< Amanani 5 >

1 INkosi yasikhuluma kuMozisi isithi:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Laya abantwana bakoIsrayeli ukuthi bakhuphe enkambeni wonke umlephero, laye wonke olokugobhoza, laye wonke ongcolileyo ngofileyo.
“Lamula Aisraeli kuti achotse mu msasa aliyense amene ali ndi matenda opatsirana a pa khungu kapena matenda otuluka madzi mʼthupi a mtundu uliwonse, kapena aliyense wodetsedwa chifukwa cha munthu wakufa.
3 Kusukela kowesilisa kusiya kowesifazana lizabakhupha, kuze kube ngaphandle kwenkamba lizabakhupha, ukuze bangangcolisi izinkamba zabo, engihlala phakathi kwazo.
Muchotse amuna komanso amayi ndipo muwatulutsire kunja kwa msasa kuti asadetse msasa wawo kumene Ine ndimakhala pakati pawo.”
4 Abantwana bakoIsrayeli basebesenza njalo, babakhupha baze baba ngaphandle kwenkamba; njengokutsho kweNkosi kuMozisi, benza njalo abantwana bakoIsrayeli.
Aisraeli anachitadi zimenezi. Anawatulutsira kunja kwa msasa monga momwe Yehova analamulira Mose.
5 INkosi yasikhuluma kuMozisi isithi:
Yehova anati kwa Mose,
6 Tshono ebantwaneni bakoIsrayeli uthi: Indoda kumbe umfazi, uba besenza loba yisiphi isono somuntu, ngokuphambeka isiphambeko eNkosini, lowomuntu ulecala.
“Uza Aisraeli kuti, ‘Pamene mwamuna kapena mayi walakwira mnzake mwa njira iliyonse, ndiye kuti ndi wosakhulupirika pamaso pa Yehova. Munthuyo ndi wochimwa ndithu ndipo
7 Njalo bazavuma isono sabo abasenzileyo, abesehlawula icala lakhe ngokupheleleyo kwalo, engezelele phezu kwalo ingxenye yesihlanu yalo, anike lowo alecala kuye.
ayenera kuwulula tchimo limene anachitalo. Ayenera kubweza zonse zimene anawononga, ndipo awonjezerepo chimodzi mwa magawo asanu ndi kuzipereka kwa munthu amene anamulakwirayo.
8 Kodwa uba lowomuntu engelamhlengi oyisihlobo okungahlawulwa kuso icala, icala lizahlawulwa eNkosini kube ngokompristi, ngaphandle kwenqama yenhlawulo yokuthula, azamenzela inhlawulo yokuthula ngayo.
Ngati wolakwiridwayo alibe mʼbale komwe kungapite zinthu zobwezedwazo, zinthuzo zikhale za Yehova ndipo azipereke kwa wansembe, pamodzi ndi nkhosa yayimuna ya nsembe yopepesera tchimo lake.
9 Lawo wonke umnikelo wazo zonke izinto ezingcwele zabantwana bakoIsrayeli, abaziletha kumpristi, uzakuba ngowakhe.
Zopereka zonse zopatulika zomwe Aisraeli abwera nazo kwa wansembe zikhale za wansembeyo.
10 Lezinto ezingcwele zawo wonke umuntu zizakuba ngezakhe; lokhu loba ngubani akunika umpristi kuzakuba ngokwakhe.
Mphatso zilizonse zopatulika ndi za munthuyo, koma zomwe wapereka kwa wansembe ndi za wansembeyo.’”
