< Esaias 19 >

1 Utsagn om Egypten. Se, Herren farer frem på en lett sky og kommer til Egypten, og Egyptens avguder bever for hans åsyn, og egypternes hjerter smelter i deres indre.
Uthenga onena za Igupto: Taonani, Yehova wakwera pa mtambo waliwiro, ndipo akupita ku Igupto. Mafano a ku Igupto akunjenjemera pamaso pake, ndipo mitima ya Aigupto yachokamo ndi mantha.
2 Og jeg vil egge egypter mot egypter, så de skal stride hver mot sin bror og hver mot sin næste, by mot by, rike mot rike.
“Ine ndidzadzutsa Aigupto kuti amenyane okhaokha; mʼbale adzamenyana ndi mʼbale wake, mnansi ndi mnansi wake, mzinda ndi mzinda unzake, ndiponso ufumu ndi ufumu unzake.
3 Og egypternes ånd skal svikte i deres indre, og deres råd vil jeg gjøre til intet; de skal søke til sine avguder og trollmenn og dødningemanere og sannsigere.
Aigupto adzataya mtima popeza ndidzalepheretsa zolinga zawo; adzapempha nzeru kwa mafano awo ndiponso kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa, kwa amawula ndi kwa oyankhula ndi mizimu.
4 Jeg vil overgi Egypten i en hård herres hånd, og en streng konge skal herske over dem, sier Herren, Israels Gud, hærskarenes Gud.
Ndidzawapereka Aigupto kwa olamulira ankhanza, ndipo mfumu yoopsa idzawalamulira,” akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.
5 Og vannet i havet blir borte, og elven blir tørr, aldeles uttørret,
Madzi a mu mtsinje wa Nailo adzaphwa, ndipo mʼmbali mwa mtsinje mudzangʼaluka ndi kuwuma.
6 og elvene stinker, Egyptens strømmer minker og blir tørre; rør og siv visner;
Ngalande zake zidzanunkha; ndipo mitsinje ya Igupto idzayamba kuchepa ndi kuwuma. Bango ndi dulu zidzafota,
7 engene ved strømmen, ved strømmens bredd, og alt akerland ved strømmen tørker bort, spredes av vinden og er ikke mere.
ndiponso zomera za mʼmphepete mwa Nailo ndi ku mathiriro a mtsinjewo. Zonse zodzalidwa mʼmbali mwa Nailo zidzawuma, zidzawuluzika ndipo sizidzaonekanso.
8 Fiskerne klager, og alle de som kaster krok i strømmen, sørger, og de som setter garn i vannet, er motløse,
Asodzi adzabuwula ndi kudandaula, onse amene amaponya mbedza mu Nailo; onse amene amaponya makoka mʼmadzi adzalira.
9 og de som arbeider med heklet lin, blir til skamme, og de som vever fint hvitt tøi.
Amene amagwira ntchito yopota thonje adzataya mtima, anthu oluka nsalu zofewa zabafuta adzataya chiyembekezo.
10 Landets grunnpiller er knust; alle de som arbeider for lønn, er sorgfulle i hu.
Akatswiri opanga nsalu adzangoti kakasi, ndipo anthu onse ogwira ntchito yolipidwa adzatheratu mphamvu.
11 Bare dårer er Soans høvdinger; de viseste blandt Faraos rådgivere gir uforstandige råd. Hvorledes kan I si til Farao: Jeg er en ætling av vismenn, en ætling av fortidens konger?
Akuluakulu a ku Zowani ndi zitsiru; aphungu a nzeru a Farao amalangiza zopusa. Kodi mungathe kunena bwanji kwa Farao kuti, “Ine ndine mmodzi mwa anthu anzeru, wophunzira wa mafumu akale?”
12 Hvor er de da dine vismenn, at de kunde forkynne dig, at de kunde forstå hvad råd Herren, hærskarenes Gud, har tatt om Egypten?
Iwe Farao, anthu ako anzeru ali kuti? Abweretu kuti akuwuze ndi kukudziwitsa zimene Yehova Wamphamvuzonse wakonza kuchitira dziko la Igupto.
13 Soans høvdinger er blitt dårer, Nofs høvdinger er blitt narret, og overhodene for stammene har ført Egypten vill.
Akuluakulu a ku Zowani asanduka zitsiru, atsogoleri a ku Mefisi anamizidwa; atsogoleri a dziko la Igupto asocheretsa anthu a dzikolo.
14 Herren har utøst i deres indre en svimmelhets-ånd, og de har ført Egypten vill i all dets gjerning, som en drukken mann forvillet tumler om i sitt spy.
