< Matteus 10 >

1 Og han kalte sine tolv disipler til sig og gav dem makt over urene ånder, til å drive dem ut, og til å helbrede all sykdom og all skrøpelighet.
Yesu anayitana ophunzira ake khumi ndi awiri ndipo anawapatsa ulamuliro otulutsa mizimu yoyipa ndi kuchiritsa nthenda iliyonse ndi zofowoka zilizonse.
2 Men dette er de tolv apostlers navn: Først Simon, som kalles Peter, og Andreas, hans bror; Jakob, Sebedeus' sønn, og Johannes, hans bror;
Mayina a atumwi khumi ndi awiriwo ndi awa: woyamba, Simoni (wotchedwa Petro) ndi mʼbale wake Andreya; Yakobo mwana wa Zebedayo ndi mʼbale wake Yohane,
3 Filip og Bartolomeus; Tomas og Matteus, tolderen; Jakob, Alfeus' sønn, og Lebbeus med tilnavnet Taddeus;
Filipo ndi Bartumeyu, Tomasi ndi Mateyu wolandira msonkho, Yakobo mwana wa Alufeyo ndi Tadeyo;
4 Simon Kananeus og Judas Iskariot, han som forrådte ham.
Simoni Mzerote ndi Yudasi Isikarioti, amene anamupereka Iye.
5 Disse tolv sendte Jesus ut og bød dem: Gå ikke ut på veien til hedningene, og gå ikke inn i nogen av samaritanenes byer,
Yesu anatuma khumi ndi awiriwo ndi kuwalamula kuti, “Musapite kwa anthu a mitundu ina kapena kulowa mʼmudzi uliwonse wa Asamariya.
6 men gå heller til de fortapte får av Israels hus!
Koma pitani kwa nkhosa zotayika za banja la Israeli.
7 Og når I går avsted, da forkynn dette budskap: Himlenes rike er kommet nær!
Pamene mukupita, muzikalalikira uthenga uwu: ‘Ufumu wakumwamba wayandikira.’
8 Helbred syke, opvekk døde, rens spedalske, driv ut onde ånder! For intet har I fått det, for intet skal I gi det.
Chiritsani odwala, ukitsani akufa, chiritsani akhate, tulutsani ziwanda. Munalandira kwaulere, perekani kwaulere.
9 I skal ikke ta gull eller sølv eller kobber med i eders belter,
“Musatenge ndalama zagolide kapena zasiliva kapena zakopala mʼzikwama mwanu;
10 ikke skreppe til reisen, ikke to kjortler, ikke sko, ikke stav; for arbeideren er sin føde verd.
musatenge thumba la paulendo, kapena malaya awiri kapena nsapato kapena ndodo; pakuti wantchito ayenera kulandira chakudya chake.
11 Og hvor I kommer inn i en by eller landsby, der skal I spørre efter hvem som er det verd i den by; og bli hos ham til I drar bort derfra!
Mukalowa mu mzinda ndi mʼmudzi uliwonse, funafunani munthu woyenera ndipo mukhale mʼnyumba mwake kufikira mutachoka.
12 Og når I kommer inn i et hus, da skal I hilse det;
Pamene mulowa mʼnyumba mupereke moni.
13 og dersom huset er det verd, da komme eders fred over det; men dersom det ikke er det verd, da vende eders fred tilbake til eder!
Mtendere wanu ukhale pa a mʼnyumbayo ngati ndi oyenera. Koma ngati siwoyenera, mtendere wanu ubwerere kwa inu.
14 Og om nogen ikke tar imot eder og ikke hører på eders ord, da gå ut av det hus eller den by, og ryst støvet av eders føtter!
Ngati wina aliyense sakakulandirani kapena sakamvera mawu anu, musase fumbi la kumapazi anu pamene mutuluka mʼnyumbayo kapena mu mzindawo.
