< Jeremias 25 >

1 Dette er det ord som kom til Jeremias om hele Judas folk i Judas konge Jojakims, Josias' sønns fjerde år, det er Babels konge Nebukadnesars første år,
Yehova anayankhula ndi Yeremiya za anthu onse a ku Yuda mʼchaka chachinayi cha ufumu wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda, chimene chinali chaka choyamba cha ufumu wa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni.
2 og som profeten Jeremias talte til hele Judas folk og til alle Jerusalems innbyggere:
Choncho mneneri Yeremiya anawuza anthu onse a ku Yuda pamodzi ndi onse amene amakhala mu Yerusalemu kuti:
3 Fra Judas konge Josias', Amons sønns trettende år og like til denne dag, nu i tre og tyve år, er Herrens ord kommet til mig, og jeg har talt til eder tidlig og sent, men I hørte ikke.
Kwa zaka 23, kuyambira chaka cha 13 cha ufumu wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya ku Yuda mpaka lero lino, Yehova wakhala akundipatsa mauthenga ake ndipo ine ndakhala ndikuyankhula ndi inu kawirikawiri, koma inu simunamvere.
4 Og Herren sendte til eder alle sine tjenere, profetene, tidlig og sent; men I hørte ikke, og I bøide ikke eders øre til å høre.
Ndipo ngakhale Yehova kawirikawiri wakhala akukutumizirani atumiki ake onse, aneneri, inuyo simunamvere kapena kutchera khutu.
5 Han sa: Vend om, hver fra sin onde vei, og fra eders onde gjerninger! Så skal I få bo i det land Herren gav eder og eders fedre, fra evighet og til evighet.
Aneneriwo ankanena kuti, “Ngati aliyense wa inu abwerere, kusiya njira zake zoyipa ndi machitidwe ake oyipa, ndiye kuti mudzakhala mʼdziko limene Yehova anapereka kwa makolo anu kwamuyaya.
6 Følg ikke andre guder, så I dyrker dem og tilbeder dem, og vekk ikke min harme ved eders henders verk, forat jeg ikke skal gjøre eder noget ondt!
Musatsatire milungu ina nʼkuyitumikira ndi kuyipembedza. Musapute mkwiyo wanga ndi mafano amene mwapanga ndi manja anu. Mukatero Ine sindidzakuwonongani.
7 Men I hørte ikke på mig, sier Herren, I vakte min harme ved eders henders verk, til ulykke for eder selv.
“Koma inu simunandimvere,” akutero Yehova, “ndipo munaputa mkwiyo wanga ndi mafano amene munapanga ndi manja anu. Choncho munadziwononga nokha.”
8 Derfor sier Herren, hærskarenes Gud, så: Fordi I ikke har hørt på mine ord,
Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Chifukwa simunamvere mawu anga,
9 se, så sender jeg bud og henter alle Nordens folkeslag, sier Herren, og jeg sender bud til Babels konge Nebukadnesar, min tjener, og jeg lar dem komme over dette land og over dets innbyggere og over alle folkeslagene her rundt omkring, og jeg slår dem med bann og gjør dem til en forferdelse og til en spott og deres land til evige ørkener,
ndidzayitana mafuko onse akumpoto, pamodzi ndi mtumiki wanga Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni,” akutero Yehova, “ndipo adzathira nkhondo dziko lino ndi anthu ake pamodzi ndi mitundu yonse ya anthu ozungulira dzikoli. Ndidzawawononga kwathunthu ndi kuwasandutsa chinthu chochititsa mantha ndi chonyozeka, mpaka muyaya.
10 og jeg lar fryds røst og gledes røst, brudgoms røst og bruds røst, lyd av kvern og lys av lampe bli borte hos dem.
Ndidzathetsa mfuwu wachimwemwe ndi wachisangalalo, mawu a mkwati ndi mkwatibwi, phokoso la mphero ndi kuwala kwa nyale.
11 Og hele dette land skal bli til en ørken, til en ødemark, og disse folkeslag skal tjene Babels konge i sytti år.
Dziko lonse lidzakhala bwinja ndi chipululu, ndipo mitundu ina idzatumikira mfumu ya ku Babuloni kwa 70.
12 Men når sytti år er til ende, da vil jeg hjemsøke kongen i Babel og folket der, sier Herren, for deres misgjernings skyld, og jeg vil hjemsøke kaldeernes land og gjøre det til evige ørkener.
