< 2 Krønikebok 13 >

1 I kong Jeroboams attende år blev Abia konge over Juda.
Mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yeroboamu, Abiya analowa ufumu wa Yuda,
2 Han regjerte tre år i Jerusalem. Hans mor hette Mikaja; hun var datter av Uriel og var fra Gibea. Mellem Abia og Jeroboam var det krig.
ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka zitatu. Dzina la amayi ake linali Maaka mwana wa Urieli wa ku Gibeya. Koma panali nkhondo pakati pa Abiya ndi Yeroboamu.
3 Abia begynte krigen med en hær av djerve stridsmenn, fire hundre tusen utvalgte menn; men Jeroboam stilte sig i fylking mot ham med åtte hundre tusen utvalgte menn, også djerve stridsmenn.
Abiya anapita ku nkhondo ndi asilikali odziwa bwino nkhondo 400,000, ndipo Yeroboamu anandandalitsa ankhondo, asilikali 800,000 odziwa bwino nkhondo, osankhidwa ndi amphamvu, woti amenyane naye.
4 Abia gikk op på fjellet Semara'im, som hører til Efra'im-fjellene, og trådte frem og sa: Hør på mig, Jeroboam og hele Israel!
Abiya anayima pa phiri la Zemaraimu, mʼdziko lamapiri la Efereimu, ndipo anati, “Yeroboamu ndi Aisraeli onse, tandimverani!
5 Skulde I ikke vite at Herren, Israels Gud, har gitt David kongedømmet over Israel til evig tid, ham og hans sønner, ved en saltpakt?
Kodi inu simukudziwa kuti Yehova, Mulungu wa Israeli, wapereka ufumu wa Israeli kwa Davide ndi zidzukulu zake mpaka muyaya ndiponso pangano la mchere?
6 Men Jeroboam, Nebats sønn, Salomos, Davids sønns tjener, gjorde oprør mot sin herre.
Komabe Yeroboamu mwana wa Nebati, mtumiki wa Solomoni mwana wa Davide, anawukira mbuye wake.
7 Og det samlet sig om ham en flokk løse folk og onde mennesker, og de satte sig med vold op imot Rehabeam, Salomos sønn; og Rehabeam var ung og motløs og kunde ikke stå sig mot dem.
Ndipo anthu ena achabechabe anasonkhana kwa iye ndipo anatsutsana ndi Rehobowamu mwana wa Solomoni pamene anali wamngʼono ndi wosalimba mtima ndi wopanda mphamvu kuti athe kulimbana nawo.
8 Og nu tenker I at I kan stå eder mot Herrens kongedømme, som Davids sønner har i hende, fordi I er en stor hop og har hos eder de gullkalver som Jeroboam lot gjøre forat de skulde være eders guder.
“Ndipo tsopano inu mwakonzekera kutsutsana ndi ufumu wa Yehova, umene uli mʼmanja mwa zidzukulu za Davide. Inu ndithu mulipo ankhondo ambirimbiri ndipo muli ndi ana angʼombe agolide amene Yeroboamu anapanga kuti akhale milungu yanu.
9 Har I ikke jaget bort Herrens prester, Arons sønner, og levittene og selv gjort eder prester, som folkene i hedningelandene gjør? Hver den som kommer med en ung okse og syv værer for å fylle sin hånd, han blir prest for disse guder som ikke er guder.
Koma kodi inu simunathamangitse ansembe a Yehova, ana a Aaroni ndiponso Alevi ndi kudzisankhira ansembe anuanu monga anthu ena amachitira? Aliyense amene amabwera kuti adzipatule atatenga mwana wangʼombe wamwamuna ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri amakhala wansembe wa zinthu zimene sizili milungu.
10 Men vår Gud er Herren; vi har ikke forlatt ham, og sønner av Aron tjener Herren som prester, og levittene utfører sitt arbeid;
“Koma kunena za ife, Yehova ndiye Mulungu wathu, ndipo sitinamusiye. Ansembe amene amatumikira Yehova ndi ana a Aaroni ndipo amathandizidwa ndi Alevi.
11 hver morgen og aften brenner de brennoffer og velluktende røkelse for Herren og legger frem skuebrød på bordet av rent gull og holder gull-lysestaken og dens lamper i stand og tender den hver aften; vi tar vare på hvad Herren vår Gud vil ha varetatt, men I har forlatt ham.