15 Sannelig sier jeg eder: Det skal gå Sodomas og Gomorras land tåleligere på dommens dag enn den by.
Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti pa tsiku lachiweruziro, mlandu wa Sodomu ndi Gomora udzachepa kusiyana ndi wa mzindawo.
16 Se, jeg sender eder som får midt iblandt ulver; vær derfor kloke som slanger og enfoldige som duer!
“Taonani ndikukutumizani inu monga nkhosa pakati pa mimbulu. Chifukwa chake khalani ochenjera ngati njoka ndi woona mtima ngati nkhunda.
17 Men vokt eder for menneskene! for de skal overgi eder til domstolene og hudstryke eder i sine synagoger;
Chenjerani ndi anthu pakuti adzakuperekani ku mabwalo amilandu nadzakukwapulani mʼmasunagoge mwawo.
18 og I skal føres frem for landshøvdinger og konger for min skyld, til vidnesbyrd for dem og for hedningene.
Chifukwa cha Ine, mudzaperekedwa kwa olamulira ndi kwa mafumu kuti mukhale mboni kwa iwo ndi kwa a mitundu ina.
19 Men når de overgir eder, da vær ikke bekymret for hvorledes eller hvad I skal tale; for det skal gis eder i samme stund hvad I skal tale.
Koma pamene akumangani, inu musadandaule kuti mukanena bwanji kapena mukanena chiyani. Mudzapatsidwa pa nthawi imeneyo zoti munene,
20 For det er ikke I som taler, men det er eders Faders Ånd som taler i eder.
pakuti sindinu mudzanena, koma Mzimu Woyera wa Atate anu, adzayankhula mwa inu.
21 Og bror skal overgi bror til døden, og en far sitt barn, og barn skal reise sig mot foreldre og volde deres død;
“Mʼbale adzapereka mʼbale kuti aphedwe ndi abambo mwana wawo: ndipo ana adzawukira makolo awo ndi kuwapereka kuti aphedwe.
22 og I skal hates av alle for mitt navns skyld; men den som holder ut til enden, han skal bli frelst.
Anthu onse adzada inu chifukwa cha Ine, koma iye amene apirira mpaka kumapeto, adzapulumuka.
23 Men når de forfølger eder i den ene by, da fly til den andre! for sannelig sier jeg eder: I skal ikke komme til ende med Israels byer før Menneskesønnen kommer.
Pamene akuzunzani pamalo ena thawirani kwina. Pakuti ndikuwuzani zoonadi kuti simudzamaliza mizinda yonse ya Israeli Mwana wa Munthu asanabwere.
24 En disippel er ikke over sin mester, heller ikke en tjener over sin herre;
“Wophunzira saposa mphunzitsi wake ndipo wantchito saposa bwana wake.
25 det er nok for disippelen at han blir som sin mester, og tjeneren som sin herre; har de kalt husbonden Be'elsebul, hvor meget mere da hans husfolk!
Nʼkoyenera kuti wophunzira akhale ngati mphunzitsi wake, ndi wantchito akhale ngati bwana wake. Ngati mwini banja atchedwa Belezebabu, koposa kotani a mʼnyumba mwake!
26 Frykt derfor ikke for dem! for intet er skjult som ikke skal bli åpenbaret, og intet er dulgt som ikke skal bli kjent;
“Chifukwa chake musaope iwo. Pakuti palibe chinthu chobisika chimene sichidzavundukulidwa, ndi chobisika chimene sichidzadziwika.
27 det jeg sier eder i mørket, det skal I si i lyset, og det som hviskes eder i øret, det skal I forkynne på takene.
Chimene ndikuwuzani Ine mu mdima, muchiyankhule poyera; chimene akunongʼonezani mʼkhutu, muchilalikire muli pa denga.