“Koma zaka 70 zikadzatha, ndidzalanga mfumu ya ku Babuloni pamodzi ndi anthu ake, chifukwa cha zolakwa zawo,” akutero Yehova, “ndipo dziko lawo lidzakhala chipululu mpaka muyaya.
13 Og jeg vil la komme over det land alle de ord som jeg har talt om det, alt det som er skrevet i denne bok, det som Jeremias har profetert om alle folkeslagene.
Ndidzachita zinthu zonse zimene ndinayankhula zotsutsa dzikolo, zonse zimene zalembedwa mʼbuku lino, ndiponso zonse zimene Yeremiya analosera zotsutsa anthu amenewa.
14 For mange folkeslag og store konger skal gjøre også dem til træler, og jeg vil gjengjelde dem efter deres gjerning og efter deres henders verk.
Iwo eni adzakhala akapolo a anthu a mitundu yochuluka ndi mafumu amphamvu. Ndidzawabwezera molingana ndi zochita zawo ndi ntchito za manja awo.”
15 For så sa Herren, Israels Gud, til mig: Ta dette beger med vredesvin av min hånd og gi alle de folk jeg sender dig til, å drikke av det!
Yehova, Mulungu wa Israeli, anandiwuza kuti, “Tenga chikho ichi chodzaza ndi vinyo wa ukali wanga, ndipo ukamwetse anthu a mitundu yonse kumene ndikukutuma.
16 Og de skal drikke og rave og te sig som rasende for det sverd jeg sender iblandt dem.
Akadzamwa adzayamba kudzandira ndi kuchita misala chifukwa cha nkhondo imene ndikuyitumiza pakati pawo.”
17 Og jeg tok begeret av Herrens hånd, og jeg gav alle de folk å drikke som Herren hadde sendt mig til:
Choncho ine ndinatenga chikhocho mʼdzanja la Yehova ndipo ndinamwetsa mitundu yonse ya anthu kumene Iye ananditumako:
18 Jerusalem og Judas byer og dets konger og dets høvdinger, for å gjøre dem til en ørken, til en ødemark, til en spott og til en forbannelse, således som det er på denne dag,
Anandituma ku Yerusalemu ndi ku mizinda ya Yuda, kwa mafumu ake ndi nduna zake kuti ndikawasandutse ngati bwinja ndi chinthu chochititsa mantha ndi chonyozeka ndiponso chotembereredwa, monga mmene alili lero lino.
19 Egyptens konge Farao og hans tjenere og hans høvdinger og hele hans folk
Ananditumanso kwa Farao, mfumu ya ku Igupto, kwa atumiki ake, nduna zake ndi kwa anthu ake onse,
20 og alle hans fremmede undersåtter og alle kongene i landet Us og alle kongene i filistrenes land, i Askalon og Gasa og Ekron og det som er tilbake av Asdod,
ndi kwa anthu ena onse a mitundu yachilendo; mafumu onse a ku Uzi; mafumu onse a Afilisti, a ku Asikeloni, ku Gaza, ku Ekroni ndiponso kwa anthu a ku chigwa chotsala cha Asidodi;
21 Edom og Moab og Ammons barn
Edomu, Mowabu ndi Amoni.
22 og alle Tyrus' konger og alle Sidons konger og kongene over kystlandet på hin side havet,
Ananditumanso kwa mafumu onse a ku Turo ndi ku Sidoni; kwa mafumu a kutsidya la nyanja;
23 Dedan og Tema og Bus og alle med rundklippet hår
ku Dedani, ku Tema, ku Buzi ndi kwa onse ometa chamʼmbali.
24 og alle Arabias konger og alle kongene over de fremmede folk som bor i ørkenen,
Ananditumanso kwa mafumu onse a ku Arabiya ndi mafumu onse a anthu achilendo amene amakhala mʼchipululu.
25 og alle Simris konger og alle Elams konger og alle Medias konger
Anandituma kwa mafumu onse a ku Zimuri, Elamu ndi Mediya;
26 og alle Nordens konger, nær og fjern, den ene med den andre, og alle verdens riker utover hele jorden; og Sesaks konge skal drikke efter dem.
ndiponso kwa mafumu onse a kumpoto, akufupi ndi kutali omwe, mafumu onse a dziko lapansi. Ndipo potsiriza pake, idzamwenso ndi mfumu Sesaki.
27 Og du skal si til dem: Så sier Herren, hærskarenes Gud, Israels Gud: Drikk og bli drukne og spy og fall og reis eder ikke mere - for det sverd jeg sender iblandt eder!
