< 2 Mosebok 11 >

1 Herren hadde sagt til Moses: Ennu én plage vil jeg la komme over Farao og over Egypten, så skal han la eder fare herfra; ja, når han lar eder fare, skal han endog drive eder herfra med alt det I har.
Tsopano Yehova anati kwa Mose, “Ine ndidzalanga Farao pamodzi ndi Aigupto onse ndi mliri umodzi wotsiriza. Zikadzachitika izi iye adzakulolani kuti mutuluke mʼdziko lino. Ndithu pamene azidzakutulutsani adzachita ngati akukuyingitsani.
2 Si nu så folket hører det at hver mann skal be sin granne og hver kvinne sin grannekvinne om smykker av sølv og gull.
Awuze anthu kuti mwamuna aliyense ndi mkazi aliyense apemphe kwa mnansi wake ziwiya zasiliva ndi golide.”
3 Og Herren gav folket yndest hos egypterne; og så var også Moses en meget stor mann i Egypten, både for Faraos tjenere og for folket.
Tsono Yehova anachititsa Aigupto kuti akomere mtima Aisraeli. Komanso Mose anali wotchuka kwambiri mʼdziko la Igupto, pamaso pa nduna za Farao ndi anthu onse.
4 Og Moses sa: Så sier Herren: Ved midnatts tid vil jeg gå midt gjennem Egypten.
Tsono Mose anawuza Farao kuti, “Pakati pa usiku, Yehova adzayenda pakati pa anthu a ku Igupto.
5 og alle førstefødte i Egyptens land skal dø, fra den førstefødte sønn av Farao, som sitter på sin trone, til den førstefødte sønn av trælkvinnen, som står bak håndkvernen, og alt førstefødt blandt buskapen.
Ndipo mwana aliyense wamwamuna wachisamba adzafa, kuyambira mwana wamwamuna wa Farao amene amakhala pa mpando waufumu, mpaka mwana wamwamuna wachisamba wa mdzakazi wake amene ali naye pa mtondo, komanso ana oyamba a ziweto.
6 Og det skal i hele Egyptens land bli et stort skrik som det ikke har vært maken til og heller ikke mere skal bli.
Kudzakhala kulira kwakukulu mʼdziko lonse la Igupto, kumene sikunachitikepo ndipo sikudzachitikanso.
7 Men ikke en hund skal gjø mot nogen av Israels barn, hverken mot folk eller fe, så I skal kjenne at Herren gjør forskjell på egypterne og Israel.
Koma pakati pa Aisraeli, ngakhale galu sadzawuwa munthu aliyense kapena chiweto!” Kotero mudzadziwa kuti Yehova ndiye wasiyanitsa pakati pa Igupto ndi Israeli.
8 Da skal alle disse dine tjenere komme ned til mig og bøie sig for mig og si: Dra ut, både du og hele det folk som følger dig! Og så skal jeg dra ut. Og han gikk bort fra Farao i brennende harme.
Nduna zanu zonse zidzabwera kwa ine, kugwada pamaso panga ndi kunena kuti, “Pita iwe ndi anthu ako onse amene akukutsatirawa! Zimenezi zikadzachitika ine ndidzachoka.” Ndipo Mose anachoka kwa Farao atakwiya kwambiri.
9 Som Herren hadde sagt til Moses og Aron: Farao skal ikke høre på eder, så jeg kan få gjort mange under i Egyptens land,
Yehova ananena kwa Mose kuti, “Farao adzakana kukumvera, kuti zodabwitsa zanga zichuluke mʼdziko la Igupto.”
10 så gjorde Moses og Aron alle disse under for Farao; men Herren forherdet Faraos hjerte, så han ikke lot Israels barn dra bort fra sitt land.
Mose ndi Aaroni anachita zodabwitsa zonsezi pamaso pa Farao koma Yehova anawumitsa mtima wa Farao, ndipo sanalole kuti Aisraeli atuluke mʼdziko lake.

< 2 Mosebok 11 >