< Esaias 1 >

1 Dette er de syner som Esaias, sønn av Amos, så om Juda og Jerusalem i de dager da Ussias, Jotam, Akas og Esekias var konger i Juda.
Masomphenya wonena za Yuda ndi Yerusalemu, amene Yesaya mwana wa Amozi, anaona pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a Yuda.
2 Hør, I himler, og lytt til, du jord! For Herren taler: Barn har jeg opfødd og fostret; men de er falt fra mig.
Tamverani, miyamba inu! Tchera khutu, iwe dziko lapansi! Pakuti Yehova wanena kuti, “Ndinabala ana ndi kuwalera, koma anawo andiwukira Ine.
3 En okse kjenner sin eiermann, og et asen sin herres krybbe; Israel kjenner intet, mitt folk forstår intet.
Ngʼombe imadziwa mwini wake, bulu amadziwa kumene kuli gome la mbuye wake, koma Israeli sadziwa, anthu anga samvetsa konse.”
4 Ve det syndige folk, det folk med tung misgjerning, den yngel av ugjerningsmenn, de vanartede barn! De har forlatt Herren, har foraktet Israels Hellige, er veket fra ham.
Haa, mtundu wochimwa, anthu olemedwa ndi machimo, obadwa kwa anthu ochita zoyipa, ana odzipereka ku zoyipa! Iwo asiya Yehova; anyoza Woyerayo wa Israeli ndipo afulatira Iyeyo.
5 Hvorfor vil I la eder slå fremdeles? Hvorfor øker I eders frafall? Hvert hode er sykt, og hvert hjerte er svakt.
Chifukwa chiyani mukufuna kuti muzingolangidwabe? Chifukwa chiyani mukupitirira kukhala mʼmoyo wowukira? Mutu wanu wonse uli ndi mabala, mtima wanu wonse wafowokeratu.
6 Fra fotsåle til hode er der intet helt på det; sår, buler og friske slag! De er ikke klemt ut og ikke forbundet og ikke utbløtt med olje.
Kuchokera ku phazi mpaka ku mutu palibe pabwino, paliponse pali mikwingwirima ndi zilonda, mabala ali magazi chuchuchu, mabala ake ngosatsuka, ngosamanga ndiponso ngosapaka mafuta ofewetsa.
7 Eders land er en ørken, eders byer opbrent med ild; eders jord opetes av fremmede for eders øine, og en ørken er der, som efter fremmedes herjing.
Dziko lanu lasanduka bwinja, mizinda yanu yatenthedwa ndi moto; minda yanu ikukololedwa ndi alendo inu muli pomwepo, dziko lanu lasanduka bwinja monga ngati lagonjetsedwa ndi alendo.
8 Bare Sions datter er blitt igjen som en løvhytte i en vingård, som en vekterhytte på en agurkmark, som en kringsatt by.
Mwana wamkazi wa Ziyoni watsala yekha ngati nsanja mʼmunda wampesa, ngati chisimba mʼmunda wa minkhaka, ngati mzinda wozingidwa ndi nkhondo.
9 Hadde ikke Herren, hærskarenes Gud, levnet oss en liten rest, da var vi som Sodoma, da lignet vi Gomorra.
Yehova Wamphamvuzonse akanapanda kutisiyira opulumuka, tikanawonongeka ngati Sodomu, tikanakhala ngati anthu a ku Gomora.
10 Hør Herrens ord, I Sodomafyrster! Lytt til vår Guds lov, du Gomorra-folk!
Imvani mawu a Yehova, inu olamulira Sodomu; mverani lamulo la Mulungu wathu, inu anthu a ku Gomora!
11 Hvad skal jeg med eders mange slaktoffer? sier Herren; jeg er mett av brennoffer av værer og av gjøkalvers fett, og til blod av okser og lam og bukker har jeg ikke lyst.
Yehova akuti, “Kodi ndili nazo chiyani nsembe zanu zochuluka?” “Zandikola nsembe zanu zopsereza za nkhosa zazimuna ndiponso mafuta a nyama zonenepa; sindikusangalatsidwanso ndi magazi angʼombe zamphongo ndi a ana ankhosa ndi ambuzi zazimuna.
12 Når I kommer for å vise eder for mitt åsyn, hvem har da krevd dette av eder at I skal nedtrede mine forgårder?
Ndani anakulamulirani kuti mubwere nazo pamaso panga? Ndani anakuwuzani kuti muzipondaponda mʼmabwalo a nyumba yanga?
13 Kom ikke mere frem med tomt matoffer! Det er mig en vederstyggelig røkelse. Nymåne og sabbat, festlig forsamling - jeg tåler ikke høitid og urett sammen.
Siyani kubweretsa nsembe zachabechabezo! Nsembe zanu zofukiza zimandinyansa Ine. Sindingapirire misonkhano yanu yoyipa, kapenanso zikondwerero za Mwezi Watsopano ndi Masabata.
14 Eders nymåner og fester hater min sjel, de er blitt mig en byrde; jeg er trett av å bære dem.
Zikondwerero zanu za Mwezi Watsopano ndi masiku anu opatulika ndimadana nazo. Zasanduka katundu wondilemera; ndatopa kuzinyamula.