Yehova wasocheretsa anthu a ku Igupto. Iwo akuchita kudzandira pa zonse zimene akuchita, ngati chidakwa choterereka pa masanzi ake.
15 Og ikke skal nogen gjerning lykkes for Egypten, enten det så er hode eller hale, palmegren eller siv som gjør den.
Palibe chimene munthu wa mu Igupto angachite, mtsogoleri kapena wotsatira, nthambi ya kanjedza kapena bango.
16 På den tid skal Egypten være som kvinner; det skal forferdes og frykte for Herrens, hærskarenes Guds løftede hånd, som han svinger imot det.
Tsiku limenelo Aigupto adzakhala ngati amayi. Adzanjenjemera ndi kuchita mantha akadzaona Yehova Wamphamvuzonse, atakweza dzanja lake kufuna kuwalanga.
17 Og Juda land skal være en redsel for Egypten; så ofte nogen nevner det for dem, skal de skjelve for det råd som Herren, hærskarenes Gud, tar mot det.
Ndipo dziko la Yuda lidzaopsa dziko la Aigupto. Aliyense amene adzamve dzina la Yuda adzaopsedwa chifukwa cha zimene Yehova Wamphamvuzonse wakonzekera kuchitira dziko la Igupto.
18 På den tid skal det være fem byer i Egyptens land som taler Kana'ans tungemål og sverger Herren, hærskarenes Gud, troskap; en av dem skal kalles Ir-Haheres.
Tsiku limenelo ku dziko la Igupto kudzakhala mizinda isanu yoyankhula chiyankhulo cha Akanaani, ndipo anthu ake adzalumbira kwa Yehova Wamphamvuzonse kuti adzamutumikira. Umodzi mwa mizindayo udzatchedwa Mzinda Wachilungamo.
19 På den tid skal det være et alter for Herren midt i Egyptens land, og en støtte for Herren ved dets landemerke.
Tsiku limenelo mʼkati mwa dziko la Igupto mudzakhala guwa lansembe la Yehova, ndipo mʼmalire mwake adzayikira Yehova mwala wachikumbutso.
20 Og det skal være til et tegn og et vidne i Egyptens land for Herren, hærskarenes Gud; når de roper til Herren over undertrykkerne, skal han sende dem en frelser og stridsmann og fri dem ut.
Zimenezo zidzakhala umboni wozindikiritsa kuti Yehova Wamphamvuzonse alimo mʼdziko la Igupto. Pamene Aigupto adzalirira Yehova chifukwa cha owapondereza, Iye adzawatumizira mpulumutsi ndi mtetezi ndipo adzawalanditsa.
21 Og Herren skal gi sig til kjenne for Egypten, og egypterne skal kjenne Herren på den tid, og de skal bære frem slaktoffer og matoffer og gjøre løfter til Herren og holde dem.
Kotero Yehova adzadziulula yekha kwa Aigupto, ndipo tsiku limenelo adzadziwa Yehova. Adzapembedza Yehova popereka nsembe ndi popereka zopereka zachakudya; Adzalumbira kwa Yehova ndipo adzachita zimene alumbirazo.
22 Herren skal slå Egypten, han skal slå, men også læge, og de skal vende om til Herren, og han skal bønnhøre dem og læge dem.
Yehova adzakantha Aigupto ndi mliri. Iye adzawakanthadi ndipo kenaka adzawachiritsa. Aigupto adzatembenukira kwa Yehova ndipo Iye adzamva madandawulo awo ndi kuwachiritsa.
23 På den tid skal det være en ryddet vei fra Egypten til Assyria, og assyrerne skal komme til Egypten, og egypterne til Assyria, og egypterne skal tjene Herren sammen med assyrerne.
Tsiku limenelo kudzakhala msewu waukulu wochoka ku Igupto kupita ku Asiriya. Aasiriya adzapita ku Igupto ndi Aigupto ku Asiriya. Aigupto ndi Aasiriya adzapembedza pamodzi.
24 På den tid skal Israel være den tredje med Egypten og med Assyria, en velsignelse midt på jorden,
Tsiku limenelo Israeli adzakhala pamodzi ndi Igupto ndi Asiriya, mayiko atatuwa adzakhala dalitso pa dziko lapansi.
25 fordi Herren, hærskarenes Gud, har velsignet det og sagt: Velsignet være mitt folk Egypten og mine henders verk Assyria og min arv Israel!
Yehova Wamphamvuzonse adzawadalitsa, ndi mawu awa, “Adalitsike anthu anga Aigupto, Aasiriya, ntchito ya manja anga, ndi Aisraeli osankhidwa anga.”

< Esaias 19 >