< Esaias 29 >

1 Ve Ariel, Ariel, du by hvor David slo leir! Legg år til år, la høitidene gå sin rundgang!
Tsoka kwa iwe, Arieli, Arieli, mzinda umene Davide anakhazikitsamo zithando za nkhondo! Papite chaka chimodzi kapena ziwiri ndipo masiku a zikondwerero zanu azipitirirabe ndithu.
2 Da vil jeg gjøre det trangt for Ariel, og der skal være sorg og jammer; men så skal det bli mig et virkelig Ariel.
Komatu Ine ndidzathira nkhondo Arieli ndipo kudzakhala kulira ndi kudandaula, mzindawo udzasanduka ngati ngʼanjo ya guwa lansembe.
3 Jeg vil slå leir rundt omkring dig, og jeg vil kringsette dig med vaktposter og bygge voller mot dig.
Ine ndidzamanga misasa ya nkhondo kulimbana ndi mzindawo; ndidzakuzungulira ndi nsanja za nkhondo ndi kumanga mitumbira yanga ya nkhondo kulimbana nawe.
4 Da skal du tale lavmælt fra jorden, og fra støvet skal du mumle frem dine ord; og din røst skal lyde fra jorden likesom fra en dødningemaner, og fra støvet skal din tale hviskes.
Utagwetsedwa pansi, iwe udzayankhula kuchokera mʼnthaka, mawu ako adzatuluka uli mʼfumbi, adzamveka ngati a mzukwa. Mawu ako adzamveka ngati onongʼona kuchokera mʼfumbi.
5 Men så skal dine fienders mengde bli som fint støv, og voldsmennenes flokk som fykende agner, og det skal skje i et øieblikk, med ett.
Koma chigulu cha adani ako chidzasanduka chifwirimbwiti. Chigulu cha ankhondo achilendo chidzabalalika ngati mungu wowuluzika ndi mphepo. Mwadzidzidzi ndi mosayembekezereka,
6 Fra Herren, hærskarenes Gud, skal det komme en hjemsøkelse med bulder og brak og veldige drønn, hvirvelvind og storm og fortærende ildslue.
Yehova Wamphamvuzonse adzabwera ndi mabingu ndi chivomerezi ndi phokoso lalikulu, kamvuluvulu ndi namondwe ndi malawi a moto wonyeketsa.
7 Og mengden av alle de hedningefolk som strider mot Ariel, skal bli som en drøm, et syn om natten, alle de som strider mot det og dets borg, og som trenger inn på det.
Tsono chigulu chankhondo cha mitundu ina yonse chimene chikulimbana ndi mzinda wa Arieli nʼkumathira nkhondo mzindawo, malinga ake ndi kuwuzinga, chigulu chonsecho chidzazimirira ngati maloto, gati zinthu zoziona mʼmasomphenya usiku.
8 Og det skal gå som når den sultne drømmer og synes han eter, men når han våkner, da er han tom, og som når den tørste drømmer og synes han drikker, men når han våkner, se, da er han matt, og hans sjel blir maktløs; således skal det gå alle de mange hedningefolk som strider mot Sions berg.
Chidzakhala ngati munthu wanjala wolota akudya, koma podzuka ali nayobe njala; kapena ngati munthu waludzu wolota akumwa, koma podzuka, ali nalobe ludzu, kummero kwake kuli gwaa. Izi zidzachitika pamene chigulu cha nkhondo cha mitundu ina yonse chikunthira nkhondo Phiri la Ziyoni.
9 Stirr på hverandre og bli forvirret! Stirr eder blinde, og vær blinde! I er drukne, men ikke av vin; I raver, men ikke av sterk drikk.
Pitirizani kuledzera ndipo mudzakhala opusa. Dzitsekeni mʼmaso ndipo mukhale osapenya, ledzerani, koma osati ndi vinyo, dzandirani, koma osati ndi mowa.
10 For Herren har utøst over eder en dyp søvns ånd, og han har tillukket eders øine, profetene, og tildekket eders hoder, seerne.
Yehova wakugonetsani tulo tofa nato. Watseka maso anu, inu aneneri; waphimba mitu yanu, inu alosi.
11 Og således er synet av alt dette blitt eder likesom ordene i en forseglet bok; gir en den til en som skjønner skrift, og sier: Les dette! så sier han: Jeg kan ikke, for den er forseglet.
Kwa inu mawu onsewa ali ngati buku lotsekedwa, ndipo ngati lipatsidwa kwa wina wodziwa kuwerenga ndi kunena kuti, “Chonde tawerengani bukuli,” iye adzati, “Sindingathe popeza ndi lomatidwa.”