Mmawa uliwonse ndi madzulo aliwonse amapereka nsembe zopsereza ndi kufukiza lubani kwa Yehova. Iwo amayika buledi pa tebulo loyeretsedwa monga mwa mwambo ndipo amayatsa nyale pa zoyikapo nyale zagolide madzulo aliwonse. Ife timachita zofuna za Yehova Mulungu wathu. Koma inu mwamusiya.
12 Sannelig, Gud er med oss, han er vår fører, og vi har hans prester med larmtrompetene for å blåse til strid mot eder. I Israels barn, strid ikke mot Herren, eders fedres Gud! For det vil ikke lykkes for eder!
Mulungu ali nafe pakuti ndiye mtsogoleri wathu. Ansembe ake atanyamula malipenga, adzayimba mfuwu wankhondo kulimbana nanu. Inu Aisraeli musalimbane ndi Yehova, Mulungu wa makolo anu, pakuti simungathe kupambana.”
13 Men Jeroboam lot et bakhold dra omkring for å komme bak på dem, så de selv var foran Judas menn, og bakholdet i ryggen på dem.
Tsono Yeroboamu anali atatumiza asilikali kumbuyo mowazungulira, kotero kuti iye ali kutsogolo kwa anthu a ku Yuda, anthu owabisalira anali kumbuyo kwawo.
14 Og da Judas menn vendte sig om, fikk de se fienden både foran sig og bak sig; da ropte de til Herren, og prestene blåste i trompetene.
Asilikali a Yuda anatembenuka ndipo anaona kuti nkhondo imachitikira kutsogolo ndi kumbuyo. Ndipo iwo anafuwulira Yehova. Ansembe anayimba malipenga awo
15 Og Judas menn opløftet krigsrop; da skjedde det, at med det samme Judas menn opløftet krigsropet, da lot Gud Jeroboam og hele Israel bli slått av Abia og Juda.
ndipo asilikali a Yuda anafuwula mawu ankhondo. Atafuwula mawu ankhondowo, Mulungu anagonjetsa Yeroboamu pamodzi ndi Aisraeli onse pamaso pa Abiya ndi Yuda.
16 Israels barn flyktet for Juda, og Gud gav dem i deres hånd.
Aisraeli anathawa Ayuda. Ndipo Mulungu anawapereka mʼmanja mwawo.
17 Og Abia og hans folk voldte et stort mannefall iblandt dem, og det falt fem hundre tusen utvalgte menn av Israel.
Abiya pamodzi ndi anthu ake anapha anthu ambiri, kotero kuti Aisraeli 500,000 odziwa bwino nkhondo anaphedwa.
18 Således blev Israels barn dengang ydmyket; men Judas barn blev sterke, fordi de satte sin lit til Herren, sine fedres Gud.
Ankhondo a Israeli anagonjetsedwa pa nthawi imeneyi, ndipo ankhondo a Yuda anapambana chifukwa anadalira Yehova, Mulungu wa makolo awo.
19 Abia forfulgte Jeroboam og tok fra ham byene Betel med tilhørende småbyer og Jesana med tilhørende småbyer og Efron med tilhørende småbyer.
Abiya anathamangitsa Yeroboamu ndipo anamulanda mizinda ya Beteli, Yesana, ndi Efroni pamodzi ndi midzi yawo yozungulira.
20 Jeroboam maktet ikke mere noget så lenge Abia levde, og Herren slo ham så han døde.
Yeroboamu sanapezenso mphamvu nthawi ya Abiya. Ndipo Yehova anamukantha nafa.
21 Men Abia blev mektig. Han tok sig fjorten hustruer og fikk to og tyve sønner og seksten døtre.
Koma Abiya mphamvu zake zinakula. Iye anakwatira akazi 14 ndipo anali ndi ana aamuna 22 ndi ana aakazi 16.
22 Hvad som ellers er å fortelle om Abia, om hans ferd og hans foretagender, det er opskrevet i profeten Iddos historiebok.
Zina ndi zina zokhudza Abiya, zimene anachita ndi zimene anayankhula, zinalembedwa mʼbuku la mbiri ya mneneri Ido.

< 2 Krønikebok 13 >