11 INkosi yasikhuluma kuMozisi isithi:
Kenaka Yehova anawuza Mose kuti,
12 Tshono ebantwaneni bakoIsrayeli uthi kubo: Loba yiyiphi indoda, uba umkayo eduha, ngokungathembeki kuyo enze isenzo sokungathembeki,
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati mkazi wa munthu wina ayenda njira yosayenera nakhala wosakhulupirika kwa mwamuna wake,
13 lendoda ilala laye ngobudoda bokuhlangana, njalo kufihlakale emehlweni endoda yakhe, angabonwa, yena ungcolisiwe, njalo kungelamfakazi omelana laye, futhi yena engabanjwanga,
nakagonana ndi mwamuna wina koma mwamuna wake wosadziwa, ndipo palibe wina aliyense wadziwa za kudzidetsa kwake (pakuti palibe mboni yomuneneza chifukwa sanagwidwe akuchita),
14 lomoya wobukhwele ufike phezu kwayo, futhi ibe lobukhwele ngomkayo, njalo yena engcolisiwe, loba umoya wobukhwele ufike phezu kwayo, futhi ibe lobukhwele ngomkayo, lanxa yena engangcolanga,
mwamuna wake ndi kuyamba kuchita nsanje ndi kukayikira mkazi wakeyo kuti ndi wodetsedwa, komanso ngati amuchitira nsanje ndi kumukayikira ngakhale asanadzidetse,
15 indoda izaletha umkayo kumpristi, imlethele umnikelo wakhe, okwetshumi kwe-efa lempuphu yebhali; kayiyikuthela amafutha kuyo, ingabeki inhlaka phezu kwayo, ngoba kungumnikelo wokudla wobukhwele, umnikelo wokudla wesikhumbuzo, ukukhumbuza ububi.
apite naye mkaziyo kwa wansembe. Ndipo popita atengenso gawo lakhumi la chopereka chaufa wa barele wokwana kilogalamu imodzi mʼmalo mwa mkaziyo. Asathire mafuta pa nsembeyo kapena lubani, chifukwa ndi nsembe ya chopereka ya chakudya yopereka chifukwa cha nsanje, nsembe yozindikiritsa tchimo.’”
16 Umpristi uzasondeza-ke owesifazana, ammise phambi kweNkosi.
“‘Wansembe abwere naye mkaziyo ndi kumuyimitsa pamaso pa Yehova.
17 Umpristi athathe amanzi angcwele embizeni yebumba, lompristi athathe okothuli oluphansi ethabhanekeleni, akufake emanzini.
Ndipo wansembeyo atenge madzi oyera mʼmbiya ya dothi ndi kuyika mʼmadzimo fumbi lapansi la mʼTenti ya Msonkhano.
18 Umpristi uzamisa owesifazana phambi kweNkosi, embule ikhanda lowesifazana, abeke ezandleni zakhe umnikelo wokudla wokukhumbuza, ongumnikelo wokudla wobukhwele. Lesandleni sompristi kuzakuba lamanzi ababayo aletha isiqalekiso.
Wansembe atayimika mkaziyo pamaso pa Yehova, amumasule tsitsi lake, ndipo ayike mʼmanja mwake nsembe yozindikiritsa tchimo, nsembe yachakudya ya nsanje, wansembeyo atanyamula madzi owawa omwe amabweretsa temberero.’
19 Umpristi uzamfungisa-ke, athi kowesifazana: Uba kungelandoda elele lawe, njalo uba ungaduhelanga ekungcoleni, uphansi kwendoda yakho, khululeka emanzini la ababayo aletha isiqalekiso.
Kenaka wansembeyo alumbiritse mkaziyo ndi kuti, ‘Ngati mwamuna wina aliyense sanagonane ndi iwe ndipo sunayende njira yoyipa ndi kukhala wodetsedwa pomwe uli pa ukwati ndi mwamuna wako, madzi owawa awa omwe amabweretsa temberero asakupweteke.
20 Kodwa wena, uba uduhile, uphansi kwendoda yakho, futhi uba ungcolisiwe, lendoda yahlangana lawe, ngaphandle kwendoda yakho,
Koma ngati wayenda njira yoyipa uli pa ukwati ndi mwamuna wako ndi kudzidetsa pogonana ndi mwamuna amene si mwamuna wako,’
21 umpristi amfungise owesifazana ngesifungo sesiqalekiso, umpristi athi kuye: INkosi kayikwenze ube yisiqalekiso lesifungo phakathi kwabantu bakini, lapho iNkosi isenza ithangazi lakho liwe, lesisu sakho sikhukhumale.
pamenepo wansembe alumbiritse mkaziyo ndi mawu a matemberero ndi kumuwuza kuti, ‘Yehova achititse anthu ako kukutemberera ndi kukunyoza pamene awononga ntchafu yako ndi kutupitsa mimba yako.
