< 2 Samuel 18 >

1 David mønstret folket som var med ham, og satte høvedsmenn over dem, nogen over tusen og nogen over hundre.
Davide anasonkhanitsa anthu amene anali naye ndipo anasankha atsogoleri ena olamulira ankhondo 1,000 ndi ena olamulira ankhondo 100.
2 Så sendte David folket avsted, en tredjedel under Joab, en tredjedel under Abisai, Serujas sønn, Joabs bror, og en tredjedel under gittitten Ittai, og kongen sa til folket: Jeg vil og dra ut med eder.
Davide anatumiza asilikaliwo atawagawa patatu: gulu loyamba limalamulidwa ndi Yowabu, gulu lachiwiri limalamulidwa ndi Abisai ndipo gulu lachitatu limalamulidwa ndi Itai Mgiti. Mfumu inawuza asilikaliwo kuti, “Inenso ndipita nanu ndithu.”
3 Men folket sa: Du skal ikke dra ut; for om vi flykter, bryr ingen sig om oss, og om halvdelen av oss faller, bryr heller ingen sig om oss; men du er så god som ti tusen av oss, og nu er det bedre at du er rede til å komme oss til hjelp fra byen.
Koma anthuwo anati, “Inu musapite nafe. Ngati tidzathamangitsidwa, iwowo sadzasamala za ife. Ngakhale theka la ife litafa, iwo sadzasamalako. Koma inuyo ndinu ofunika kuposa asilikali 10,000. Nʼkwabwino kwambiri kuti inu muzititumizira chithandizo kuchokera ku mzindako.”
4 Da sa kongen til dem: Jeg skal gjøre som I synes. Så stilte kongen sig ved siden av porten, og alt folket drog ut, hundrevis og tusenvis.
Mfumu inayankha kuti, “Ine ndichita chimene chili chokukomerani.” Kotero mfumu inayima pambali pa chipata pamene ankhondo onse amayenda mʼmagulu a anthu 100 ndi a 1,000.
5 Og kongen bød Joab og Abisai og Ittai og sa: Far varsomt med den unge mann - med Absalom! Og alt folket hørte på at kongen gav alle høvedsmennene dette påbud om Absalom.
Mfumu inalamulira Yowabu, Abisai ndi Itai kuti, “Mumukomere mtima Abisalomu chifukwa cha ine.” Ndipo asilikali onse anamva pamene mfumu imalamula izi za Abisalomu kwa wolamulira aliyense.
6 Så drog folket ut i marken mot Israel, og det kom til slag i Efra'imskogen.
Ankhondo anayenda kupita kukachita nkhondo ndi Israeli, ndipo nkhondo inachitika mʼnkhalango ya Efereimu.
7 Der blev Israels folk slått av Davids menn, og det blev et stort mannefall der den dag - tyve tusen mann.
Aisraeli anagonjetsedwa kumeneko ndi ankhondo a Davide. Tsiku limenelo anaphedwa anthu okwanira 20,000.
8 Og striden bredte sig ut over hele landet deromkring, og skogen fortærte den dag flere av folket enn sverdet fortærte.
Nkhondo inafalikira ku madera onse akumidzi ndipo anthu akufa chifukwa cha zoopsa za mʼnkhalango anali ambiri tsiku limenelo kuposa akufa ndi lupanga.
9 Absalom kom like imot Davids menn; han red på sitt muldyr, og muldyret kom inn under de tette grener på en stor terebinte, så hans hode hang fast i terebinten, og han blev hengende mellem himmel og jord; for muldyret som han satt på, løp sin vei.
Tsono zinachitika kuti Abisalomu anakumana ndi asilikali a Davide. Iye anali atakwera bulu ndipo pamene buluyo amadutsa pansi pa nthambi zambiri za mtengo wa thundu, mutu wa Abisalomu unakodwa mu mtengomo. Iye anasiyidwa atatsakamira mʼmalele, pamene bulu amene anakwerapoyo amapitirira.
10 Dette fikk en mann se, meldte det til Joab og sa: Jeg så Absalom henge i terebinten der borte.
Mmodzi mwa asilikali ataona zimenezi, anamuwuza Yowabu kuti, “Ine ndamuona Abisalomu ali lende mu mtengo wa thundu.”
11 Da sa Joab til mannen som meldte ham dette: Men når du har sett det, hvorfor slo du ham da ikke til jorden med det samme? Så hadde det vært min skyldighet å gi dig ti sekel sølv og et belte.
Yowabu anati kwa munthu amene anamuwuza zimenezi, “Ukuti chiyani! Unamuona? Nʼchifukwa chiyani sunamukanthire pansi pomwepo? Ndipo ine ndikanakupatsa ndalama za siliva khumi ndi lamba wausilikali.”
12 Men mannen sa til Joab: Om jeg så fikk mig tilveid tusen sekel sølv midt op i hånden, vilde jeg ikke rekke ut min hånd mot kongens sønn; for vi hørte alle på at kongen bød dig og Abisai og Ittai og sa: Vær varsom med den unge mann, med Absalom, hvem det så er av eder!
