< Kolossenserne 1 >

1 Paulus, ved Guds vilje Kristi Jesu apostel, og broderen Timoteus
Paulo, mtumwi wa Khristu Yesu mwachifuniro cha Mulungu, ndi Timoteyo mʼbale wathu.
2 - til de hellige og troende brødre i Kristus i Kolossæ: Nåde være med eder og fred fra Gud vår Fader!
Kulembera abale oyera mtima ndi okhulupirira a ku Kolose mwa Khristu. Chisomo ndi mtendere kwa inu zochokera kwa Mulungu Atate athu.
3 Vi takker alltid Gud og vår Herre Jesu Kristi Fader når vi beder for eder,
Timayamika Mulungu Atate wa Ambuye athu Yesu Khristu, nthawi zonse pamene tikukupemphererani.
4 efterat vi har hørt om eders tro på Kristus Jesus og den kjærlighet som I har til alle de hellige,
Timayamika chifukwa tinamva za chikhulupiriro chanu mwa Khristu Yesu ndi za chikondi chanu pa oyera mtima onse.
5 for det håps skyld som er gjemt for eder i himlene, som I forut har hørt om ved sannhetens ord i evangeliet,
Chikhulupiriro ndi chikondi, gwero lake ndi chiyembekezo chomwe muli nacho chodzalandira zimene anakusungirani kumwamba. Munamva kale za zimenezi kudzera mʼmawu a choonadi, Uthenga Wabwino
6 som er kommet til eder, likesom det og er i hele verden og bærer frukt og vokser som hos eder, fra den dag I hørte det og lærte å kjenne Guds nåde i sannhet,
umene unafika kwa inu. Pa dziko lonse lapansi Uthenga Wabwino ukubereka chipatso ndi kukula monga momwe zakhala zikuchitikira pakati panu kuyambira tsiku limene munawumva ndi kuzindikira chisomo cha Mulungu mu choonadi chonse.
7 således som I har lært av Epafras, vår elskede medtjener, som er en tro Kristi tjener for eder,
Inu munaphunzira zimenezi kuchokera kwa Epafra, mtumiki mnzathu wokondedwa, amene ndi mtumiki wokhulupirika wa Khristu mʼmalo mwathu.
8 han som også har fortalt oss om eders kjærlighet i Ånden.
Iye anatiwuza za chikondi chanu chimene Mzimu anakupatsani.
9 Derfor holder vi fra den dag vi hørte det, ikke op med å gjøre bønn for eder og bede at I må fylles med kunnskap om hans vilje i all åndelig visdom og forstand,
Chifukwa cha ichi, kuyambira tsiku limene tinamva za inu, sitinasiye kukupemphererani ndi kumupempha Mulungu kuti akudzazeni ndi chidziwitso cha chifuniro chake kudzera mu nzeru yonse yauzimu ndi kumvetsetsa.
10 at I kan vandre verdig for Herren til velbehag i alt, så I bærer frukt og vokser i all god gjerning ved kunnskapen om Gud,
Ndipo tikupempherera zimenezi ndi cholinga chakuti inu mukhale moyo oyenera Ambuye ndi kumukondweretsa mʼnjira zonse. Kubereka chipatso pa ntchito iliyonse yabwino, ndi kukula mʼchidziwitso cha Mulungu.
11 så I styrkes med all styrke efter hans herlighets kraft til all tålmodighet og langmodighet,
Timapempheranso kuti Mulungu akulimbikitseni ndi mphamvu yake yonse ya ulemerero wake, kuti muzipirira zonse ndi mitima yofatsa ndi ya chimwemwe
12 så I med glede takker Faderen, som gjorde oss skikkede til å få del i de helliges arvelodd i lyset,
ndi kuyamika Atate nthawi zonse, amene wakuyenerezani kuti mulandire nawo chuma cha oyera mtima mu ufumu wa kuwunika.
13 han som fridde oss ut av mørkets makt og satte oss over i sin elskede Sønns rike,
Pakuti Iye anatipulumutsa ku ulamuliro wa mdima ndi kutibweretsa mu ufumu wa Mwana wake wokondedwa.
14 i hvem vi har forløsningen, syndenes forlatelse.
Mwa Iyeyu ife tinawomboledwa ndi kukhululukidwa machimo.
15 Og han er et billede av Gud den usynlige, den førstefødte fremfor enhver skapning;
Mwanayu ndiye chithunzi cha Mulungu wosaonekayo. Iye ndiye Mwana wake woyamba kubadwa ndi wolamulira zolengedwa zonse.