15 Og når I breder ut eders hender, skjuler jeg mine øine for eder; om I enn beder meget, hører jeg ikke; eders hender er fulle av blod.
Mukamatambasula manja anu popemphera, Ine sindidzakuyangʼanani; ngakhale muchulukitse mapemphero anu, sindidzakumverani. Manja anu ndi odzaza ndi magazi;
16 Tvett eder, rens eder, ta eders onde gjerninger bort fra mine øine, hold op å gjøre det som er ondt!
sambani, dziyeretseni. Chotsani pamaso panu ntchito zanu zoyipa! Lekani kuchita zoyipa,
17 Lær å gjøre det gode, legg vinn på det som er rett, vis voldsmannen på rett vei, hjelp den farløse til hans rett, før enkens sak!
phunzirani kuchita zabwino! Funafunani chilungamo, thandizani oponderezedwa. Tetezani ana amasiye, muwayimirire akazi amasiye pa milandu yawo.”
18 Kom og la oss gå i rette med hverandre, sier Herren; om eders synder er som purpur, skal de bli hvite som sne; om de er røde som skarlagen, skal de bli som den hvite ull.
Yehova akuti, “Tiyeni tsono tikambe mlandu wanu. Ngakhale machimo anu ali ofiira, adzayera ngati thonje. Ngakhale ali ofiira ngati kapezi, adzayera ngati ubweya wankhosa.
19 Er I villige og hører, skal I ete landets gode ting,
Ngati muli okonzeka kundimvera mudzadya zinthu zabwino za mʼdziko;
20 men er I uvillige og gjenstridige, skal I bli opett av sverdet; for Herrens munn har talt.
koma mukakana ndi kuwukira mudzaphedwa ndi lupanga.” Pakuti Yehova wayankhula.
21 Hvor den er blitt til en horkvinne, den trofaste by, som var full av rett, hvor rettferd hadde hjemme, og nu - mordere!
Taonani momwe mzinda wokhulupirika wasandukira wadama! Mzinda umene kale unali wodzaza ndi chiweruzo cholungama; mu mzindamo munali chilungamo, koma tsopano muli anthu opha anzawo!
22 Ditt sølv er blitt til slagger, din vin blandet op med vann;
Siliva wako wasanduka wachabechabe, vinyo wako wabwino wasungunulidwa ndi madzi.
23 dine førere er oprørere og tyvers stallbrødre; enhver av dem elsker bestikkelse og jager efter gaver; den farløse hjelper de ikke til hans rett, og enkens sak tar de sig ikke av.
Atsogoleri ako ndi owukira, anthu ogwirizana ndi mbala; onse amakonda ziphuphu ndipo amathamangira mphatso. Iwo sateteza ana amasiye; ndipo samvera madandawulo a akazi amasiye.
24 Derfor sier Herren, Israels Gud, hærskarenes Gud, Israels Veldige: Ve! Jeg vil kjøle min harme på mine motstandere og ta hevn over mine fiender.
Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvu, Wamphamvuyo wa Israeli, akunena kuti, “Haa, odana nane ndidzawatha, ndipo ndidzawabwezera ndekha adani anga.
25 Og jeg vil igjen ta mig av dig og smelte ut dine slagger som med lutsalt og skille ut alt ditt bly.
Ndidzatambasula dzanja langa kuti ndilimbane nawe; ndidzasungunula machimo ako nʼkuwachotsa, monga mmene amachotsera dzimbiri ndi mankhwala.
26 Og jeg vil atter gi dig slike dommere som i førstningen og rådsherrer som i begynnelsen; derefter skal du kalles rettferdighetens stad, en trofast by.
Ndidzabwezeretsa oweruza ako ngati masiku amakedzana, aphungu ako ndidzawabwezeretsa ngati poyamba paja. Kenaka iweyo udzatchedwa mzinda wolungama, mzinda wokhulupirika.”
27 Sion skal forløses ved rett, og de omvendte der ved rettferdighet.
Ziyoni adzawomboledwa mwa chiweruzo cholungama, anthu ake olapadi adzapulumutsidwa mwachilungamo.
28 Men undergang skal ramme alle overtredere og syndere, og de som forlater Herren, skal omkomme;
Koma owukira ndi ochimwa adzawawonongera pamodzi, ndipo amene asiya Yehova adzatheratu.
29 for de skal få skam av de eketrær som er eders lyst, og I skal bli til skamme ved de haver som I har så kjær;
“Mudzachita nayo manyazi mitengo ya thundu imene inkakusangalatsani; mudzagwetsa nkhope chifukwa cha minda imene munayipatula.
30 for I skal bli som en ek med visne blad og som en have uten vann.
Mudzakhala ngati mtengo wa thundu umene masamba ake akufota, mudzakhala ngati munda wopanda madzi.
31 Og den sterke skal bli til stry, og hans gjerning til en gnist, og de skal brenne begge tilsammen, og der er ingen som slukker.
Munthu wamphamvu adzasanduka ngati udzu wowuma, ndipo ntchito zake zidzakhala ngati mbaliwali; motero zonse zidzayakira limodzi, popanda woti azimitse motowo.”

< Esaias 1 >