+ 1 Mosebok 1 >

1 I begynnelsen skapte Gud himmelen og jorden.
Pachiyambi Mulungu analenga kumwamba ndi dziko lapansi.
2 Og jorden var øde og tom, og det var mørke over det store dyp, og Guds Ånd svevde over vannene.
Dziko lapansi linali losakonzedwa ndi lopanda kanthu. Mdima wandiweyani unakuta nyanja ndipo Mzimu wa Mulungu unkayendayenda pamwamba pa madziwo.
3 Da sa Gud: Det bli lys! Og det blev lys.
Pamenepo Mulungu anati, “Kuwale” ndipo kunawaladi.
4 Og Gud så at lyset var godt, og Gud skilte lyset fra mørket.
Mulungu anaona kuti kuwalako kunali bwino ndipo Iye analekanitsa kuwala ndi mdima.
5 Og Gud kalte lyset dag, og mørket kalte han natt. Og det blev aften, og det blev morgen, første dag.
Mulungu anatcha kuwalako “usana” ndipo mdima anawutcha “usiku.” Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku loyamba.
6 Og Gud sa: Det bli en hvelving midt i vannene, og den skal skille vann fra vann.
Kenaka Mulungu anati, “Pakhale thambo pakati pa madzi kuti lilekanitse madzi a mʼmwamba ndi madzi a pansi.”
7 Og Gud gjorde hvelvingen og skilte vannet som er under hvelvingen, fra vannet som er over hvelvingen. Og det blev så.
Ndipo Mulungu anapanga thambo nalekanitsa madzi amene anali pansi ndi pamwamba pa thambo lija, ndipo zinachitikadi.
8 Og Gud kalte hvelvingen himmel. Og det blev aften, og det blev morgen, annen dag.
Mulungu anatcha thambo lija “kumwamba.” Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachiwiri.
9 Og Gud sa: Vannet under himmelen samle sig til ett sted, og det tørre land komme til syne! Og det blev så.
Mulungu anati, “Madzi a pansi pa thambo asonkhane pa malo amodzi kuti mtunda uwoneke,” ndipo zinachitikadi.
10 Og Gud kalte det tørre land jord, og vannet som hadde samlet sig, kalte han hav. Og Gud så at det var godt.
Mulungu anawutcha mtundawo “dziko,” madzi osonkhana pamodziwo anawatcha “nyanja.” Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
11 Og Gud sa: Jorden bære frem gress, urter som sår sig, frukttrær som bærer frukt med deres frø i, på jorden, hvert efter sitt slag. Og det blev så.
Kenaka Mulungu anati, “Dziko libereke zomera zobala mbewu, mitengo yobala zipatso za mbewu, molingana ndi mitundu yake.” Ndipo zinachitikadi.
12 Og jorden bar frem gress, urter som sår sig, hver efter sitt slag, og trær som bærer frukt med deres frø i, hvert efter sitt slag. Og Gud så at det var godt.
Dziko linabereka zomera zokhala ndi mbewu monga mwa mitundu yake ndi mitengo yokhala ndi zipatso za mbewu mʼkati mwake monga mwa mitundu yake. Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
13 Og det blev aften, og det blev morgen, tredje dag.
Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachitatu.
14 Og Gud sa: Det bli lys på himmelhvelvingen til å skille dagen fra natten! Og de skal være til tegn og fastsatte tider og dager og år.
Mulungu anati, “Pakhale zowunikira kuthambo kuti zilekanitse usana ndi usiku. Ndipo zimenezi zikhale zizindikiro zoonetsa nyengo, masiku ndi zaka;
15 Og de skal være til lys på himmelhvelvingen, til å lyse over jorden. Og det blev så.
zikhale kuthambo kuti ziwunikire pa dziko lapansi. Ndipo zinachitikadi.”
16 Og Gud gjorde de to store lys, det største til å råde om dagen og det mindre til å råde om natten, og stjernene.
Mulungu anapanga zowunikira zazikulu ziwiri; chachikulu chilamulire usana ndi chachingʼono chilamulire usiku. Iye anapanganso nyenyezi.
17 Og Gud satte dem på himmelhvelvingen til å lyse over jorden
Mulungu anaziyika mlengalenga kuti ziziwunikira pa dziko lapansi,
18 og til å råde om dagen og om natten og til å skille lyset fra mørket. Og Gud så at det var godt.
kuti zilamulire usana ndi usiku, ndi kuti zilekanitse kuwala ndi mdima. Mulungu anaona kuti zinali bwino.
19 Og det blev aften, og det blev morgen, fjerde dag.
Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachinayi.