16 for i ham er alle ting skapt, de i himlene og de på jorden, de synlige og de usynlige, enten det så er troner eller herredømmer eller makter eller myndigheter; alt er det skapt ved ham og til ham,
Pakuti zinthu zonse zinalengedwa kudzera mwa Iye. Zinthu zakumwamba ndi za pa dziko lapansi, zooneka ndi zosaoneka, maufumu, akuluakulu, aulamuliro ndi amphamvu. Zinthu zonse zinalengedwa kudzera mwa Iye ndipo anazilengera Iyeyo.
17 og han er før alle ting, og alle ting står ved ham.
Iyeyo analipo zinthu zonse zisanalengedwe ndipo zinthu zonse zimamangika pamodzi mwa Iye.
18 Og han er hovedet for legemet, som er menigheten, han som er ophavet, den førstefødte av de døde, forat han i alle deler skulde være den ypperste;
Iye ndiyenso mutu wa thupi, limene ndi mpingo. Iye ndiye chiyambi chake, woyamba kuuka kwa akufa, kuti Iyeyo akhale wopambana zonse.
19 for det var Guds vilje at hele hans fylde skulde ta bolig i ham,
Pakuti kunamukomera Mulungu kuti umulungu wake wonse ukhalemo mwa Khristu.
20 og ved ham å forlike alle ting med sig, idet han gjorde fred ved hans korses blod, - ved ham, enten det er de på jorden eller de i himlene.
Ndipo kudzera mwa Iye Mulungu ayanjanitsenso zinthu zonse ndi Iye mwini, zinthu za pa dziko lapansi, kapena zinthu za kumwamba. Iye anachita mtendere kudzera mʼmagazi ake, wokhetsedwa pa mtanda.
21 Også eder, som fordum var fremmede og fiender ved eders sinnelag, i de onde gjerninger,
Kale inu munali kutali ndi Mulungu ndipo munali adani a Mulungu mʼmaganizo mwanu chifukwa cha khalidwe lanu loyipa.
22 eder har han nu forlikt i hans jordiske legeme ved døden, for å fremstille eder hellige og ulastelige og ustraffelige for sitt åsyn,
Koma tsopano Iye anakuyanjanitsani mʼthupi la Khristu kudzera mu imfa kuti akuperekeni pamaso pake oyera, opanda banga ndi opanda chotsutsidwa nacho
23 så sant I blir ved i troen, grunnfestet og faste, og ikke lar eder rokke fra det håp evangeliet gir, det som I har hørt, som er blitt forkynt for enhver skapning under himmelen, og som jeg, Paulus, er blitt tjener for.
ngati mupitirirabe kukhala mʼchikhulupiriro chanu, okhazikika ndi olimba, osasunthidwa kuchoka pa chiyembekezo chimene munachigwira mu Uthenga Wabwino. Uwu ndi Uthenga Wabwino umene munawumva, umene wakhala ukulalikidwa kwa olengedwa onse a pansi pa thambo, ndi umenenso, ine Paulo ndinakhala mtumiki wake.
24 Nu gleder jeg mig over mine lidelser for eder og utfyller i mitt kjød det som ennu fattes i Kristi trengsler, for hans legeme, som er menigheten,
Tsopano ine ndikukondwa kuti ndinavutika chifukwa cha inu, ndipo ndikukwaniritsa mʼthupi langa zimene zikuperewera pa masautso a Khristu, chifukwa cha thupi lake, limene ndi Mpingo.
25 hvis tjener jeg er blitt efter den Guds husholdning som er mig gitt iblandt eder, det vil si å fullføre Guds ord,
Ine ndakhala mtumiki wake mwa lamulo limene Mulungu anandipatsa kuti ndipereke Mawu a Mulungu athunthu,
26 den hemmelighet som har vært skjult fra alle tiders og slekters ophav, men nu er blitt åpenbaret for hans hellige, (aiōn g165)
chinsinsi chimene chakhala chikubisika kwa nthawi ndi mibado, koma tsopano chawululidwa kwa oyera mtima. (aiōn g165)
27 for hvem Gud vilde kunngjøre hvor rik på herlighet denne hemmelighet er iblandt hedningene, det er Kristus iblandt eder, håpet om herlighet.
Kwa iwo amene Mulungu anawasankha kuti awadziwitse pakati pa a mitundu ina, ulemerero wa chuma cha chinsinsi ichi, amene ndi Khristu mwa inu, chiyembekezo cha ulemerero.
28 Og ham forkynner vi, idet vi formaner hvert menneske og lærer hvert menneske med all visdom for å fremstille hvert menneske fullkomment i Kristus.
Ife tikulalikira Khristu, kulangiza ndi kuphunzitsa aliyense mwa nzeru zonse kuti timupereke aliyense wangwiro mwa Khristu.
29 For dette arbeider jeg og, idet jeg strider ved hans kraft, som virker i mig med styrke.
Ndi cholinga chimenechi, ine ndikugwira ntchito molimbika ndi mwamphamvu zonse zimene Iye anachita mwa ine.

< Kolossenserne 1 >