Koma munthuyo anayankha kuti, “Ngakhale atandipatsa mʼmanja mwanga ndalama zasiliva 1,000, sindingatambasule dzanja langa kupha mwana wa mfumu. Ife tikumva, mfumu inalamula inu Abisai ndiponso Itai kuti, ‘Mutetezeni mnyamatayo Abisalomu chifukwa cha ine!’
13 Men om jeg hadde gått svikefullt frem og tatt hans liv, så blir jo ingen ting skjult for kongen, og du vilde nok holde dig unda.
Ndipo sindikanayika moyo wanga pa chiswe pakuti palibe chimene chimabisika pamaso pa mfumu komanso inu simukanditeteza.”
14 Da sa Joab: Jeg kan ikke stå her med dig og hefte mig bort. Og han tok tre kastespyd i sin hånd og støtte dem i Absaloms hjerte, mens han ennu hang levende midt i terebinten.
Yowabu anati, “Ine sinditayanso nthawi ndi iwe.” Ndipo anatenga mikondo itatu mʼmanja mwake ndipo anabaya pamtima pa Abisalomu, Abisalomuyo akanali ndi moyo pa mtengo wa thundu.
15 Så stilte ti unge menn - Joabs våbensvenner - sig rundt omkring og hugg til Absalom og drepte ham.
Ndipo anthu khumi onyamula zida za Yowabu anazungulira Abisalomu, kumubaya ndi kumupha.
16 Da støtte Joab i basunen, og folket holdt op med å forfølge Israel; for Joab holdt folket tilbake.
Kenaka Yowabu analiza lipenga ndipo asilikali analeka kuthamangitsa Israeli pakuti Yowabu anawaletsa.
17 Og de tok Absalom og kastet ham i en stor grøft i skogen og reiste en stor stenrøs over ham; og hele Israel flyktet, hver til sitt hjem.
Iwo anatenga Abisalomu ndi kumuponya mʼdzenje lalikulu mʼchipululumo ndipo anawunjikapo miyala ikuluikulu. Nthawiyi Aisraeli onse anathawa kupita ku nyumba zawo.
18 Men Absalom hadde, mens han levde, tatt og reist sig den støtte som står i Kongedalen; for han sa: Jeg har ingen sønn som kan holde oppe minnet om mitt navn. Han gav støtten navn efter sig selv, og den er blitt kalt Absaloms minnesmerke inntil denne dag.
Abisalomu ali ndi moyo anadzimangira chipilala mʼchigwa cha mfumu, pakuti ankaganiza kuti, “Ine ndilibe mwana wamwamuna amene adzakhale chikumbutso changa.” Chipilalacho anachitchula dzina lake lomwe ndipo mpaka lero chimatchedwa chipilala cha Abisalomu.
19 Akima'as, Sadoks sønn, sa til Joab: La mig få springe avsted til kongen med det gledelige budskap at Herren har hjulpet ham til hans rett mot hans fiender!
Tsono Ahimaazi mwana wa Zadoki anati, “Ndiloleni ndithamange ndi kukapereka uthenga kwa mfumu kuti Yehova wayipulumutsa mʼdzanja la adani ake.”
20 Men Joab sa til ham: Ikke vil du idag bli en mann med gledelig budskap; en annen dag kan du komme med gledelig budskap; men idag vilde du ikke komme med noget gledelig budskap, siden kongens sønn er død.
Yowabu anamuwuza iye kuti, “Iwe si amene uti ukanene zimenezi lero. Ukapereka uthenga nthawi ina, koma usatero lero, chifukwa mwana wa mfumu wafa.”
21 Derefter sa Joab til kusitten: Gå og meld kongen hvad du har sett! Og kusitten bøide sig for Joab og sprang avsted.
Kenaka Yowabu anawuza Mkusi kuti, “Pita ukawuze mfumu zimene waona.” Mkusiyo anawerama pamaso pa Yowabu ndipo anathamanga kupita.
22 Men Akima'as, Sadoks sønn, tok atter til orde og sa til Joab: Det får gå som det vil, men la også mig få springe avsted efter kusitten! Joab sa: Hvorfor vil du endelig gjøre det, min sønn? Du har jo ikke noget gledelig budskap som du kunde få lønn for.
Ahimaazi mwana wa Zadoki ananenanso kwa Yowabu kuti, “Zivute zitani, chonde mundilole kuti ndipite pambuyo pa Mkusiyo.” Koma Yowabu anayankha kuti, “Mwana wanga, nʼchifukwa chiyani ukufuna kupita? Ulibe nkhani yoti ukalandire nayo mphotho.”
23 Han svarte: Det får gå som det vil, jeg springer avsted. Og han sa til ham: Så spring da! Da sprang Akima'as bort efter veien gjennem Jordansletten og kom forbi kusitten.
