< Klagesangene 2 >

1 Hvor Herren i sin vrede har innhyllet Sions datter i mørke skyer! Han har kastet Israels herlighet fra himmelen til jorden, og han har ikke kommet i hu sine føtters skammel på sin vredes dag.
Haa, Ambuye waphimba mwana wamkazi wa Ziyoni ndi mtambo wa mkwiyo wake! Iye wataya pansi ulemerero wa Israeli kuchoka kumwamba. Pa tsiku la mkwiyo wake Iye sanakumbukirenso popondapo mapazi ake.
2 Herren har uten skånsel tilintetgjort alle Jakobs boliger, han har i sin vrede brutt ned Judas datters festninger, kastet dem til jorden; han har vanhelliget riket og dets fyrster.
Ambuye anawononga midzi yonse ya Yakobo mopanda chifundo; mu mkwiyo wake anagwetsa malinga a mwana wamkazi wa Yuda. Anagwetsa pansi mochititsa manyazi maufumu ndi akalonga ake.
3 Han har i brennende vrede avhugget hvert horn i Israel, dradd sin høire hånd tilbake for fiendens åsyn og satt Jakob i brand lik en ildslue som fortærer rundt omkring.
Atakwiya kwambiri, Ambuye anathyola nyanga iliyonse ya Israeli. Anabweza dzanja lake lamanja pamene mdani anamuyandikira. Ambuye anatentha fuko la Yakobo ngati moto wonyeketsa umene umawononga zinthu zonse zomwe zili pafupi.
4 Han har spent sin bue som en fiende, stilt sig med sin høire hånd som en motstander og drept alt som var en lyst for vårt øie; i Sions datters telt har han utøst sin vrede som ild.
Wakokera uta wake pa ife ngati ndife adani; wayimiritsa dzanja lake pa ife ngati ndife adani, ndipo anapha onse amene tinkawayangʼana monyadira. Ukali wake ukuyaka ngati moto pa tenti ya mwana wamkazi wa Ziyoni.
5 Herren er blitt som en fiende, han har tilintetgjort Israel, tilintetgjort alle dets palasser, ødelagt dets festninger og hopet sorg på sorg over Judas datter.
Ambuye ali ngati mdani; wawonongeratu Israeli; wawonongeratu nyumba zake zonse zaufumu ndipo wawononga malinga ake. Iye wachulukitsa kubuma ndi kulira kwa mwana wamkazi wa Yuda.
6 Han har med vold revet ned sitt gjerde som gjerdet om en have, han har ødelagt sitt forsamlingssted; Herren har latt høitid og sabbat bli glemt i Sion, og i sin vrede og harme forskutt konge og prest.
Wagwetsa malo ake okhalamo ngati khumbi la mʼmunda; wawononga malo ake a msonkhano. Yehova wayiwalitsa Ziyoni maphwando ake oyikika ndi masabata ake. Mokwiya kwambiri, Iye ananyoza mfumu ndi wansembe.
7 Herren har forkastet sitt alter, forsmådd sin helligdom; han har overgitt dets palassers murer i fiendens vold; de lot sin røst høre i Herrens hus som på en høitidsdag.
Ambuye wakana guwa lake la nsembe ndipo wasiya malo ake opatulika. Iye wapereka makoma a nyumba zake zaufumu kwa mdani wake; adaniwo anafuwula mʼnyumba ya Yehova ngati kuti ndi pa tsiku la chikondwerero.
8 Herren tenkte på å ødelegge Sions datters mur, han strakte ut målesnoren, han drog ikke sin hånd tilbake fra herjing, og han lot voller og murer sørge; forfalne ligger de der alle.
Yehova anatsimikiza kugwetsa makoma a mwana wamkazi wa Ziyoni. Anawayesa ndi chingwe ndipo sanafune kuleka kuwagwetsa. Analiritsa malinga ndi makoma; onse anawonongeka pamodzi.
9 Dets porter er sunket i jorden, han har ødelagt og sprengt dets bommer; dets konge og dets høvdinger bor blandt hedningene, så der ikke er nogen lov; heller ikke har dets profeter fått noget syn fra Herren.
Zipata za Yerusalemu zalowa pansi; wathyola ndi kuwononga mipiringidzo yake. Mfumu ndi akalonga ake agwidwa ukapolo pakati pa mitundu ya anthu, palibenso lamulo, ndipo aneneri ake sakupeza masomphenya kuchokera kwa Yehova.
10 Sions datters eldste sitter tause på jorden; de har strødd støv på sitt hode, omgjordet sig med sekk; Jerusalems jomfruer har senket sitt hode til jorden.
Akuluakulu a mwana wamkazi wa Ziyoni akhala chete pansi; awaza fumbi pa mitu yawo ndipo avala ziguduli. Anamwali a Yerusalemu aweramitsa mitu yawo pansi.
11 Mine øine er borttæret av tårer, det gjærer i mitt indre, min lever er utøst til jorden, fordi mitt folks datter er ødelagt, fordi de små barn og de diende vansmektet på byens gater;
Maso anga atopa ndi kulira, ndazunzika mʼmoyo mwanga, mtima wanga wadzaza ndi chisoni chifukwa anthu anga akuwonongeka, chifukwa ana ndi makanda akukomoka mʼmisewu ya mu mzinda.
