< Esaias 28 >

1 Ve Efra'ims drukne menns stolte krone og den falmende blomst, hans fagre pryd, som troner over den fete dal, der de ligger drukne av vin.
Tsoka ufumu wonyada wa zidakwa za ku Efereimu. Tsoka kwa ulemerero wake wokongola umene ukufota ngati duwa limene lili pa mutu pa anthu oledzera a mʼchigwa chachonde.
2 Se, Herren sender en som er sterk og veldig, lik en haglskur, en ødeleggende storm; som en flom av mektige, overstrømmende vann slår han alt til jorden med makt.
Taonani, ambuye ali naye wina wamphamvu ndi nyonga. Iye adzabwera ngati mkuntho wamatalala ndi namondwe wowononga, ngati madzi amphamvu osefukira a mvula yamkuntho; ndipo adzawagwetsa pansi mwankhanza.
3 Med føtter skal den tredes ned, Efra'ims drukne menns stolte krone,
Ulamuliro wa atsogoleri oledzera a ku Efereimu adzawuthetsa.
4 og med den falmende blomst, hans fagre pryd, som troner over den fete dal, skal det gå som med den fiken som er moden før sommeren er der: Så snart en ser den, sluker han den, mens den ennu er i hans hånd.
Ndipo ulemerero wokongola wa mzinda umene uli ngati duwa lofota pamutu pa anthu oledzera a mʼchigwa chachonde uja, udzakhala ngati nkhuyu yoyambirira kupsa imene munthu akangoyiona amayithyola nthawi yokolola isanakwane.
5 På den tid skal Herren, hærskarenes Gud, være en fager krone og en herlig krans for resten av sitt folk,
Tsiku limenelo Yehova Wamphamvuzonse adzakhala ngati nkhata yaufumu, chipewa chokongola kwa anthu ake otsala.
6 og en doms ånd for den som sitter til doms, og styrke for dem som driver krigen tilbake til porten.
Iye adzapereka mtima wachilungamo kwa oweruza, adzakhala chilimbikitso kwa amene amabweza adani pa zipata za mzinda.
7 Men også de som er her, raver av vin og tumler av sterk drikk; prest og profet raver av sterk drikk, er overveldet av vin, tumler av sterk drikk; de raver i sine syner, vakler i sine dommer;
Nawonso awa ali dzandidzandi chifukwa cha vinyo ndipo akusochera chifukwa cha mowa: ansembe ndi aneneri akudzandira chifukwa cha mowa ndipo akusokonezeka chifukwa cha vinyo; akusochera chifukwa cha mowa, akudzandira pamene akuona masomphenya, kupunthwa pamene akupereka chigamulo.
8 for alle bord er fulle av vemmelig spy, det finnes ikke en ren flekk.
Pa matebulo onse pali masanzi okhaokha ndipo palibenso malo wopanda zonyansa.
9 Hvem vil han lære kunnskap, og hvem vil han få til å forstå budskap? Er det barn som nettop er avvent fra melken, tatt bort fra brystet?
Iwo akuti, “Kodi munthu ameneyu akufuna aphunzitse ndani? Uthengawu akufuna kufotokozera yani? Ndi kwa ana amene aleka kuyamwa, kwa makanda ongowachotsa kumene ku bere?
10 For bud på bud, bud på bud, regel på regel, regel på regel, litt her, litt der.
Akuyesa kumatiphunzitsa pangʼonopangʼono lemba ndi lemba, mzere ndi mzere, phunziro ndi phunziro. Zonsezi akungoti apa pangʼono apa pangʼono.”
11 Ja, ved folk med stammende leber og i et annet tungemål skal han tale til dette folk,
Mulungu adzayankhula kwa anthu ake kudzera mwa anthu aziyankhulo zachilendo, ziyankhulo zosamveka bwino. Mulungu adzayankhula kwa anthu awa, amene
12 han som sa til dem: Dette er ro, unn den mødige ro, og dette er hvile. Men de vilde ikke høre.
anakuwuzani kuti, “Malo opumulira ndi ano, otopa apumule, malo owusira ndi ano.” Koma inu simunamvere.
13 Så skal da Herrens ord bli dem bud på bud, bud på bud, regel på regel, regel på regel, litt her, litt der, så de skal gå og falle baklengs og knuses og bindes og fanges.
Choncho Yehova adzakuphunzitsani pangʼonopangʼono lemba ndi lemba, mzere ndi mzere, phunziro ndi phunziro. Kotero mudzayenda ndi kugwa chambuyo, adzapweteka ndi kukodwa mu msampha ndipo adzakutengani ku ukapolo.
14 Derfor hør Herrens ord, I spottere, I som hersker over folket her i Jerusalem!
Nʼchifukwa chake imvani mawu a Yehova, inu anthu achipongwe amene mumalamulira anthu awa mu Yerusalemu.
15 Fordi I sier: Vi har gjort en pakt med døden og et forbund med dødsriket; når den susende svepe farer frem, skal den ikke nå oss; for vi har gjort løgn til vår tilflukt og svik til vårt skjul - (Sheol h7585)
Inu mumayankhula monyada kuti, “Ife tinachita pangano ndi imfa, ife tachita mgwirizano ndi manda. Pamene mliri woopsa ukadzafika sudzatikhudza ife, chifukwa timadalira bodza ngati pothawirapo pathu ndi chinyengo ngati malo anthu obisalapo.” (Sheol h7585)
16 derfor sier Herren, Israels Gud, så: Se, jeg har lagt i Sion en grunnsten, en prøvet sten, en kostelig, fast hjørnesten; den som tror, haster ikke.