Iye anati, “Zivute zitani ine ndikufuna kuti ndipite.” Choncho Yowabu anati “Pita!” Ndipo Ahimaazi anathamanga kudzera njira ya ku chigwa ndipo anamupitirira Mkusi uja.
24 Imidlertid satt David mellem begge portene, og vekteren gikk på taket over porten, bort på muren, og så utover. Da fikk han se en mann som kom springende alene.
Nthawi imeneyo nʼkuti Davide atakhala pakati pa zipata ziwiri, chakubwalo ndi chamʼkati. Mlonda anakwera pa khoma nakayimirira pa denga la chipata. Anati atayangʼana, anaona munthu akuthamanga yekhayekha.
25 Vekteren ropte og meldte det til kongen. Da sa kongen: Er han alene, så er det et gledelig budskap i hans munn. Og han kom nærmere og nærmere.
Mlonda uja anapita kwa mfumu ndipo anafotokoza. Mfumu inati, “Ngati ali yekha ali ndi nkhani yabwino” Ndipo munthuyo anayandikira.
26 Da så vekteren en annen mann som kom springende, og vekteren ropte til portneren og sa: Se, det kommer en mann springende alene. Da sa kongen: Han kommer og med gledelig budskap.
Mlonda uja anaonanso munthu wina akuthamanga, ndipo anayitana woyangʼanira pa chipata, “Taona, munthu winanso akuthamanga ali yekha!” Mfumu inati, “Iye akubweretsanso nkhani yabwino.”
27 Og vekteren sa: Jeg synes den første springer så likt Akima'as, Sadoks sønn. Kongen sa: Det er en god mann; han kommer med godt budskap.
Mlonda uja anati, “Munthu akuthamanga patsogoloyo, kathamangidwe kake kakufanafana ndi mmene amathamangira Ahimaazi, mwana wa Zadoki.” Mfumu inati, “Ameneyo ndi munthu wabwino, ndipo akubwera ndi nkhani yabwino.”
28 Og Akima'as ropte til kongen: Fred! Og han kastet sig på sitt ansikt til jorden for kongen og sa: Lovet være Herren din Gud, som har gitt de menn som løftet sin hånd mot min herre kongen, i din makt!
Ndipo Ahimaazi anafuwula kwa mfumu, “Zonse zili bwino!” Iye anagwada pamaso pa mfumu nkhope yake atagunditsa pansi ndipo anati, “Yehova Mulungu wathu alemekezedwe! Iye wapereka mʼdzanja lathu anthu amene anawukira inu mbuye wanga mfumu.”
29 Og kongen sa: Står det vel til med den unge mann - med Absalom? Akima'as svarte: Jeg så det var et stort opstyr, da Joab sendte kongens tjener og mig, din tjener, avsted; men jeg vet ikke hvad det var.
Mfumu inafunsa, “Kodi mnyamata uja Abisalomu watetezedwa?” Ahimaazi anayankha, “Pamene Yowabu amati azindituma ine mtumiki wanu ndinaona chipiringu cha anthu, koma sindikudziwa chinali chiyani.”
30 Kongen sa: Gå til side og stå der! Så gikk han til side og blev stående der.
Mfumu inati, “Ima apo ndipo udikire.” Kotero iye anapita pa mbali nayima pamenepo.
31 Straks efter kom kusitten, og han sa: Min herre kongen motta det gledelige budskap at Herren idag har hjulpet dig til din rett mot alle dem som hadde reist sig imot dig!
Kenaka Mkusi uja anafika ndipo anati, “Mbuye wanga mfumu imvani nkhani yabwino! Yehova wakupulumutsani inu lero kwa onse amene anakuwukirani.”
32 Kongen spurte kusitten: Står det vel til med den unge mann - med Absalom? Kusitten svarte: Gid det må gå min herre kongens fiender og alle som reiser sig imot dig og vil gjøre ondt, som det gikk den unge mann!
Mfumu inafunsa Mkusiyo kuti, “Kodi mnyamata uja Abisalomu watetezedwa?” Mkusiyo anayankha kuti, “Adani anu mbuye wanga mfumu, pamodzi ndi anthu onse amene amakuwukirani, ziwaonekere zomwe zamuonekera mnyamatayo.”
33 Da blev kongen dypt rystet. Han gikk op på salen over porten og gråt, og mens han gikk, sa han så: Min sønn Absalom! Min sønn, min sønn Absalom! O, at jeg var død i ditt sted! Absalom, min sønn, min sønn!
Mfumu inanthunthumira. Inapita ku chipinda cha mmwamba cha pa chipata kukalira. Pamene imapita, inkati: “Iwe mwana wanga Abisalomu! Mwana wanga! Mwana wanga Abisalomu! Zikanakhala bwino ndikanafa ndine mʼmalo mwako! Iwe Abisalomu, mwana wanga, mwana wanga!”

< 2 Samuel 18 >