakonza ndi ansembe ena ndipo aliyense amakonza khoma loyangʼanana ndi nyumba yake.
29 Efter dem arbeidet Sadok, Immers sønn, midt imot sitt eget hus, og efter ham Semaja, Sekanjas sønn, som hadde vaktholdet ved den østre port.
Motsatana nawo, Zadoki mwana wa Imeri anakonza chigawo china choyangʼanana ndi nyumba yake. Motsatana naye, Semeya mwana wa Sekaniya, mlonda wa Chipata cha Kummawa, anakonzanso khoma.
30 Efter ham arbeidet Hananja, Selemjas sønn, og Hanun, Salafs sjette sønn, på et annet stykke, og efter dem Mesullam, Berekjas sønn, midt imot sitt kammer.
Hananiya mwana wa Selemiya ndiponso Hanuni mwana wachisanu ndi chimodzi wa Zalafi anakonza chigawo china. Motsatana naye, Mesulamu mwana wa Berekiya anakonza chigawo choyangʼanana ndi chipinda chake.
31 Efter ham arbeidet Malkia, en av gullsmedene, frem til tempeltjenernes og kremmernes hus, midt imot Mønstringsporten og frem til Hjørnesalen.
Motsatana naye, Malikiya mmodzi mwa amisiri a golide anakonza chigawo china mpaka ku nyumba ya atumiki a ku Nyumba ya Mulungu ndiponso ku nyumba ya anthu amalonda moyangʼanana ndi chipata cha Mifikade ndiponso mpaka pa chipinda chapamwamba chapangodya.
32 Og mellem Hjørnesalen og Fåreporten arbeidet gullsmedene og kremmerne.
Ndipo pakati pa chipinda chapamwamba chapangodya ndi Chipata cha Nkhosa anakonza ndi amisiri a golide ndi anthu amalonda.

< Nehemias 3 >