Tsono zimene Ambuye Yehova akunena ndi izi: “Taonani, ndikuyika mwala wovomerezeka ndi amisiri ngati maziko mu Ziyoni, mwala wapangodya, wamtengowapatali wopanga maziko amphamvu; munthu amene awukhulupirira sadzagwedezeka.
17 Og jeg vil gjøre rett til målesnor og rettferdighet til lodd, og hagl skal rive bort løgnens tilflukt, og skjulet skal vannene skylle bort.
Ntchito zolungama zidzakhala ngati chingwe choyezera maziko ake, ndipo chilungamo chidzakhala chowongolera mzere; matalala adzawononga malo anu othawirapo, amene ndi mabodza, ndipo madzi adzamiza malo anu obisalako.
18 Og eders pakt med døden skal slettes ut, og eders forbund med dødsriket skal ikke stå fast; når den susende svepe farer frem, da skal I bli trådt ned. (Sheol h7585)
Pangano limene munachita ndi imfa lidzathetsedwa; mgwirizano wanu ndi manda udzachotsedwa. Pakuti mliri woopsa udzafika, ndipo udzakugonjetsani. (Sheol h7585)
19 Hver gang den farer frem, skal den rive eder bort; hver morgen skal den fare frem, både dag og natt, og det skal være bare redsel å forstå budskapet;
Ndipo ukadzangofika udzakutengani. Udzafika mmawa uliwonse, usiku ndi usana.” Anthu akadzamvetsetsa uthenga umenewu adzaopsedwa kwambiri.
20 for sengen er for kort til å strekke sig ut i, og teppet for smalt til å svøpe sig i.
Mudzakhala ngati munthu wogona pa bedi lalifupi kwambiri kuti sangathe kutambalitsapo miyendo; ndiponso mudzakhala ngati munthu amene wafunda bulangeti lochepa kwambiri kuti sangathe nʼkufunda komwe.
21 For Herren skal reise sig likesom ved Perasim-fjellet, som i dalen ved Gibeon skal han vredes, for å gjøre sin gjerning? en underlig gjerning, og utrette sitt arbeid, et uhørt arbeid.
Yehova adzamenya nkhondo monga anachitira ku phiri la Perazimu adzakalipa monga anachitira ku chigwa cha Gibiyoni; adzagwira ntchito yake yooneka ngati yachilendo, ndipo zimene ati adzachite zidzakhala ngati zodabwitsa.
22 Og nu, spott ikke, forat ikke eders bånd skal bli strammet! For tilintetgjørelse og fast besluttet straffedom over hele jorden har jeg hørt fra Herren, Israels Gud, hærskarenes Gud.
Tsopano lekani kunyoza, mukapanda kutero maunyolo anu adzakuthinani kwambiri; Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse wandiwuza kuti, “Ndagamula kuti ndidzawononga dziko lapansi.”
23 Vend øret til og hør min røst, gi akt og hør min tale!
Tcherani khutu ndipo mumve mawu anga; mvetserani ndipo mumve zimene ndikunena.
24 Når plogmannen vil så, holder han da alltid på med å pløie, åpne og harve sin jord?
Kodi mlimi wofuna kudzala mbewu amangokhalira kutipula kokhakokha? Kodi amangokhalira kugawula ndi kugalawuza kokhakokha?
25 Når han har jevnet sin aker, spreder han da ikke ut dill og karve og sår hvete i rader og bygg på avmerket sted og spelt i kanten?
Pamene iye wasalaza mundawo, kodi samafesa mawere ndi chitowe? Kodi suja samadzala tirigu ndi barele mʼmizere yake, nadzala mchewere mʼphepete mwa mundawo?
26 Hans Gud har vist ham den rette måte, han lærte ham det.
Mulungu wake amamulangiza ndi kumuphunzitsa njira yabwino.
27 For en tresker ikke dill med treskeslede, ruller heller ikke vognhjul over karve; men med stav banker en ut dill, og karve med kjepp.
Mawere sapunthira chopunthira cha galeta lopanda mikombero, kapena chitowe sapuntha popondetsapo mikombero ya galeta; mawere amapuntha ndi ndodo ndipo chitowe amapuntha ndi kamtengo.
28 Blir vel brødkorn knust? Nei, en tresker det ikke uavlatelig, og når en driver sine vognhjul og sine hester over det, knuser en det ikke.
Tirigu ayenera kusinjidwa kuti apangire buledi, komabe munthu samangokhalira kupuntha tiriguyo osalekeza, kuopa kuti angatekedzeke. Ngakhale kuti amapuntha tiriguyo poyendetsapo mikombero ya galeta, koma akavalo ake satekedza tiriguyo.
29 Også dette kommer fra Herren, hærskarenes Gud; han er underfull i råd, stor i visdom.
Izinso zimachokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, wa uphungu wodabwitsa ndi wa nzeru zopambana.

< Esaias 28 >