< Jobs 27 >

1 Og Job blev ved å fremføre sin visdomstale og sa:
Ndipo Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
2 Så sant Gud lever, som har tatt min rett fra mig, den Allmektige, som har voldt mig bitter sorg
“Ndithu pali Mulungu wamoyo, amene wakana kundiweruza molungama, Wamphamvuzonse, amene wawawitsa mtima wanga,
3 - for ennu er hele mitt livspust i mig og den Allmektiges ånde i min nese -:
nthawi zonse pamene ndili ndi moyo, mpweya wa Mulungu uli mʼmphuno mwanga,
4 Mine leber taler ikke urett, og min tunge taler ikke svik.
pakamwa panga sipadzatuluka mawu oyipa, lilime langa silidzayankhula zachinyengo.
5 Det være langt fra mig å gi eder rett! Inntil jeg opgir ånden, lar jeg ikke min brødefrihet tas fra mig.
Sindidzavomereza kuti inu mukunena zoona; mpaka imfa yanga, sindidzataya ungwiro wanga.
6 Jeg holder fast på min rettferdighet og slipper den ikke; mitt hjerte laster mig ikke for nogen av mine dager.
Ndidzasunga chilungamo changa ndipo sindidzalola kuti chindichokere; chikumbumtima changa sichidzanditsutsa nthawi yonse ya moyo wanga.
7 La min fiende stå der som en ugudelig, og min motstander som en urettferdig!
“Mdani wanga akhale ngati woyipa, wondiwukira akhale ngati munthu wosalungama!
8 For hvad håp har den gudløse, når Gud avskjærer hans liv, når han tar hans sjel fra ham?
Nanga chiyembekezo cha munthu wosapembedza nʼchiyani pamene aphedwa, pamene Mulungu achotsa moyo wake?
9 Hører vel Gud hans skrik når trengsel kommer over ham?
Kodi Mulungu amamva kulira kwake pamene zovuta zamugwera?
10 Eller kan han glede sig i den Allmektige, kan han påkalle Gud til enhver tid?
Kodi adzapeza chikondwerero mwa Wamphamvuzonse? Kodi adzapemphera kwa Mulungu nthawi zonse?
11 Jeg vil lære eder om Guds hånd; jeg vil ikke dølge hvad den Allmektige har i sinne.
“Ndidzakuphunzitsani za mphamvu ya Mulungu ndipo sindidzabisa njira za Wamphamvuzonse.
12 I har jo alle selv sett det; hvorfor fører I da så tom en tale?
Inu mwadzionera nokha zonsezi. Nanga bwanji mukuyankhula zopanda pake?
13 Dette er det ugudelige menneskes lodd hos Gud og den arv som voldsmennene får av den Allmektige:
“Pano pali chilango chimene Mulungu amasungira woyipa, cholowa chimene munthu wankhanza amalandira kuchokera kwa Wamphamvuzonse.
14 Får han mange barn, så er de hjemfalt til sverdet; hans ætlinger får ikke brød å mette sig med.
Angakhale ana ake achuluke chotani adzaphedwa ndi lupanga ndipo zidzukulu zake zidzasowa zakudya.
15 De av dem som slipper unda, legges i graven ved pest, og enkene holder ikke sørgefest over dem.
Amene adzatsalireko adzafa ndi mliri, ndipo akazi awo amasiye sadzawalira.
16 Når han dynger op sølv som støv og samler sig klær som lere,
Ngakhale aunjike siliva ngati fumbi, ndi kukundika zovala ngati mchenga,
17 så blir det de rettferdige som klær sig med det han har samlet, og sølvet skal de skyldfrie dele.
zimene wasungazo wolungama ndiye adzavale, ndipo anthu osalakwa ndiwo adzagawane siliva wakeyo.
18 Som møllet har han bygget sitt hus og som den hytte en markvokter lager sig.
Nyumba imene akuyimanga ili ngati mokhala kadziwotche, ili ngati msasa umene mlonda amamanga.
19 Rik legger han sig, og intet er tatt bort; han slår sine øine op, og det er der ikke.
Amapita kokagona ali wolemera koma kutha kwake nʼkomweko; akatsekula maso ake, chuma chake chonse chapita.
20 Som en vannflom innhenter redsler ham, om natten fører en storm ham bort.
Zoopsa zimamukokolola ngati madzi achigumula; mphepo yamkuntho imamunyamula usiku.
21 Østenvinden løfter ham op, så han farer avsted, og den blåser ham bort fra hans sted.
Mphepo ya kummawa imamuwulutsa ndipo iye saonekanso ndipo imamuchotsa pamalo pake.
22 Gud skyter sine piler mot ham og sparer ham ikke; for hans hånd flyr han i hast.
Imakuntha pa iye osamuchitira chisoni, pamene akuyesa kuthawa mphamvu zake mwaliwiro.
23 Folk klapper i hendene og håner ham og piper ham bort fra hans sted.
Mphepoyo imamuwomba ndithu ndipo kuchokera pamalo pake imamuopseza.”

< Jobs 27 >