< Isambulo 21 >

1 Ngasengibona izulu elitsha lomhlaba omutsha; ngoba izulu lokuqala lomhlaba wokuqala kwasekudlulile, lolwandle lungasekho.
Kenaka ndinaona kumwamba kwatsopano ndi dziko lapansi latsopano pakuti kumwamba koyamba ndi dziko lapansi loyamba zinapita ndipo kunalibenso nyanja ina iliyonse.
2 Mina Johane ngasengibona umuzi ongcwele, iJerusalema entsha, usehla uvela kuNkulunkulu ezulwini, ulungisiwe njengomakoti ececiselwe umkakhe.
Ndinaona mzinda wopatulika, Yerusalemu watsopano, ukutsika kuchokera kumwamba kwa Mulungu, utakonzedwa ngati mkwatibwi wovala zokongola kukonzekera mwamuna wake.
3 Ngasengisizwa ilizwi elikhulu livela ezulwini, lisithi: Khangela, ithabhanekele likaNkulunkulu lisebantwini, njalo uzahlala labo, futhi bona bazakuba ngabantu bakhe, loNkulunkulu uqobo uzakuba labo, enguNkulunkulu wabo;
Ndipo ndinamva mawu ofuwula kuchokera ku Mpando Waufumu kuti, “Taonani! Malo wokhalapo Mulungu ali pakati pa anthu, ndipo Iye adzakhala ndi anthuwo. Iwo adzakhala anthu ake ndipo Mulungu mwini adzakhala nawo nakhala Mulungu wawo.
4 njalo uNkulunkulu uzakwesula zonke izinyembezi emehlweni abo, lokufa kakusayikuba khona; kumbe ukulila, kumbe ukukhala, loba ubuhlungu abusayikuba khona; ngoba izinto zakuqala sezidlulile.
‘Mulungu adzapukuta misozi yonse mʼmaso mwawo. Sikudzakhalanso imfa kapena kukhuza maliro kapena kulira kapena ululu popeza zakale zapita.’”
5 Wasesithi ohlezi esihlalweni sobukhosi: Khangela, ngenza zonke izinto zibentsha. Wasesithi kimi: Bhala; ngoba lamazwi aqinisile njalo athembekile.
Amene anakhala pa mpando waufumuyo anati, “Ndikulenga zinthu zonse zikhale zatsopano!” Ndipo anati, “Lemba izi, pakuti mawu awa ndi okhulupirika ndi woona.”
6 Wasesithi kimi: Sekwenzakele. Mina nginguAlfa loOmega, ukuqala lokucina. Mina ngizamnika owomileyo okuvela emthonjeni wamanzi empilo ngesihle.
Iye anandiwuza kuti, “Kwatha. Ine ndine Alefa ndi Omega, Woyamba ndi Wotsiriza. Kwa onse akumva ludzu, ndidzawapatsa zakumwa zaulere zochokera ku kasupe wamadzi amoyo.
7 Onqobayo uzakudla ilifa lazo zonke izinto; njalo ngizakuba nguNkulunkulu wakhe, laye abe yindodana yami.
Iye amene adzapambane adzalandira zonsezi, ndipo ndidzakhala Mulungu wake ndi Iye adzakhala mwana wanga.
8 Kodwa amagwala labangakholwayo labanengekayo lababulali leziphingi labathakathi labakhonza izithombe labo bonke abaqambimanga, bazakuba lesabelo sabo echibini elivutha umlilo lesibabule, okuyikufa kwesibili. (Limnē Pyr g3041 g4442)
Koma amantha, osakhulupirira, okonda zonyansa, opha anthu, achiwerewere, amatsenga, opembedza mafano ndi abodza, malo awo adzakhala nyanja yamoto ya sulufule wotentha. Iyi ndi imfa yachiwiri.” (Limnē Pyr g3041 g4442)
9 Kwasekusiza kimi enye yengilosi eziyisikhombisa ezazilemiganu eyisikhombisa egcwele izinhlupheko zokucina eziyisikhombisa, yasikhuluma lami, isithi: Woza lapha, ngizakutshengisa umakoti, umkaWundlu.
Mmodzi wa angelo asanu ndi awiri aja, anali ndi mbale zisanu ndi ziwiri zodzaza ndi miliri yotsiriza isanu ndi iwiri anandiwuza kuti, “Bwera, ine ndidzakuonetsa mkwatibwi wa Mwana Wankhosa.”
10 Yasingithwala ngikuMoya yaya entabeni enkulu lende, yasingitshengisa umuzi omkhulu, iJerusalema engcwele, usehla uvela ezulwini kuNkulunkulu,
Ndipo anandinyamula mwa Mzimu Woyera kupita nane ku phiri lalikulu ndi lalitali nandionetsa mzinda wopatulika, Yerusalemu ukutsika kuchokera kumwamba kwa Mulungu.
11 ulenkazimulo kaNkulunkulu; ukukhanya kwawo kwakunjengelitshe eliligugu elikhulukazi njengelitshe ijaspi, likhanyisa njengekristali;
Unawala ndi ulemerero wa Mulungu, ndipo kuthwanima kwake kunali ngati mwala wamtengowapatali, ngati jasipa; woyera ngati krustalo.
12 njalo ulomduli omkhulu lophakemeyo, ulamasango alitshumi lambili, lemasangweni ingilosi ezilitshumi lambili, lamabizo ebhalwe kiwo, angawezizwe ezilitshumi lambili zabantwana bakoIsrayeli.
Mzindawo unali ndi mpanda waukulu ndi wautali, unali ndi zipata khumi ndi ziwiri, ndipo panali angelo khumi ndi awiri. Pa chipata chilichonse panayima mngelo. Pa chipata chilichonse panalembedwa dzina la fuko la Israeli.
