< Amos 4 >

1 Hør dette ord, I Basan-kyr på Samarias fjell, I som undertrykker de ringe, som knuser de fattige, som sier til eders menn: Kom med vin, så vi får drikke!
Imvani mawu awa, inu ngʼombe zazikazi za ku Basani, okhala pa Phiri la Samariya, inu akazi amene mumapondereza anthu osauka ndi kuzunza anthu osowa ndi kumanena kwa amuna anu kuti, “Tipatseni zakumwa!”
2 Herren, Israels Gud, har svoret ved sin hellighet: Se, dager kommer over eder da I skal slepes bort med haker, og den siste levning av eder med fiskekroker,
Ambuye Yehova, mwa kuyera mtima kwake walumbira kuti, “Nthawi idzafika ndithu pamene adzakukokani ndi ngowe, womaliza wa inu adzakokedwa ndi mbedza.
3 og I skal gå ut gjennem murbruddene, hver rett frem for sig, og I skal bli slengt bort i palasset, sier Herren.
Mudzatulukira mʼmingʼalu ya pa khoma aliyense payekhapayekha, ndipo mudzatayidwa ku Harimoni,” akutero Yehova.
4 Gå til Betel og synd, til Gilgal og synd til gagns, og bær hver morgen frem eders slaktoffer, hver tredje dag eders tiender,
“Bwerani ku Beteli mudzachimwe; ndi ku Giligala kuti mudzapitirize kuchimwa. Bweretsani nsembe zanu mmawa uliwonse, bweretsani chakhumi chanu masiku atatu aliwonse.
5 og la røk av syret brød stige op som takkoffer og tillys frivillige offer og kunngjør det! For så vil I jo gjerne ha det, I Israels barn, sier Herren, Israels Gud.
Wotchani buledi wokhala ndi yisiti ngati nsembe yachiyamiko ndi kumanyadira poyera za zopereka zanu zaufulu. Inu Aisraeli, zinyadireni nsembezo, pakuti izi ndi zimene mumakonda kuchita,” akutero Ambuye Yehova.
6 Og jeg har da latt eder gå med tom munn i alle eders byer og latt eder mangle brød i alle eders hjem; men I har ikke omvendt eder til mig, sier Herren.
“Ndine amene ndinakusendetsani milomo mʼmizinda yanu yonse, ndipo munasowa chakudya mʼmizinda yanu. Komatu inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
7 Jeg har forholdt eder regnet da det ennu var tre måneder igjen til høsten, og har latt det regne over en by, men ikke over en annen; et stykke land fikk regn, og et annet stykke blev fortørket, fordi det ikke kom regn på det,
“Ndinenso amene ndinamanga mvula patangotsala miyezi itatu kuti mukolole. Ndinagwetsa mvula pa mzinda wina, koma pa mzinda wina ayi, mvula inkagwa pa munda wina; koma sinagwe pa munda wina ndipo mbewu zinawuma.
8 og to, tre byer ravet avsted til en og samme by for å drikke vann, men fikk ikke nok; men I har ikke omvendt eder til mig, sier Herren.
Anthu ankayenda mzinda ndi mzinda kufuna madzi, koma sanapeze madzi okwanira kumwa. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
9 Jeg har slått eder med kornbrand og rust; gresshoppene åt op eders mange haver og vingårder og fikentrær og oljetrær; men I har ikke omvendt eder til mig, sier Herren.
“Nthawi zambiri ndinakantha mbewu zanu ndiponso minda ya mpesa, ndinayikantha ndi chinsikwi ndiponso ndi chiwawu. Dzombe linawononga mikuyu yanu ndi mitengo ya olivi. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
10 Jeg har sendt pest blandt eder likesom dengang i Egypten, jeg har drept eders unge menn med sverdet og latt eders hester bli hærfang, og jeg lot stanken fra eders hær stige op i eders nese; men I har ikke omvendt eder til mig, sier Herren.
“Ine ndinabweretsa miliri pakati panu monga ndinachitira ku Igupto. Ndinapha anyamata anu ndi lupanga, ndinapereka akavalo anu kwa adani. Ndinakununkhitsani fungo la mitembo lochokera mʼmisasa yanu ya nkhondo. Komatu inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
11 Jeg har omstyrtet byer iblandt eder, således som Gud omstyrtet Sodoma og Gomorra, og I blev som en brand som er revet ut av ilden; men I har ikke omvendt eder til mig, sier Herren.
“Ndinawononga ena mwa inu monga ndinawonongera Sodomu ndi Gomora. Inu munali ngati chikuni choyaka chimene chafumulidwa pa moto. Komabe inu simunabwerere kwa Ine,” akutero Yehova.
12 Derfor vil jeg gjøre med dig, Israel, så som jeg har sagt. Og fordi jeg vil gjøre således med dig, så gjør dig rede til å møte din Gud, Israel!
“Choncho izi ndi zimene ndidzakuchitire iwe Israeli, chifukwa ndidzakuchitira zimenezi, konzekera kukumana ndi Mulungu wako, iwe Israeli.”
13 For se, han som danner fjellene og skaper vinden og åpenbarer menneskene deres tanker, han som gjør morgenrøden til mørke og farer frem over jordens høider - Herren, hærskarenes Gud, er hans navn.
Iye amene amawumba mapiri, amalenga mphepo, ndipo amawululira munthu za mʼmaganizo ake, Iye amene amasandutsa usana kuti ukhale mdima, ndipo amayenda pa zitunda za dziko lapansi, dzina lake ndi Yehova Mulungu Wamphamvuzonse.

< Amos 4 >