< Jobs 1 >

1 I landet Us var det en mann som hette Job; han var en ulastelig og rettskaffen mann, som fryktet Gud og vek fra det onde.
Mʼdziko la Uzi munali munthu wina, dzina lake Yobu. Munthu ameneyu anali wosalakwa ndi wolungama mtima, ankaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa.
2 Han fikk syv sønner og tre døtre,
Anali ndi ana aamuna asanu ndi awiri ndi ana aakazi atatu,
3 og han eide syv tusen får og tre tusen kameler og fem hundre par okser og fem hundre aseninner og hadde en stor mengde tjenere; han var mektigere enn alle Østens barn.
ndipo anali ndi nkhosa 7,000, ngamira 3,000, ngʼombe zantchito 1,000 ndi abulu aakazi 500, ndiponso anali ndi antchito ambiri. Iye anali munthu wotchuka kwambiri pakati pa anthu onse a mʼmayiko a kummawa.
4 Hans sønner pleide å holde gjestebud på hver sin dag i hver sitt hus, og de sendte da bud til sine tre søstre og innbød dem til å ete og drikke sammen med dem.
Ana ake aamuna ankachita phwando mosinthanasinthana mʼnyumba zawo, ndipo ankayitana alongo awo atatu aja kudzadya ndi kumwa nawo.
5 Og så ofte en omgang av disse gjestebud var til ende, sendte Job bud efter dem og helliget dem; han stod tidlig op om morgenen og ofret brennoffer, ett for hver av dem; for Job sa: Kanskje mine sønner har syndet og sagt Gud farvel i sitt hjerte. Således gjorde Job alltid.
Masiku aphwandowo atatha, Yobu ankawayitana kuti adzawayeretse. Mmamawa iye ankapereka nsembe yopsereza kuperekera mwana aliyense, poganiza kuti, “Mwina ana anga achimwa ndi kutukwana Mulungu mʼmitima yawo.” Umu ndi mmene Yobu ankachitira nthawi zonse.
6 Så hendte det en dag at Guds sønner kom og stilte sig frem for Herren, og blandt dem kom også Satan.
Ana a Mulungu atabwera kudzadzionetsa pamaso pa Yehova, nayenso Satana anafika nawo limodzi.
7 Og Herren sa til Satan: Hvor kommer du fra? Satan svarte Herren: Jeg har faret og flakket omkring på jorden.
Yehova anati kwa Satanayo, “Kodi iwe ukuchokera kuti?” Satana anayankha Yehova kuti, “Ndakhala ndikungoyendayenda ndi kumangozungulira mʼdzikoli.”
8 Da sa Herren til Satan: Har du gitt akt på min tjener Job? For det er ingen på jorden som han - en ulastelig og rettskaffen mann, som frykter Gud og viker fra det onde.
Pamenepo Yehova anati kwa Satana, “Kodi unalingalirapo za mtumiki wanga Yobu? Palibe wina pa dziko lapansi wofanana naye; ndi munthu wosalakwa ndi wolungama mtima, munthu amene amaopa Mulungu ndi kupewa zoyipa.”
9 Men Satan svarte Herren: Mon Job frykter Gud for intet?
Satana anayankha kuti, “Kodi Yobu amaopa Mulungu popanda chifukwa?”
10 Har du ikke hegnet om ham og om hans hus og om alt som hans er, på alle kanter? Hans henders gjerning har du velsignet, og hans hjorder har bredt sig vidt utover i landet.
“Kodi Inu simumamuteteza iyeyo, nyumba yake ndi zonse zimene ali nazo? Mwadalitsa ntchito ya manja ake, kotero kuti nkhosa ndi ngʼombe zake zili ponseponse mʼdzikomo.
11 Men rekk bare ut din hånd og rør ved alt som hans er! Da vil han visselig si dig farvel like i ditt ansikt.
Koma tatambasulani dzanja lanu ndi kukantha zonse ali nazo ndipo iyeyo adzakutukwanani ndithu pamaso panu.”