13 Empumalanga kwakulamasango amathathu; enyakatho, amasango amathathu; eningizimu, amasango amathathu; lentshonalanga, amasango amathathu.
Kummawa kunali zipata zitatu, kumpoto zitatu, kummwera zitatu ndi kumadzulo zitatu.
14 Lomduli womuzi wawulezisekelo ezilitshumi lambili, lakuzo amabizo abaphostoli abalitshumi lambili beWundlu.
Mpanda wa mzindawu unali ndi maziko khumi ndi awiri ndipo pa mazikopo panali mayina khumi ndi awiri a atumwi a Mwana Wankhosa.
15 Lowayekhuluma lami wayelomhlanga wegolide, ukuze alinganise umuzi, lamasango awo, lomduli wawo.
Mngelo amene ankayankhula nane uja anali ndi ndodo yagolide yoyezera mzindawo, zipata zake ndi mpanda wake.
16 Umuzi wawumiswe walingana inhlangothi zozine, lobude bawo babungangobubanzi. Waselinganisa umuzi ngomhlanga waba ngamastadiyu azinkulungwane ezilitshumi lambili; ubude lobubanzi lokuphakama kwawo kuyalingana.
Mzindawo unamangidwa mofanana kutalika kwake, mulitali ndi mulifupi munali mofanana. Anayeza mzindawo ndi ndodo ija ndipo anapeza kuti mulitali, mulifupi ndi msinkhu wake kutalika kwake kunali makilomita 2,200.
17 Waselinganisa umduli wawo, ingalo ezilikhulu lamatshumi amane lane, isilinganiso somuntu, esingesengilosi.
Anayesa mpanda uja ndipo kuchindikala kwake kunali kopitirirapo mamita 65 monga mwa muyeso wa anthu umene mngelo anagwiritsa ntchito.
18 Njalo kwakulesakhiwo somduli wawo phakathi, ijaspi; lomuzi uligolide elicwengekileyo, njengengilazi ehlanzekileyo.
Mpandawo unapangidwa ndi yasipa, ndipo mzindawo unali wagolide oyengeka owala ngati galasi.
19 Lezisekelo zomduli womuzi zaziceciswe ngalo lonke ilitshe eliligugu. Isisekelo sokuqala, ijaspi; esesibili, isafire; esesithathu, ikalkedoni; esesine, i-emeraldi;
Maziko a mpanda wa mzindawo anali okongoletsedwa ndi miyala yamtengowapatali ya mtundu uliwonse. Maziko oyamba anali yasipa, achiwiri anali safiro, achitatu ndi kalikedo, achinayi ndi simaragido,
20 esesihlanu, isaridonikisi; esesithupha, isardiyusi; esesikhombisa, ikrisolite; esesificaminwembili, ibherule; esesificamunwemunye, itopazi; esetshumi, ikrisoprase; esetshumi lanye, ihiyakinte; esetshumi lambili, i-ametiste.
achisanu ndi sardiyo, achisanu ndi chiwiri ndi krusolito, achisanu ndi chitatu ndi berulo, achisanu ndi chinayi ndi topaziyo, a khumi ndi krusoprazo, a khumi ndi chimodzi ndi huakito, a khumi ndi chiwiri ndi emetusto.
21 Lamasango alitshumi lambili angamapharele alitshumi lambili; yilelo ngalinye ngalinye lamasango lilipharele linye; njalo isitalada somuzi sasiligolide elicwengekileyo, njengengilazi ekhanyayo.
Zipata khumi ndi ziwiri zija zinapangidwa ndi ngale, chipata chilichonse chinapangidwa ndi ngale imodzi. Misewu ya mzindawo inali yopangidwa ndi golide oyengeka, owala ngati galasi.
22 Njalo kangibonanga ithempeli phakathi kwawo; ngoba iNkosi uNkulunkulu uSomandla ulithempeli lawo, leWundlu.
Ine sindinaone Nyumba ya Mulungu iliyonse mu mzindawo chifukwa Ambuye Mulungu Wamphamvuzonse ndi Mwana Wankhosa ndiwo Nyumba yake.
23 Lomuzi kawusweli langa, kumbe inyanga, ukuthi kukhanyise kuwo; ngoba inkazimulo kaNkulunkulu iyawukhanyisa, lesibane sawo liWundlu;
Palibe chifukwa choti dzuwa kapena mwezi ziwale popeza mu mzindawo ulemerero wa Mulungu ndiwo umawalamo ndipo nyale yake ndi Mwana Wankhosa uja.
24 lezizwe zabasindisiweyo zizahamba ekukhanyeni kwawo; lamakhosi omhlaba aletha ubukhosi lodumo lwawo kuwo;
Mitundu ya anthu idzayenda mʼkuwala kwake ndipo mafumu a dziko lapansi adzabweretsa ulemerero wawo mu mzindamo.
25 lamasango awo kawasoze avalwe emini, ngoba kakuyikuba khona ubusuku lapho;
Zipata zake sizidzatsekedwa ngakhale tsiku limodzi lomwe pakuti sikudzakhala usiku kumeneko.
26 njalo bazaletha kuwo ubukhosi lodumo lwezizwe;
Ulemerero ndi ulemu wa mitundu ya anthu adzapita nazo kumeneko.
27 njalo kakusoze kwangena lolulodwa ulutho olungcolileyo kuwo, njalo lokwenza okunengekayo lamanga; ngaphandle kwabalotshiweyo egwalweni lwempilo lweWundlu.
Kanthu kosayeretsedwa sikadzalowamo, kuphatikizanso aliyense wochita zinthu zochititsa manyazi ndi zachinyengo, koma okhawo amene mayina awo alembedwa mʼbuku lamoyo la Mwana Wankhosa.

< Isambulo 21 >