< Jeremias 37 >

1 Og Sedekias, Josias' sønn, blev konge efter Konja, Jojakims sønn for Babels konge Nebukadnesar hadde satt ham til konge i Juda land.
Nebukadinezara mfumu ya Babuloni, inakhazika pa mpando waufumu Zedekiya mwana wa Yosiya kukhala mfumu ya Yuda. Iye analowa mʼmalo mwa Yehoyakini mwana wa Yehoyakimu.
2 Men han og hans tjenere og landets folk hørte ikke på Herrens ord, som han talte ved profeten Jeremias.
Koma Zedekiya kapena atumiki ake ngakhalenso anthu a mʼdzikomo sanasamalire mawu a Yehova amene anayankhula kudzera mwa mneneri Yeremiya.
3 Og kong Sedekias sendte Jehukal, Selemjas sønn, og presten Sefanja, Ma'asejas sønn, til profeten Jeremias og lot si: Bed for oss til Herren vår Gud!
Tsono Zedekiya anatuma Yehukali mwana wa Selemiya ndi wansembe Zefaniya mwana wa Maseya kwa mneneri Yeremiya ndi uthenga uwu: “Chonde tipempherereni kwa Yehova Mulungu wathu.”
4 Jeremias gikk dengang inn og ut blandt folket; de hadde ennu ikke satt ham i fengsel.
Nthawi imeneyinso nʼkuti Yeremiya ali ndi ufulu woyenda pakati pa anthu chifukwa anali asanaponyedwe mʼndende.
5 Og Faraos hær hadde da draget ut fra Egypten, og da kaldeerne, som holdt Jerusalem kringsatt, spurte det, drog de bort fra Jerusalem.
Nthawi imeneyinso nʼkuti gulu lankhondo la Farao litatuluka mʼdziko la Igupto. Ndipo Ababuloni amene anali atazinga Yerusalemu atamva zimenezi, anachoka ku Yerusalemuko.
6 Da kom Herrens ord til profeten Jeremias, og det lød så:
Tsono Yehova anawuza mneneri Yeremiya kuti,
7 Så sier Herren, Israels Gud: Så skal I si til Judas konge, som sendte eder til mig for å spørre mig: Se, Faraos hær, som har draget ut for å komme eder til hjelp, skal vende tilbake til sitt land, Egypten,
“Uyiwuze mfumu ya Yuda imene inakutuma kuti udzapemphe nzeru kwa ine kuti Ine Yehova, Mulungu wa Israeli ndikuti, gulu lankhondo la Farao limene linatuluka kuti lidzakuthandize lidzabwerera kwawo ku Igupto.
8 og kaldeerne skal komme igjen og stride mot denne by, og de skal innta den og brenne den op med ild.
Ndipo Ababuloni adzabwerera kudzathira nkhondo mzinda uno. Iwo adzawugonjetsa ndi kuwutentha.
9 Så sier Herren: I må ikke dåre eder selv og si: Kaldeerne skal visselig dra bort fra oss! For de skal ikke dra bort;
“Yehova akuti: Musadzinyenge, nʼkumaganiza kuti, ‘Ndithu Ababuloni adzatisiya.’ Ndithudi sadzakusiyani!
10 om I så slo hele kaldeernes hær som strider mot eder, og det bare blev nogen hårdt sårede tilbake iblandt dem, så skulde disse stå op, hver i sitt telt, og brenne denne by op med ild.
Ngakhale mutagonjetsa gulu lonse lankhondo la Ababuloni limene likukuthirani nkhondo ndipo mʼmatenti mwawo ndikutsala anthu ovulala okhaokha, amenewo adzabwera ndi kudzatentha mzinda uno.”
11 Og da kaldeernes hær hadde draget bort fra Jerusalem for Faraos hærs skyld,
Gulu lankhondo la Ababuloni litaleka kuthira nkhondo mzinda wa Yerusalemu chifukwa choopa gulu lankhondo la Farao,
12 da gikk Jeremias ut av Jerusalem midt iblandt folket for å gå til Benjamins land og hente sin arvelodd derfra.