“Ndipo uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Imwani, ledzerani ndipo musanze, mugwe osadzukanso chifukwa cha nkhondo imene ndikutumiza pakati panu.’
28 Men dersom de ikke vil ta begeret av din hånd og drikke, da skal du si til dem: Så sier Herren, hærskarenes Gud: Drikke skal I.
Koma ngati akana kutenga chikhocho mʼdzanja lako ndi kumwa, uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti: Muyenera kumwa ndithu!’”
29 For se, den by som er kalt med mitt navn, lar jeg ulykken ramme først, og så skulde I bli ustraffede? Nei, I skal ikke bli ustraffede; for sverd kaller jeg hit over alle dem som bor på jorden, sier Herren, hærskarenes Gud.
Taonani, tsopano ndiyamba kulanga mzinda uno umene umadziwika ndi dzina langa. Kodi inu muganiza kuti simudzalangidwa? Ayi, simudzapulumuka chifukwa ndikutumiza nkhondo pa onse okhala pa dziko lapansi, akutero Yehova Wamphamvuzonse.
30 Og du skal profetere for dem alt dette og si til dem: Herren skal brøle fra det høie og la sin røst høre fra sin hellige bolig; ja, brøle skal han over sin beitemark, et skrik lik deres som treder vinpersen, skal han opløfte over alle dem som bor på jorden.
“Tsopano iwe nenera mawu owatsutsa ndipo uwawuze kuti, “‘Yehova adzabangula kumwamba; mawu ake adzamveka ngati bingu kuchokera ku malo ake opatulika. Adzabangula mwamphamvu kukalipira dziko lake. Iye adzafuwula ngati anthu oponda mphesa, kukalipira onse amene akukhala pa dziko lapansi.
31 Bulderet når til jordens ende, for Herren har strid med folkene, han går i rette med alt kjød; de ugudelige overgir han til sverdet, sier Herren.
Phokoso lalikulu lidzamveka mpaka kumalekezero a dziko lonse lapansi, chifukwa Yehova adzazenga mlandu anthu a mitundu yonse; adzaweruza mtundu wonse wa anthu ndipo oyipa adzawapha ndi lupanga,’” akutero Yehova.
32 Så sier Herren, hærskarenes Gud: Se, ulykke går ut fra folk til folk, og en svær storm reiser sig fra jordens ytterste ende.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani! Mavuto akuti akachoka pa mtundu wina akukagwa pa mtundu wina; mphepo ya mkuntho ikuyambira ku malekezero a dziko.”
33 Og de som Herren har drept, skal på den dag ligge fra jordens ene ende til den andre; ingen skal gråte over dem, ingen skal samle dem op og begrave dem; til gjødsel utover jorden skal de bli.
Pa tsiku limenelo, onse ophedwa ndi Yehova adzangoti mbwee ponseponse, pa dziko lonse lapansi. Palibe amene adzawalire kapena kusonkhanitsa mitemboyo kuti ikayikidwe mʼmanda, koma idzakhala mbwee ngati ndowe.
34 Hyl, I hyrder, og skrik og velt eder i støvet, I som er de gjeveste i hjorden! For tiden er kommet da I skal slaktes, og jeg vil adsprede eder, og I skal falle som et kostelig kar,
Khetsani misozi ndi kufuwula mwamphamvu, abusa inu; gubudukani pa fumbi, inu atsogoleri a nkhosa. Pakuti nthawi yanu yophedwa yafika; mudzagwa ndi kuphwanyika ngati mbiya yabwino kwambiri.
35 og hyrdene skal ikke mere ha noget tilfluktssted, og de gjeveste i hjorden skal ikke finne redning.
Abusa adzasowa kothawira, atsogoleri a nkhosa adzasowa malo opulumukira.
36 Hør hvorledes hyrdene skriker og de gjeveste i hjorden hyler! For Herren ødelegger deres beite,
Imvani kulira kwa abusa, atsogoleri a nkhosa akulira, chifukwa Yehova akuwononga msipu wawo.
37 og de fredelige enger blir øde for Herrens brennende vrede.
Makola awo a nkhosa amene anali pamtendere adzasanduka bwinja chifukwa cha mkwiyo woopsa wa Yehova.
38 Som en ung løve går han frem fra sitt skjul; ja, deres land blir til en ødemark for det herjende sverd og for hans brennende vrede.
Ngati mkango, Yehova wasiya phanga lake, pakuti dziko lawo lasanduka chipululu chifukwa cha nkhondo ya owazunza ndiponso chifukwa cha mkwiyo woopsa wa Yehova.

< Jeremias 25 >