< Esaias 14 >

1 For Herren skal forbarme sig over Jakob og igjen utvelge Israel og bosette dem i deres land, og fremmede skal slå sig sammen med dem og holde sig til Jakobs hus.
Yehova adzachitira chifundo Yakobo; adzasankhanso Israeli ndi kuwalola kuti akhalenso mʼdziko lawo. Alendo adzabwera kudzakhala nawo ndi kudziphatika okha kukhala ngati a mʼnyumba ya Yakobo.
2 Og folkeslag skal ta dem og føre dem hjem igjen, og Israels hus skal få dem i eie i Herrens land og gjøre dem til træler og trælkvinner, og de skal nu holde dem fanget som har holdt dem selv fanget, og herske over sine voldsherrer.
Anthu a mitundu ina adzaperekeza a Israeli ku dziko lawo. Tsono Aisraeli adzasandutsa anthu a mitundu ina aja kukhala antchito awo aamuna ndi aakazi mʼdziko la Yehova. Ndiye kuti Aisraeli adzasandutsa akapolo anthu amene kale anali ambuye awo. Iwo adzasandutsa akapolo anthu amene kale ankawalamulira ndi kuwazunza.
3 På den dag Herren gir dig ro for din møie og din angst og for den hårde trældom som blev lagt på dig,
Yehova akadzakupumitsani ku zowawa ndi mavuto, ndiponso kuntchito yakalavulagaga imene ankakugwiritsani,
4 da skal du istemme denne spottesang over Babels konge og si: Se, hvad ende det har tatt med voldsherren, med trengselsstedet!
mudzayankhula monyogodola mfumu ya Babuloni kuti, Wopsinja uja watha! Ukali wake uja watha!
5 Herren har brutt i stykker de ugudeliges stav, herskernes spir,
Yehova wathyola chikwapu cha anthu oyipa, Iye waphwanya ndodo ya olamulira.
6 som slo folkeferd i harme med slag på slag, som underkuet folkeslag i vrede og forfulgte dem uten skånsel.
Mfumu ya ku Babuloni inkakantha mitundu ya anthu mwaukali powamenya kosalekeza, Iyo inkagonjetsa anthu a mitundu ina mwaukali ndikuwazunza kosalekeza.
7 All jorden har nu fått hvile og ro; de bryter ut i jubelrop.
Koma tsopano mayiko onse ali pa mpumulo ndi pa mtendere; ndipo akuyimba mokondwa.
8 Også cypressene gleder sig over dig, Libanons sedrer: Siden du falt og blev liggende, stiger ingen hugger op til oss.
Ngakhale mitengo ya payini ndi mikungudza ya ku Lebanoni ikuyimba za iwe mokondwa ndipo ikuti, “Chigwetsedwere chako pansi, palibe wina anabwera kudzatigwetsa.”
9 Dødsriket der nede kommer i uro for din skyld, når det skal ta imot dig; for din skyld vekker det dødninger, alle jordens fyrster; det får alle folkenes konger til å stå op fra sine troner. (Sheol h7585)
Ku manda kwatekeseka kuti akulandire ukamabwera; mizimu ya anthu akufa, aja amene anali atsogoleri a dziko lapansi, yadzutsidwa. Onse amene anali mafumu a mitundu ya anthu ayimiritsidwa pa mipando yawo. (Sheol h7585)
10 De tar alle til orde og sier til dig: Også du er blitt kraftløs som vi; du er blitt lik oss.
Onse adzayankha; adzanena kwa iwe kuti, “Iwenso watheratu mphamvu ngati ife; Iwe wafanana ndi ife.”
11 Nedstøtt til dødsriket er din herlighet, dine harpers klang; under dig er redt et leie av ormer, og ditt dekke er makk. (Sheol h7585)
Ulemerero wako wonse walowa mʼmanda, pamodzi ndi nyimbo za azeze ako; mphutsi zayalana pogona pako ndipo chofunda chako ndi nyongolotsi. (Sheol h7585)
12 Hvor er du ikke falt ned fra himmelen, du strålende stjerne, du morgenrødens sønn! Hvor er du ikke felt til jorden, du som slo ned folkeslag!
Wagwa pansi bwanji kuchoka kumwamba, iwe nthanda, mwana wa mʼbandakucha! Wagwetsedwa pansi pa dziko lapansi, Iwe amene unagonjetsapo mitundu ya anthu!
13 Det var du som sa i ditt hjerte: Til himmelen vil jeg stige op, høit over Guds stjerner vil jeg reise min trone, og jeg vil ta sete på gudenes tingfjell i det ytterste nord,
Mu mtima mwako unkanena kuti, “Ndidzakwera mpaka kumwamba; ndidzakhazika mpando wanga waufumu pamwamba pa nyenyezi za Mulungu; ndidzakhala pa mpando waufumu pa phiri losonkhanirako, pamwamba penipeni pa phiri la kumpoto.
14 jeg vil stige op over skyenes topper, jeg vil gjøre mig lik den Høieste.
Ndidzakwera pamwamba pa mitambo; ndidzafanana ndi Wammwambamwamba.”
15 Nei, til dødsriket skal du støtes ned, til hulens dypeste bunn. (Sheol h7585)
Koma watsitsidwa mʼmanda pansi penipeni pa dzenje. (Sheol h7585)
16 De som ser dig, skal stirre på dig, undres over dig og si: Er dette den mann som fikk jorden til å beve, kongeriker til å skjelve,
Anthu akufa adzakupenyetsetsa nadzamalingalira za iwe nʼkumati, “Kodi uyu ndi munthu uja anagwedeza dziko lapansi ndi kunjenjemeretsa maufumu,
17 som gjorde jorderike til en ørken og rev ned dets byer, og som ikke slapp sine fanger hjem?
munthu amene anasandutsa dziko lonse chipululu, amene anagwetsa mizinda yake ndipo sankalola kuti anthu ogwidwa abwerere kwawo?”