12 Da sa Herren til Satan: Se, alt som hans er, er i din hånd; men mot ham selv må du ikke rekke ut din hånd. Så gikk Satan bort fra Herrens åsyn.
Yehova anati kwa Satana, “Chabwino, tsono zonse zimene ali nazo ndaziyika mʼmanja mwako, koma iye yekhayo usamukhudze.” Pamenepo Satana anachoka pamaso pa Yehova.
13 Så hendte det en dag mens hans sønner og døtre åt og drakk vin i den eldste brors hus,
Tsiku lina pamene ana aamuna ndi ana aakazi a Yobu ankachita phwando ndi kumwa vinyo mʼnyumba mwa mkulu wawo,
14 da kom det et bud til Job og sa: Oksene pløide, og aseninnene beitet tett ved;
wamthenga anabwera kwa Yobu ndipo anati, “Ngʼombe zanu zotipula ndipo abulu anu amadya chapafupi pomwepo,
15 da kom sabeerne over dem og tok dem, og drengene hugg de ned med sverdet, og bare jeg alene slapp unda, så jeg kunde melde dig det.
tsono panabwera Aseba kudzatithira nkhondo ndi kutenga zonse. Apha antchito ndi lupanga, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
16 Mens han ennu talte, kom en annen og sa: Guds ild fór ned fra himmelen og rammet småfeet og drengene og brente dem op, bare jeg alene slapp unda, så jeg kunde melde dig det.
Iyeyo akuyankhulabe, wamthenga wina anabwera nati, “Kunagwa mphenzi ndipo yapsereza nkhosa ndi antchito anu onse, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
17 Mens han ennu talte, kom en annen og sa: Kaldeerne delte sig i tre flokker og overfalt kamelene og tok dem, og drengene hugg de ned med sverdet, og bare jeg alene slapp unda, så jeg kunde melde dig det.
Iyeyo akuyankhulabe, wamthenga wina anabwera nati, “Akasidi anadzigawa mʼmagulu atatu ankhondo ndipo anafika pa ngamira zanu ndi kuzitenga. Apha antchito anu onse ndi lupanga, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
18 Mens han ennu talte, kom en annen og sa: Dine sønner og døtre åt og drakk vin i den eldste brors hus;
Iyeyo akuyankhulabe, panafikanso wamthenga wina nati, “Ana anu aamuna ndi aakazi amachita phwando ndi kumwa vinyo mʼnyumba ya mkulu wawo,
19 da kom det med ett en sterk storm fra hin side ørkenen og støtte mot alle fire hjørner av huset, så det falt sammen over de unge folk, og de omkom, og bare jeg alene slapp unda, så jeg kunde melde dig det.
mwadzidzidzi chinayamba chimphepo champhamvu chochokera ku chipululu, nʼkudzawomba nyumba mbali zonse zinayi. Nyumbayo yawagwera ndipo afa, ndipo ine ndekha ndiye ndapulumuka kuti ndidzakuwuzeni!”
20 Da reiste Job sig og sønderrev sin kappe og klipte håret av sitt hode og kastet sig ned på jorden og tilbad
Atamva zimenezi, Yobu anayimirira nangʼamba mkanjo wake, ndi kumeta tsitsi lake. Kenaka anadzigwetsa pansi napembedza Mulungu,
21 og sa: Naken kom jeg av min mors liv, og naken skal jeg vende dit tilbake. Herren gav, og Herren tok; Herrens navn være lovet!
nati, “Ndinatuluka maliseche mʼmimba mwa amayi anga, namonso mʼmanda ndidzalowa wamaliseche. Yehova ndiye anapereka ndipo Yehova watenga; litamandike dzina la Yehova.”
22 Under alt dette syndet Job ikke, og han lastet ikke Gud for det som hadde hendt ham.
Mu zonsezi, Yobu sanachimwe kapena kunena kuti, “Mulungu walakwa.”

< Jobs 1 >