22 Lamanzi la aletha isiqalekiso kawangene emibilini yakho, akwenze isisu sikhukhumale lokwenza ithangazi liwe. Owesifazana abesesithi: Ameni, Ameni.
Madzi awa obweretsa temberero alowe mʼthupi mwako ndi kutupitsa mimba yako ndi kuwononga ntchafu yako.’” “Pamenepo mkaziyo anene kuti, ‘Ameni, ameni.’”
23 Umpristi uzabhala-ke iziqalekiso lezi egwalweni, azesule ngamanzi ababayo,
“‘Wansembe alembe matemberero amenewa mʼbuku ndi kuwanyika mʼmadzi owawa aja.
24 anathise owesifazana amanzi ababayo aletha isiqalekiso, lamanzi aletha isiqalekiso azangena kuye, abe ngokubabayo.
Amwetse mkaziyo madzi owawawo omwe amabweretsa temberero, ndipo madzi amenewo adzalowa mʼmimba mwake ndi kuyambitsa ululu woopsa.
25 Umpristi uzathatha-ke esandleni sowesifazana umnikelo wokudla wobukhwele, awuzunguze umnikelo wokudla phambi kweNkosi, awusondeze elathini,
Wansembe achotse mʼmanja mwa mkaziyo nsembe yachakudya ya nsanje ija, nayiweyula pamaso pa Yehova ndi kuyipereka pa guwa lansembe.
26 umpristi acuphe isandla esigcweleyo somnikelo wokudla, sibe yisikhumbuzo sawo, asitshise elathini, lemva kwalokho amnathise owesifazana amanzi.
Tsono wansembeyo atapeko ufa dzanja limodzi kuti ukhale wachikumbutso ndi kuwutentha pa guwa lansembe. Atatha izi, amwetse mkaziyo madzi aja.
27 Esemnathisile amanzi, kuzakuthi uba engcolile, enze ngokungathembeki isenzo sokungathembeki endodeni yakhe, amanzi aletha isiqalekiso esengenile kuye abe ngokubabayo, isisu sakhe sizakhukhumala lethangazi lakhe liwe, lowesifazana uzakuba yisiqalekiso phakathi kwabantu bakibo.
Ndipo ngati mkaziyo anadzidetsadi ndi kukhala wosakhulupirika kwa mwamuna wake, pamene amwa madzi obweretsa matemberero aja, nalowa mʼmimba mwake, adzamva ululu woopsa. Mimba yake idzatupa ndi ntchafu yake idzawonongeka ndipo adzakhala wotembereredwa pakati pa anthu ake.
28 Kodwa uba owesifazana engangcolanga, kodwa ehlambulukile, uzakhululeka, uzakwemukela inhlanyelo.
Koma ngati mkaziyo sanadzidetse ndi kuti alibe tchimo, adzakhala wopanda mlandu ndipo adzabereka ana.
29 Lo ngumlayo wobukhwele, lapho umfazi eduha, ephansi kwendoda yakhe, abesengcoliswa,
“‘Limeneli ndiye lamulo la nsanje pamene mkazi wayenda njira yoyipa ndi kudzidetsa ali pa ukwati ndi mwamuna wake,
30 kumbe indoda, uba umoya wobukhwele ufika phezu kwayo ibe lobukhwele ngomkayo; immise owesifazana phambi kweNkosi, lompristi enze kuye umlayo lo wonke.
kapena pamene maganizo a nsanje abwera kwa mwamuna wake chifukwa chokayikira mkazi wakeyo. Wansembe azitenga mkazi wotere ndi kumuyimiritsa pamaso pa Yehova ndipo agwiritse ntchito lamulo lonseli kwa mkaziyo.
31 Indoda izakhululeka-ke ecaleni, kodwa lowo owesifazana uzathwala icala lakhe.
Mwamunayo adzakhala wopanda tchimo lililonse, koma mkaziyo adzasenza zotsatira za tchimo lake.’”

< Amanani 5 >