12 Eller en rekker boken til en som ikke skjønner skrift, med de ord: Les dette! så sier han: Jeg skjønner ikke skrift.
Kapena ngati lipatsidwa kwa amene sadziwa kuwerenga ndi kunena kuti, “Chonde werenga bukuli,” iye adzayankha kuti, “Ine sindidziwa kuwerenga.”
13 Og Herren sier: Fordi dette folk holder sig nær til mig med sin munn og ærer mig med sine leber, men holder sitt hjerte langt borte fra mig, og deres frykt for mig er et menneskebud som de har lært,
Ambuye akuti, “Anthu awa amandipembedza Ine ndi pakamwa pawo, ndi kundilemekeza Ine ndi milomo yawo, koma mitima yawo ili kutali ndi Ine. Kundipembedza kwawo ndi kwa chiphamaso. Amandipembedza motsata malamulo a anthu amene anaphunzitsidwa.
14 se, derfor vil jeg bli ved å gå underlig frem mot dette folk, underlig og forunderlig, og dets vismenns visdom skal forgå, og dets forstandige menns forstand skal skjule sig.
Nʼchifukwa chakenso Ine ndidzapitirira kuwachitira ntchito zodabwitsa; nzeru za anthu anzeru zidzatha, luntha la anthu aluntha Ine ndidzalinyoza.”
15 Ve dem som vil skjule i det dype for Herren hvad de har fore, og hvis gjerninger skjer i mørke, og som sier: Hvem ser oss, og hvem kjenner oss?
Tsoka kwa amene amayesetsa kubisira Yehova maganizo awo, amene amachita ntchito zawo mu mdima nʼkumanena kuti, “Ndani amene akundiona kapena ndani akudziwa zimene ndikuchita?”
16 Hvor forvendte I er! - Er pottemakeren å akte som hans ler, så verket kunde si om ham som gjorde det: Han har ikke gjort mig, og det som er laget, si om ham som laget det: Han skjønner det ikke?
Inu mumazondotsa zinthu ngati kuti dothi lasanduka wowumba mbiya. Kodi chinthu chopangidwa chingawuze wochipanga kuti “Sunandipange ndi iwe?” Kapena mʼphika kunena kwa amene anawuwumba kuti, “Iwe sudziwa chilichonse?”
17 Ennu bare en liten stund, så skal Libanon bli til fruktbar mark, og den fruktbare mark aktes som skog.
Kodi Lebanoni posachedwapa sadzasanduka munda wachonde, ndipo kodi munda wachondewo ngati nkhalango?
18 Og på den dag skal de døve høre bokens ord, og ut fra mulm og mørke skal de blindes øine se,
Tsiku limenelo anthu osamva adzamva mawu a mʼbuku, ndipo anthu osaona amene ankakhala mu mdima adzapenya.
19 Og de saktmodige skal glede sig enn mere i Herren, og de fattige blandt menneskene skal fryde sig i Israels Hellige;
Anthu odzichepetsa adzakhalanso ndi chimwemwe mwa Yehova; ndipo anthu osowa adzakondwa chifukwa cha Woyerayo wa Israeli.
20 for det er forbi med voldsmannen, og det er ute med spotteren, og utryddet blir alle de som er årvåkne til å gjøre urett,
Koma anthu ankhanza adzazimirira, oseka anzawo sadzaonekanso, ndipo onse okopeka ndi zoyipa adzawonongedwa.
21 de som gjør et menneske til synder for et ords skyld og legger snarer for den som hevder retten på tinget, og som ved løgn bøier retten for den rettferdige.
Yehova adzalanga amene amasinjirira munthu kuti apezeke wolakwa, kapena kuphophonyetsa anthu ozenga mlandu ndi umboni wonama kuti osalakwa asaweruzidwe mwachilungamo.
22 Derfor sier Herren så til Jakobs hus, Herren som forløste Abraham: Nu skal Jakob ikke bli til skamme, og nu skal hans åsyn ikke blekne;
Choncho Yehova amene anawombola Abrahamu, akunena kwa zidzukulu za Yakobo kuti, “Anthu anga sadzachitanso manyazi; nkhope zawo sizidzagwanso ndi manyazi.
23 for når han og hans barn ser mine henders gjerning i sin midte, så skal de hellige mitt navn, og de skal hellige Jakobs Hellige, og Israels Gud skal de frykte.
Akadzaona ana awo ndi ntchito ya manja anga pakati pawo, adzatamanda dzina langa loyera; adzazindikira kuyera kwa Woyerayo wa Yakobo, ndipo adzachita naye mantha Mulungu wa Israeli.
24 Og de hvis ånd fór vill, skal lære forstand, og de knurrende skal ta imot lærdom.
Anthu opusa adzapeza nzeru; onyinyirika adzalandira malangizo.”

< Esaias 29 >