12 de ropte til sine mødre: Hvor er korn og vin? - da de vansmektet på byens gater lik sårede, da de opgav ånden ved sine mødres barm.
Anawo akufunsa amayi awo kuti, “Kodi tirigu ndi vinyo zili kuti?” pamene akukomoka ngati anthu olasidwa mʼmisewu ya mʼmizinda, pamene miyoyo yawo ikufowoka mʼmanja mwa amayi awo.
13 Hvad skal jeg vidne for dig, hvad skal jeg ligne dig med, du Jerusalems datter? Hvad skal jeg stille ved siden av dig, så jeg kunde trøste dig, du jomfru, Sions datter? For stor som havet er din skade; hvem kan læge dig?
Ndinganene chiyani za iwe? Ndingakufanizire ndi chiyani, iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu? Kodi ndingakufanizire ndi yani kuti ndikutonthoze, iwe namwali wa Ziyoni? Chilonda chako ndi chozama ngati nyanja, kodi ndani angakuchiritse?
14 Dine profeter har skuet for dig tomme og dårlige ting; de åpenbarte ikke din misgjerning for å avvende ditt fangenskap, men de forkynte dig tomme og villedende spådommer.
Masomphenya a aneneri ako anali abodza ndi achabechabe. Iwo sanakupulumutse kuti usapite ku ukapolo poyika poyera mphulupulu zako. Mauthenga amene anakupatsa anali achabechabe ndi osocheretsa.
15 De slår hendene sammen over dig alle de som går forbi på veien; de spotter og ryster på hodet over Jerusalems datter: Er dette den stad de kalte skjønnhetens krone, all jordens glede?
Onse oyenda mʼnjira yako akukuwombera mʼmanja; akugwedeza mitu yawo ndi kukunyodola iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu: “Kodi mzinda uja ndi uwu umene unkatchedwa wokongola kotheratu, chimwemwe cha dziko lonse lapansi?”
16 Alle dine fiender spiler op sin munn mot dig, de spotter og skjærer tenner, de sier: Vi har ødelagt den; ja, dette er den dag vi har ventet på; vi har oplevd den, vi har sett den.
Adani ako onse akutsekulira pakamwa ndi kukunyoza; iwo akunyogodola ndi kukukuta mano awo, ndipo akuti, “Tamumeza. Tsiku ili ndi lomwe timayembekezera; tili ndi moyo kuti tilione.”
17 Herren har gjort det han hadde tenkt, han har fullbyrdet sitt ord som han hadde forkynt alt i fordums dager, han har brutt ned uten skånsel; og han lot fienden glede sig over dig, han lot dine motstandere bære sine horn høit.
Yehova wachita chimene anakonzeratu; wakwaniritsa mawu ake, amene anatsimikiza kale lomwe. Wakuwononga mopanda chifundo, walola mdani kuti akondwere chifukwa cha kugwa kwako, wakweza mphamvu za adani ako.
18 Deres hjerte roper til Herren. - Du Sions datters mur! La tårer rinne som bekker dag og natt, unn dig ikke nogen hvile, la ikke ditt øie ha ro!
Mitima ya anthu ikufuwulira Ambuye. Iwe khoma la mwana wamkazi wa Ziyoni, misozi yako itsike ngati mtsinje usana ndi usiku; usadzipatse wekha mpumulo, maso ako asaleke kukhetsa misozi.
19 Stå op, rop høit om natten, når nattevaktene begynner! Utøs ditt hjerte som vann for Herrens åsyn! Løft dine hender til ham for dine barns liv, de som vansmekter av hunger på alle gatehjørner!
Dzuka, fuwula usiku, pamene alonda ayamba kulondera; khuthula mtima wako ngati madzi pamaso pa Ambuye. Kweza manja ako kwa Iye chifukwa cha miyoyo ya ana ako, amene akukomoka ndi njala mʼmisewu yonse ya mu mzinda.
20 Se, Herre, se! Hvem har du gjort således med? Skal kvinner ete sin livsfrukt, de spede barn som bæres på armen? Skal prest og profet slås ihjel i Herrens helligdom?
Inu Yehova, onani, ndipo ganizirani: kodi ndani amene mwamuchitirapo zinthu ngati izi? Kodi amayi adye ana awo, amene amawasamalira? Kodi ansembe ndi aneneri awaphere mʼmalo opatulika a Ambuye?
21 Ung og gammel ligger på jorden i gatene, mine jomfruer og mine unge menn er falt for sverdet; du slo ihjel på din vredes dag, du slaktet uten skånsel.
Anyamata ndi okalamba aligone pamodzi pa fumbi la mʼmisewu ya mu mzinda; anyamata anga ndi anamwali anga aphedwa ndi lupanga. Inu Yehova mwawapha pa tsiku la mkwiyo wanu; mwawapha mopanda chifundo.
22 Som på en høitidsdag kalte du redsler over mig fra alle kanter, og det var ikke på Herrens vredes dag nogen som slapp unda eller blev reddet; dem som jeg hadde båret på armen og opfostret, dem ødela min fiende.
Ngati momwe mumayitanira pa tsiku la phwando, chimodzimodzinso mwandiyitanira zoopsa mbali zonse. Pa tsiku limene Yehova wakwiya palibe amene angathawe ndi kukhala ndi moyo; mdani wanga wawononga onse amene ndinkawasamala ndi kuwalera.

< Klagesangene 2 >