Yeremiya ananyamuka kuchoka ku Yerusalemu ndi kumapita ku dziko la Benjamini kuti akalandire gawo lake la minda ya makolo ake.
13 Og da han var i Benjamin-porten, så stod der en høvedsmann for vakten ved navn Jerija, sønn av Selemja, sønn av Hananja; han grep fatt i profeten Jeremias og sa: Du vil gå over til kaldeerne.
Koma atafika pa Chipata cha Benjamini, mkulu wa alonda amene dzina lake linali Iriya mwana wa Selemiya, mwana wa Hananiya, anagwira mneneri Yeremiyayo ndipo anati, “Iwe ukuthawira kwa Ababuloni!”
14 Da sa Jeremias: Det er løgn; jeg vil ikke gå over til kaldeerne. Men Jerija hørte ikke på Jeremias, han grep ham og førte ham til høvdingene.
Yeremiya anati, “Zimenezo si zoona! Ine sindikuthawira kwa Ababuloni.” Koma Iriya sanamumvere. Mʼmalo mwake anagwira Yeremiya nʼkupita naye kwa akuluakulu.
15 Da blev høvdingene vrede på Jeremias og slo ham, og de satte ham i fangehuset, i statsskriveren Jonatans hus; for det hadde de gjort til fengsel.
Akuluakuluwo anamupsera mtima Yeremiya ndipo anamukwapula ndi kumuyika mʼnyumba ya mlembi Yonatani, imene anayisandutsa ndende.
16 Da Jeremias var kommet i fangehullet, i kjelleren, og hadde sittet der i mange dager,
Yeremiya anayikidwa mʼndende ya pansi pa nthaka, kumene anakhalako nthawi yayitali.
17 sendte kong Sedekias bud og lot ham hente, og kongen spurte ham i sitt hus i lønndom og sa: Er det noget ord fra Herren? Jeremias svarte: Ja, det er. Og så sa han: Du skal bli gitt i Babels konges hånd.
Kenaka Mfumu Zedekiya inatuma anthu kuti akayitane Yeremiya ndipo anabwera naye ku nyumba ya mfumu. Atafika mfumu inamufunsa mwamseri kuti, “Kodi pali mawu ena amene Yehova wakuwuza?” Yeremiya anayankha kuti, “Inde. Inu mfumu mudzaperekedwa kwa mfumu ya ku Babuloni.”
18 Derefter sa Jeremias til kong Sedekias: Hvad har jeg syndet mot dig og dine tjenere og dette folk, siden I har satt mig i fengsel?
Pamenepo Yeremiya anafunsa Mfumu Zedekiya kuti, “Kodi ndakulakwirani chiyani inuyo kapena akuluakulu anu kapenanso anthu awa, kuti mundiyike mʼndende?
19 Og hvor er nu eders profeter, de som profeterte for eder og sa: Babels konge skal ikke komme over eder og over dette land?
Kodi ali kuti aneneri anu amene anakuloserani kuti, ‘Mfumu ya ku Babuloni sidzakuthirani nkhondo pamodzi ndi dziko lino’?
20 Og hør nu, herre konge! La min ydmyke bønn bæres frem for ditt åsyn og send mig ikke tilbake til statsskriveren Jonatans hus, forat jeg ikke skal dø der!
Koma tsopano, mbuye wanga mfumu, chonde tamverani. Loleni ndinene pempho langa pamaso panu: Musandibwezere ku nyumba ya mlembi Yonatani, kuopa kuti ndingakafere kumeneko.”
21 På kong Sedekias' bud holdt de Jeremias i varetekt i vaktgården og gav ham et brød til hver dag fra bakernes gate, inntil alt brødet i byen var fortært. Og Jeremias blev sittende i vaktgården.
Tsono Mfumu Zedekiya analamula kuti Yeremiya asungidwe mʼbwalo la alonda. Ankamupatsa buledi tsiku ndi tsiku amene ankamugula kwa ophika buledi. Anapitiriza kutero mpaka buledi yense anatha mu mzindamo. Choncho Yeremiya anapitirira kukhala mʼbwalo la alonda.

< Jeremias 37 >