20 Og Gud sa: Det vrimle av liv i vannet, og fugler flyve over jorden under himmelhvelvingen!
Mulungu anati, “Mʼmadzi mukhale zamoyo zochuluka ndipo mbalame ziwuluke mlengalenga pamwamba pa dziko lapansi.”
21 Og Gud skapte de store sjødyr og alt levende som rører sig, som det vrimler av i vannet, hvert efter sitt slag, og alle vingede fugler, hver efter sitt slag. Og Gud så at det var godt.
Choncho Mulungu analenga zamoyo zikuluzikulu za mʼnyanja ndi chamoyo chamtundu uliwonse chokhala mʼmadzi ndi mbalame iliyonse ya mapiko monga mwa mtundu wake. Mulungu anaona kuti zinali bwino.
22 Og Gud velsignet dem og sa: Vær fruktbare og bli mange og opfyll vannet i havet, og fuglene skal bli tallrike på jorden!
Mulungu anazidalitsa nati, “Muswane, ndi kudzaza mʼmadzi a mʼnyanja, ndipo mbalame zichuluke pa dziko lapansi.”
23 Og det blev aften, og det blev morgen, femte dag.
Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachisanu.
24 Og Gud sa: Jorden la fremgå levende vesener, hvert efter sitt slag, fe, kryp og ville dyr, hvert efter sitt slag! Og det blev så.
Kenaka Mulungu anati, “Dziko lapansi litulutse zolengedwa zamoyo monga mwa mitundu yawo: ziweto, zolengedwa zokwawa ndi nyama zakuthengo, iliyonse monga mwa mtundu wake.” Ndipo zinaterodi.
25 Og Gud gjorde de ville dyr, hvert efter sitt slag, og feet efter sitt slag og alt jordens kryp, hvert efter sitt slag. Og Gud så at det var godt.
Mulungu anapanga nyama zakuthengo monga mwa mitundu yawo, nyama zoweta monga mwa mitundu yawo ndi nyama zokwawa monga mwa mitundu yawo. Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
26 Og Gud sa: La oss gjøre mennesker i vårt billede, efter vår lignelse, og de skal råde over fiskene i havet og over fuglene under himmelen og over feet og over all jorden og over alt kryp som rører sig på jorden.
Zitatha izi Mulungu anati, “Tipange munthu mʼchifanizo chathu, mofanana ndi ife kuti alamulire nsomba za mʼnyanja, mbalame zamlengalenga, nyama zonse zoweta ndi zonse zokwawa za pa dziko lapansi ndi zamoyo zonse zakutchire.”
27 Og Gud skapte mennesket i sitt billede, i Guds billede skapte han det; til mann og kvinne skapte han dem.
Ndipo Mulungu analenga munthu mʼchifanizo chake. Anawalengadi mʼchifanizo cha Mulungu; analenga iwo, mwamuna ndi mkazi.
28 Og Gud velsignet dem og sa til dem: Vær fruktbare og bli mange og opfyll jorden og legg den under eder, og råd over fiskene i havet og over fuglene under himmelen og over hvert dyr som rører sig på jorden!
Mulungu anawadalitsa nati kwa iwo, “Muberekane, muchulukane, mudzaze dziko lapansi ndipo muligonjetse. Mulamulire nsomba zamʼnyanja, mbalame zamlengalenga ndi cholengedwa chamoyo chilichonse chimene chimayenda mokwawa pa dziko lapansi.”
29 Og Gud sa: Se, jeg gir eder alle urter som sår sig, alle som finnes på jorden, og alle trær med frukt som sår sig; de skal være til føde for eder.
Kenaka Mulungu anati, “Ine ndakupatsani chomera chilichonse cha pa dziko lapansi chimene chili ndi mbewu komanso mtengo uliwonse wobala zipatso zokhala ndi mbewu mʼkati mwake kuti zikhale chakudya chanu.
30 Og alle dyr på jorden og alle fugler under himmelen og alt som rører sig på jorden, alt som det er livsånde i, gir jeg alle grønne urter å ete. Og det blev så.
Ndaperekanso msipu kwa nyama zonse za pa dziko lapansi ndi kwa mbalame zamlengalenga ndi kwa cholengedwa chamoyo chilichonse chimene chimakwawa, chilichonse chimene chili ndi moyo.” Ndipo zinachitikadi.
31 Og Gud så på alt det han hadde gjort, og se, det var såre godt. Og det blev aften, og det blev morgen, sjette dag.
Mulungu anaona zonse zimene anazilenga kuti zinali zabwino kwambiri. Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa, tsiku lachisanu ndi chimodzi.

+ 1 Mosebok 1 >