< Jobs 8 >

1 Da tok Bildad fra Suah til orde og sa:
Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 Hvor lenge vil du tale så? Hvor lenge skal din munns ord være som et veldig vær?
“Kodi udzakhala ukuyankhula zoterezi mpaka liti? Mawu ako ali ngati mphepo yamkuntho.
3 Skulde vel Gud forvende retten, eller den Allmektige forvende rettferdigheten?
Kodi Mulungu amapotoza chiweruzo cholungama? Kodi Wamphamvuzonse amalephera kuchita zachilungamo?
4 Har dine sønner syndet mot ham, så har han gitt dem deres brøde i vold.
Pamene ana ako anamuchimwira Mulungu, Iye anawapereka kuti alangidwe chifukwa cha tchimo lawo.
5 Hvis du vender dig til Gud og beder den Allmektige om nåde,
Koma utayangʼana kwa Mulungu, ndi kudandaulira Wamphamvuzonse,
6 hvis du er ren og opriktig, da vil han våke over dig og gjenreise din rettferds bolig,
ngati uli wangwiro ndi wolungama mtima ngakhale tsopano Iye adzachitapo kanthu mʼmalo mwako ndipo adzakubwezeretsa pa malo ako oyenera.
7 og din forrige lykke vil bli ringe mot din senere lykke, for den skal være overmåte stor.
Chiyambi chako chidzaoneka ngati chochepa koma chimaliziro chako chidzakhala chopambana.
8 For spør bare fremfarne slekter og akt på det som deres fedre har gransket ut
“Funsa kwa anthu amvulazakale ndipo upeze zimene makolo awo anaziphunzira
9 - for vi er fra igår og vet intet; for en skygge er våre dager på jorden -
pakuti ife ndife ana adzulodzuloli ndipo sitidziwa chilichonse, ndipo moyo wathu pa dziko lapansi uli ngati chithunzithunzi.
10 de skal lære dig og si dig det og bære frem ord fra sitt hjerte.
Kodi iwo sadzakulangiza ndi kukufotokozera? Kodi sadzakuwuza mawu ochokera pa zimene amazidziwa?
11 Vokser sivet op hvor det ikke er myrlendt? Blir starrgresset stort uten vann?
Kodi bango nʼkumera pa nthaka yopanda chinyontho? Nanga mawango nʼkukula bwino popanda madzi?
12 Ennu står det friskt og grønt og blir ikke skåret; da visner det før alt annet gress.
Popanda madzi, zimenezi zimafota zikanali zaziwisi ndi zosadula; zimawuma msangamsanga kuposa bango.
13 Således går det alle dem som glemmer Gud, og den gudløses håp går til grunne;
Ndimo mmene amachitira anthu onse amene amayiwala Mulungu; ndi mmene chiyembekezo cha munthu wosapembedza Mulungu chimathera.
14 hans tillit avskjæres, og det han trøster sig til, er spindelvev.
Kulimba mtima kwake kumafowoka; zimene iye amadalira zili ngati ukonde wa kangawude.
15 Han støtter sig på sitt hus, men det står ikke; han holder sig fast i det, men det står ikke fast.
Iye amatsamira ukonde wake, koma umaduka; amawugwiritsitsa koma sulimba.
16 Frodig står han der i solens skinn, og hans skudd breder sig ut over hans have;
Munthu woyipayo ali ngati chomera chothiriridwa bwino chimene chili pa dzuwa, nthambi zake zimatambalala pa munda wake;
17 om en stenrøs slynger sig hans røtter, mellem stener trenger han sig frem.
mizu yake imayanga pa mulu wa miyala ndi kufunafuna malo woti izikike pa miyalapo.
18 Ryddes han bort fra sitt sted, så kjennes det ikke ved ham, men sier: Jeg har aldri sett dig.
Koma pamene yachotsedwa pamalo pakepo, pamalopo pamakana chomeracho ndi kuti, ‘Ine sindinakuonepo.’
19 Se, det er gleden på hans vei, og av mulden spirer andre frem.
Ndithudi chomeracho chimafota, ndipo pa nthakapo pamatuluka zomera zina.
20 Nei, Gud forkaster ikke en som er ulastelig, og han holder ikke ugudelige ved hånden.
“Ndithudi, Mulungu sakana munthu amene alibe cholakwa kapena kulimbikitsa anthu ochita zoyipa.
21 Ennu vil han fylle din munn med latter og dine leber med jubel.
Iye adzadzaza mʼkamwa mwako ndi phwete ndipo milomo yako idzafuwula ndi chimwemwe.
22 De som hater dig, skal klædes med skam, og de ugudeliges telt skal ikke mere finnes.
Adani ako adzachita manyazi, ndipo malo okhalamo anthu oyipa sadzaonekanso.”

< Jobs 8 >