28 Og frykt ikke for dem som slår legemet ihjel, men ikke kan slå sjelen ihjel; men frykt heller for ham som kan ødelegge både sjel og legeme i helvede! (Geenna g1067)
Musamaope amene amapha thupi koma sangathe kuchotsa moyo. Koma muziopa Iye amene akhoza kupha mzimu ndi kuwononga thupi mu gehena. (Geenna g1067)
29 Selges ikke to spurver for en øre? Og ikke en av dem faller til jorden uten at eders Fader vil.
Kodi suja amagulitsa mbalame ziwiri ndi ndalama imodzi? Koma palibe imodzi ya izo imene idzagwa pansi wopanda chifuniro cha Atate anu.
30 Men endog hårene på eders hode er tellet alle sammen.
Ndipo ngakhale tsitsi la mʼmutu mwanu linawerengedwa kale.
31 Frykt derfor ikke! I er mere enn mange spurver.
Potero musaope; inu ndinu a mtengo woposa mbalame zambiri.
32 Derfor, hver den som kjennes ved mig for menneskene, ham skal også jeg kjennes ved for min Fader i himmelen;
“Aliyense amene avomereza Ine pamaso pa anthu, Inenso ndidzavomereza pamaso pa Atate anga akumwamba.
33 men den som fornekter mig for menneskene, ham skal også jeg fornekte for min Fader i himmelen.
Koma iye amene andikana Ine pamaso pa anthu, Inenso ndidzamukana pamaso pa Atate anga akumwamba.
34 I må ikke tro at jeg er kommet for å sende fred på jorden; jeg er ikke kommet for å sende fred, men sverd.
“Musaganize kuti Ine ndabweretsa mtendere pa dziko lapansi. Sindinabwere kudzapereka mtendere koma lupanga.
35 For jeg er kommet for å sette splid mellem en mann og hans far, og mellem en datter og hennes mor, og mellem en svigerdatter og hennes svigermor,
Pakuti Ine ndabwera kudzalekanitsa “‘Munthu ndi abambo ake, mwana wamkazi ndi amayi ake, mtengwa kulekanitsidwa ndi apongozi ake,
36 og en manns husfolk skal bli hans fiender.
adani a munthu adzakhala a mʼbanja mwake momwe.’
37 Den som elsker far eller mor mere enn mig, er mig ikke verd, og den som elsker sønn eller datter mere enn mig, er mig ikke verd,
“Aliyense amene akonda abambo kapena amayi ake koposa Ine sayenera kukhala wanga; aliyense amene akonda mwana wake wamwamuna kapena wamkazi koposa Ine sayenera kukhala wanga.
38 og den som ikke tar sitt kors og følger efter mig, er mig ikke verd.
Aliyense amene satenga mtanda wake ndi kunditsata Ine sayenera kukhala wanga.
39 Den som finner sitt liv, skal miste det, og den som mister sitt liv for min skyld, skal finne det.
Aliyense amene asunga moyo wake adzawutaya koma aliyense amene ataya moyo chifukwa cha Ine adzawupeza.
40 Den som tar imot eder, tar imot mig, og den som tar imot mig, tar imot ham som sendte mig.
“Iye amene alandira inu alandira Ine, ndipo amene alandira Ine alandiranso amene anandituma Ine.
41 Den som tar imot en profet fordi han er en profet, skal få en profets lønn, og den som tar imot en rettferdig fordi han er rettferdig, skal få en rettferdigs lønn.
Aliyense amene alandira mneneri chifukwa chakuti ndi mneneri alandira mphotho ya mneneri, ndipo aliyense amene alandira munthu wolungama chifukwa chakuti ndi munthu wolungama, adzalandira mphotho ya wolungama.
42 Og den som gir én av disse små endog bare et beger koldt vann å drikke fordi han er disippel, sannelig sier jeg eder: Han skal ingenlunde miste sin lønn.
Ngati aliyense apereka madzi ozizira a mʼchikho kwa mmodzi wa angʼonoangʼono awa chifukwa cha kuti ndi ophunzira anga, ndikuwuzani zoona, ndithudi sadzataya mphotho yake.”

< Matteus 10 >