< Jeremias 28 >

1 I det samme år, i begynnelsen av Judas konge Sedekias' regjering, i det fjerde år, i den femte måned, sa Hananja, Assurs sønn, profeten fra Gibeon, til mig i Herrens hus i prestenes og alt folkets nærvær:
Chaka chomwecho mwezi wachisanu wa chaka chachinayi, poyambirira pa ulamuliro wa Zedekiya mfumu ya Yuda, mneneri Hananiya mwana wa Azuri, amene amachokera ku Gibiyoni, anandiwuza ine mʼNyumba ya Yehova pamaso pa ansembe ndi anthu onse kuti,
2 Så sier Herren, hærskarenes Gud, Israels Gud: Jeg har brutt i stykker Babels konges åk.
“Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akuti, ‘Ndidzathyola goli la mfumu ya ku Babuloni.
3 Om to år fører jeg tilbake til dette sted alle de kar i Herrens hus som Babels konge Nebukadnesar tok fra dette sted og førte til Babel.
Pasanathe zaka ziwiri ndidzabweretsa pa malo ano ziwiya zonse za ku Nyumba ya Yehova zimene Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni anazichotsa pa malo pano ndi kupita nazo ku Babuloni.
4 Og Judas konge Jekonja, Jojakims sønn, og alle de bortførte fra Juda som er kommet til Babel, fører jeg tilbake til dette sted, sier Herren; for jeg vil bryte Babels konges åk.
Ndidzabweretsanso pa malo pano Yekoniya mwana wa Yehoyakimu mfumu ya Yuda pamodzi ndi akapolo ena onse ochokera ku Yuda amene anapita ku Babuloni,’ akutero Yehova, ‘chifukwa ndidzathyola goli la mfumu ya ku Babuloni.’”
5 Da sa profeten Jeremias til profeten Hananja så prestene og alt folket som stod i Herrens hus, hørte det -
Pamenepo mneneri Yeremiya anayankha mneneri Hananiya pamaso pa ansembe ndi anthu onse amene anasonkhana mʼNyumba ya Yehova.
6 profeten Jeremias sa: Amen! Det gjøre Herren! Herren opfylle de ord som du profeterte, så han fører karene i Herrens hus og alle de bortførte tilbake fra Babel til dette sted!
Anati, “Ameni! Yehova achitedi zomwezo! Yehova akwaniritse mawu amene waloserawo. Iye abweretsenso pa malo pano ziwiya za mʼNyumba ya Yehova ndi akapolo onse kuchokera ku Babuloni.
7 Men hør nu dette ord som jeg taler for dine og for alt folkets ører:
Komabe, tamvera zimene nditi ndikuwuze iweyo pamodzi ndi anthu onse:
8 De profeter som har vært før mig og før dig fra fordums tid, de profeterte mot mange land og mot store riker om krig og ulykke og pest.
Kunali aneneri kalelo, ine ndi iwe tisanabadwe. Iwowa analosera za nkhondo, mavuto ndi mliri kuti zidzagwera mayiko ambiri ndi maufumu amphamvu.
9 Den profet som profeterer om fred, når hans ord går i opfyllelse, da kan alle se at han er en profet som Herren i sannhet har sendt.
Koma mneneri amene amalosera zamtendere adzadziwika kuti ndi woona ndi kuti watumidwa ndi Yehova ngati zimene wanenera zachitikadi.”
10 Da tok profeten Hananja åket av profeten Jeremias' nakke og brøt det i stykker.
Pamenepo mneneri Hananiya anachotsa goli mʼkhosi mwa mneneri Yeremiya nalithyola,
11 Og Hananja sa i alt folkets nærvær: Så sier Herren: Således vil jeg om to år bryte i stykker Babels konge Nebukadnesars åk og ta det av alle folkeslags nakke. Da gikk profeten Jeremias sin vei.
ndipo anawuza anthu onse kuti, “Yehova akuti, ‘Umu ndi mmene ndidzathyolere goli la Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni mʼkhosi mwa anthu a mitundu yonse pasanathe zaka ziwiri.’” Zitatero, mneneri Yeremiya anachoka.
12 Men efterat profeten Hananja hadde brutt i stykker åket og tatt det av profeten Jeremias' nakke, kom Herrens ord til Jeremias, og det lød så:
Patapita nthawi pangʼono, mneneri Hananiya atathyola goli mʼkhosi mwa mneneri Yeremiya, Yehova anawuza Yeremiya kuti,
13 Gå og si til Hananja: Så sier Herren: Et åk av tre har du brutt i stykker, men i stedet for det har du gjort et åk av jern.
“Pita, kawuze mneneri Hananiya kuti, ‘Yehova akuti: Iwe wathyola goli lamtengo, mʼmalo mwake Ine ndidzayika goli lachitsulo.
14 For så sier Herren, hærskarenes Gud, Israels Gud: Et åk av jern har jeg lagt på alle disse folkeslags nakke, forat de skal tjene Babels konge Nebukadnesar, og de skal tjene ham; også markens dyr har jeg gitt ham.
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Ndidzayika goli lachitsulo mʼkhosi mwa anthu a mitundu yonseyi kuti atumikire Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, ndipo iwo adzamutumikiradi. Ndipo ndamupatsanso ulamuliro ngakhale pa nyama zakuthengo.’”
15 Da sa profeten Jeremias til profeten Hananja: Hør nu, Hananja! Herren har ikke sendt dig, og du har fått dette folk til å sette sin lit til løgn.
Ndipo mneneri Yeremiya anawuza mneneri Hananiya kuti, “Tamvera, Hananiya! Iweyo Yehova sanakutume, koma iwe wanyenga anthuwa kuti akhulupirire zabodza.
16 Derfor sier Herren så: Se, jeg tar dig bort fra jorden; i dette år skal du dø, fordi du har preket frafall fra Herren.
Nʼchifukwa chake Yehova akuti, ‘Ndatsala pangʼono kukuchotsa pa dziko lapansi. Iwe ufa chaka chino chisanathe, chifukwa wakhala ukulalikira zowukira Yehova.’”
17 Og profeten Hananja døde i det samme år, i den syvende måned.
Mʼmwezi wachisanu ndi chiwiri wa chaka chomwecho, mneneri Hananiya anamwaliradi.

< Jeremias 28 >