18 Alle folkenes konger, alle sammen, de ligger med ære, hver i sitt hus;
Mafumu onse a mitundu ya anthu akugona mwaulemu aliyense mʼmanda akeake.
19 men du er slengt bort, langt fra din grav, lik en foraktet kvist, du ligger dekket av drepte, som er gjennemboret av sverd, og som kastes ned i en stengrav - lik et nedtrådt åtsel.
Koma iwe watayidwa kunja kwa manda ako, ngati nthambi yowola ndi yonyansa. Mtembo wako waphimbidwa ndi anthu ophedwa; amene anabayidwa ndi lupanga, anatsikira mʼdzenje lamiyala ngati mtembo woponderezedwa.
20 Du skal ikke bli jordet som de, for ditt land har du ødelagt, ditt folk har du myrdet; ugjerningsmenns avkom skal aldri mere nevnes.
Sudzayikidwa nawo mʼmanda mwaulemu, chifukwa unawononga dziko lako ndi kupha anthu ako. Zidzukulu za anthu oyipa sizidzakumbukika nʼpangʼono pomwe.
21 Gjør et blodbad på hans sønner for deres fedres misgjerning! De skal ikke få reise sig og ta jorden i eie og fylle jorderike med byer.
Konzani malo woti muphere ana ake aamuna chifukwa cha machimo a makolo awo; kuti angadzuke ndi kulanda dziko lapansi ndi kulidzaza dziko lonselo ndi mizinda yawo.
22 Jeg vil reise mig mot dem, sier Herren, hærskarenes Gud, og jeg vil utrydde av Babel både navn og levning, både barn og barnebarn, sier Herren.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndidzathira nkhondo mzinda wa Babuloni. Ndidzachotseratu mu Babuloni dzina lake ndi onse otsaliramo. Ndiye kuti sipadzakhala ana kapena zidzukulu,” akutero Yehova.
23 Og jeg vil gjøre det til et hjem for pinnsvin og fylle det med vannpytter, og jeg vil feie det bort med ødeleggelsens feiekost, sier Herren, hærskarenes Gud.
“Ndidzawusandutsa mzindawo malo okhalamo anungu ndiponso dambo lamatope; ndidzawusesa ndi tsache lowononga,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
24 Herren, hærskarenes Gud, har svoret og sagt: Sannelig, som jeg har tenkt, så skal det skje, og det jeg har besluttet, det skal stå fast.
Yehova Wamphamvuzonse walumbira kuti, “Ndithudi, monga ndaganizira ndidzachitadi choncho, ndipo monga momwe ndatsimikizira zidzakhala momwemo ndithu.
25 Jeg vil knuse Assur i mitt land og trede ham ned på mine fjell, og hans åk skal tas fra dem, og hans byrde skal løftes fra deres skulder.
Ndidzawawononga Asiriya mʼdziko langa; ndidzawapondereza ndi mapazi pa mapiri anga; ndidzachotsa goli lawo pa anthu anga, ndipo ndidzachotsa katundu wawo pa mapewa awo.”
26 Dette er det råd som er tatt om all jorden, og dette er den hånd som er rakt ut over alle folkene;
Izi ndizo ndakonza kuti zichitike pa dziko lonse lapansi, ndatambasula dzanja pa anthu a mitundu yonse.
27 for Herren, hærskarenes Gud, har besluttet det, og hvem gjør det til intet? Og hans hånd er det som er utrakt, og hvem kan vende den bort?
Pakuti Yehova Wamphamvuzonse watsimikiza, ndipo ndani angamuletse? Dzanja lake latambasulidwa ndipo ndani angalibweze?
28 I kong Akas' dødsår kom dette utsagn:
Uthenga uwu unabwera chaka chimene mfumu Ahazi anamwalira:
29 Gled dig ikke, hele du Filisterland, fordi den stav som slo dig, er brutt i stykker! For av ormens rot skal en basilisk komme frem, og dens frukt er en flyvende serafslange.
Musakondwere inu Afilisti nonse kuti Asiriya amene anali ngati ndodo yokukanthani anathedwa; chifukwa kuchokera ku njoka yomweyi (mfumu ya Aasiriya) mudzatuluka mphiri, ndipo chipatso chake chidzakhala njoka yaliwiro ndiponso yaululu.
30 Og de ringeste blandt de ringe skal finne rikelig føde, og de fattige hvile i trygghet, og jeg vil drepe din rot ved hunger, og din levning skal han slå ihjel.
Osaukitsitsa adzapeza chakudya ndipo amphawi adzakhala mwamtendere. Koma anthu ako ndidzawawononga ndi njala, ndipo njalayo idzapha ngakhale opulumuka ako.
31 Hyl, du port! Skrik, du by! Skjelv, hele du Filisterland! For fra Norden kommer en røk, og blandt fiendens skarer er det ingen som ligger efter.
Lirani kwambiri, anthu a pa chipata! Fuwulani kwambiri, anthu a mu mzinda! Njenjemerani ndi mantha, inu Afilisti nonse! Mtambo wa utsi ukuchokera kumpoto, ndipo palibe wamantha pakati pa ankhondo ake.
32 Hvad skal vi da svare hedningefolkets sendebud? - At Herren har grunnfestet Sion, og at der finner de ly de elendige i hans folk.
Kodi tidzawayankha chiyani amithenga a ku Filisitiya? “Yehova wakhazikitsa Ziyoni, ndipo mu mzinda wakewu, anthu ozunzika apeza populumukira.”

< Esaias 14 >